Machitidwe a Atumwi 9 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Machitidwe a Atumwi 9:1-43

Kutembenuka Mtima kwa Saulo

1Pa nthawi imeneyi, Saulo ankaopsezabe okhulupirira Ambuye nafuna kuwapha. Iye anapita kwa mkulu wa ansembe, 2ndi kukapempha makalata a chilolezo kuti apite nawo ku masunagoge a ku Damasiko, kuti ngati atakapezeka ena kumeneko otsata Njirayo, kaya ndi amuna kapena amayi, akawamange ndi kuwatenga kubwera nawo ku Yerusalemu. 3Akuyandikira ku Damasikoku paulendo wake, mwadzidzidzi kuwala kochokera kumwamba kunamuzungulira iye. 4Iye anagwa pansi ndipo anamva mawu akuti, “Saulo, Saulo ukundizunziranji Ine?”

5Saulo anafunsa kuti, “Ndinu yani Ambuye?”

Ambuye anayankha kuti, “Ndine Yesu amene iwe ukumuzunza.” 6“Tsopano dzuka, lowa mu mzindamo, ndipo udzawuzidwa zoyenera kuchita.”

7Anthu amene anali naye paulendo, anasowa chonena; iwo anamva mawu koma sanaone wina aliyense. 8Saulo anayimirira, ndipo pamene anatsekula maso ake sanathe kuona. Kotero anamugwira dzanja ndi kulowa naye mu Damasiko. 9Anakhala wosaona kwa masiku atatu ndiponso sanadye kapena kumwa kanthu kalikonse.

10Ku Damasiko kunali wophunzira wina dzina lake Hananiya. Ambuye anamuyitana mʼmasomphenya kuti, “Hananiya!”

Iye anayankha kuti, “Ine Ambuye.”

11Ambuye anamuwuza iye kuti, “Nyamuka, pita ku nyumba ya Yudasi imene ili pa Njira Yolunjika ndipo ukafunse za munthu wochokera ku Tarisisi dzina lake Saulo, pakuti akupemphera. 12Ndipo waona mʼmasomphenya munthu, dzina lake Hananiya atabwera ndi kumusanjika manja kuti aonenso.”

13Hananiya anayankha kuti, “Ambuye, ndinamva zambiri za munthu uyu ndi zonse zoyipa anachitira oyera mtima a ku Yerusalemu. 14Ndipo wabwera kuno ndi ulamuliro wa akulu ansembe kuti adzamange onse amene amayitana pa dzina lanu.”

15Koma Ambuye anati kwa Hananiya, “Pita! Munthu uyu ndi chida changa chosankhika chonyamulira dzina langa pamaso pa anthu a mitundu ina ndi mafumu awo ndiponso kwa anthu a Israeli. 16Ine ndidzamuonetsa zowawa zonse zimene ayenera kumva chifukwa cha dzina langa.”

17Pamenepo Hananiya ananyamuka ndi kukalowa mʼnyumbayo. Anamusanjika manja Sauloyo ndipo anati, “Mʼbale Saulo, Ambuye Yesu, amene anakuonekera pa msewu pamene umabwera kuno wandituma kuti uwonenso ndi kudzazidwa ndi Mzimu Woyera.” 18Nthawi yomweyo mʼmaso mwa Saulo munachoka zinthu zokhala ngati mamba ansomba, ndipo anayambanso kuona. Iye anayimirira nabatizidwa, 19ndipo atadya chakudya, anapezanso mphamvu.

Saulo Alalikira ku Damasiko

Saulo anakhala masiku angapo ndi ophunzira a ku Damasiko. 20Posakhalitsa anayamba kulalikira mʼsunagoge kuti Yesu ndiye Mwana wa Mulungu. 21Onse amene anamva iye akulalikira anadabwa ndipo anafunsa kuti, “Kodi uyu si munthu amene anayambitsa kuzunza okhulupirira ku mpingo wa ku Yerusalemu? Kodi siwabwera kuno kuti awamange ndi kuwapereka kwa akulu a ansembe?” 22Koma mphamvu za Saulo zinali kukulirakulira ndipo anathetsa nzeru Ayuda okhala ku Damasiko powatsimikizira kuti Yesu ndi Mpulumutsi.

