Masalimo 107 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 107:1-43

BUKU LACHISANU

Masalimo 107–150

Salimo 107

1Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino;

pakuti chikondi chake ndi chosatha.

2Owomboledwa a Yehova anene zimenezi

amene Iyeyo anawawombola mʼdzanja la mdani,

3iwo amene anawasonkhanitsa kuchokera ku mayiko,

kuchokera kumadzulo ndi kummawa, kuchokera kumpoto ndi kummwera.

4Ena anayendayenda mʼchipululu mopanda kanthu,

osapeza njira yopitira ku mzinda kumene akanakakhazikikako.

5Iwo anamva njala ndi ludzu,

ndipo miyoyo yawo inafowokeratu.

6Pamenepo analirira Yehova mʼmavuto awo

ndipo Iye anawapulumutsa ku masautso awo.

7Iye anawatsogolera mʼnjira yowongoka

kupita ku mzinda umene anakakhazikikako.

8Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha

ndi chifukwa cha machitidwe ake odabwitsa kwa anthu onse,

9pakuti Iye wapha ludzu la munthu womva ludzu

ndipo wakhutitsa wanjala ndi zinthu zabwino.

10Ena anakhala mu mdima ndi mʼchisoni chachikulu,

amʼndende ovutika mʼmaunyolo achitsulo,

11pakuti iwowo anawukira mawu a Mulungu

ndi kunyoza uphungu wa Wammwambamwamba.

12Kotero Iye anawapereka kuti agwire ntchito yakalavulagaga;

anagwa pansi ndipo panalibe woti awathandize.

13Pamenepo analirira Yehova mʼmasautso awo

ndipo Iye anawapulumutsa ku masautso awo.

14Yehova anawatulutsa mu mdima ndi mʼchisoni chachikulu

ndipo anadula maunyolo awo.

15Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha

ndi machitidwe ake odabwitsa kwa anthu onse,

16pakuti Iye amathyola zipata zamkuwa

ndi kudula pakati mipiringidzo yachitsulo.

17Ena anakhala zitsiru chifukwa cha njira zawo zowukira,

ndipo anamva zowawa chifukwa cha mphulupulu zawo.

18Iwo ananyansidwa ndi chakudya chilichonse

ndipo anafika pafupi ndi zipata za imfa.

19Pamenepo analirira Yehova mʼmasautso awo

ndipo Iye anawapulumutsa ku masautso awowo.

20Iye anatumiza mawu ake ndi kuwachiritsa;

anawalanditsa ku manda.

21Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha

ndi machitidwe ake odabwitsa kwa anthu.

22Apereke nsembe yachiyamiko

ndi kufotokoza za ntchito zake ndi nyimbo zachimwemwe.

23Ena anayenda pa nyanja mʼsitima zapamadzi;

Iwo anali anthu amalonda pa nyanja yayikulu.

24Anaona ntchito za Yehova,

machitidwe ake odabwitsa mʼnyanja yakuya.

25Pakuti Iye anayankhula ndi kuwutsa mphepo yamkuntho

imene inabweretsa mafunde ataliatali.

26Sitima za pamadzizo zinatukulidwa mmwamba ndi kutsikira pansi pakuya;

pamene amawonongeka, kulimba mtima kwawo kunasungunuka.

27Anachita chizungulire ndi kudzandira ngati anthu oledzera;

anali pa mapeto a moyo wawo.

28Pamenepo analirira Yehova mʼmasautso awo

ndipo Iyeyo anawapulumutsa ku masautso awo.

29Yehova analetsa namondwe,

mafunde a mʼnyanja anatontholetsedwa.

30Anali osangalala pamene kunakhala bata,

ndipo Iye anawatsogolera ku dooko limene amalifuna.

31Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha

ndi machitidwe ake odabwitsa kwa anthu.

32Akuze Iye mu msonkhano wa anthu

ndi kumutamanda pabwalo la akuluakulu.

33Iye anasandutsa mitsinje kukhala chipululu,

akasupe otuluka madzi kukhala nthaka yowuma,

34ndiponso nthaka yachonde kukhala nthaka yamchere,

chifukwa cha kuyipa kwa amene amakhala kumeneko.

35Anasandutsa chipululu kukhala mayiwe a madzi

ndi nthaka yowuma kukhala akasupe a madzi oyenda;

36kumeneko Iye anabweretsa anthu anjala kuti azikhalako,

ndipo iwo anamanga mzinda woti akhazikikeko.

