Maliro 1 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Maliro 1:1-22

1Haa! Mzinda uja wasiyidwa wokhawokha,

umene kale unali wodzaza ndi anthu!

Kale unali wotchuka pakati pa mitundu ya anthu!

Tsopano wasanduka ngati mkazi wamasiye.

Kale unali mfumukazi ya onse pa dziko lapansi,

tsopano wasanduka kapolo.

2Ukulira mowawidwa mtima usiku wonse,

misozi ili pa masaya pake.

Mwa abwenzi ake onse,

palibe ndi mmodzi yemwe womutonthoza.

Abwenzi ake onse amuchitira chiwembu;

onse akhala adani ake.

3Yuda watengedwa ku ukapolo,

kukazunzika ndi kukagwira ntchito yolemetsa.

Iye akukhala pakati pa anthu a mitundu ina;

ndipo alibe malo opumulira.

Onse omuthamangitsa iye amupitirira,

ndipo alibe kwina kothawira.

4Misewu yopita ku Ziyoni ikulira,

chifukwa palibe ndi mmodzi yemwe akubwera ku maphwando ake.

Zipata zake zonse zili pululu,

ansembe akubuwula.

Anamwali ake akulira,

ndipo ali mʼmasautso woopsa.

5Adani ake asanduka mabwana ake;

odana naye akupeza bwino.

Yehova wamubweretsera mavuto

chifukwa cha machimo ake ambiri.

Ana ake atengedwa ukapolo

pamaso pa mdani.

6Ulemerero wonse wa mwana wamkazi wa Ziyoni

wachokeratu.

Akalonga ake ali ngati mbawala

zosowa msipu;

alibe mphamvu zothawira

owathamangitsa.

7Pa masiku a masautso ndi kuzunzika kwake,

Yerusalemu amakumbukira chuma chonse

chimene mʼmasiku amakedzana chinali chake.

Anthu ake atagwidwa ndi adani ake,

panalibe aliyense womuthandiza.

Adani ake ankamuyangʼana

ndi kumuseka chifukwa cha kuwonongeka kwake.

8Yerusalemu wachimwa kwambiri

ndipo potero wakhala wodetsedwa.

Onse amene ankamulemekeza pano akumunyoza,

chifukwa aona umaliseche wake.

Iye mwini akubuwula

ndipo akubisa nkhope yake.

9Uve wake umaonekera pa zovala zake;

iye sanaganizire za tsogolo lake.

Nʼchifukwa chake kugwa kwake kunali kwakukulu;

ndipo analibe womutonthoza.

“Inu Yehova, taonani masautso anga,

pakuti mdani wapambana.”

10Adani amulanda

chuma chake chonse;

iye anaona mitundu ya anthu achikunja ikulowa mʼmalo ake opatulika,

amene Inu Mulungu munawaletsa

kulowa mu msonkhano wanu.

11Anthu ake onse akubuwula

pamene akufunafuna chakudya;

asinthanitsa chuma chawo ndi chakudya

kuti akhale ndi moyo.

“Inu Yehova, taonani ndipo ganizirani,

chifukwa ine ndanyozeka.”

12“Kodi zimenezi mukuziyesa zachabe, inu nonse mukudutsa?

Yangʼanani ndipo muone.

Kodi pali mavuto ofanana ndi

amene andigwerawa,

amene Ambuye anandibweretsera

pa tsiku la ukali wake?

13“Anatumiza moto kuchokera kumwamba,

unalowa mpaka mʼmafupa anga.

Anayala ukonde kuti ukole mapazi anga

ndipo anandibweza.

Anandisiya wopanda chilichonse,

wolefuka tsiku lonse.

14“Wazindikira machimo anga onse

ndipo ndi manja ake anawaluka pamodzi.

Machimowa afika pakhosi panga,

ndipo Ambuye wandithetsa mphamvu.

Iye wandipereka

kwa anthu amene sindingalimbane nawo.

15“Ambuye wakana

anthu anga onse amphamvu omwe ankakhala nane:

wasonkhanitsa gulu lankhondo kuti lilimbane nane,

kuti litekedze anyamata anga;

mʼmalo ofinyira mphesa Ambuye wapondereza

anamwali a Yuda.

16“Chifukwa cha zimenezi ndikulira

ndipo maso anga adzaza ndi misozi.

Palibe aliyense pafupi woti anditonthoze,

palibe aliyense wondilimbitsa mtima.

Ana anga ali okhaokha

chifukwa mdani watigonjetsa.

17“Ziyoni wakweza manja ake,

koma palibe aliyense womutonthoza.

Yehova walamula kuti abale ake

a Yakobo akhale adani ake;

Yerusalemu wasanduka

chinthu chodetsedwa pakati pawo.

18“Yehova ndi wolungama,

koma ndine ndinawukira malamulo ake.

Imvani inu anthu a mitundu yonse;

onani masautso anga.