23Patapita masiku ambiri, Ayuda anapangana zoti aphe Saulo, 24koma iye anadziwa za chiwembucho. Anthu ankadikirira usana ndi usiku pa zipata za mzindawo kuti amuphe. 25Koma ophunzira ake anamutenga usiku, namutsitsira kunja kwa mpandawo mʼdengu.

Saulo ku Yerusalemu

26Saulo atafika ku Yerusalemu, anayesetsa kulowa mʼgulu la ophunzira koma onse anamuopa chifukwa sanakhulupirire kuti anali wophunziradi. 27Koma Barnaba anamutenga napita naye kwa atumwi. Iye anawafotokozera iwo za mmene Saulo anaonera Ambuye pa njira paja, ndi kuti Ambuye anamuyankhula, ndi momwe analalikira ku Damasiko mʼdzina la Yesu mosaopa. 28Kotero Saulo anakhala nawo nayendayenda mwaufulu mu Yerusalemu akulalikira molimba mtima mʼdzina la Ambuye. 29Anayankhula ndi kutsutsana ndi Ayuda a Chihelene, koma iwo ankafuna kumupha. 30Abale atadziwa zimenezi, anamutenga Saulo ndi kupita naye ku Kaisareya, ndipo anamutumiza ku Tarisisi.

31Pamenepo mpingo wa ku Yudeya konse, ku Galileya ndi ku Samariya unakhala pamtendere, unalimbikitsidwa; ndi kupatsidwa mphamvu ndi Mzimu Woyera, unakula mʼchiwerengero, ndi kukhala moopa Ambuye.

Eneya ndi Tabita

32Pamene Petro amayendera mpingo, anapita kukachezera oyera mtima a ku Luda. 33Kumeneko anakapeza munthu dzina lake Eneya, wofa ziwalo amene anagona pa mphasa kwa zaka zisanu ndi zitatu. 34Petro anati kwa iye, “Eneya, Yesu Khristu akukuchiritsa iwe, dzuka ndipo yalula mphasa yako.” Nthawi yomweyo Eneya anayimirira. 35Anthu onse amene anakhala ku Luda ndi ku Sharoni anamuona ndipo anatembenukira kwa Ambuye.

36Ku Yopa kunali wophunzira wina dzina lake Tabita (mʼChigriki amati Dorika) amene nthawi zonse ankachita zachifundo ndiponso kuthandiza osauka. 37Nthawi imeneyi anadwala ndipo anamwalira, anasambitsa thupi lake, namugoneka mʼchipinda chammwamba. 38Popeza ku Yopa kunali pafupi ndi Luda; pamene ophunzira anamva kuti Petro anali ku Luda, anatuma anthu awiri kuti akamudandaulire kuti, “Chonde bwerani kuno msanga!”

39Petro ananyamuka, napita nawo, ndipo atafika anamutengera ku chipinda chammwamba. Amasiye onse anayima momuzungulira akulira ndi kumuonetsa mwinjiro ndi zovala zina zimene Dorika ankapanga akanali moyo.

40Petro anatulutsa anthu onse mʼchipindamo; ndipo anagwada pansi ndi kupemphera. Anatembenukira mtembo uja nati, “Tabita, dzuka,” Tabita anatsekula maso ake, ndipo ataona Petro anakhala pansi. 41Petro anamugwira dzanja, namuyimiritsa. Ndipo anayitana okhulupirira ndi amasiye namupereka wamoyo. 42Zimenezi zinadziwika ku Yopa konse, ndipo anthu ambiri anakhulupirira Ambuye. 43Petro anakhala ku Yopa kwa masiku ambiri kwa munthu wina, dzina lake Simoni, mmisiri wa zikopa.

