Luka 12 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Luka 12:1-59

Chenjezo ndi Chilimbikitso

1Nthawi yomweyo, anthu miyandamiyanda atasonkhana, ndi kumapondanapondana, Yesu anayamba kuyankhula poyamba kwa ophunzira ake, nati, “Chenjereni ndi yisiti wa Afarisi, amene ndi chinyengo. 2Palibe chinthu chophimbika chimene sichidzawululika, kapena chobisika chimene sichidzadziwika. 3Chimene mwanena mu mdima chidzamveka dzuwa likuwala, ndipo zimene mwanongʼona mʼkhutu mʼchipinda chamʼkati, zidzayankhulidwa pa denga la nyumba.

4“Ine ndikuwuzani, abwenzi anga, musachite mantha ndi amene amapha thupi chifukwa akatero sangachitenso kanthu. 5Koma Ine ndidzakuonetsani amene muyenera kumuopa: Wopani Iye, amene pambuyo pakupha thupi, ali ndi mphamvu yakukuponyani ku gehena. Inde, Ine ndikuwuzani, muopeni Iye. 6Kodi atimba asanu samagulidwa ndi ndalama ziwiri? Ngakhale zili chomwecho palibe imodzi ya izo imene imayiwalika ndi Mulungu. 7Ndithudi, tsitsi lonse la mʼmutu mwanu ndi lowerengedwa. Musachite mantha; inu ndi oposa kwambiri mpheta zambiri.

8“Ine ndikukuwuza kuti, aliyense amene avomereza Ine pamaso pa anthu, Mwana wa Munthu adzamuvomerezanso pamaso pa angelo a Mulungu. 9Koma iye amene andikana Ine pamaso pa anthu adzakanidwanso pamaso pa angelo a Mulungu. 10Ndipo aliyense amene ayankhulira Mwana wa Munthu mawu oyipa adzakhululukidwa, koma iye wochitira mwano Mzimu Woyera sadzakhululukidwa.

11“Akadzakutengerani ku masunagoge pamaso pa oweruza ndi a maulamuliro, musadere nkhawa mmene mudzadzitchinjirizire nokha kapena chimene mudzayankhule, 12pakuti Mzimu Woyera nthawi imeneyo adzakuphunzitsani zoyenera kunena.”

Fanizo la Munthu Wachuma Wopusa

13Munthu wina mʼgulu la anthu anati kwa Iye, “Aphunzitsi, muwuzeni mʼbale wanga andigawireko chuma chamasiye.”

14Yesu anayankha kuti, “Munthu iwe, ndani anandiyika Ine kukhala woweruza kapena wogawa chuma pakati panu?” 15Kenaka Iye anawawuza kuti, “Chenjerani! Khalani tcheru ndi makhalidwe onse adyera; moyo wa munthu sukhala chifukwa cha kuchuluka kwa zimene ali nazo.”

16Ndipo Iye anawawuza fanizo ili, “Munda wa munthu wina wachuma unabereka kwambiri. 17Iye anaganiza kuti, ‘Ndichite chiyani? Ndilibe malo osungiramo mbewu zanga.’

18“Ndipo Iye anati, ichi ndi chimene ndidzachite: Ndidzaphwasula nkhokwe zanga zonse ndi kumanga zokulirapo, ndipo ndidzasungira mʼmenemo mbewu ndi katundu. 19Ndipo ndidzawuza moyo wanga kuti, ‘Uli nazo zinthu zabwino zambiri zimene zikhalepo zaka zambiri, usapupulume; idya, imwa ndi kukondwera.’ ”

20“Koma Mulungu anati kwa iye, ‘Iwe wopusa! Usiku womwe uno moyo wako udzachotsedwa kwa iwe, ndipo ndi ndani amene adzatenge zimene iwe wadzikonzera?’

21“Umu ndi mmene zidzakhalire ndi aliyense amene amadziwunjikira chuma, koma si wachuma pamaso pa Mulungu.”

Musadere Nkhawa

22Kenaka Yesu anati kwa ophunzira ake, “Choncho Ine ndikuwuzani kuti musadere nkhawa za moyo wanu, zimene mudzadya; kapena za thupi lanu, zimene mudzavala. 23Moyo uposa chakudya, ndi thupi liposa chovala. 24Taonani makwangwala: iwo safesa kapena kukolola, alibe nyumba zosungamo zinthu kapena nkhokwe; komabe, Mulungu amawadyetsa. Koposa kotani inu amene ndi ofunikira kuposa mbalame. 25Ndi ndani wa inu akhoza kuwonjeza ora pa moyo wake chifukwa cha kudandaula? 26Popeza simungathe kuchita kanthu kakangʼono aka, nʼchifukwa chiyani mumadandaula ndi zinazi?

