Luka 20 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Luka 20:1-47

Amufunsa Yesu za Ulamuliro Wake

1Tsiku lina pamene Iye ankaphunzitsa anthu mʼmabwalo a Nyumba ya Mulungu ndi kuphunzitsa Uthenga Wabwino, akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo, pamodzi ndi akuluakulu anabwera kwa Iye. 2Iwo anati, “Mutiwuze mukuchita izi ndi ulamuliro wayani? Ndani anakupatsani ulamuliro uwu?”

3Iye anayankha kuti, “Inenso ndikufunsani, mundiyankhe, 4‘Kodi ubatizo wa Yohane, unali wochokera kumwamba, kapena wochokera kwa anthu?’ ”

5Iwo anakambirana pakati pawo ndikuti, “Ngati ife tinena kuti, ‘Kuchokera kumwamba’ Iye akatifunsa kuti, ‘chifukwa chiyani simunamukhulupirire iye?’ 6Koma ngati ife tinena kuti, ‘kuchokera kwa anthu,’ anthu onse atigenda miyala, chifukwa amatsimikiza kuti Yohane anali mneneri.”

7Pamenepo iwo anayankha kuti, “Ife sitidziwa kumene unachokera.”

8Yesu anati, “Ngakhale Inenso sindikuwuzani kuti ndi ulamuliro wanji umene ndikuchitira zimenezi.”

Fanizo la Olima Mʼmunda Wamphesa

9Iye anapitirira kuwawuza anthu fanizo ili: “Munthu wina analima munda wamphesa, nabwereketsa kwa alimi ena ndipo anachoka kwa nthawi yayitali. 10Pa nthawi yokolola, iye anatumiza wantchito wake kwa alimi aja kuti amupatseko zina mwa zipatso za munda wamphesawo. Koma alimi aja anamumenya namubweza wopanda kanthu. 11Iye anatumiza wantchito wina, koma uyunso anamumenya namuchita zachipongwe ndi kumubweza wopanda kanthu. 12Iye anatumizanso wina wachitatu ndipo iwo anamuvulaza namuponya kunja.

13“Kenaka mwini mundawo anati, ‘Kodi ndichite chiyani? Ndidzatumiza mwana wanga wamwamuna, amene ndimukonda; mwina iwo adzamuchitira ulemu.’

14“Koma alimiwo ataona mwanayo, anakambirananso. Iwo anati, ‘Uyu ndiye wodzamusiyira chumachi. Tiyeni timuphe ndipo chumachi chikhala chathu.’ 15Ndipo anamuponya kunja kwa mundawo ndi kumupha.

“Nanga tsono mwini munda wamphesayo adzawatani anthuwa? 16Iye adzabwera ndi kupha alimi aja ndi kupereka mundawo kwa ena.”

Pamene anthu anamva izi, anati, “Musatero ayi.”

17Yesu anawayangʼanitsitsa ndipo anafunsa kuti, “Kodi tanthauzo lake ndi chiyani la zimene zinalembedwa kuti,

“ ‘Mwala umene omanga nyumba anawukana

wasanduka mwala wa pa ngodya.

18Aliyense amene agwa pa mwalawu adzapweteka, koma iye amene udzamugwera udzamuphwanya.’ ”

19Aphunzitsi amalamulo ndi akulu a ansembe amafuna njira yoti amuphe nthawi yomweyo, chifukwa anadziwa kuti ananena fanizo ili powatsutsa iwo. Koma iwo anali ndi mantha chifukwa cha anthu.

Za Kupereka Msonkho kwa Kaisara

20Pamene ankamulondalonda Iye, iwo anatumiza akazitape amene amaoneka ngati achilungamo. Iwo ankafuna kumutapa mʼkamwa Yesu mu china chilichonse chimene Iye ananena kuti amupereke Iye kwa amene anali ndi mphamvu ndi ulamuliro oweruza. 21Potero akazitapewo anamufunsa Iye kuti, “Aphunzitsi, tidziwa kuti mumayankhula ndi kuphunzitsa zimene zili zoonadi, ndi kuti simuonetsa tsankho koma mumaphunzitsa njira ya Mulungu mwachoonadi. 22Kodi ndi bwino kwa ife kumapereka msonkho kwa Kaisara kapena kusapereka?”

23Iye anaona chinyengo chawo ndipo anawawuza kuti, 24“Onetseni ndalama. Chithunzi ndi malembawa ndi zayani?”

25Iwo anayankha kuti, “Za Kaisara.”

Iye anawawuza kuti, “Ndiye perekani kwa Kaisara zake za Kaisara ndi kwa Mulungu zimene ndi za Mulungu.”

