Masalimo 124 – CCL & NASV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 124:1-8

Salimo 124

Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

1Akanapanda kukhala mbali yathu Yehova,

anene tsono Israeli,

2akanapanda kukhala mbali yathu Yehova,

potiwukira anthuwo,

3iwo atatipsera mtima,

akanatimeza amoyo;

4chigumula chikanatimiza,

mtsinje ukanatikokolola,

5madzi a mkokomo

akanatikokolola.

6Atamandike Yehova,

amene sanalole kuti tikhale chakudya cha mano awo.

7Moyo wathu wawonjoka ngati mbalame

yokodwa mu msampha wa mlenje;

msampha wathyoka,

ndipo ife tapulumuka.

8Thandizo lathu lili mʼdzina la Yehova

wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.

New Amharic Standard Version

መዝሙር 124:1-8

መዝሙር 124

የእስራኤል አዳኝ

የዳዊት መዝሙረ መዓርግ።

1እስራኤል እንዲህ ይበል፤

እግዚአብሔር ከእኛ ጋር ባይሆን ኖሮ፣

2ሰዎች በእኛ ላይ በተነሡ ጊዜ፣

እግዚአብሔር ከእኛ ጋር ባይሆን ኖሮ፣

3ቍጣቸው በላያችን በነደደ ጊዜ፣

በቁመናችን በዋጡን ነበር፤

4ጐርፍ ባጥለቀለቀን፣

ፈረሰኛው ውሃ ባሰጠመን፣

5ደራሽ ውሃም ጠራርጎ በወሰደን ነበር።

6በጥርሳቸው ከመዘንጠል የጠበቀን፣

እግዚአብሔር ይባረክ።

7ነፍሳችን እንደ ወፍ፣

ከዐዳኝ ወጥመድ አመለጠች፤

ወጥመዱ ተሰበረ፤

እኛም አመለጥን።

8የሰማይና የምድር ፈጣሪ፣

የእግዚአብሔር ስም ረዳታችን ነው።