27“Taonani mmene maluwa amakulira. Iwo sagwira ntchito kapena kusoka zovala. Koma Ine ndikuwuzani kuti, ngakhale Solomoni muulemelero wake wonse sanavalepo ngati limodzi la awa. 28Ngati umu ndi mmene Mulungu amavekera udzu wakuthengo, umene lero ulipo ndipo mawa uponyedwa pa moto, nanga Iye adzakuvekani inu motani. Haa! Inu achikhulupiriro chochepa! 29Ndipo musayike mtima wanu pa zimene mudzadye kapena kumwa; musade nazo nkhawa. 30Pakuti anthu akunja amathamanga kufunafuna zinthu zotere, ndipo Atate amadziwa kuti mumazifuna zimenezi. 31Koma funafunani ufumu wake, ndipo mudzapatsidwa zonsezi.

Chuma cha Kumwamba

32“Musachite mantha, inu kagulu kankhosa, pakuti zinakondweretsa Atate anu kuti akupatseni ufumu. 33Gulitsani zonse zimene muli nazo, ndipo ndalama zake mupereke kwa osauka. Dzipezereni zikwama zandalama zimene sizidzatha, ndi kudzikundikira chuma chomwe sichidzatha kumwamba, kumene mbala sizingafikeko, ndipo dzimbiri silingawononge. 34Popeza kumene kuli chuma chanu, mtima wanunso udzakhala komweko.”

Kukhala a Atcheru

35“Khalani okonzekeratu ndipo nyale zanu ziziyaka, 36ngati anthu oyembekezera kubwera kwa mbuye wawo kuchokera kuphwando la ukwati, kuti pamene afika ndi kugogoda akhoza nthawi yomweyo kumutsekulira chitseko. 37Zidzakhala bwino kwa antchitowo amene mbuye wawo pobwera adzawapeze akudikira. Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti adzakonzekera kuwatumikira, adzakhala nawo pa tebulo ndipo adzabwera ndi kuwatumikira. 38Zidzakhala bwino kwa antchitowo amene mbuye wawo adzawapeze ali okonzeka, ngakhale iye atabwera pa ora lachiwiri kapena lachitatu usiku. 39Koma zindikirani izi: Ngati mwini nyumba akanadziwa ora limene mbala ibwera, sakanalola kuti nyumba yake ithyoledwe. 40Inunso muyenera kukhala okonzeka, chifukwa Mwana wa Munthu adzabwera pa ora limene simukumuyembekezera Iye.”

Wantchito Wokhulupirika ndi Wosakhulupirika

41Petro anafunsa kuti, “Kodi mukunena fanizoli kwa ife, kapena kwa aliyense?”

42Ambuye anayankha kuti, “Kodi tsono woyangʼanira wokhulupirika ndi wanzeru ndani? Kodi ndi amene mbuye wake wamuyika kukhala oyangʼanira antchito ake kuti aziwapatsa ndalama yachakudya pa nthawi yake yoyenera? 43Zidzamukhalira bwino wantchito amene mbuye wake adzamupeza akuchita zimene pamene iye abwera. 44Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti adzamuyika kukhala woyangʼanira katundu wake yense. 45Koma tiyerekeze kuti wantchitoyo aziganiza mu mtima mwake kuti, ‘Bwana wanga akuchedwa kwambiri kubwera,’ ndipo kenaka ndi kuyamba kumenya antchito aamuna ndi aakazi ndi kudya, kumwa ndi kuledzera. 46Mbuye wake adzabwera tsiku limene iye sakumuyembekezera ndi ora limene iye sakudziwa. Iye adzamulanga ndi kumusiya kumalo kumene kuli osakhulupirira.

47“Wantchito amene amadziwa chifuniro cha mbuye wake koma wosakonzeka kapena wosachita chimene mbuye wake akufuna adzakwapulidwa zikwapu zambiri. 48Koma wantchito amene sadziwa koma nʼkuchita zinthu zoyenera chilango, adzakwapulidwa zikwapu zochepa. Aliyense amene anapatsidwa zambiri, adzayenera kubwezanso zambiri; ndipo amene anamusungitsa zambiri, adzamulamula kuti abweze zambirinso.”