26Iwo analephera kumupeza cholakwa pa zimene ankayankhula pamaso pa anthu. Ndipo pothedwa nzeru ndi yankho lake, iwo anakhala chete.

Za Kuuka kwa Akufa ndi Ukwati

27Ena mwa Asaduki, amene ankanena kuti kulibe kuuka kwa akufa, anabwera kwa Yesu ndi funso. 28Iwo anati, “Aphunzitsi, Mose anatilembera kuti munthu akamwalira ndi kusiya mkazi wopanda ana, mʼbale wa munthu womwalirayo akuyenera kukwatira mkaziyo kuti amuberekere ana mʼbale wakeyo. 29Tsopano panali abale asanu ndi awiri. Woyambayo anakwatira mkazi ndipo anafa wopanda mwana. 30Wachiwiri 31ndipo kenaka wachitatuyo anamukwatira iye, ndipo chimodzimodzi asanu ndi awiri aja anafa osasiya ana. 32Pa mapeto pake mkaziyo anafanso. 33Tsopano, pa nthawi ya kuukanso, kodi mkaziyu adzakhala wayani popeza onse asanu ndi awiri anamukwatirapo?”

34Yesu anayankha kuti, “Anthu a mʼbado uno amakwatira ndi kukwatiwa. 35Koma mʼmoyo umene ukubwerawo, anthu amene adzaukitsidwe kwa akufa sadzakwatira kapena kukwatiwa. 36Ndipo sadzafanso, pakuti adzakhala ngati angelo. Iwo ndi ana a Mulungu, chifukwa adzakhala ataukitsidwa kwa akufa. 37Ngakhale pa nkhani yachitsamba choyaka moto, Mose anaonetsa kuti akufa amauka, pakuti anatcha Ambuye ‘Mulungu wa Abrahamu, Mulungu wa Isake ndi Mulungu wa Yakobo.’ 38Mulungu si Mulungu wa akufa, koma wa amoyo, pakuti kwa Iye onse ali ndi moyo.”

39Ena mwa aphunzitsi amalamulo anayankha kuti, “Mwanena bwino mphunzitsi!” 40Ndipo panalibe wina amene akanalimba mtima kumufunsa Iye mafunso ena.

Khristu ndi Mwana wa Ndani?

41Kenaka Yesu anawawuza kuti, “Zikutheka bwanji kuti aziti Khristu ndi mwana wa Davide? 42Davide mwini wake akunenetsa mʼbuku la Masalimo kuti,

“Ambuye anati kwa Ambuye anga:

‘Khalani ku dzanja langa lamanja,

43mpaka Ine nditasandutsa adani anu

chopondapo mapazi anu?’

44Davide akumutcha Iye ‘Ambuye.’ Nanga zingatheke bwanji kuti Iye akhale mwana wake?”

Achenjeza za Aphunzitsi Amalamulo

45Pamene anthu onse ankamvetsera, Yesu anati kwa ophunzira ake, 46“Chenjerani ndi aphunzitsi amalamulo. Iwo amakonda kuyenda atavala mikanjo ndipo amakonda kulonjeredwa mʼmisika ndipo amakhala mʼmipando yofunika mʼmasunagoge ndi mʼmalo aulemu mʼmaphwando. 47Amawadyera akazi amasiye chuma chawo ndi kuchita mapemphero aatali kuti awaone. Anthu oterewa adzalangidwa kwambiri.”

New Russian Translation

Луки 20:1-47

Религиозные вожди ставят под вопрос власть Иисуса

(Мат. 21:23-27; Мк. 11:27-33)

1В один из дней, когда Иисус учил в храме, проповедуя Радостную Весть, к Нему пришли первосвященники и учители Закона со старейшинами.

2– Скажи нам, чьей властью Ты все это делаешь и кто дал Тебе эту власть? – спросили они.

3В ответ Иисус сказал:

– Я тоже задам вам вопрос. Скажите, 4откуда Иоанн получил свое право крестить, с Небес или от людей?

5Они стали совещаться между собой:

– Если мы скажем: «С Небес», то Он спросит: «Почему же вы ему не поверили?» 6Если скажем: «От людей», то весь народ побьет нас камнями, ведь они убеждены, что Иоанн был пророком.

7– Мы не знаем, от кого, – ответили они.

8– Тогда и Я вам не скажу, чьей властью Я все это делаю, – сказал им Иисус.

Притча о злых виноградарях

(Мат. 21:33-46; Мк. 12:1-12)

9Он начал рассказывать народу притчу:

– Один человек посадил виноградник20:9 См. Ис. 5:1-2.. Он отдал его внаем виноградарям, а сам уехал в чужие края на долгое время. 10Когда пришло время, он послал слугу к виноградарям, чтобы они дали причитающуюся ему часть урожая. Виноградари же избили слугу и отослали его с пустыми руками. 11Он послал другого слугу, но они и этого избили, поиздевались над ним и отослали с пустыми руками. 12Он послал третьего слугу. Они и этого изранили и выбросили из виноградника.

