Machitidwe a Atumwi 15 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Machitidwe a Atumwi 15:1-41

Msonkhano wa ku Yerusalemu

1Anthu ena ochokera ku Yudeya anafika ku Antiokeya ndipo amaphunzitsa abale kuti, “Ngati simuchita mdulidwe potsata mwambo wa Mose, simungapulumuke.” 2Zimenezi zinachititsa Paulo ndi Barnaba kuti atsutsane nawo kwambiri. Kotero Paulo ndi Barnaba anasankhidwa pamodzi ndi abale ena kuti apite ku Yerusalemu kukaonana ndi atumwi ndi akulu ampingo kukakambirana za nkhaniyi. 3Mpingo unawaperekeza, ndipo pamene amadutsa ku Foinike ndi Samariya, iwo anafotokoza momwe a mitundu ina anatembenukira mtima. Nkhani imeneyi inakondweretsa kwambiri abale onse. 4Atafika ku Yerusalemu, iwo analandiridwa ndi mpingo, pamodzi ndi atumwi ndiponso akulu ampingo. Paulo ndi Barnaba anawafotokozera zonse zimene Mulungu anachita kudzera mwa iwo.

5Kenaka, okhulupirira ena amene kale anali a gulu la Afarisi anayimirira ndipo anati, “Anthu a mitundu ina ayenera kuchita mdulidwe ndi kusunga malamulo a Mose.”

6Atumwi ndi akulu ampingo anasonkhana kuti akambirane za nkhaniyi. 7Atakambirana kwambiri Petro anayimirira, ndipo anawayankhula nati: “Abale, mukudziwa kuti masiku oyambirira Mulungu anandisankha ine pakati panu kuti anthu a mitundu ina amve kuchokera pakamwa panga mawu a Uthenga Wabwino ndi kukhulupirira. 8Mulungu amene amadziwa mtima wa munthu, Iye anaonetsa kuti anawalandira powapatsa Mzimu Woyera, monga momwe anachita kwa ife. 9Iye sanasiyanitse pakati pa ife ndi iwo, pakuti anayeretsa mitima yawo mwachikhulupiriro. 10Tsopano, chifukwa chiyani mukuyesa Mulungu poyika goli mʼkhosi la ophunzira, limene ngakhale ife kapena makolo athu sangathe kulisenza? 11Osatero! Ife tikukhulupirira kuti tinapulumutsidwa mwachisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu, monga iwonso anachitira.”

12Gulu lonse linakhala chete pamene amamvetsera Barnaba ndi Paulo akuwawuza za zizindikiro zodabwitsa zimene Mulungu anazichita pakati pa anthu a mitundu ina kudzera mwa iwo. 13Iwo atatha kuyankhula, Yakobo anayankhula nati: “Abale, tandimverani. 14Simoni watifotokozera mmene Mulungu poyamba paja anaonetsa kukhudzidwa kwake pomwe anatenga anthu a mitundu ina kukhala ake. 15Mawu a aneneri akuvomereza zimenezi, monga kwalembedwa kuti,

16“ ‘Zitatha izi Ine ndidzabwerera

ndipo ndidzamanganso nyumba ya Davide imene inagwa.

Ndidzakonzanso malo amene anagumuka,

ndi kuyimanganso,

17kuti anthu otsalawo afunefune Ambuye,

ndi anthu onse a mitundu ina amene atchedwa ndi dzina langa,

akutero Ambuye, amene amachita zinthu zimenezi

18zinaululidwa kuyambira kalekale.’

19“Chifukwa chake, ine ndikuweruza kuti tisamavute anthu a mitundu ina amene atembenuka mtima kutsata Mulungu. 20Koma tiwalembere iwo, kuwawuza kuti asadye chakudya choperekedwa kwa mafano, apewenso dama, asadyenso nyama zochita kupotola kapena kudya magazi. 21Pakuti malamulo a Mose akhala akulalikidwa mu mzinda uliwonse, kuyambira kalekale ndipo amawerengedwa mʼMasunagoge tsiku la Sabata.”

Kalata Yopita kwa Anthu a Mitundu ina

22Pamenepo atumwi ndi akulu ampingo, pamodzi ndi mpingo onse, anagwirizana zosankha anthu ena pakati pawo kuti awatume ku Antiokeya pamodzi ndi Paulo ndi Bamaba. Iwo anasankha Yudasi, wotchedwa Barsaba ndi Sila, anthu awiri amene anali atsogoleri pakati pa abale, 23kuti akapereke kalata yonena kuti,

Kuchokera kwa atumwi ndi akulu ampingo, abale anu,

Kwa anthu a mitundu ina okhulupirira a ku Antiokeya, Siriya ndi Kilikiya:

Tikupereka moni.