Za Kugawikana

49“Ine ndabwera kudzayatsa moto pa dziko lapansi, ndipo ndikanakonda ukanayaka kale. 50Koma Ine ndiyenera kubatizidwa, ndipo ndikusautsika mu mtima mpaka utachitika! 51Kodi mukuganiza kuti Ine ndinabwera kudzabweretsa mtendere pa dziko lapansi? Ayi, Ine ndikukuwuzani kuti, ndinabweretsa kugawikana. 52Kuyambira tsopano mpaka mʼtsogolo mʼbanja limodzi mudzakhala anthu asanu ndipo adzawukirana wina ndi mnzake, atatu kuwukira awiri, ndipo awiri kuwukira atatu. 53Anthu adzawukirana. Abambo kudzawukira mwana wawo wamwamuna, mwana wawoyo adzawukira abambo ake. Amayi adzawukira mwana wawo wamkazi, mwana wawoyo adzawukira amayi ake. Amayi adzawukira mpongozi wawo wamkazi, mpongoziyo adzawukira amayiwo.”

Kumasulira Nthawi

54Iye anati kwa gulu la anthu, “Pamene mukuona mtambo ukukwera kummawa, nthawi yomweyo inu mumati, ‘kugwa mvula,’ ndipo imagwadi. 55Ndipo pamene mphepo yakummwera ikuwomba, inu mumati ‘kutentha’ ndipo kumaterodi. 56Achiphamaso inu! Inu mumadziwa kutanthauzira maonekedwe a dziko lapansi ndi thambo. Zikutheka bwanji kuti simukudziwa kumasulira kwa nthawi ino?

57“Bwanji simukuzindikira nokha zoyenera kuchita? 58Pamene mukupita kwa woweruza ndi amene munalakwirana naye, yesetsani kwambiri kuti muyanjane naye mʼnjiramo, chifukwa mukapanda kutero akhoza kukutengerani ku bwalo la milandu ndipo woweruzayo adzakuperekani kwa woyangʼanira ndende, ndipo woyangʼanira ndendeyo adzakuponyani mʼndende. 59Ine ndikuwuzani kuti, simudzatulukamo mpaka mutalipira ndalama zonse.”

New Serbian Translation

Лука 12:1-59

Упозорење против лицемерја

1У међувремену се окупило на хиљаде људи, тако да су газили једни друге. Тада Исус прво поче да говори својим ученицима: „Чувајте се фарисејског квасца, који је лицемерје. 2Нема ничег што је скривено, да се неће открити, нити тајног, да се неће дознати. 3Јер, што сте рекли у тами, чуће се на светлости дана, и што сте рекли иза затворених врата, разгласиће се са кровова.

Кога се треба бојати?

4Пријатељи моји, кажем вам, не бојте се оних који убијају тело, јер после тога не могу више ништа да учине. 5Рећи ћу вам кога да се бојите: бојте се Бога, који, пошто убије, има власт да баци у пакао. Да, кажем вам, њега се бојте. 6Зар се не продају пет врабаца за два новчића? Ипак, ни један од њих није заборављен од Бога. 7А вама су и све власи на глави пребројане. Зато се не бојте: ви вредите много више од јата врабаца.

8Кажем вам: свако ко ме призна пред људима, признаћу и ја њега пред анђелима Божијим. 9А ко се мене одрекне пред људима, одрећи ћу се и ја њега пред анђелима Божијим. 10Свако ко каже реч против Сина Човечијег, биће му опроштено, али ко изговори хулу против Светога Духа, томе се неће опростити.

11Када вас буду изводили у синагоге да вам суде, или пред намеснике и владаре, не брините се како ћете се бранити, или шта ћете говорити, 12јер ће вас Свети Дух поучити шта да кажете у тај час.“

13Неко из народа рече: „Учитељу, реци мом брату да подели са мном наследство!“

14Исус му рече: „Човече, ко је мене поставио да судим или делим имовину међу вама?“ 15Онда се обратио свима: „Пазите и чувајте се сваке похлепе, јер ничији живот не зависи од обиља његових добара, колико год да их има.“

16Онда им исприча једну причу: „Неком богатом човеку обилно родила њива. 17Човек је размишљао у себи: ’Шта да урадим? Немам где да сакупим летину.’

18Онда рече: ’Овако ћу учинити: срушићу своје житнице и саградићу веће, па ћу тамо сместити све жито и остала добра. 19Онда ћу рећи себи: „Душо моја, имаш многа добра смештена за дуго година. Одмарај, једи, пиј и уживај!“’

20Али Бог му рече: ’Безумниче! Још ноћас ћу узети твоју душу. Коме ли ће остати оно што си стекао?’

