Masalimo 118 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 118:1-29

Salimo 118

1Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino;

pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.

2Israeli anene kuti:

“Chikondi chake ndi chosatha.”

3Banja la Aaroni linene kuti,

“Chikondi chake ndi chosatha.”

4Iwo amene amaopa Yehova anene kuti:

“Chikondi chake ndi chosatha.”

5Ndili mʼmasautso anga ndinalirira Yehova,

ndipo Iye anayankha pondichotsa mʼmasautsowo.

6Yehova ali nane; sindidzachita mantha.

Munthu angandichite chiyani?

7Yehova ali nane; Iye ndiye thandizo langa.

Ndidzayangʼana adani anga mwachipambano.

8Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova

kusiyana ndi kudalira munthu.

9Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova

kusiyana ndi kudalira mafumu.

10Anthu a mitundu yonse anandizinga,

koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.

11Anandizinga mbali zonse,

koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.

12Anandizinga ngati njuchi,

koma anatha msanga ngati moto wapaminga;

mʼdzina la Yehova ndinawawononga.

13Anandikankha uku ndi uko ndipo ndinali pafupi kugwa,

koma Yehova anandithandiza.

14Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga;

Iye wakhala chipulumutso changa.

15Mfuwu wachimwemwe ndi chipambano

ukumveka mʼmatenti a anthu olungama mtima kuti:

“Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!

16Dzanja lamanja la Yehova latukulidwa mmwamba

Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!”

17Sindidzafa koma ndidzakhala ndi moyo

ndipo ndidzalalika za ntchito ya Yehova.

18Yehova wandilanga koopsa,

koma sanandipereke ku imfa.

19Tsekulireni zipata zachilungamo,

kuti ndifike kudzayamika Yehova.

20Ichi ndicho chipata cha Yehova

chimene olungama mtima okha adzalowerapo.

21Ndidzakuyamikani chifukwa Inu munandiyankha;

mwakhala chipulumutso changa.

22Mwala umene amisiri omanga nyumba anawukana

wasanduka wapangodya;

23Yehova ndiye wachita zimenezi

ndipo nʼzodabwitsa pamaso pathu.

24Lero ndiye tsiku limene Yehova walipanga;

tiyeni tikondwere ndi kusangalala nalo.

25Inu Yehova, tipulumutseni;

Yehova, tipambanitseni.

26Wodala amene akubwera mʼdzina la Yehova.

Tikukudalitsani kuchokera ku nyumba ya Yehova.

27Yehova ndi Mulungu,

ndipo kuwala kwake kwatiwunikira Ife.

Lowani nawo pa mʼdipiti wa ku chikondwerero mutanyamula nthambi mʼdzanja lanu,

mpaka ku nyanga za guwa.

28Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakuyamikani;

Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakukwezani.

29Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino;

pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

诗篇 118:1-29

第 118 篇

为胜利而感恩

1你们要称谢耶和华,

因为祂是美善的,

祂的慈爱永远长存。

2以色列人说:

“祂的慈爱永远长存。”

3亚伦家说:

“祂的慈爱永远长存。”

4愿那些敬畏耶和华的人说:

“祂的慈爱永远长存。”

5我在苦难中求告耶和华,

祂就答应我,救我脱离困境。

6有耶和华与我同在,

我必不惧怕,

人能把我怎么样?

7耶和华与我同在,帮助我,

我必看见那些恨我的人一败涂地。

8投靠耶和华胜过倚靠人。

9投靠耶和华胜过倚靠权贵。

10列国围住我,

但我靠着耶和华消灭了他们。

11他们四面围住我,

但我靠着耶和华消灭了他们。

12他们如蜜蜂围住我,

然而他们必像燃烧的荆棘,

转瞬消逝;

我靠着耶和华必消灭他们。

13我受到猛烈的攻击,

几乎要倒下了,

但耶和华帮助了我。

14耶和华是我的力量,

是我的诗歌;

祂拯救了我。

15义人的帐篷里传出胜利的欢呼声:

“耶和华伸出右手施展了大能!

16耶和华高举右手,

耶和华的右手施展了大能!”

17我必不至于死,

我要活着,

并要述说耶和华的作为。

18耶和华虽然重重地惩罚我,

却没有置我于死地。

19给我打开圣殿的门吧,

我要进去称谢耶和华。

20这是耶和华的门,

义人都可以进去。

21耶和华啊!我称谢你,

因为你听了我的祷告,

拯救了我。

22工匠丢弃的石头已成了房角石。

23这是耶和华的作为,

在我们看来奇妙莫测。

24这是耶和华得胜的日子,

我们要欢喜快乐。

25耶和华啊,求你拯救我们;

耶和华啊,求你使我们亨通。

26奉耶和华之名而来的当受称颂!

我们要在耶和华的殿中祝福你们。

27耶和华是上帝,

祂的光照亮我们。

要用绳索拴住祭牲,

牵到祭坛的角那里。

28你是我的上帝,我要称谢你;

你是我的上帝,我要尊崇你。

29你们要称谢耶和华,

因为祂是美善的,

祂的慈爱永远长存。