Luka 19 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Luka 19:1-48

Zakeyu Apulumutsidwa

1Yesu analowa mu Yeriko napitirira. 2Kunali munthu kumeneko dzina lake Zakeyu; iye anali mkulu wa wolandira msonkho ndipo anali wolemera. 3Iye ankafuna kuona Yesu kuti ndani, koma pokhala wamfupi sanathe chifukwa cha gulu la anthu. 4Choncho iye anathamangira patsogolo ndipo anakwera mu mtengo wamkuyu kuti amuone Iye, pakuti Yesu ankadutsa njira imeneyo.

5Yesu atafika pa malopo, anayangʼana mmwamba ndipo anati kwa iye, “Zakeyu, tsika msangamsanga. Ine ndiyenera kukhala mʼnyumba mwako lero.” 6Ndipo nthawi yomweyo anatsika ndipo anamulandira mosangalala.

7Anthu onse ataona zimenezi anayamba kungʼungʼudza, nati, “Iye akupita kuti akakhale mlendo wa wochimwa.”

8Koma Zakeyu anayimirira ndipo anati kwa Ambuye, “Taonani Ambuye! Theka la chuma changa ndipereka kwa osauka ndipo ngati ndinamubera wina aliyense pa chilichonse, ndidzamubwezera mochulukitsa kanayi.”

9Yesu anati kwa iye, “Lero chipulumutso chafika mʼnyumba ino, chifukwa munthu uyu nayenso ndi mwana wa Abrahamu. 10Pajatu Mwana wa Munthu anabwera kudzafunafuna ndi kupulumutsa chotayikacho.”

Antchito Opindula Mosiyana

11Pamene iwo ankamvera izi, Iye anapitiriza kuwawuza fanizo, chifukwa Iye anali kufupi ndi Yerusalemu ndipo anthu ankaganiza kuti ufumu wa Mulungu ukanaoneka nthawi yomweyo. 12Iye anati, “Munthu wa banja laufumu anapita ku dziko lakutali kukadzozedwa ufumu ndipo kenaka abwerenso kwawo. 13Tsono iye anayitana antchito ake khumi ndi kuwapatsa ndalama khumi. Iye anati, ‘Gwiritsani ntchito ndalama izi mpaka nditabwerera.’

14“Koma anthu ake anamuda ndipo anatuma nthumwi pambuyo pake kukanena kuti, ‘Sitikufuna munthuyu kuti akhale mfumu yathu.’

15“Iye analandira ufumuwo ngakhale zinali zotero, ndipo anabwerera kwawo. Kenaka iye anatumiza uthenga kwa antchito ake amene anawapatsa ndalama aja, ndi cholinga chakuti adziwe chimene anapindula nazo.

16“Woyamba anabwera ndipo anati, ‘Bwana ndalama zanu zapindula khumi zina.’

17“Bwana wakeyo anayankha kuti, Wachita bwino wantchito wabwino. ‘Chifukwa wakhulupirika pa zinthu zazingʼono, lamulira mizinda khumi.’

18“Wachiwiri anabwera ndipo anati, ‘Bwana, ndalama zanu zapindula zisanu zina.’

19“Bwana anayankha kuti, ‘Iwe lamulira mizinda isanu.’

20“Kenaka wantchito wina anabwera ndipo anati, ‘Bwana, ndalama yanu nayi; ine ndinayibisa ndi kuyisunga mʼkansalu. 21Ine ndimakuopani, chifukwa ndinu munthu wowuma mtima. Inu mumatenga chimene simunachiyike ndi kukolola chimene simunadzale.’

22“Bwana wake anayankha kuti, ‘Ine ndikukuweruza iwe ndi mawu ako omwewo. Ndiwe wantchito woyipa. Kani umadziwa kuti ndine munthu wowuma mtima ndi wotenga chimene sindinasungitse, ndi kukolola chimene sindinadzale? 23Nanga nʼchifukwa chiyani sunasungitse ndalama yanga, kuti ine pobwera, ndidzayitenge ndi chiwongoladzanja?’

24“Ndipo iye anawuza amene anayimirira pafupi kuti, ‘Tengani ndalama yake ndi kumupatsa amene ali ndi ndalama khumiyo!’ ”

25Iwo anati, “Bwana iyeyu ali nazo kale khumi!”

26Iye anayankha kuti, “Ndikukuwuzani kuti, aliyense amene ali nazo, adzapatsidwa zambiri, koma amene alibe, adzalandidwa ngakhale chimene ali nacho. 27Tsono adani anga aja amene sankafuna kuti ndikhale mfumu yawo, abweretseni pano ndi kuwapha ine ndikuona.”