24Ife tamva kuti anthu ena ochokera pakati pathu, amene sitinawatume anakusokonezani maganizo ndi kukuvutitsani ndi zimene amakuwuzani. 25Tsono ife tagwirizana kuti, tisankhe anthu ena ndi kuwatumiza kwa inu pamodzi ndi abale athu okondedwa Paulo ndi Barnaba, 26anthu amene anapereka moyo wawo chifukwa cha dzina la Ambuye athu Yesu Khristu. 27Nʼchifukwa chake, tikutumiza Yudasi ndi Sila kuti adzachitire umboni ndi mawu a pakamwa pawo za zimene ife talemba. 28Pakuti zinakomera Mzimu Woyera ndiponso ife kuti tisakusenzetseni katundu wina, kupatula zoyenera zokhazi: 29Mupewe kudya chakudya choperekedwa nsembe kwa mafano, musadye magazi, kapena nyama yopha mopotola ndiponso musachite dama. Mudzachita bwino mukapewa zimenezi.

Tsalani bwino.

30Anthu aja anatumidwa ndipo anafika ku Antiokeya, kumene anasonkhanitsa mpingo pamodzi napereka kalatayo. 31Anthuwo anawerenga kalatayo ndipo abalewo anakondwa chifukwa cha mawu ake achirimbikitso. 32Yudasi ndi Sila amene analinso aneneri, ananena zambiri zowalimbikitsa ndi kuwapatsa mphamvu abalewo. 33Atakhala kumeneko kwa kanthawi, abale aja anatsanzikana nawo mwamtendere kuti abwerere kwa amene anawatuma. 34Koma Sila anasankha kuti akhale komweko. 35Koma Paulo ndi Barnaba anatsalira ku Antiokeya kumene iwo pamodzi ndi ena ambiri anaphunzitsa ndi kulalikira Mawu a Ambuye.

Paulo Asiyana ndi Barnaba

36Patapita masiku ena Paulo anati kwa Barnaba, “Tiyeni tibwerere kuti tikaone abale ku mizinda yonse imene tinalalika Mawu a Ambuye ndipo tikaone mmene akuchitira.” 37Barnaba anafuna kutenga Yohane, wotchedwanso Marko, kuti apite nawo. 38Koma Paulo anaganiza kuti sichinali cha nzeru kumutenga Yohane chifukwa iye anawathawa ku Pamfiliya ndipo sanapitirire nawo pa ntchito. 39Iwo anatsutsana kwambiri kotero kuti anapatukana. Barnaba anatenga Marko ndipo anakwera sitima ya pamadzi kupita ku Kupro. 40Paulo anasankha Sila. Abale atawapempherera kwa Ambuye kuti alandire chisomo, ananyamuka. 41Iye anadutsa ku Siriya ndi ku Kilikiya kupita akulimbikitsa mipingo.

New Russian Translation

Деяния 15:1-41

Встреча руководителей церкви в Иерусалиме

1Из Иудеи в Антиохию пришли люди, которые стали учить братьев:

– Если вы не будете обрезаны по обряду, установленному Моисеем, вы не можете быть спасены.

2Это привело к разногласиям и горячему спору между ними с одной стороны и Павлом и Варнавой – с другой. Тогда Павлу и Варнаве поручили пойти вместе с несколькими другими верующими в Иерусалим и обсудить этот вопрос с апостолами и старейшинами. 3Получив помощь от церкви, они пошли через Финикию и Самарию, рассказывая там об обращении язычников. Эта весть вызывала у всех верующих большую радость.

4В Иерусалиме они были приняты членами церкви, апостолами и старейшинами и рассказали им обо всем, что Бог совершил через них. 5Но верующие, принадлежавшие к группе фарисеев, говорили, что язычников следует обрезывать и требовать от них соблюдения Закона Моисея.

6Апостолы и старейшины собрались, чтобы рассмотреть этот вопрос. 7После долгих обсуждений Петр поднялся и сказал:

– Братья, как вы знаете, прошло уже много времени с того дня, как Бог выбрал из всех нас меня возвещать слово Радостной Вести язычникам, чтобы и они уверовали. 8Бог знает сердца людей, и Он дал свидетельство того, что принимает и уверовавших язычников, даровав им Святого Духа так же, как и нам. 9Он не делает никакой разницы между нами и ими, потому что Он через веру очистил и их сердца! 10Так зачем же вы испытываете Бога, возлагая на шеи учеников бремя, которое не в состоянии были нести ни наши отцы, ни мы? 11Ведь мы верим в то, что получаем спасение по благодати Господа Иисуса так же, как и они.

