Masalimo 107 – CCL & NVI-PT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 107:1-43

BUKU LACHISANU

Masalimo 107–150

Salimo 107

1Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino;

pakuti chikondi chake ndi chosatha.

2Owomboledwa a Yehova anene zimenezi

amene Iyeyo anawawombola mʼdzanja la mdani,

3iwo amene anawasonkhanitsa kuchokera ku mayiko,

kuchokera kumadzulo ndi kummawa, kuchokera kumpoto ndi kummwera.

4Ena anayendayenda mʼchipululu mopanda kanthu,

osapeza njira yopitira ku mzinda kumene akanakakhazikikako.

5Iwo anamva njala ndi ludzu,

ndipo miyoyo yawo inafowokeratu.

6Pamenepo analirira Yehova mʼmavuto awo

ndipo Iye anawapulumutsa ku masautso awo.

7Iye anawatsogolera mʼnjira yowongoka

kupita ku mzinda umene anakakhazikikako.

8Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha

ndi chifukwa cha machitidwe ake odabwitsa kwa anthu onse,

9pakuti Iye wapha ludzu la munthu womva ludzu

ndipo wakhutitsa wanjala ndi zinthu zabwino.

10Ena anakhala mu mdima ndi mʼchisoni chachikulu,

amʼndende ovutika mʼmaunyolo achitsulo,

11pakuti iwowo anawukira mawu a Mulungu

ndi kunyoza uphungu wa Wammwambamwamba.

12Kotero Iye anawapereka kuti agwire ntchito yakalavulagaga;

anagwa pansi ndipo panalibe woti awathandize.

13Pamenepo analirira Yehova mʼmasautso awo

ndipo Iye anawapulumutsa ku masautso awo.

14Yehova anawatulutsa mu mdima ndi mʼchisoni chachikulu

ndipo anadula maunyolo awo.

15Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha

ndi machitidwe ake odabwitsa kwa anthu onse,

16pakuti Iye amathyola zipata zamkuwa

ndi kudula pakati mipiringidzo yachitsulo.

17Ena anakhala zitsiru chifukwa cha njira zawo zowukira,

ndipo anamva zowawa chifukwa cha mphulupulu zawo.

18Iwo ananyansidwa ndi chakudya chilichonse

ndipo anafika pafupi ndi zipata za imfa.

19Pamenepo analirira Yehova mʼmasautso awo

ndipo Iye anawapulumutsa ku masautso awowo.

20Iye anatumiza mawu ake ndi kuwachiritsa;

anawalanditsa ku manda.

21Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha

ndi machitidwe ake odabwitsa kwa anthu.

22Apereke nsembe yachiyamiko

ndi kufotokoza za ntchito zake ndi nyimbo zachimwemwe.

23Ena anayenda pa nyanja mʼsitima zapamadzi;

Iwo anali anthu amalonda pa nyanja yayikulu.

24Anaona ntchito za Yehova,

machitidwe ake odabwitsa mʼnyanja yakuya.

25Pakuti Iye anayankhula ndi kuwutsa mphepo yamkuntho

imene inabweretsa mafunde ataliatali.

26Sitima za pamadzizo zinatukulidwa mmwamba ndi kutsikira pansi pakuya;

pamene amawonongeka, kulimba mtima kwawo kunasungunuka.

27Anachita chizungulire ndi kudzandira ngati anthu oledzera;

anali pa mapeto a moyo wawo.

28Pamenepo analirira Yehova mʼmasautso awo

ndipo Iyeyo anawapulumutsa ku masautso awo.

29Yehova analetsa namondwe,

mafunde a mʼnyanja anatontholetsedwa.

30Anali osangalala pamene kunakhala bata,

ndipo Iye anawatsogolera ku dooko limene amalifuna.

31Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha

ndi machitidwe ake odabwitsa kwa anthu.

32Akuze Iye mu msonkhano wa anthu

ndi kumutamanda pabwalo la akuluakulu.

33Iye anasandutsa mitsinje kukhala chipululu,

akasupe otuluka madzi kukhala nthaka yowuma,

34ndiponso nthaka yachonde kukhala nthaka yamchere,

chifukwa cha kuyipa kwa amene amakhala kumeneko.

35Anasandutsa chipululu kukhala mayiwe a madzi

ndi nthaka yowuma kukhala akasupe a madzi oyenda;

36kumeneko Iye anabweretsa anthu anjala kuti azikhalako,

ndipo iwo anamanga mzinda woti akhazikikeko.

37Anafesa mbewu mʼminda ndi kudzala mipesa

ndipo anakolola zipatso zochuluka;

38Yehova anawadalitsa, ndipo chiwerengero chawo chinachuluka kwambiri,

ndipo Iye sanalole kuti ziweto zawo zithe.