Persian Contemporary Bible

اعمال رسولان 9:1‏-43

پولس، دشمن مسيح، پيرو مسيح می‌شود

1‏-2و اما پولُس كه از تهديد و كشتار پيروان مسيح هيچ كوتاهی نمی‌كرد، نزد كاهن اعظم اورشليم رفت و از او معرفی نامه‌هايی خطاب به كنيسه‌ها و عبادتگاه‌های دمشق، پايتخت سوريه خواست تا ايشان با او در امر دستگيری پيروان عيسی، چه مرد و چه زن، همكاری كنند و او بتواند ايشان را دست بسته به اورشليم بياورد.

3پس او رهسپار شد. در راه، در نزديكی دمشق، ناگهان نوری خيره كننده از آسمان گرداگرد پولس تابيد، 4به طوری كه بر زمين افتاد و صدايی شنيد كه به او می‌گفت: «پولس، پولس، چرا اينقدر مرا رنج می‌دهی؟»

5پولس پرسيد: «آقا، شما كيستيد؟»

آن صدا جواب داد: «من عيسی هستم، همان كسی كه تو به او آزار می‌رسانی! 6اكنون برخيز، به شهر برو و منتظر دستور من باش.»

7همسفران پولس مبهوت ماندند، چون صدايی می‌شنيدند ولی كسی را نمی‌ديدند! 8‏-9وقتی پولس به خود آمد و از زمين برخاست، متوجه شد كه چيزی نمی‌بيند. پس دست او را گرفتند و به دمشق بردند. در آنجا سه روز نابينا بود و در اين مدت چيزی نخورد و ننوشيد.

10در دمشق، شخصی مسيحی به نام حنانيا زندگی می‌كرد. خداوند در رؤيا به او فرمود: «حنانيا!»

حنانيا جواب داد: «بلی، ای خداوند!»

11خداوند فرمود: «برخيز و به كوچهٔ راست، به خانهٔ يهودا برو و سراغ پولس طرسوسی را بگير. الان او مشغول دعاست. 12من در رؤيا به او نشان داده‌ام كه شخصی به نام حنانيا می‌آيد و دست بر سر او می‌گذارد تا دوباره بينا شود!»

13حنانيا عرض كرد: «خداوندا، ولی من شنيده‌ام كه اين شخص به ايمانداران اورشليم بسيار آزار رسانده است! 14و می‌گويند از طرف كاهنان اعظم اجازه دارد كه تمام ايمانداران دمشق را نيز بازداشت كند!»

15اما خداوند فرمود: «برو و آنچه می‌گويم، انجام بده چون او را انتخاب كرده‌ام تا پيام مرا به قومها و پادشاهان و همچنين بنی‌اسرائيل برساند. 16من به او نشان خواهم داد كه چقدر بايد در راه من زحمت بكشد.»

17پس حنانيا رفته، پولس را يافت و دست خود را بر سر او گذاشت و گفت: «برادر پولس، خداوند يعنی همان عيسی كه در راه به تو ظاهر شد، مرا فرستاده است كه برای تو دعا كنم تا از روح‌القدس پر شوی و چشمانت نيز دوباره بينا شود.»

18در همان لحظه، چيزی مثل پولک از چشمان پولس افتاد و بينا شد. او بی‌درنگ برخاست و غسل تعميد يافت. 19سپس غذا خورد و قوت گرفت.

پولس در دمشق و اورشليم

پولس چند روز در دمشق نزد ايمانداران ماند. 20آنگاه به كنيسه‌های يهود رفت و به همه اعلام كرد كه عيسی در حقيقت فرزند خداست!

21كسانی كه سخنان او را می‌شنيدند، مات و مبهوت می‌ماندند و می‌گفتند: «مگر اين همان نيست كه در اورشليم پيروان عيسی را شكنجه می‌داد و اينجا نيز آمده است تا آنان را بگيرد و زندانی كند و برای محاكمه نزد كاهنان اعظم ببرد؟»

22ولی پولس با شور و اشتياق فراوان موعظه می‌كرد و برای يهوديان دمشق با دليل و برهان ثابت می‌نمود كه عيسی در حقيقت همان مسيح است.

