Masalimo 104 – CCL & ASCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 104:1-35

Salimo 104

1Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.

Inu Yehova Mulungu wanga, ndinu wamkulu kwambiri;

mwavala ulemerero ndi ufumu.

2Iye wadzifunditsa kuwala ngati chovala;

watambasula miyamba ngati tenti

3ndipo wayika pa madzi mitanda ya chipinda chake.

Iye amasandutsa mitambo kukhala galeta lake,

ndi kuwuluka pa mapiko a mphepo.

4Amapanga mphepo kukhala amithenga ake,

malawi amoto kukhala atumiki ake.

5Anakhazikitsa dziko lapansi pa maziko ake;

silingasunthike.

6Munaliphimba ndi nyanja yozama ngati chovala;

madzi anayimirira pamwamba pa mapiri.

7Koma pakudzudzula kwanu madzi anathawa,

pa mkokomo wa bingu lanu iwo anamwazika;

8Inu munamiza mapiri,

iwo anatsikira ku zigwa

kumalo kumene munawakonzera.

9Inu munayika malire ndipo sangathe kudutsa,

iwo sadzamizanso dziko lapansi.

10Iye achititsa akasupe kutulutsa madzi kupita ku zigwa;

madziwo amayenda pakati pa mapiri.

11Iwo amapereka madzi kwa zirombo zonse zakuthengo;

abulu akuthengo amapha ludzu lawo.

12Mbalame zamlengalenga zimayika zisa mʼmbali mwa madzi;

zimayimba pakati pa thambo.

13Iye amathirira mapiri kuchokera ku zipinda zake zapamwamba;

dziko lapansi limakhutitsidwa ndi chipatso cha ntchito yake.

14Amameretsa udzu kuti ngʼombe zidye,

ndi zomera, kuti munthu azilima

kubweretsa chakudya kuchokera mʼdziko lapansi:

15vinyo amene amasangalatsa mtima wa munthu,

mafuta amene amachititsa nkhope yake kuwala,

ndi buledi amene amapereka mphamvu.

16Mitengo ya Yehova ndi yothiriridwa bwino,

mikungudza ya ku Lebanoni imene Iye anadzala.

17Mbalame zimamanga zisa zawo;

kakowa ali ndi malo ake mʼmikungudzamo.

18Mapiri ataliatali ndi a mbalale;

mʼmingʼalu ya miyala ndi mobisalamo mbira.

19Mwezi umasiyanitsa nyengo

ndipo dzuwa limadziwa nthawi yake yolowera.

20Inu mumabweretsa mdima nukhala usiku,

ndipo zirombo zonse za ku nkhalango zimatuluka.

21Mikango imabangula kufuna nyama,

ndi kufunafuna chakudya chawo kuchokera kwa Mulungu.

22Dzuwa limatuluka ndipo iyo imapita kukabisala;

imabwerera kukagona pansi mʼmapanga awo.

23Pamenepo munthu amapita ku ntchito yake,

kukagwira ntchito yake mpaka madzulo.

24Ntchito zanu ndi zochulukadi Inu Yehova!

Munazipanga zonse mwanzeru,

dziko lapansi ladzaza ndi zolengedwa zanu.

25Kuli nyanja yayikulu ndi yotambalala,

yodzaza ndi zolengedwa zosawerengeka,

zamoyo zanu zazikulu ndi zazingʼono zomwe.

26Kumeneko sitima zapamadzi zimayenda uku ndi uku,

ndiponso Leviyatani amene munamulenga kuti asewere kumeneko.

27Zonsezi zimayangʼana kwa Inu

kuti muzipatse chakudya chawo pa nthawi yake yoyenera.

28Mukazipatsa,

zimachisonkhanitsa pamodzi;

mukatsekula dzanja lanu,

izo zimakhutitsidwa ndi zinthu zabwino.

29Mukabisa nkhope yanu,

izo zimachita mantha aakulu;

mukachotsa mpweya wawo,

zimafa ndi kubwerera ku fumbi.

30Mukatumiza mzimu wanu,

izo zimalengedwa

ndipo mumakozanso maonekedwe a dziko lapansi.

31Ulemerero wa Yehova ukhalebe mpaka muyaya;

Yehova akondwere ndi ntchito ya manja ake;

32Iye amene amayangʼana dziko lapansi ndipo limanjenjemera,

amene amakhudza mapiri ndipo amatuluka utsi.

33Ine ndidzayimbira Yehova moyo wanga wonse;

ndidzayimbira matamando Mulungu wanga nthawi yonse imene ndili ndi moyo.

34Zolingalira zanga zikhale zomukomera Iye,

pamene ndikusangalala mwa Yehova.

35Koma anthu ochimwa awonongeke pa dziko lapansi

ndipo anthu oyipa asapezekenso.

Tamanda Yehova, Iwe moyo wanga.

Tamandani Yehova.

Asante Twi Contemporary Bible

Nnwom 104:1-35

Dwom 104

1Ao me ɔkra, kamfo Awurade!