39Kenaka chiwerengero chawo chinachepa ndipo iwo anatsitsidwa

chifukwa cha mazunzo, mavuto ndi chisoni;

40Iye amene amakhuthulira mʼnyozo pa olemekezeka

anawachititsa kuyendayenda mʼmalo owumawo wopanda njira.

41Koma Iyeyo anakweza anthu osowa kuchoka ku masautso awo

ngati magulu a nkhosa.

42Anthu olungama mtima amaona ndi kusangalala,

koma anthu onse oyipa amatseka pakamwa pawo.

43Aliyense wanzeru asamalitse zinthu zimenezi

ndi kuganizira za chikondi chachikulu cha Yehova.

Nova Versão Internacional

Salmos 107:1-43

QUINTO LIVRO

Salmo 107

1Deem graças ao Senhor porque ele é bom;

o seu amor dura para sempre.

2Assim o digam os que o Senhor resgatou,

os que livrou das mãos do adversário

3e reuniu de outras terras,

do oriente e do ocidente, do norte e do sul107.3 Hebraico: mar..

4Perambularam pelo deserto e por terras áridas

sem encontrar cidade habitada.

5Estavam famintos e sedentos;

sua vida ia se esvaindo.

6Na sua aflição, clamaram ao Senhor,

e ele os livrou da tribulação em que se encontravam

7e os conduziu por caminho seguro

a uma cidade habitada.

8Que eles deem graças ao Senhor

por seu amor leal

e por suas maravilhas em favor dos homens,

9porque ele sacia o sedento

e satisfaz plenamente o faminto.

10Assentaram-se nas trevas e na sombra mortal,

aflitos, acorrentados,

11pois se rebelaram contra as palavras de Deus

e desprezaram os desígnios do Altíssimo.

12Por isso ele os sujeitou a trabalhos pesados;

eles tropeçaram, e não houve quem os ajudasse.

13Na sua aflição, clamaram ao Senhor,

e ele os salvou da tribulação em que se encontravam.

14Ele os tirou das trevas e da sombra mortal

e quebrou as correntes que os prendiam.

15Que eles deem graças ao Senhor,

por seu amor leal

e por suas maravilhas em favor dos homens,

16porque despedaçou as portas de bronze

e rompeu as trancas de ferro.

17Tornaram-se tolos por causa dos seus caminhos rebeldes,

e sofreram por causa das suas maldades.

18Sentiram repugnância por toda comida

e chegaram perto das portas da morte.

19Na sua aflição, clamaram ao Senhor,

e ele os salvou da tribulação em que se encontravam.

20Ele enviou a sua palavra e os curou,

e os livrou da morte.

21Que eles deem graças ao Senhor,

por seu amor leal

e por suas maravilhas em favor dos homens.

22Que eles ofereçam sacrifícios de ação de graças

e anunciem as suas obras com cânticos de alegria.

23Fizeram-se ao mar em navios,

para negócios na imensidão das águas,

24e viram as obras do Senhor,

as suas maravilhas nas profundezas.

25Deus falou e provocou um vendaval

que levantava as ondas.

26Subiam aos céus e desciam aos abismos;

diante de tal perigo, perderam a coragem.

27Cambaleavam, tontos como bêbados,

e toda a sua habilidade foi inútil.

28Na sua aflição, clamaram ao Senhor,

e ele os tirou da tribulação em que se encontravam.

29Reduziu a tempestade a uma brisa

e serenou as ondas.

30As ondas sossegaram, eles se alegraram,

e Deus os guiou ao porto almejado.

31Que eles deem graças ao Senhor

por seu amor leal

e por suas maravilhas em favor dos homens.

32Que o exaltem na assembleia do povo

e o louvem na reunião dos líderes.

33Ele transforma os rios em deserto

e as fontes em terra seca,

34faz da terra fértil um solo estéril,

por causa da maldade dos seus moradores.

35Transforma o deserto em açudes

e a terra ressecada em fontes.

36Ali ele assenta os famintos,

para fundarem uma cidade habitável,

37semearem lavouras, plantarem vinhas

e colherem uma grande safra.

38Ele os abençoa, e eles se multiplicam;

e não deixa que os seus rebanhos diminuam.

39Quando, porém, reduzidos,

são humilhados com opressão, desgraça e tristeza.

40Deus derrama desprezo sobre os nobres

e os faz vagar num deserto sem caminhos.

41Mas tira os pobres da miséria

e aumenta as suas famílias como rebanhos.

42Os justos veem tudo isso e se alegram,

mas todos os perversos se calam.

43Reflitam nisso os sábios

e considerem a bondade do Senhor.