Marko 13 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Marko 13:1-37

Zizindikiro za Kutha kwa Masiku Yomaliza

1Iye atachoka mʼNyumba ya Mulungu, mmodzi wa ophunzira ake anati kwa Iye, “Aphunzitsi taonani! Miyala ikuluikulu! Nyumba zikongolerenji!”

2Yesu anayankha kuti, “Kodi mukuziona nyumba zikuluzikuluzi? Palibe mwala ndi umodzi pano umene udzakhala pa unzake; uliwonse udzagwetsedwa pansi.”

3Yesu atakhala pansi pa phiri la Olivi moyangʼanana ndi Nyumba ya Mulungu, Petro, Yakobo, Yohane ndi Andreya anamufunsa Iye pambali kuti, 4“Tatiwuzani, izi zidzachitika liti? Nanga chizindikiro chakuti zatsala pangʼono kukwaniritsidwa chidzakhala chiyani?”

5Yesu anawawuza kuti, “Chenjerani kuti wina asakunyengeni. 6Anthu ambiri adzabwera mʼdzina langa, nadzati, ‘Ine ndi Iyeyo,’ ndipo adzanamiza anthu ambiri. 7Pamene mudzamva zankhondo ndi mbiri zankhondo, musadzadzidzimuke. Zinthu zotere ziyenera kuchitika, koma sikuti chimaliziro chafika kale ayi. 8Mtundu udzawukira mtundu unzake, ndi ufumu kuwukira ufumu unzake. Kudzakhala zivomerezi mʼmalo osiyanasiyana, ndi njala. Izi ndi chiyambi chabe cha zowawa monga mayi pobereka.

9“Muyenera kukhala tcheru. Mudzaperekedwa ku mabwalo oweruza ndi kukwapulidwa mwankhanza mʼmasunagoge. Mudzayima pamaso pa abwanamkubwa ndi mafumu monga mboni kwa iwo chifukwa cha Ine. 10Ndipo Uthenga Wabwino uyenera kuyamba walalikidwa kwa anthu a mitundu yonse. 11Nthawi iliyonse pamene mwamangidwa ndi kuyimbidwa mlandu, musadandaule za zimene mudzanena. Zimene mudzapatsidwe pa nthawiyo yankhulani; pakuti sindinu amene mudzayankhula, koma Mzimu Woyera.

12“Mʼbale adzapereka mʼbale kuti aphedwe, ndipo abambo adzapereka mwana wawo. Ana adzawukira makolo awo ndi kuwapereka kuti aphedwe. 13Anthu onse adzakudani chifukwa cha Ine, koma amene adzalimbika mpaka potsiriza, ameneyo ndiye adzapulumuke.

14“Mukadzaona ‘chinthu chonyansa chosakaza’ chitayima pa malo amene si ake, owerenga azindikire. Pamenepo amene ali ku Yudeya athawire kumapiri. 15Aliyense amene ali pa denga la nyumba yake asatsike kapena kulowa mʼnyumba kukatenga kanthu kalikonse. 16Aliyense amene ali ku munda asabwerere kukatenga mkanjo wake. 17Kudzakhala koopsa mʼmasiku amenewo kwa amayi oyembekezera ndi amayi oyamwitsa! 18Pempherani kuti zimenezi zisadzachitike nthawi yozizira, 19chifukwa masiku amenewo adzakhala owawitsa osafanana ndi ena kuyambira pachiyambi, pamene Mulungu analenga dziko, kufikira lero ndipo sadzafanananso ndi ena. 20Ambuye akanapanda kufupikitsa masikuwo, palibe amene akanapulumuka. Koma chifukwa cha osankhidwiratu, amene anawasankha, Iye anawafupikitsa. 21Pa nthawi imeneyo, ngati wina adzati kwa inu, ‘Taonani, Khristu ali kuno, kapena, Taonani, uyo ali apoyo!’ musakhulupirire. 22Pakuti akhristu onama ndi aneneri onama adzaonekera ndipo adzachita zizindikiro ndi zodabwitsa kuti anyenge osankhidwiratu ngati kutakhala kotheka kutero. 23Choncho khalani tcheru; ndakuwuzani zonse nthawi isanafike.