12Тогда все затихли и стали слушать рассказ Варнавы и Павла о знамениях и чудесах, которые Бог совершил через них среди язычников. 13Когда они закончили, Иаков сказал:

– Братья, послушайте меня. 14Симон15:14 Симон – т. е. Петр (см. 15:7; 10:5). рассказал нам о том, как Бог впервые решил составить из язычников народ для Себя. 15Это полностью согласуется со словами пророков, где сказано:

16«Затем Я возвращусь

и восстановлю павшую скинию Давида.

Я восстановлю ее руины

и воссоздам ее,

17чтобы остальные люди

и все народы, которые были названы Моим именем,

стали искать Господа. Так говорит Господь,

18Который объявил об этом издревле»15:16-18 См. Ам. 9:11-12..

19Поэтому я считаю, что мы не должны создавать трудностей для язычников, обращающихся к Богу. 20Напротив, мы должны написать им письмо, предупредив лишь, чтобы они воздерживались от вещей, оскверненных идолами, от разврата, от мяса удушенных животных и от крови15:20 См. Быт. 9:4; Исх. 34:15-17; Лев. 17:10-16; 18:6-23. Удушенных животных запрещалось употреблять в пищу потому, что в них оставалась кровь.. И чтобы не делали другим того, чего себе не желают15:20 Слова: «И чтобы не делали другим того, чего себе не желают» – отсутствуют в наиболее авторитетных древних рукописях.. 21Ведь Закон Моисея издавна возвещается в каждом городе и читается в синагогах каждую субботу.

Письмо совета к братьям из язычников

22Апостолы и старейшины вместе со всей церковью решили выбрать несколько человек из своей среды и послать их с Павлом и Варнавой в Антиохию. Они выбрали Иуду, которого еще называли Варсавой, и Силу. Эти двое были руководителями среди братьев. 23С ними передали такое письмо:

«Братья апостолы и старейшины

братьям из язычников, находящимся в Антиохии, Сирии и Киликии.

Приветствуем вас!

24До нас дошли слухи о том, что некоторые люди, пришедшие от нас, привели вас в замешательство своими словами и взволновали ваши умы, но мы ничего им не поручали. 25Поэтому мы с общего согласия решили выбрать из нашей среды несколько человек и послать их к вам вместе с нашими дорогими Варнавой и Павлом, 26которые рисковали своей жизнью ради имени нашего Господа Иисуса Христа. 27Мы посылаем к вам также Иуду и Силу, чтобы они на словах подтвердили то, что мы пишем. 28Святой Дух и мы решили не обременять вас ничем, кроме следующих требований: 29воздерживайтесь от пищи, принесенной в жертву идолам, от крови, от мяса удушенных животных и от разврата. И не делайте другим того, чего себе не желаете15:29 Слова: «И не делайте другим того, чего себе не желаете» – отсутствуют в наиболее авторитетных древних рукописях.. Если вы будете соблюдать это, то поступите правильно.

Будьте здоровы!»

30Посланные отправились и пришли в Антиохию. Там они собрали церковь и вручили письмо. 31Люди читали его и радовались ободряющей вести. 32Иуда и Сила, которые сами были пророками, своими словами ободряли и воодушевляли братьев. 33Они провели там некоторое время, и братья с миром отпустили их к тем, кто их послал. 34Сила, однако же, решил остаться, а Иуда вернулся в Иерусалим15:34 В наиболее авторитетных древних рукописях ст. 34 отсутствует.. 35Павел и Варнава остались в Антиохии, где они со многими другими братьями учили и возвещали слово Господа.

Разногласия между Павлом и Варнавой

36Спустя некоторое время Павел предложил Варнаве:

– Давай посетим братьев во всех городах, где мы возвещали слово Господне, и посмотрим, как у них идут дела.

37Варнава хотел взять с собой Иоанна, которого еще называли Марком, 38но Павел не хотел брать с собой того, кто оставил их в Памфилии и не помог исполнить порученную им работу.

39Разногласие по этому вопросу было столь острым, что они расстались. Варнава взял Марка и отплыл на Кипр, 40а Павел выбрал Силу и, будучи вверен братьями благодати Господа, отправился в путь. 41Павел проходил через Сирию и Киликию, утверждая церкви.