37Anafesa mbewu mʼminda ndi kudzala mipesa

ndipo anakolola zipatso zochuluka;

38Yehova anawadalitsa, ndipo chiwerengero chawo chinachuluka kwambiri,

ndipo Iye sanalole kuti ziweto zawo zithe.

39Kenaka chiwerengero chawo chinachepa ndipo iwo anatsitsidwa

chifukwa cha mazunzo, mavuto ndi chisoni;

40Iye amene amakhuthulira mʼnyozo pa olemekezeka

anawachititsa kuyendayenda mʼmalo owumawo wopanda njira.

41Koma Iyeyo anakweza anthu osowa kuchoka ku masautso awo

ngati magulu a nkhosa.

42Anthu olungama mtima amaona ndi kusangalala,

koma anthu onse oyipa amatseka pakamwa pawo.

43Aliyense wanzeru asamalitse zinthu zimenezi

ndi kuganizira za chikondi chachikulu cha Yehova.

New Serbian Translation

Псалми 107:1-43

Књига Пета

Псалми 107–150

Псалам 107

1Хвалите Господа јер је добар,

јер је милост његова довека!

2Нек говоре тако они што их је Господ откупио,

они откупљени из руке душмана;

3које је окупио из земаља истока и запада,

са севера и с мора.

4Тек, тумарали су по пустињи,

по беспућу и нису нашли место да се скрасе.

5А били су и гладни и жедни,

душу своју да испусте.

6Господу су завапили у чемеру своме

и он их је избавио од њихових мука!

7Равним путем их је повео

да се скрасе, да се скуће.

8Нек Господа они хвале за његову милост,

за чудеса над потомцима људи!

9Јер он поји грло жедном,

добрим сити душу гладном.

10Чаме у мраку, у тами;

оковани и бедом и гвожђем;

11јер Божијим речима пркосе,

презрели су савет Свевишњега.

12А он им је патњом срца понизио;

срљали су, а помоћи ниоткуда.

13Господу су завапили у чемеру своме

и он их је спасао од њихових мука!

14Извео их је из мрака, из таме,

окове им поломио.

15Нек Господа они хвале за његову милост,

за чудеса над потомцима људи!

16Јер је он разбио бронзана врата,

изломио гвоздене вратнице.

17Побудалише због својих преступничких путева,

мучише се због својих кривица.

18Души им се сва храна згадила

и до самих врата смрти су пристигли.

19Господу су завапили у чемеру своме

и он их је спасао од њихових мука!

20Реч своју им је послао, па су оздравили;

из рака њихових их је извукао.

21Нек Господа они хвале за његову милост,

за чудеса над потомцима људи!

22Нек жртвују жртве захвалнице;

нек му дела објављују, нека кличу!

23Они што су морем бродовима пловили,

што су трговали на великим водама;

24они су видели дела Господња,

његова чудеса у дубини;

25када је заповедио, ветру наредио

да таласе мора олуја подигне.

26И они се дижу до небеса,

ломе се до дубина,

па им се душа топи од зебње.

27Љуљају се, тетурају ко пијани,

нестаје им сва вештина.

28Господу су завапили у чемеру своме

и он их је извео из њихових мука!

29Олују је умирио

и таласи мора утихнуше.

30А када се стишају, поморци се радују;

он их води до жељене луке.

31Нек Господа они хвале за његову милост,

за чудеса над потомцима људи!

32Нека га уздижу на народном сабору

и нека га славе у старешинском збору!

33Он претвара реке у пустињу,

врела воде у тло спарушено;

34плодну земљу у слатину

због зла оних који на њој живе.

35Од пустиње он језеро чини,

од земље пусте водене изворе.

36Ту је гладне населио

и они су град подигли;

37поља су засејали, винограде посадили

и они обиље плодова рађају.

38И он их је благословио

па су се веома умножили;

ни стока им се проредила није.

39Али због тлачења, невоље и јада

они се проредише, погурише.

40Он излива презир на племиће,

пушта да тумарају пустаром беспутном;

41док убогог уздиже, од невоље склања,

попут стада његов пород множи.

42Виде то праведни па се радују,

а сви неправедни затварају своја уста.

43Ко је мудар? Тај нек ово памти,

у Господњу милост нек прониче!