Masalimo 132 – CCL & HTB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 132:1-18

Salimo 132

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

1Inu Yehova, kumbukirani Davide

ndi mavuto onse anapirira.

2Iye analumbira kwa Yehova

ndi kulonjeza kwa Wamphamvu wa Yakobo kuti,

3“Sindidzalowa mʼnyumba mwanga

kapena kugona pa bedi langa:

4sindidzalola kuti maso anga agone,

kapena zikope zanga ziwodzere,

5mpaka nditamupezera malo Yehova,

malo okhala a Wamphamvu wa Yakobo.”

6Zoonadi, tinamva za Bokosi la Chipangano ku Efurata,

tinalipeza mʼminda ya ku Yaara:

7“Tiyeni tipite ku malo ake okhalamo;

tiyeni tikamulambire pa mapazi ake.

8‘Dzukani Yehova, ndipo bwerani ku malo anu opumulira,

Inuyo ndi Bokosi la Chipangano limene limafanizira mphamvu zanu.

9Ansembe anu avekedwe chilungamo;

anthu anu oyera mtima ayimbe nyimbo mwachimwemwe.’ ”

10Chifukwa cha Davide mtumiki wanu,

musakane wodzozedwa wanu.

11Yehova analumbira kwa Davide,

lumbiro lotsimikizika kuti Iye sadzasintha:

“Mmodzi wa ana ako

ndidzamuyika pa mpando waufumu;

12ngati ana ako azisunga pangano langa

ndi malamulo amene ndiwaphunzitsa,

pamenepo ana awo adzakhala pa mpando

wako waufumu kwamuyaya ndi muyaya.”

13Pakuti Yehova wasankha Ziyoni,

Iye wakhumba kuti akhale malo ake okhalamo:

14“Awa ndi malo anga opumapo ku nthawi za nthawi;

ndidzakhala pano pa mpando waufumu, pakuti ndakhumba zimenezi.

15Ndidzadalitsa mzindawu ndi zinthu zambiri;

anthu ake osauka ndidzawakhutitsa ndi chakudya.

16Ndidzaveka ansembe ake chipulumutso,

ndipo anthu ake oyera mtima adzayimba nthawi zonse nyimbo zachimwemwe.

17“Pano ndidzachulukitsa mphamvu za Davide

ndi kuyikapo nyale ya wodzozedwa wanga.

18Ndidzaveka adani ake manyazi,

koma chipewa chaufumu pamutu pake chidzakhala chowala.”

Het Boek

Psalmen 132:1-18

1Een bedevaartslied. Blijf David gedenken, o Jahweh, En alle moeite, die hij zich troostte, 2Omdat hij Jahweh had gezworen, Jakobs Sterke had beloofd: 3Ik zal mijn woontent niet ingaan, Mijn legerstede niet beklimmen, 4Mijn ogen geen slaap gunnen, Mijn wimpers geen sluimer: 5Voordat ik een plaats heb gevonden voor Jahweh, Voor Jakobs Sterke een woning! 6Zie, wij hoorden, dat zij in Efráta was, Wij vonden haar weer in de velden van Jáar; 7Laat ons naar zijn Woning gaan, En ons voor zijn voetbank werpen! 8Jahweh, trek op naar uw rustplaats, Gij zelf en de ark uwer glorie! 9Mogen uw priesters met gerechtigheid worden bekleed, En uw vromen een jubellied zingen! 10Om wille van David, uw dienaar, Wijs het gebed van uw gezalfde niet af! 11En Jahweh heeft aan David gezworen, Een trouwe Belofte, waarvan Hij niet afwijkt: Van de vrucht van uw schoot Zet Ik er een op uw troon! 12En zo uw zonen mijn verbond onderhouden, En de vermaningen, die Ik hun gaf, Dan zullen ook hùn zonen voor eeuwig Op uw troon blijven zitten! 13Want Jahweh heeft Sion verkoren, En Zich tot woning begeerd! 14“Hij is mijn rustplaats voor eeuwig; Hier wil Ik wonen, want hèm heb Ik verkoren! 15Zijn mondkost zal Ik ruimschoots zegenen, Zijn armen verzadigen met brood; 16Zijn priesters zal Ik met heil bekleden. Zijn vromen zullen een jubellied zingen! 17Hier zal Ik David een Hoorn doen ontspruiten, Een lamp ontsteken voor mijn Gezalfde; 18Zijn vijanden zal Ik met schande bedekken, Mijn kroon zal schitteren op zijn hoofd!”