Masalimo 121 – CCL & HTB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 121:1-8

Salimo 121

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

1Ndikweza maso anga ku mapiri;

kodi thandizo langa limachokera kuti?

2Thandizo langa limachokera kwa Yehova,

wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.

3Sadzalola kuti phazi lako literereke;

Iye amene amakusunga sadzawodzera.

4Taonani, Iye amene amasunga Israeli

sadzawodzera kapena kugona.

5Yehova ndiye amene amakusunga;

Yehova ndiye mthunzi wako ku dzanja lako lamanja.

6Dzuwa silidzakupweteka nthawi ya masana,

kapena mwezi nthawi ya usiku.

7Yehova adzakuteteza ku zoyipa zonse;

adzasunga moyo wako.

8Yehova adzayangʼanira kutuluka kwako ndi kulowa kwako;

kuyambira tsopano mpaka muyaya.

Het Boek

Psalmen 121:1-8

1Een bedevaartslied. Ik hef mijn ogen omhoog naar de bergen: “Vanwaar komt mijn hulp?” 2Mijn hulp komt van Jahweh, Die hemel en aarde heeft gemaakt! 3Neen, Hij laat uw voeten niet struikelen, Hij slaapt niet, uw Wachter; 4Neen, Hij sluimert noch dommelt, Israëls Beschermer! 5Jahweh is uw Behoeder, Uw schaduw aan uw rechterhand: 6Overdag zal de zon u niet hinderen, En de maan niet des nachts. 7Jahweh behoedt u voor iedere ramp, Hij is bezorgd voor uw leven; 8Jahweh waakt over uw komen en gaan Van nu af tot in eeuwigheid.