Luka 3 – CCL & NVI

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Luka 3:1-38

Yohane Mʼbatizi Akonza Njira

1Mʼchaka cha 15 mu ulamuliro wa Tiberiyo Kaisara, Pontiyo Pilato ali bwanamkubwa wa Yudeya, Herode ankalamulira ku Galileya, mʼbale wake Filipo ankalamulira ku Iturea ndi ku dera la Trakoniti, ndipo Lusaniyo ankalamulira ku Abilene. 2Inalinso nthawi ya mkulu wa ansembe wa Anasi ndi Kayafa, pamene mawu a Mulungu anabwera kwa Yohane mwana wa Zakariya mʼchipululu. 3Iye anapita ku dziko lonse lozungulira mtsinje wa Yorodani, nalalikira ubatizo wa kulapa ndi kukhululukidwa kwa machimo. 4Monga analembera mʼbuku la Yesaya mneneri kuti:

“Mawu a wofuwula mʼchipululu,

konzani njira ya Ambuye,

wongolani njira zake.

5Chigwa chilichonse chidzadzazidwa

ndipo phiri lililonse ndi mtunda uliwonse zidzasalazidwa,

misewu yokhotakhota idzawongoledwa,

ndi njira zosasalala zidzasalazidwa.

6Ndipo anthu onse adzaona chipulumutso cha Mulungu.”

7Yohane anati kwa magulu a anthu amene amabwera kudzabatizidwa ndi iye, “Ana anjoka inu! Anakuchenjezani ndani kuti muthawe mkwiyo umene ukubwera? 8Onetsani zipatso zakutembenuka mtima, ndipo musamanene mwa inu nokha kuti, ‘Tili nalo kholo lathu Abrahamu,’ pakuti ndikuwuzani kuti kuchokera ku miyala iyi, Mulungu akhoza kumuwutsira Abrahamuyo ana. 9Nkhwangwa ili kale pa muzu wamitengo, ndipo mtengo uliwonse umene subala chipatso chabwino udzadulidwa ndi kuponyedwa pa moto.”

10Gulu la anthuwo linafunsa kuti, “Nanga tsono tichite chiyani?”

11Yohane anayankha kuti, “Munthu amene ali ndi malaya awiri apatseko amene alibe, ndi amene ali ndi chakudya achitenso chimodzimodzi.”

12Amisonkho nawonso anabwera kudzabatizidwa. Iwo anafunsa kuti, “Aphunzitsi, ife tichite chiyani?”

13Iye anawawuza kuti, “Musalandire moposa zimene muyenera.” 14Kenaka asilikali ena anamufunsa kuti, “Nanga ife tichite chiyani?”

Iye anayankha kuti, “Musamalande ndalama moopseza ndipo musamanamizire anthu, khutitsidwani ndi malipiro anu.”

15Anthu ankadikira ndi chiyembekezo ndipo ankasinkhasinkha mʼmitima mwawo kuti mwina Yohane nʼkukhala Khristu. 16Yohane anayankha onse kuti, “Ine ndikubatizani ndi madzi. Koma wina wondiposa ine mphamvu adzabwera amene sindili woyenera kumasula lamba wa nsapato zake. Iyeyu adzakubatizani inu ndi Mzimu Woyera ndi moto. 17Mʼdzanja lake muli chopetera kuti ayeretse powomberapo tirigu ndi kusonkhanitsa tirigu ndipo adzatentha zotsalira zonse ndi moto wosazimitsika.” 18Ndipo ndi mawu ena ambiri, Yohane anawachenjeza anthu ndi kuwalalikira Uthenga Wabwino.

19Koma pamene Yohane anadzudzula Herode wolamulirayo chifukwa chokwatira Herodia, mkazi wa mʼbale wake, ndi zoyipa zina zonse anazichita, 20Herode anawonjezanso choyipa ichi pa zonsezo: Anatsekera Yohane mʼndende.

Ubatizo wa Yesu

21Pamene anthu onse ankabatizidwa, Yesu anabatizidwanso. Ndipo akupemphera, kumwamba kunatsekuka. 22Mzimu Woyera anatsika pa Iye mumaonekedwe a nkhunda ndipo mawu anamveka kuchokera kumwamba: “Iwe ndiwe Mwana wanga wokondedwa; ndimakondwera nawe.”

Makolo a Yesu

23Ndipo Yesu anali ndi zaka makumi atatu pamene anayamba ntchito yake. Monga mmene anthu ankaganizira, Iyeyo anali mwana wa Yosefe,

