1Inu Yehova, kumbukirani zimene zinatichitikira;
yangʼanani ndipo muone kunyozeka kwathu.
2Apereka cholowa chathu kwa obwera,
nyumba zathu kwa alendo.
3Takhala amasiye ndi wopanda abambo,
amayi athu ali ngati akazi amasiye.
4Tiyenera kugula madzi amene timamwa,
nkhuni zathunso nʼzogula.
5Otilondola atigwira pakhosi;
tafowoka ndipo sakutilola kupumula.
6Tinadzipereka kwa Aigupto ndi kwa Asiriya
kuti tipeze chakudya.
7Makolo athu anachimwa ndipo anafa kale,
koma chilango chawo chili pa ife.
8Akapolo akutilamulira,
ndipo palibe ndi mmodzi yemwe angatimasule mʼdzanja lawo.
9Timapeza chakudya chathu poyika miyoyo yathu pa chiswe
chifukwa cha lupanga mʼchipululu.
10Khungu lathu latentha ngati uvuni mʼngʼanjo,
chifukwa cha kuwawa kwa njala.
11Amayi agwiriridwa mu Ziyoni,
ndi anamwali mʼmizinda ya Yuda.
12Akalonga athu akuwapachika pomangirira manja awo,
akuluakulu sakuwalemekeza.
13Achinyamata akukakamizidwa kupera tirigu;
anyamata akudzandira ndi mitolo ya nkhuni.
14Akuluakulu anachokapo pa chipata cha mzinda;
achinyamata aleka nyimbo zawo.
15Chimwemwe chachoka mʼmitima yathu;
kuvina kwathu kwasanduka maliro.
16Chipewa chathu chaufumu chagwa pamutu pathu.
Tsoka kwa ife, chifukwa tachimwa!
17Mitima yathu yakomoka chifukwa cha zimenezi,
chifukwa cha zinthu zimenezi maso athu sakuona bwino,
18pakuti phiri la Ziyoni, limene lasanduka bwinja,
nkhandwe zikungoyendayendapo.
19Inu Yehova, lamulirani kwamuyaya;
mpando wanu waufumu udzakhalabe ku mibadomibado.
20Chifukwa chiyani mumatiyiwala nthawi zonse?
Chifukwa chiyani mwatitaya nthawi yayitali chotere?
21Yehova mutitembenuzire kwa Inu, kuti tibwerere;
mukonzenso masiku athu akhale monga akale,
22pokhapokha ngati mwatitaya kotheratu,
ndi kuti mwatikwiyira kobzola muyeso.
1-2ای خداوند، به ياد آور كه چه بر سر ما آمده است. ببين چگونه رسوا شدهايم. سرزمين ما به دست دشمنان افتاده است و خانههای ما را بيگانگان تصرف كردهاند. 3ما يتيميم؛ پدرانمان كشته و مادرانمان بيوه شدهاند. 4آب خود را میخريم و مینوشيم و هيزم ما به ما فروخته میشود. 5در زير فشار و آزار دشمنان به ستوه آمدهايم و آسايش نداريم. 6خود را تسليم مصر و آشور كردهايم تا نان به دست آوريم و از گرسنگی نميريم.
7پدرانمان گناه كردند و مردند، و اينک جور گناهانشان را ما میكشيم.
8نوكران ديروزمان، اربابان امروزمان شدهاند و كسی نيست كه ما را از دست آنها نجات دهد. 9برای يک لقمه نان، در بيابانها جانمان را به خطر میاندازيم. 10از شدت گرسنگی در تب میسوزيم و پوست بدنمان مثل تنور داغ شده است. 11زنان و دختران ما را در يهودا بیعصمت كردهاند. 12رهبرانمان را به دار كشيدهاند و ريشسفيدانمان را بیحرمت نمودهاند. 13جوانان ما را مانند غلامان، در آسياب به كارهای سخت وا میدارند و كودكان ما زير بارهای سنگين هيزم، افتان و خيزان راه میروند.
14پيران ما ديگر در كنار دروازههای شهر نمینشينند؛ جوانان ما ديگر نمیرقصند و آواز نمیخوانند. 15شادی دلهای ما رفته و رقص ما به ماتم تبديل شده است. 16وای بر ما كه گناه كردهايم و شكوه و جلال خود را از دست دادهايم. 17دلهايمان بیتاب و چشمانمان تار شدهاند، 18زيرا خانهٔ خدا ويران گشته و پناهگاه شغالها شده است.
19ای خداوند، تو تا ابد باقی هستی و تخت سلطنت تو بیزوال است. 20مدت مديدی است كه تو ما را ترک كردهای و ديگر ما را به ياد نمیآوری. 21-22ای خداوند، آيا تو ما را به کلی طرد كردهای و تا ابد بر ما غضبناک خواهی بود؟ اگر چنين نيست، پس ما را به سوی خود بازگردان و شكوه دوران گذشتهٔ ما را به ما باز ده.