Masalimo 108 – CCL & NEN

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 108:1-13

Salimo 108

Nyimbo. Salimo la Davide.

1Mtima wanga ndi wokhazikika, Inu Mulungu;

ndidzayimba nyimbo, inde ndidzayimba nyimbo zotamanda ndi moyo wanga wonse.

2Dzukani, zeze ndi pangwe!

Ine ndidzadzutsa mʼbandakucha.

3Ndidzakutamandani Yehova, pakati pa anthu a mitundu ina;

ndidzayimba za Inu pakati pa anthu a mitundu ina.

4Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu, kutalika kwake kuposa kumwamba;

kukhulupirika kwanu kumafika mlengalenga.

5Kwezekani Inu Mulungu, kuposa mayiko akumwamba,

ndipo ulemerero wanu uphimbe dziko lonse lapansi.

6Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja

kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.

7Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika:

“Mwachipambano Ine ndidzagawa Sekemu

ndipo ndidzayesa chigwa cha Sukoti.

8Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso;

Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera,

Yuda ndi ndodo yanga yaufumu.

9Mowabu ndi mbale yanga yosambiramo

ndidzaponya nsapato zanga pa Edomu;

ndidzafuwula mopambana pa Filisitiya.”

10Ndani adzandifikitsa ku mzinda wotetezedwa?

Ndani adzanditsogolera ku Edomu?

11Kodi sindinu Mulungu, Inu amene mwatikana

ndipo simuperekezanso magulu athu ankhondo?

12Tithandizeni ife kulimbana ndi mdani,

pakuti thandizo la munthu ndi lopanda pake.

13Chifukwa cha Mulungu wathu, ife tidzapeza chipambano,

ndipo adzapondereza pansi adani athu.

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Zaburi 108:1-13

Zaburi 108

Kuomba Msaada Dhidi Ya Adui

(Zaburi 57:7-11; 60:5-12)

Wimbo. Zaburi ya Daudi.

1108:1 Za 112:7; 119:30, 112; 18:49Ee Mungu, moyo wangu ni thabiti;

nitaimba na kusifu kwa moyo wangu wote.

2108:2 Ay 21:12Amka, kinubi na zeze!

Nitayaamsha mapambazuko.

3Nitakusifu wewe, Ee Bwana, katikati ya mataifa;

nitaimba habari zako, katikati ya jamaa za watu.

4108:4 Hes 14:18; Kum 7:9; Kut 34:6; Za 36:5; Mik 7:18-20Kwa maana upendo wako ni mkuu, ni juu kuliko mbingu;

uaminifu wako unazifikia anga.

5108:5 Za 8:1; 57:5Ee Mungu, utukuzwe juu ya mbingu,

utukufu wako na uenee duniani kote.

6108:6 Ay 40:14Tuokoe na utusaidie kwa mkono wako wa kuume,

ili wale uwapendao wapate kuokolewa.

7108:7 Za 89:35; 68:35; 102:19; Mwa 12:6; 33:17Mungu amenena kutoka patakatifu pake:

“Nitaigawa Shekemu kwa ushindi

na kulipima Bonde la Sukothi.

8108:8 Za 78:68; Mwa 49:10Gileadi ni yangu, Manase ni yangu,

Efraimu ni kofia yangu ya chuma,

nayo Yuda ni fimbo yangu ya utawala.

9108:9 Mwa 19:37; 2Sam 8:1, 13-14Moabu ni sinia langu la kunawia,

juu ya Edomu natupa kiatu changu;

nashangilia kwa kushindwa kwa Ufilisti.”

10108:10 Za 60:9Ni nani atakayenipeleka hadi mji wenye ngome?

Ni nani atakayeniongoza hadi nifike Edomu?

11108:11 Za 44:9Ee Mungu, si ni wewe uliyetukataa sisi,

na hutoki tena na majeshi yetu?

12108:12 Isa 10:3; 30:3, 5; 31:3; Yer 2:36; 17:7; Za 118:8; 146:3Tuletee msaada dhidi ya adui,

kwa maana msaada wa mwanadamu haufai kitu.

13108:13 Za 44:5; Isa 22:5; 63:3, 6; 25:10; Mao 1:15; Mal 4:3; Ufu 14:9Kwa msaada wa Mungu tutapata ushindi,

naye atawaponda adui zetu.