23پس طولی نكشيد كه سران قوم يهود تصميم گرفتند او را بكشند. 24پولس از نقشهٔ آنان باخبر شد و دانست كه شب و روز كنار دروازه‌های شهر كشيک می‌دهند تا او را به قتل برسانند. 25پس طرفداران پولس يک شب او را در سبدی گذاشتند و از شكاف حصار شهر پايين فرستادند.

26وقتی به اورشليم رسيد بسيار كوشيد تا نزد ايمانداران برود. ولی همه از او می‌ترسيدند و تصور می‌كردند كه حيله‌ای در كار است. 27تا اينكه برنابا او را نزد رسولان آورد و برای ايشان تعريف كرد كه چگونه پولس در راه دمشق خداوند را ديده و خداوند به او چه فرموده و اينكه چگونه در دمشق با قدرت به نام عيسی وعظ كرده است. 28آنگاه او را در جمع خود راه دادند و پولس از آن پس هميشه با ايمانداران بود، و به نام خداوند با جرأت موعظه می‌كرد. 29ولی عده‌ای از يهوديان يونانی زبان كه پولس با ايشان بحث می‌كرد، توطئه چيدند تا او را بكشند. 30وقتی ساير ايمانداران از وضع خطرناک پولس آگاه شدند، او را به قيصريه بردند و از آنجا به خانه‌اش در طرسوس روانه كردند.

31به اين ترتيب، پولس پيرو مسيح شد، و كليسا آرامش يافت و قوت گرفت و در يهوديه و جليل و سامره پيشرفت كرد. ايمانداران در ترس خدا و تسلی روح‌القدس زندگی می‌كردند و تعدادشان زياد می‌شد.

پطرس زن مرده‌ای را زنده می‌كند

32پطرس نيز به همه جا می‌رفت و به وضع ايمانداران رسيدگی می‌كرد. در يكی از اين سفرها، نزد ايمانداران شهر لُده رفت. 33در آنجا شخصی را ديد به نام اينياس كه به مدت هشت سال فلج و بستری بود.

34پطرس به او گفت: «اينياس، عيسی مسيح تو را شفا داده است! برخيز و بسترت را جمع كن!» او نيز بلافاصله شفا يافت. 35آنگاه تمام اهالی لده و شارون با ديدن اين معجزه به خداوند ايمان آوردند.

36در شهر يافا زن ايمانداری بود به نام طبيتا كه به يونانی او را دوركاس يعنی «غزال» می‌گفتند. او زن نيكوكاری بود و هميشه در حق ديگران خصوصاً فقرا خوبی می‌كرد. 37ولی در همين زمان بيمار شد و فوت كرد. دوستانش او را غسل دادند و در بالاخانه‌ای گذاشتند تا ببرند و او را دفن كنند. 38در اين هنگام، شنيدند كه پطرس در شهر لده، نزديک يافا است. پس دو نفر را فرستادند تا از او خواهش كنند كه هر چه زودتر به يافا بيايد. 39همين كه پطرس آمد، او را به بالاخانه‌ای كه جسد دوركاس در آن بود، بردند. در آنجا بيوه‌زنان گرد آمده، گريه‌كنان لباسهایی را كه دوركاس در زمان حيات خود برای ايشان دوخته بود، به او نشان می‌دادند. 40ولی پطرس خواست كه همه از اتاق بيرون روند. آنگاه زانو زد و دعا نمود. سپس رو به جنازه كرد و گفت: «دوركاس، برخيز!» آن زن چشمان خود را باز كرد و همين كه پطرس را ديد، برخاست و نشست! 41پطرس دستش را گرفت و او را برخيزانيد و ايمانداران و بيوه‌زنان را خواند و او را زنده به ايشان سپرد.

42اين خبر به سرعت در شهر پيچيد و بسياری به خداوند ايمان آوردند. 43پطرس نيز مدتی در آن شهر نزد شمعون دباغ اقامت گزيد.