21Тако бива са сваким који згрће себи богатство, а пред Богом је сиромашан.“

Поуздање у Бога

22Исус рече својим ученицима: „Стога вам кажем: не брините се за живот, шта ћете јести, или за тело, шта ћете обући, 23јер је живот вреднији од хране и тело од одеће. 24Погледајте гавране! Они нити сеју, нити жању, немају ни складишта ни житнице, а Бог их храни. Ви вредите много више од птица. 25Ко од вас може бринући се продужити себи живот, макар само и за кратко време? 26Дакле, ако не можете да учините ни то што је најмање, зашто се бринете за остало?

27Погледајте љиљане како расту! Не труде се, нити преду, а ја вам кажем да ни Соломон у свој својој раскоши није био одевен као и један од њих. 28Па ако Бог тако одева биље које је данас у пољу, а већ сутра се баца у пећ, колико ли ће пре оденути вас, о, маловерни! 29Зато се не оптерећујте тиме шта ћете јести или пити и не брините се око тога, 30јер све то траже и многобошци у овоме свету. Ваш Отац зна да вам је све то потребно. 31Него, тражите Царство његово, а Бог ће вам ово додати.

32Не бој се, мало стадо, јер је Оцу било по вољи да вам да Царство. 33Продајте своју имовину и дајте је као милостињу. Опремите се торбама које неће дотрајати и неисцрпним благом са неба, које лопов не краде нити мољац уништава. 34Јер, где је ваше благо, тамо ће бити и ваше срце.

Спремност и будност

35Опашите своје бокове, а ваше светиљке нека горе. 36Будите као слуге које очекују свога господара да се врати са свадбе, да му одмах отворе врата кад он дође и покуца. 37Благо оним слугама које господар, кад се врати, нађе будне. Заиста вам кажем да ће се сам господар опасати, посадити их за трпезу и послуживати их. 38Благо оним слугама које господар, када дође, нађе будне и приправне у поноћ или пред свитање. 39Ово знајте: ако би домаћин знао у које доба ће лопов доћи, не би дозволио да му провали у кућу. 40Тако и ви будите спремни, јер ће Син Човечији доћи у час када не мислите.“

41Петар упита: „Господе, говориш ли ову причу само нама или и свима осталима?“

42Господ одговори: „Ко је, дакле, верни и мудри управитељ? То је онај кога Господар постави да се стара о осталим слугама да добијају оброке на време. 43Блажен је онај слуга кога Господар, када дође, затекне да овако ради. 44Заиста вам кажем да ће му поверити управу над целим својим имањем. 45Али ако тај слуга каже: ’Мој Господар се задржао на путу’, па почне да туче слуге и слушкиње, да једе, пије и опија се, 46доћи ће Господар ових слугу у дан у који га не очекује, те ће га посећи и одредити му место међу неверницима.

47Слуга који зна господареву вољу, а не извршује је и није приправан, биће ишибан јако. 48А слуга који не зна, а учини оно што заслужује казну, биће мало шибан. Од свакога коме је много дано, много ће се и захтевати. Коме је више поверено, од тога ће се још више захтевати.

Исус – узрок поделе

49Дошао сам да бацим огањ на земљу. О, како бих волео да већ пламти! 50Треба и крштење да примим, и како ми је тешко док се то не сврши! 51Мислите ли да сам дошао да донесем мир на земљу? Не, кажем вам, него раздор. 52Наиме, од сада ће се петоро у кући поделити: троје против двоје и двоје против троје, 53отац против сина и син против оца, мајка против ћерке и ћерка против мајке, свекрва против снахе и снаха против свекрве.“

Знаци времена

54А мноштву је рекао: „Када видите да се облак појављује на западу, одмах кажете да ће бити невреме, и буде невреме. 55А кад дуне ветар с југа, ви кажете да ће бити врућина, и тако и буде. 56Лицемери! Изглед земље и неба знате да протумачите; како онда не знате да протумачите ово време?

57Зар сами не увиђате шта је праведно? 58Ако те зајмодавац потера на суд, настој колико можеш да изгладиш ствар са њим док сте још на путу. У противном, одвешће те пред судију и судија ће те предати судском службенику, па ће те овај бацити у тамницу. 59Кажем ти да нећеш изаћи оданде док не исплатиш и последњи новчић.“