Masalimo 145 – CCL & JCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 145:1-21

Salimo 145

Salimo la matamando la Davide.

1Ndidzakukwezani Mulungu wanga, Mfumu yanga;

ndidzatamanda dzina lanu ku nthawi za nthawi.

2Ndidzakutamandani tsiku ndi tsiku

ndi kulemekeza dzina lanu ku nthawi za nthawi.

3Yehova ndi wamkulu ndi woyenera matamando onse;

ukulu wake palibe angawumvetsetse.

4Mʼbado wina udzayamikira ntchito yanu kwa mʼbado wina;

Iwo adzafotokoza za machitidwe anu amphamvu.

5Adzayankhula ulemerero wokongola waufumu wanu,

ndipo ine ndidzalingalira za ntchito zanu zodabwitsa.

6Iwo adzafotokoza za mphamvu ya ntchito zanu zoopsa kwambiri,

ndipo ine ndidzalengeza za ntchito zanu zazikulu.

7Adzakondwerera kuchuluka kwa ubwino wanu,

ndi kuyimba mwachimwemwe za chilungamo chanu.

8Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo,

wosakwiya msanga ndi wodzaza ndi chikondi chosasinthika.

9Yehova ndi wabwino kwa onse;

amachitira chifundo zonse zimene anazipanga.

10Zonse zimene munazipanga zidzakutamandani, Inu Yehova;

oyera mtima adzakulemekezani.

11Iwo adzafotokoza za ulemerero wa ufumu wanu

ndi kuyankhula za mphamvu yanu,

12kuti anthu onse adziwe za machitidwe anu amphamvu

ndi ulemerero wokongola wa ufumu wanu.

13Ufumu wanu ndi ufumu wamuyaya,

ndipo ulamuliro wanu ndi wosatha pa mibado yonse.

Yehova ndi wokhulupirika pa malonjezo ake onse

ndi wokonda zonse zimene Iye anazipanga.

14Yehova amagwiriziza onse amene akugwa

ndipo amakweza onse otsitsidwa.

15Maso a onse amayangʼana kwa Inu,

ndipo Inu mumawapatsa chakudya chawo pa nthawi yoyenera.

16Mumatsekula dzanja lanu

ndi kukwaniritsa zokhumba za chamoyo chilichonse.

17Yehova ndi wolungama mʼnjira zake zonse,

ndi wokonda zonse zimene anazipanga.

18Yehova ali pafupi ndi onse amene amamuyitana,

onse amene amamuyitana Iye mʼchoonadi.

19Iye amakwaniritsa zokhumba za iwo amene amamuopa;

amamva kulira kwawo ndi kuwapulumutsa.

20Yehova amayangʼana onse amene amamukonda

koma adzawononga anthu onse oyipa.

21Pakamwa panga padzayankhula zotamanda Yehova.

Cholengedwa chilichonse chitamande dzina lake loyera

ku nthawi za nthawi.

Japanese Contemporary Bible

詩篇 145:1-21

145

1-2私の王である神よ。

私は毎日、そしていつまでも、

あなたをほめたたえます。

3声の限り、偉大な主をたたえましょう。

神の偉大さは、一生かけても

窮めることができません。

4それぞれの時代に生きる人々が、

その子どもたちに、神のすばらしさを

伝えていきますように。

5そのまぶしいばかりの栄光、威光、それに奇跡を、

私は深く思い巡らします。

6だれもが、神のなさる

恐ろしいみわざについて語ります。

私はその偉大さを伝えます。

7人々は、神の恵み深さと、正しさについて歌います。

8主は優しく、あわれみ深く、すぐには怒らず、

愛にあふれておられます。

9だれにでも恵み深い主の思いやりは、

造られたすべてのものに注がれます。

10主よ。いのちあるものはみな、

あなたに感謝をささげます。

あなたの民は賛美し、

11栄光に輝くあなたの王国について語り、

その力について語り合うでしょう。

12また、主の行われた奇跡と、

栄光に包まれたご支配についても語るでしょう。

13あなたの王国に終わりはなく、

その統治は、代々限りなく続くからです。

14主は倒れた人を起こし、

あまりの重荷に身をかがめている人の

背筋を伸ばされます。

15すべての人が、あなたに助けを求め、

必要な食べ物を頂くのです。

16あなたはいつも、生きているすべての者の

願いに答えてくださいます。

17主はいつでも公平で、恵みにあふれています。

18そして、真心から願い出る人の

そば近くにいてくださるのです。

19主は、敬虔な心で信頼を寄せる人々の願いを、

かなえてくださいます。

助けを呼び求める声を聞いてくださいます。

20主を慕う人はみな守られ、悪者どもは滅ぼされます。

21私は主をほめたたえ、世界中の人に、

神のきよい御名をいつまでもあがめるようにと

呼びかけます。