mwana wa Heli, 24mwana wa Matate,

mwana wa Levi, mwana wa Meliki,

mwana wa Yaneyi, mwana wa Yosefe

25mwana wa Matati, mwana wa Amosi,

mwana wa Naomi, mwana wa Esli,

mwana wa Nagai, 26mwana wa Maati,

mwana wa Matatiyo, mwana wa Simeoni,

mwana wa Yosefe, mwana wa Yoda

27mwana wa Yohanani, mwana wa Resa,

mwana wa Zerubabeli, mwana wa Salatieli,

mwana wa Neri, 28mwana wa Meliki,

mwana wa Adi, mwana wa Kosamu,

mwana wa Elmadama, mwana wa Ere,

29mwana wa Jose, mwana wa Eliezara,

mwana wa Yorimu, mwana wa Matati,

mwana wa Levi, 30mwana wa Simeoni,

mwana wa Yuda, mwana wa Yosefe,

mwana wa Yonamu, mwana wa Eliakimu,

31mwana wa Meleya, mwana wa Mena,

mwana wa Matata, mwana wa Natani,

mwana wa Davide, 32mwana wa Yese,

mwana wa Obedi, mwana wa Bowazi,

mwana wa Salimoni, mwana wa Naasoni,

33mwana wa Aminadabu, mwana wa Arni,

mwana wa Hezronu, mwana wa Perezi,

mwana wa Yuda, 34mwana wa Yakobo,

mwana wa Isake, mwana wa Abrahamu,

mwana wa Tera, mwana wa Nakoro,

35mwana wa Serugi, mwana wa Reu,

mwana wa Pelegi, mwana wa Eberi,

mwana wa Sela, 36mwana wa Kainane,

mwana wa Arfaksadi, mwana wa Semu,

mwana wa Nowa, mwana wa Lameki,

37mwana wa Metusela, mwana wa Enoki,

mwana wa Yaredi mwana wa Malaleeli,

mwana wa Kainane, 38mwana wa Enosi,

mwana wa Seti,

mwana wa Adamu, mwana wa Mulungu.

Nueva Versión Internacional

Lucas 3:1-38

El mensaje de Juan el Bautista

1En el año quince del reinado de Tiberio César, Poncio Pilato gobernaba la provincia de Judea. Herodes gobernaba en Galilea, y su hermano Felipe en Iturea y Traconite. Lisanias gobernaba en Abilinia. 2En ese mismo tiempo, Anás y Caifás fueron los sumos sacerdotes. Fue por ese entonces que Dios le habló a Juan hijo de Zacarías, en el desierto. 3Juan recorría toda la región del Jordán predicando el bautismo de arrepentimiento para el perdón de pecados. 4Así está escrito en el libro del profeta Isaías:

«Voz de uno que grita en el desierto:

“Preparen el camino del Señor,

háganle sendas derechas.

5Todo valle será rellenado,

toda montaña y colina será allanada.

Los caminos torcidos se enderezarán,

las sendas disparejas serán niveladas.

6Y toda la humanidad verá la salvación de Dios”».

7Muchos venían a Juan para que los bautizara.

―¡Nido de víboras! —les dijo—. ¿Quién les dijo que huyeran del castigo que se acerca? 8Den muestras de verdadero arrepentimiento. Y no se pongan a pensar: “Somos descendientes de Abraham”. Pues les digo que Dios puede convertir estas piedras en descendientes de Abraham. 9Es más, el hacha ya está puesta en la base de los árboles. Todo árbol que no produzca buen fruto será cortado y echado al fuego.

10―¿Entonces qué debemos hacer? —le preguntaba la gente.

11―El que tiene dos camisas debe compartir con el que no tiene ninguna —les contestó Juan—, y el que tiene comida debe hacer lo mismo.

12Llegaron también unos cobradores de impuestos para que los bautizara.

―Maestro, ¿qué debemos hacer nosotros? —le preguntaron.

13―No cobren más de lo debido —les respondió.

14―Y nosotros, ¿qué debemos hacer? —le preguntaron unos soldados.

Y les dijo:

―No exijan dinero a cambio de favores, ni hagan denuncias falsas. Más bien confórmense con lo que les pagan.

15La gente vivía esperando al Cristo, y todos se preguntaban si acaso sería Juan.

16―Yo los bautizo a ustedes con agua —les dijo Juan a todos—. Pero está por llegar uno más poderoso que yo, a quien ni siquiera merezco desatarle la correa de sus sandalias. Él los bautizará con el Espíritu Santo y fuego. 17Tiene la pala en la mano para limpiar su campo y recoger el trigo en su granero. La paja la quemará con fuego que nunca se apagará.

18Y con muchas otras palabras, Juan llamaba la atención de la gente y le anunciaba la buena noticia. 19Reprendió al gobernador Herodes por el asunto de su cuñada Herodías, y por todas las otras maldades que había cometido. 20Entonces Herodes llegó hasta el colmo de encerrar a Juan en la cárcel.

El bautismo de Jesús

21Un día en que todos venían hasta donde estaba Juan para que los bautizara, Jesús fue bautizado también. Y, mientras oraba, se abrió el cielo, 22y el Espíritu Santo bajó sobre él en forma de paloma. Entonces se oyó una voz del cielo que decía: «Tú eres mi Hijo amado; estoy muy contento contigo».

Los antepasados de Jesús

23Jesús tenía unos treinta años cuando comenzó su ministerio. Esta es la lista de sus antepasados:

José, Elí, 24Matat,

Leví, Melquí, Janay,

José, 25Matatías, Amós,

Nahúm, Eslí, Nagay,

26Máat, Matatías, Semeí,

Josec, Judá, 27Yojanán,

Resa, Zorobabel, Salatiel,

Neri, 28Melquí, Adí,

Cosán, Elmadán, Er,

29Josué, Eliezer, Jorín,

Matat, Leví, 30Simeón,

Judá, José, Jonán,

Eliaquín, 31Melea, Mainán,

Matata, Natán, David,

32Isaí, Obed, Booz,

Salmón, Naasón, 33Aminadab,

Admín, Arní, Jezrón,

Fares, Judá, 34Jacob,

Isaac, Abraham, Taré,

Najor, 35Serug, Ragau,

Péleg, Éber, Selaj,

36Cainán, Arfaxad, Sem,

Noé, Lamec, 37Matusalén,

Enoc, Jared, Malalel,

Cainán, 38Enós, Set, Adán,

Dios.