Yesu Alowa mu Yerusalemu Mwaulemerero

28Yesu atatha kunena izi, anayendabe kupita ku Yerusalemu. 29Iye atayandikira ku Betifage ndi Betaniya pa phiri lotchedwa Olivi, Iye anatuma awiri a ophunzira nati kwa iwo, 30“Pitani mʼmudzi uli patsogolo panu, mukakalowa mʼmudzimo, mukapeza mwana wabulu womangiriridwa amene wina aliyense sanakwerepo. Mukamumasule ndi kubwera naye kuno. 31Ngati wina aliyense akakufunsani kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani mukumumasula mwana buluyo?’ Mukamuwuze kuti, ‘Ambuye akumufuna.’ ”

32Otumidwawo anapita nakamupeza mwana wabulu monga momwe Yesu anawawuzira. 33Pamene ankamasula mwana wabuluyo, eni ake anawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukumasula mwana wabuluyo?”

34Iwo anayankha kuti, “Ambuye akumufuna.”

35Iwo anabweretsa buluyo kwa Yesu, naponya zovala zawo pa bulupo ndi kumukwezapo Yesu. 36Pamene ankapita, anthu anayala zovala zawo mu msewu.

37Iye atafika pafupi ndi pamene msewu umatsikira ku phiri la Olivi, gulu lonse la ophunzira linayamba kuyamika Mulungu mwachimwemwe ndi mawu ofuwula chifukwa cha zodabwitsa zonse anaziona.

38“Yodala mfumu imene ikubwera mʼdzina la Ambuye!”

“Mtendere kumwamba ndi ulemerero mmwambamwamba!”

39Ena mwa Afarisi mʼgulumo anati kwa Yesu, “Aphunzitsi, adzudzuleni ophunzira anu!”

40Iye anayankha kuti, “Ine ndikukuwuzani kuti, ngati atakhala chete, miyala idzafuwula.”

41Iye atayandikira ku Yerusalemu ndi kuona mzindawo, anawulirira 42nati, “Iwe ukanadziwa lero lino zinthu zokubweretsera mtendere, koma tsopano zabisikira maso ako. 43Pakuti masiku adzabwera pamene adani ako adzamanga mitumbira yankhondo nakuzungulira, nadzakutsekereza mbali zonse. 44Iwo adzakugwetsera pansi, iwe, ana ako onse a mʼkati mwako. Iwo sadzasiya mwa iwe mwala wina pa unzake, chifukwa sunazindikire nthawi ya kubwera kwa Mulungu.”

Yesu mʼNyumba ya Mulungu

45Kenaka Iye analowa mʼdera la Nyumba ya Mulungu ndi kuyamba kutulutsa kunja amene amachita malonda. 46Iye anawawuza kuti, “Zinalembedwa kuti Nyumba yanga idzakhala nyumba ya mapemphero, koma inu mwayisadutsa phanga la achifwamba.”

47Tsiku lililonse amaphunzitsa mʼNyumba ya Mulungu. Koma akulu a ansembe, aphunzitsi amalamulo ndi atsogoleri pakati pa anthu amayesetsa kuti amuphe. 48Komabe iwo sanathe kupeza njira ina iliyonse kuti achite izi, chifukwa anthu onse anakhulupirira mawu ake.

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Луко 19:1-48

Покаяние сборщика налогов Заккая

1Исо вошёл в Иерихон и проходил через город. 2Там был человек, которого звали Заккай, он был начальником сборщиков налогов и богатым человеком. 3Он пытался увидеть, кто же Этот Исо, но не мог из-за толпы, потому что был маленького роста. 4Тогда, чтобы увидеть Его, Заккай забежал вперёд и залез на тутовое дерево, росшее в том месте, где Исо должен был проходить. 5Когда Исо подошёл к этому месту, Он посмотрел вверх и сказал:

– Заккай, спускайся скорее, потому что сегодня Я должен быть у тебя в доме.

6Заккай быстро спустился и с радостью принял Его. 7Все, кто видел это, начали возмущаться:

– Он пошёл в гости к грешнику!

8Заккай же встал и сказал Исо:

– Повелитель! Половину моего имущества я раздам бедным, а если я с кого-либо взял лишнее, я возвращу ему вчетверо! 9Тогда Исо сказал ему:

– Сегодня в этот дом пришло спасение, потому что этот человек тоже сын Иброхима!19:9 Иброхим, получив оправдание перед Всевышним через свою веру (см. Нач. 15:6), был назван отцом всех верующих (см. Рим. 4:11-12). И хотя Заккай был физическим потомком Иброхима, здесь он показал себя сыном Иброхима и в духовном плане (см. Ин. 8:39; Гал. 3:29). 10Ведь Ниспосланный как Человек пришёл, чтобы найти и спасти потерянное.