Ao Awurade me Onyankopɔn, woyɛ ɔkɛseɛ!

Wɔafira tumi ne animuonyam.

2Ɔde hann akata ne ho sɛ atadeɛ;

ɔtrɛ ɔsoro mu te sɛ ntomadan,

3na ɔde ne mpia mpunan sisi nsuo so.

Ɔde omununkum yɛ ne teaseɛnam

na ɔde nante mframa ntaban so.

4Ɔsoma nʼabɔfoɔ sɛ mframa,

na ɔsoma nʼasomfoɔ sɛ ogyadɛreɛ.

5Ɔde asase asi ne fapem so

na ɛrenhinhim da.

6Wode ebunu kataa so sɛ atadeɛ

na nsuo gyinaa mmepɔ no so.

7Nanso wʼanimka maa nsuo no dwaneeɛ,

wʼaprannaa nnyegyeeɛ ma wɔdwaneeɛ;

8Wɔtenetenee faa mmepɔ so,

kɔɔ mmɔnhwa mu tɔnn,

kɔguu baabi a wode ama wɔn no.

9Wotoo ɔhyeɛ a wɔrentumi ntra;

na wɔammɛkata asase so bio.

10Ɔma nsuwa tene fa abɔn mu;

ɛtene fa mmepɔ ntam.

11Ɔma wiram mmoa nyinaa nsuo nom;

ɔma afunumu nsuo de kum wɔn sukɔm.

12Ewiem nnomaa nwene wɔn pirebuo wɔ nsuo no ho;

na wɔto nnwom wɔ nnua no mman so.

13Ɔfiri ne soro mpia mu tɔ nsuo gugu mmepɔ so;

Awurade nnwuma so aba mee asase.

14Ɔma ɛserɛ fifiri ma anantwie,

na ɔbɔɔ nnua maa onipa sɛ ɔnnua

na ɛmma aduane mfiri asase mu:

15na onipa anya nsã ama nʼakoma atɔ ne yam,

na onipa anya ngo ama nʼanim atɔ so,

na aduane nso akura onipa akoma.

16Wɔgugu Awurade nnua no so yie,

Lebanon ntweneduro a ɔduaeɛ no.

17Ɛso na nnomaa yɛ wɔn mpirebuo

na asukɔnkɔn nso yɛ nʼatenaeɛ wɔ pepeaa nnua no mu.

18Mmepɔ atentene no yɛ wiram mpɔnkye dea;

na abotan yɛ dwanekɔbea ma amoakua.

19Ɔsrane kyerɛ ɛberɛ nkyekyɛmu,

na owia nim ɛberɛ a ɔkɔtɔ.

20Wode esum ba ma ɛyɛ adesaeɛ

na kwaeɛ mu mmoa nyinaa kɔ ahayɔ.

21Gyata bobom pɛ wɔn ahaboa

wɔhwehwɛ wɔn aduane firi Onyankopɔn hɔ.

22Owia pue ma wɔsane wɔn akyi;

wɔsane kɔdeda wɔn atuo mu.

23Afei, onipa kɔ nʼadwuma so

kɔyɛ adwuma ara kɔsi anwummerɛ.

24Ao Awurade, wo nnwuma dɔɔso!

Nyansa mu na woyɛɛ ne nyinaa;

wʼabɔdeɛ ahyɛ asase so ma.

25Ɛpo na ɛda hɔ tɛtrɛɛ hahanaa yi,

a abɔdeɛ bebree a ɛnni ano,

akɛseɛ ne nketewa ahyɛ no ma.

26Ɛso na ahyɛn di akɔneaba,

na dɛnkyɛmmirampɔn a woyɛɛ no di agorɔ.

27Wɔn nyinaa hwɛ wo kwan

sɛ wobɛma wɔn wɔn aduane wɔ ɛberɛ a ɛsɛ mu.

28Wodema wɔn a, wɔtase;

wobue wo nsam a, nnepa mee wɔn.

29Wode wʼanim hinta wɔn a,

wɔbɔ hu;

sɛ wogye wɔn ahomeɛ a,

wɔwuwu na wɔsane kɔ mfuturo mu.

30Sɛ wode wo Honhom no ma wɔn a

na wɔabɔ wɔn,

na woyɛ asase ani foforɔ.

31Ma Awurade animuonyam ntena hɔ daa;

ma Awurade ani nnye ne nnwuma ho,

32deɛ ɔhwɛ asase na ɛwosoɔ,

na ɔde ne nsa ka mmepɔ a wisie firi mu ba.

33Mɛto dwom ama Awurade me nkwa nna nyinaa;

sɛ mete ase yi, mɛto ayɛyie dwom ama me Onyankopɔn.

34Ɔmma mʼakoma mu mpaeɛbɔ nsɔ nʼani

ɛberɛ a meregye mʼani wɔ Awurade mu yi.

35Ma nnebɔneyɛfoɔ nyera wɔ asase so;

na amumuyɛfoɔ ase nhye.

Ao me ɔkra, kamfo Awurade.

Kamfo Awurade.