13Тогда хозяин виноградника подумал: «Что же мне делать? Пошлю своего любимого сына, может, хоть его они устыдятся». 14Когда же виноградари увидели сына, они решили: «Это наследник. Давайте убьем его, чтобы наследство стало нашим». 15Они выбросили его из виноградника и убили. Что теперь сделает с ними хозяин виноградника? 16Конечно же, он придет и убьет тех виноградарей, а виноградник отдаст другим.

Слышавшие это воскликнули:

– Пусть этого не случится!

17Но Иисус, взглянув на них, сказал:

– Что означают слова Писания:

«Камень, Который отвергли строители,

стал краеугольным»?20:17 Пс. 117:22.

18Каждый, кто упадет на Тот Камень, разобьется вдребезги, а на кого Он упадет, того раздавит.

19Учители Закона и первосвященники, поняв, что эту притчу Иисус рассказал о них, хотели немедленно арестовать Его, но побоялись народа.

Вопрос об уплате налогов

(Мат. 22:15-22; Мк. 12:13-17)

20Они стали внимательно следить за Иисусом и подослали к Нему людей, которые, притворясь искренними, попытались бы подловить Его на слове, чтобы можно было отдать Его во власть наместника. 21Те спросили Иисуса:

– Учитель, мы знаем, что Ты правильно говоришь и учишь. Ты беспристрастен и истинно учишь пути Божьему. 22Следует ли нам платить налог кесарю или нет?

23Иисус видел их лукавство и сказал:

24– Покажите Мне динарий. Кто на нем изображен, и чье на нем имя?

– Кесаря, – ответили они.

25– Вот и отдавайте кесарево кесарю, а Божье – Богу, – сказал Он им.

26Они не могли подловить Его перед народом ни на каком Его слове, и, удивленные Его ответом, замолчали.

Саддукеи задают Иисусу вопрос о воскресении мертвых

(Мат. 22:23-33; Мк. 12:18-27)

27К Иисусу подошли несколько саддукеев20:27 Саддукеи – аристократическая религиозная группа иудеев, члены которой отвергали идею воскресения мертвых, не верили в ангелов и в духов. Саддукеи имели огромное влияние в Высшем Совете иудеев., которые утверждали, что нет воскресения мертвых. Они спросили Его:

28– Учитель, Моисей написал, что если у кого-либо умрет брат, у которого была жена, но не было детей, то он должен жениться на вдове и восстановить род20:28 Букв.: «семя». своему брату20:28 См. Втор. 25:5-6.. 29Так вот, было семь братьев. Первый брат женился и умер бездетным. 30Затем второй 31и третий женились на ней, и так все семеро. И все они умерли, не оставив детей. 32Потом умерла и женщина. 33Итак, после воскресения, чьей женой она будет? Ведь все семеро были женаты на ней?

34Иисус ответил им:

– Люди этого века женятся и выходят замуж. 35Те же, кто удостоится жить в будущем веке и будет воскрешен из мертвых, не будут ни жениться, ни выходить замуж, 36и умереть уже не смогут, но будут подобны ангелам. Они сыновья Бога, потому что участвуют в воскресении. 37А то, что мертвые воскресают, показал Моисей в истории с терновым кустом, когда он назвал Господа «Богом Авраама, Богом Исаака и Богом Иакова». 38Он Бог не мертвых, а живых, потому что для Него все живы!

39Некоторые из учителей Закона сказали:

– Хорошо Ты ответил, Учитель!

40И больше уже никто не решался задавать Ему вопросы.

Кем является Иисус?

(Мат. 22:41-46; Мк. 12:35-37)

41Затем Иисус спросил их:

– Почему говорят, что Христос – Сын Давида? 42Ведь сам Давид сказал в книге Псалмов:

«Сказал Господь Господу моему:

Сядь по правую руку от Меня,

43пока Я не повергну врагов Твоих

к ногам Твоим»20:42-43 Пс. 109:1..

44Итак, Давид называет Его Господом. Как же в таком случае Он может быть ему Сыном?

Иисус предостерегает от лицемерия

(Мат. 23:1-7; Мк. 12:38-39)

45Весь народ слушал Иисуса, а Он сказал Своим ученикам:

46– Остерегайтесь учителей Закона. Они любят наряжаться в длинные одежды и любят, когда их приветствуют на площадях. Они сидят на самых почетных местах в синагогах и на званых обедах. 47Они разоряют дома вдов и напоказ долго молятся. Таких ждет очень суровое наказание.