24“Koma masiku amenewo, masautsowo atatha,

“ ‘dzuwa lidzada,

ndipo mwezi sudzawala;

25nyenyezi zidzagwa kuchokera ku thambo,

ndipo mayiko mumlengalenga adzagwedezeka!’

26“Nthawi imeneyo anthu adzaona Mwana wa Munthu akubwera mʼmitambo ndi mphamvu yayikulu ndi ulemerero. 27Ndipo adzatuma angelo ake kukasonkhanitsa osankhidwiratu ake ku mphepo zinayi, kuyambira kumalekezero a dziko lapansi mpaka ku malekezero ake enanso.

28“Tsopano phunzirani phunziro ili kuchokera ku mtengo wamkuyu. Pamene msonga za nthambi zake zikhala za nthete ndipo masamba ake ayamba kuphukira, mumadziwa kuti dzinja layandikira. 29Momwenso pamene muona zinthu izi zikuchitika, dziwani kuti wayandikira, ali pa khomo. 30Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti mʼbado uno sudzatha mpaka zinthu zonsezi zitachitika. 31Kumwamba ndi dziko lapansi zidzatha, koma mawu anga sadzatha.”

Tsiku ndi Ora Sizikudziwika

32“Palibe amene akudziwa za tsikulo kapena nthawi, ngakhale angelo akumwamba, kapena Mwana, koma Atate wokha. 33Khalani maso! Khalani tcheru! Simudziwa pamene nthawi imeneyo idzafike. 34Zili ngati munthu amene akuchokapo. Amasiyira nyumba yake antchito ake, aliyense ndi ntchito yake; ndi kumuwuza wa pa khomo kuti azikhala maso.

35“Inunso muyenera kukhala maso chifukwa simukudziwa nthawi imene mwini nyumba adzabwere, kaya madzulo, kapena pakati pa usiku, kapena tambala akulira, kapena mʼbandakucha. 36Ngati atabwera mwadzidzidzi, asadzakupezeni inu muli mtulo. 37Zimene ndikunena kwa inu, ndikunena kwa aliyense: ‘Khalani tcheru!’ ”

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Марк 13:1-37

Исо Масех говорит о будущем

(Мат. 24:1-22; Лк. 21:5-24)

1Когда Исо выходил из ворот храма, один из учеников сказал Ему:

– Учитель! Посмотри, какие камни! Какие здания!

2– Видишь эти величественные здания? – сказал в ответ Исо. – Здесь не останется и камня на камне, всё будет разрушено.

3Исо сидел на Оливковой горе напротив храма. Когда рядом больше никого не было, Петрус, Якуб, Иохан и Андер спросили Его:

4– Скажи нам, когда это произойдёт и какое знамение укажет на то, что всё это скоро исполнится?

5Исо начал говорить им:

– Смотрите, чтобы никто не обманул вас. 6Многие будут приходить под Моим именем, говоря, что они – это Я, и многих обманут. 7Когда вы услышите о войнах, настоящих и грядущих, не бойтесь. Это должно произойти, но это ещё не конец. 8Потому что народ поднимется на народ и царство на царство. В разных местах будут землетрясения и голод, но это лишь начало родовых схваток13:8 Религиозные учители иудеев говорили о периоде ужасных страданий перед пришествием Масеха, которые они сравнивали с родовыми муками..

9Будьте бдительны! Вас будут отдавать под суд и избивать в иудейских молитвенных домах. Из-за Меня вы будете стоять перед правителями и царями и свидетельствовать им. 10Но прежде Радостная Весть должна быть возвещена всем народам. 11И когда вас арестуют и поведут на суд, не беспокойтесь заранее о том, что вам сказать. Говорите то, что вам будет дано в тот час, ведь это не вы сами будете говорить, а Святой Дух.

12Брат предаст брата, а отец – своего ребёнка, тем самым обрекая их на верную смерть. Так же будут поступать и дети: восставать против родителей и предавать их. 13Все вас будут ненавидеть из-за Меня, но тот, кто выстоит до конца, будет спасён.