Anyamata ndi anamwali anga

agwidwa ukapolo.

19“Ndinayitana abwenzi anga

koma anandinyenga.

Ansembe ndi akuluakulu anga

anafa mu mzinda

pamene ankafunafuna chakudya

kuti akhale ndi moyo.

20“Inu Yehova, onani mmene ine ndavutikira!

Ndikuzunzika mʼkati mwanga,

ndipo mu mtima mwanga ndasautsidwa

chifukwa ndakhala osamvera.

Mʼmisewu anthu akuphedwa,

ndipo ku mudzi kuli imfa yokhayokha.

21“Anthu amva kubuwula kwanga,

koma palibe wonditonthoza.

Adani anga onse amva masautso anga;

iwo akusangalala pa zimene Inu mwachita.

Lifikitseni tsiku limene munalonjeza lija

kuti iwonso adzakhale ngati ine.

22“Lolani kuti ntchito zawo zoyipa zifike pamaso panu;

muwalange

ngati mmene mwandilangira ine

chifukwa cha machimo anga onse.

Ndikubuwula kwambiri

ndipo mtima wanga walefuka.”

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

耶利米哀歌 1:1-22

淒慘的耶路撒冷

1從前人煙稠密的城,

現在何其荒涼!

從前揚威萬邦的強國,

現在竟像寡婦一樣。

從前在諸省做公主的,

現在卻淪為奴婢。

2她在夜間痛哭,淚流滿面。

情人中沒有一個前來安慰。

朋友都出賣她,與她為敵。

3猶大飽受苦難和奴役,

被擄往遠方,流落異邦,

找不到安居之所。

她在走投無路之際被追敵擒獲。

4通往錫安1·4 錫安」又稱「耶路撒冷」。的道路滿目淒涼,

因為無人前去過節。

她的城門冷落,

她的祭司悲歎,

她的少女哀傷,她痛苦不已。

5敵人做了她的主人,

興旺發達。

因為她作惡多端,

耶和華叫她飽受困苦,

她的孩子被敵人擄去。

6錫安的尊榮消逝,

她的首領像找不到草吃的鹿,

無力逃脫敵人的追趕。

7在困苦流離中,

耶路撒冷想起昔日的榮華。

如今,她的人民落在敵人手中,

無人援救。

仇敵看見她,都嘲笑她的滅亡。

8耶路撒冷罪大惡極,

淪為污穢之物。

從前尊重她的人看見她赤身裸體,就蔑視她。

她只能哀歎、退避。

9她的裙子沾滿污穢,

她未曾想過自己的結局。

她的敗落無比淒慘,

無人安慰。

她哭喊道:「耶和華啊,

仇敵已經獲勝,

求你垂顧我的苦難!」

10敵人伸手奪去她的一切珍寶。

她目睹外族人闖入聖殿——那是耶和華禁止他們進入的地方。

11她的人民呻吟著四處覓食,

用珍寶換取糧食維生。

耶路撒冷的哀歎

她說:「耶和華啊,求你眷顧我,

因為我被人蔑視。

12「路人啊,你們都無動於衷嗎?

你們看看,

耶和華向我發烈怒,降禍於我,

還有誰比我更痛苦呢?

13「祂從高天降下火來,

焚燒我的骨頭;

祂在我腳前設下網羅,

使我返回;

祂使我淒涼孤寂,終日痛苦。

14「我的罪惡連接成軛,

祂親手把它們編在一起,

綁在我的頸項上,

使我精疲力盡。

主把我交給我無力抵擋的敵人。

15「主藐視我所有的勇士,

召集軍隊攻擊我,

打垮我的青年。

主踐踏猶大1·15 猶大人」希伯來文是「猶大的純潔少女」。

如同在榨酒池踩踏。

16「我為此哭泣,

淚流滿面,

卻無人安慰、鼓勵我。

我的兒女淒涼孤苦,

因為仇敵已經得勝。」

17錫安伸手求助,卻無人理睬。

耶和華已命四周鄰國與雅各為敵。

耶路撒冷在他們當中成了污穢之物。

18「但耶和華是公義的,

因為我違背了祂的命令。

萬國啊,請聽我的話,

看看我的痛苦!

我的年輕男女都被擄去。

19「我向情人們求助,

他們卻欺騙我。

我的祭司和長老在覓食求生時,

倒斃在城中。

20「耶和華啊,

看看我是多麼痛苦!

我的內臟攪動,

我的心靈翻騰,

因為我背叛了你。

街上有屠殺,

家中有死亡。

21「人們聽見我的哀歎,

卻無人安慰我。

敵人看見你降給我的災難,

都幸災樂禍。

願你應許的審判之日來臨,

叫他們像我一樣受苦!

22「願他們的惡行都擺在你眼前!

你怎樣因我的罪惡而懲罰我,

願你也照樣懲罰他們!

我歎息不絕,心中哀傷。」