Притча о порученных деньгах

(Мат. 25:14-30)

11Тем, кто это слушал, Исо рассказал притчу. (Они были уже недалеко от Иерусалима, и люди полагали, что Царство Всевышнего должно наступить немедленно.) 12Исо сказал:

– Один знатный человек отправлялся в далёкую страну, чтобы получить царскую власть и вернуться. 13Созвав десять своих рабов, он дал денег каждому в размере стодневного заработка19:13 Букв.: «он дал им десять мин». Другими словами, каждый получил по одной мине. Мина – древнегреческая монета, которая равнялась средней оплате ста рабочих дней наёмного работника.. «Пустите эти деньги в дело, пока я не возвращусь», – сказал он. 14Но жители его страны ненавидели его и послали вслед за ним посольство, чтобы заявить: «Мы не хотим, чтобы этот человек был нашим царём».

15Когда он возвратился, получив царскую власть, то приказал созвать к нему рабов, которым доверил деньги, чтобы спросить их, какую они получили прибыль. 16Первый явился и говорит: «Господин, твои деньги принесли десятикратный доход!» 17«Молодец! – похвалил хозяин. – Ты хороший раб. Ты был верен в малом, получи теперь в управление десять городов».

18Пришёл второй раб и говорит: «Господин, твои деньги принесли пятикратный доход!» 19Хозяин ответил: «Получи теперь в управление пять городов».

20Затем пришёл третий раб и говорит: «Господин, вот твои деньги, я хранил их завёрнутыми в платок. 21Я боялся тебя, так как ты человек жестокий. Ты берёшь там, где не клал, и жнёшь там, где не сеял». 22Хозяин тогда говорит: «Ах ты, негодный раб! Я буду судить тебя твоими же словами! Ты знал, что я человек жестокий и что я беру там, где не клал, и жну там, где не сеял? 23Почему же ты не пустил мои деньги в оборот, чтобы, когда я вернусь, отдать их мне с прибылью?» 24И он сказал стоявшим там: «Заберите у него его деньги и отдайте тому, у кого уже есть десятикратная прибыль». 25«Господин, – говорят ему, – да ведь у него и так уже десятикратная прибыль!»

26Хозяин ответил: «Говорю вам, что каждому, у кого есть, будет дано ещё, а у кого нет, будет отнято и то, что он имеет. 27А моих врагов, которые не хотели, чтобы я царствовал над ними, приведите сюда и убейте прямо передо мной».

Торжественный въезд в Иерусалим

(Мат. 21:1-9; Мк. 11:1-10; Ин. 12:12-15)

28Сказав это, Исо пошёл дальше к Иерусалиму. 29Приближаясь к Виффагии и Вифании, что расположены у Оливковой горы, Он послал вперёд двух учеников, 30сказав:

– Идите в селение, которое перед вами, и, войдя в него, вы найдёте там привязанного ослёнка, на которого ещё никто не садился. Отвяжите его и приведите сюда. 31Если кто-нибудь вас спросит: «Зачем вы его отвязываете?» – отвечайте: «Он нужен Повелителю».

32Ученики пошли и нашли всё так, как им сказал Исо. 33Когда они отвязывали ослёнка, его хозяева спросили их:

– Вы зачем отвязываете ослёнка?

34Они ответили:

– Он нужен Повелителю.

35Они привели ослёнка к Исо и, набросив на него свои плащи, посадили на него Исо19:35 Исо въехал в Иерусалим на осле, как миролюбивый и смиренный царь, а не на боевом коне с мечом, как это делали цари того времени.. 36Когда Он ехал, люди начали расстилать на дороге свои плащи. 37И когда Он приблизился к месту, где дорога спускается с Оливковой горы, всё множество учеников начало радостно и громко прославлять Всевышнего за все чудеса, которые они видели:

38– Благословен Царь, Который приходит во имя Вечного!19:38 Заб. 117:26.

Мир на небе и слава на высоте небес!

39Некоторые из бывших в толпе блюстителей Закона сказали Исо:

– Учитель, запрети Своим ученикам!

40Он ответил:

– Говорю вам, если они умолкнут, то камни начнут кричать.

Плач об Иерусалиме

41Когда они подходили к Иерусалиму и уже был виден город, Исо заплакал о нём:

42– Если бы и ты сегодня понял, что могло бы принести тебе мир! Но сейчас это скрыто от твоих глаз. 43Наступят дни, когда твои враги обнесут тебя осадными валами, окружат тебя и стеснят тебя со всех сторон. 44Они уничтожат тебя и твоих жителей и не оставят в тебе камня на камне, потому что ты не распознал времени, когда Всевышний посетил тебя.

Изгнание торговцев из храма

(Мат. 21:12-16; Мк. 11:15-18; Ин. 2:13-16)

45Затем Исо вошёл во двор храма и стал выгонять оттуда тех, кто там торговал.

46– Написано, – говорил Он им, – «Дом Мой будет домом молитвы»19:46 Ис. 56:7., а вы превратили его в разбойничье логово19:46 См. Иер. 7:11..

47Исо каждый день учил в храме, а главные священнослужители, учители Таврота и вожди народа искали случая, чтобы убить Его. 48Однако они не знали, как это сделать, потому что все люди слушали Исо, боясь упустить хоть одно слово.