14Когда же вы увидите «осквернение, что ведёт к опустошению»13:14 См. Дон. 9:27; 11:31; 12:11. Пророчество Дониёла исполнилось в 168 г. до н. э., когда Антиох Епифан осквернил храм в Иерусалиме, установив там статую Зевса и принеся ему в жертву свинью. Это событие было прообразом того, о чём говорил Исо Масех. Само же пророчество Исо частично исполнилось в 70 г., когда храм был разрушен римлянами, а в полноте оно свершится в конце времён (см. 2 Фес. 2:3-4; Отк. 11:2). там, где его не должно быть (пусть читающий поймёт), тогда те, кто находится в Иудее, пусть бегут в горы. 15Кто окажется на крыше, пусть не спускается и не идёт в дом за вещами, 16и кто окажется в поле, пусть не возвращается за своим плащом. 17Горе же беременным и кормящим грудью в те дни. 18Молитесь, чтобы это не случилось зимой, 19потому что в те дни будут такие бедствия, каких ещё не было от начала творения мира Всевышним и доныне и никогда больше не будет13:18-19 См. Иоиль 2:2; Дон. 12:1.. 20Если бы Вечный не сократил эти дни, то не уцелело бы ни одно живое существо, но ради избранных, которых Он Сам избрал, Он сократил эти дни.

Исо Масех говорит о Своём возвращении

(Мат. 24:23-35; Лк. 21:25-33)

21– И если кто-нибудь вам тогда скажет: «Смотрите! Масех здесь!» или «Смотрите, Он там!» – не верьте. 22Явятся лжемасехи и лжепророки и покажут знамения и чудеса, чтобы обмануть, если удастся, и избранных. 23Так что, смотрите! Я предсказал вам всё наперёд.

24Но в те дни, после тех бедствий,

«солнце померкнет,

и луна не даст света;

25звёзды будут падать с неба,

и небесные тела поколеблются»13:24-25 Ис. 13:10; 34:4; см. также Езек. 32:7; Иоиль 2:10, 31; 3:15; Агг. 2:6, 21; Отк. 6:12-13..

26И тогда люди увидят Ниспосланного как Человек, идущего на облаках с великой силой и славой13:26 См. Дон. 7:13-14.. 27Он пошлёт ангелов и соберёт Своих избранных с четырёх сторон света, от края земли до края неба.

28Пусть для вас примером будет инжир: когда почки набухают и выпускают листья, вы знаете, что приближается лето. 29Так и здесь: когда вы увидите, что это сбывается, знайте, что Он13:29 Или: «это». уже близко, у самых дверей. 30Говорю вам истину: ещё не исчезнет это поколение13:30 Это поколение – существует три основных толкования этих слов: 1) имеется в виду поколение, которое будет свидетелем всех вышеописанных космических катаклизмов и второго пришествия Исо Масеха; 2) так как стоящее здесь слово можно перевести и как «поколение», и как «род», то, возможно, здесь говорится об иудейском народе; 3) имеется в виду поколение, жившее во времена Исо Масеха и ставшее свидетелем разрушения Иерусалима в 70 г. В третьем случае слова «всё это произойдёт» относятся не к событиям последнего времени, но к пророчеству об Иерусалиме., как всё это произойдёт. 31Небо и земля исчезнут, но Мои слова останутся в силе.

Призыв к бодрствованию

(Мат. 24:36-51; Лк. 21:34-36)

32– Но о том дне или часе не знает никто, кроме Отца, – ни ангелы на небесах, ни Сын. 33Смотрите, бодрствуйте: ведь вы не знаете, когда это время наступит. 34Вот с чем можно сравнить это ожидание: человек, отправляясь в далёкое путешествие, оставляет свой дом под присмотром рабов и каждому рабу даёт особое поручение, а привратнику наказывает бодрствовать. 35Поэтому будьте всегда наготове, ведь вы не знаете, когда возвратится хозяин дома: может вечером, а может в полночь, может с пением петухов, а может на рассвете. 36Пусть же он, даже придя внезапно, не застанет вас спящими. 37А то, что Я говорю вам, говорю и всем: бодрствуйте!