Masalimo 125 – CCL & JCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 125:1-5

Salimo 125

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

1Amene amadalira Yehova ali ngati phiri la Ziyoni,

limene silingagwedezeke koma ndi lokhala mpaka muyaya.

2Monga mapiri azungulira Yerusalemu,

momwemonso Yehova azungulira anthu ake

kuyambira tsopano mpaka muyaya.

3Ndodo yaufumu ya anthu oyipa sidzakhala

pa dziko limene lapatsidwa kwa anthu olungama,

kuti anthu olungamawo

angachite nawonso zoyipa.

4Yehova chitirani zabwino amene ndi abwino,

amene ndi olungama mtima

5Koma amene amatembenukira ku njira zokhotakhota,

Yehova adzawachotsa pamodzi ndi anthu ochita zoyipa.

Mtendere ukhale pa Israeli.

Japanese Contemporary Bible

詩篇 125:1-5

125

1主を信頼する人は、シオンの山のように、

どのような状況でも動じません。

2エルサレムがその周囲の山々に守られているように、

主もご自分の民を取り囲んで、守ってくださいます。

3神を信じて従っている人々を悪者どもが支配し、

悪事を押しつけるようなことが

あってはならないからです。

4ああ主よ、心のまっすぐな

正しい人々を恵んでください。

5そして、悪者どもは、処刑場へ連れ去ってください。

イスラエルに平和がありますように。