Masalimo 103 – CCL & NVI-PT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 103:1-22

Salimo 103

Salimo la Davide.

1Tamanda Yehova, iwe moyo wanga;

ndi zonse zamʼkati mwanga zitamande dzina lake loyera.

2Tamanda Yehova, iwe moyo wanga,

ndipo usayiwale zabwino zake zonse.

3Amene amakhululuka machimo ako onse

ndi kuchiritsa nthenda zako zonse,

4amene awombola moyo wako ku dzenje

ndi kukuveka chikondi ndi chifundo chake ngati chipewa chaufumu,

5amene akwaniritsa zokhumba zako ndi zinthu zabwino,

kotero kuti umakhala wamphamvu zatsopano ngati mphungu.

6Yehova amachita chilungamo

ndipo amaweruza molungama onse opsinjika.

7Iye anadziwitsa Mose njira zake,

ntchito zake kwa Aisraeli.

8Yehova ndi wachifundo ndi wokoma mtima,

wosakwiya msanga ndi wachikondi chochuluka.

9Iye sadzatsutsa nthawi zonse,

kapena kusunga mkwiyo wake kwamuyaya;

10satichitira molingana ndi machimo athu,

kapena kutibwezera molingana ndi mphulupulu zathu.

11Pakuti monga kumwamba kuli kutali ndi dziko lapansi,

koteronso chikondi chake nʼchachikulu kwa iwo amene amamuopa;

12monga kummawa kutalikirana ndi kumadzulo,

koteronso Iye watichotsera mphulupulu zathu kuti zikhale kutali nafe.

13Monga bambo amachitira chifundo ana ake,

choncho Yehova ali ndi chifundo ndi iwo amene amamuopa;

14pakuti Iye amadziwa momwe tinawumbidwira,

amakumbukira kuti ndife fumbi.

15Kunena za munthu, masiku ake ali ngati udzu,

amaphuka ngati duwa la mʼmunda;

16koma mphepo imawombapo ndipo silionekanso

ndipo malo ake sakumbukirikanso.

17Koma kuchokera muyaya mpaka muyaya

chikondi cha Yehova chili ndi iwo amene amamuopa,

ndi chilungamo chake chili ndi ana a ana awo;

18iwo amene amasunga pangano lake

ndi kukumbukira kumvera malangizo ake.

19Yehova wakhazikitsa mpando wake waufumu mmwamba

ndipo ufumu wake umalamulira onse.

20Tamandani Yehova, inu angelo ake,

amphamvu inu amene mumachita zimene amalamula,

amene mumamvera mawu ake.

21Tamandani Yehova, zolengedwa zonse zakumwamba,

inu atumiki ake amene mumachita chifuniro chake.

22Tamandani Yehova, ntchito yake yonse

kulikonse mu ulamuliro wake.

Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.

Nova Versão Internacional

Salmos 103:1-22

Salmo 103

Davídico.

1Bendiga o Senhor a minha alma!

Bendiga o Senhor todo o meu ser!

2Bendiga o Senhor a minha alma!

Não esqueça nenhuma de suas bênçãos!

3É ele que perdoa todos os seus pecados

e cura todas as suas doenças,

4que resgata a sua vida da sepultura

e o coroa de bondade e compaixão,

5que enche de bens a sua existência,

de modo que a sua juventude se renova como a águia.

6O Senhor faz justiça

e defende a causa dos oprimidos.

7Ele manifestou os seus caminhos a Moisés;

os seus feitos, aos israelitas.

8O Senhor é compassivo e misericordioso,

mui paciente e cheio de amor.

9Não acusa sem cessar

nem fica ressentido para sempre;

10não nos trata conforme os nossos pecados

nem nos retribui conforme as nossas iniquidades.

11Pois como os céus se elevam acima da terra,

assim é grande o seu amor para com os que o temem;

12e como o Oriente está longe do Ocidente,

assim ele afasta para longe de nós as nossas transgressões.

13Como um pai tem compaixão de seus filhos,

assim o Senhor tem compaixão dos que o temem;

14pois ele sabe do que somos formados;

lembra-se de que somos pó.

15A vida do homem é semelhante à relva;

ele floresce como a flor do campo,

16que se vai quando sopra o vento;

tampouco se sabe mais o lugar que ocupava.

17Mas o amor leal do Senhor,

o seu amor eterno, está com os que o temem

e a sua justiça com os filhos dos seus filhos,

18com os que guardam a sua aliança

e se lembram de obedecer aos seus preceitos.

19O Senhor estabeleceu o seu trono nos céus,

e como rei domina sobre tudo o que existe.

20Bendigam o Senhor,

vocês, seus anjos poderosos, que obedecem à sua palavra.

21Bendigam o Senhor todos os seus exércitos,

vocês, seus servos, que cumprem a sua vontade.

22Bendigam o Senhor todas as suas obras

em todos os lugares do seu domínio.

Bendiga o Senhor a minha alma!