Masalimo 146 – CCL & HTB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 146:1-10

Salimo 146

1Tamandani Yehova.

Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.

2Ndidzatamanda Yehova ndi moyo wanga wonse;

ndidzayimba nyimbo zamatamando kwa Mulungu wanga nthawi yonse ya moyo wanga.

3Musamadalire mafumu,

anthu osakhalitsa, amene sangathe kupulumutsa.

4Pamene mizimu yawo yachoka, iwo amabwerera ku dothi;

zimene ankafuna kuchita zimatha tsiku lomwelo.

5Wodala ndi amene thandizo lake ndi

Mulungu wa Yakobo.

6Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi,

nyanja ndi zonse zili mʼmenemo;

Yehova, amene ndi wokhulupirika kwamuyaya.

7Iye amachitira chilungamo anthu oponderezedwa

ndipo amapereka chakudya kwa anthu anjala.

Yehova amamasula amʼndende,

8Yehova amatsekula maso anthu osaona,

Yehova amadzutsa onse amene awerama pansi,

Yehova amakonda anthu olungama.

9Yehova amasamalira alendo

ndipo amathandiza ana ndi akazi amasiye,

koma amasokoneza njira za anthu oyipa.

10Yehova ndiye Mfumu mpaka muyaya,

Mulungu wako iwe Ziyoni, pa mibado yonse.

Tamandani Yehova.

Het Boek

Psalmen 146:1-10

1Halleluja! Loof Jahweh mijn ziel! 2Zolang ik leef, wil ik Jahweh prijzen, Mijn God verheerlijken, zolang ik besta! 3Vertrouwt niet op vorsten, Op mensen, die niet kunnen helpen: 4Is hun adem heen, ze keren terug tot het stof, En het is met hun plannen gedaan. 5Gelukkig, wien de God van Jakob blijft helpen, Wiens hoop is gevestigd op Jahweh, zijn God: 6Die hemel en aarde heeft gemaakt, De zee met wat ze bevat. Jahweh, die trouw blijft voor eeuwig, 7De verdrukten verdedigt, Brood aan de hongerigen reikt, En de gevangenen bevrijdt! 8Jahweh opent de ogen der blinden, Jahweh richt de gebukten weer op; Jahweh heeft de rechtvaardigen lief, 9Jahweh draagt zorg voor de zwervers. Hij is een steun voor weduwen en wezen, Maar de bozen richt Hij te gronde: 10Jahweh is Koning voor eeuwig; Uw God, o Sion, van geslacht tot geslacht!