Luka 1 – CCL & TCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Luka 1:1-80

Mawu Oyamba

1Ambiri anayesa kufotokoza nkhani ya zimene zinakwaniritsidwa pakati pathu, 2monga mmene zinaperekedwera kwa ife ndi iwo amene anaona poyambirira ndi atumiki a mawu. 3Popeza inenso ndafufuza mosamalitsa chilichonse kuyambira pachiyambi, zandikomera kukulemberani mwatsatanetsatane inu wolemekezeka Tiofilo, 4kuti mudziwe bwinobwino zoona za zinthu zimene mwaphunzitsidwa.

Aneneratu za Kubadwa kwa Yohane Mʼbatizi

5Mʼmasiku a Herode, mfumu ya Yudeya, kunali wansembe dzina lake Zakariya wa gulu la ansembe la Abiya; mkazi wake Elizabeti analinso wa fuko la Aaroni. 6Onse awiri anali olungama pamaso pa Mulungu, ndipo amasunga malamulo ndi malangizo onse a Ambuye osalakwa konse. 7Koma analibe ana chifukwa Elizabeti anali wosabereka; ndipo onse anali okalamba.

8Nthawi yogwira ntchito yotumikira ansembe a gulu la Zekariya, Zekariya ankatumikira ngati wansembe pamaso pa Mulungu, 9Zakariyayo anasankhidwa mwa maere, monga mwa mwambo wa unsembe, kupita mʼNyumba ya Ambuye kukafukiza lubani. 10Ndipo nthawi yofukiza lubani itafika, gulu lonse lopembedza linkapemphera kunja.

11Kenaka mngelo wa Ambuye anaonekera kwa iye, atayimirira ku dzanja lamanja la guwa lofukizira. 12Zakariya ataona mngeloyo, anadzidzimuka ndipo anagwidwa ndi mantha. 13Koma mngeloyo anati kwa iye: “Usachite mantha, Zakariya; pemphero lako lamveka. Mkazi wako Elizabeti adzakuberekera iwe mwana wamwamuna ndipo udzamutche dzina loti Yohane. 14Ndipo adzakhala chimwemwe ndi chisangalalo kwa iwe, ndipo ambiri adzasangalala chifukwa cha kubadwa kwake, 15chifukwa adzakhala wamkulu pamaso pa Ambuye. Iye sadzamwa vinyo kapena chakumwa choledzeretsa, ndipo adzazadzidwa ndi Mzimu Woyera kuyambira pa kubadwa. 16Iye adzabweretsanso Aisraeli ambiri kwa Ambuye Mulungu wawo. 17Ndipo iye adzabwera Ambuye asanabwere mu mzimu ndi mphamvu ya Eliya. Adzatembenuzira mitima ya abambo kwa ana awo ndi osamvera ku nzeru ya olungama, kuthandiza anthu kuti akonzekere kubwera kwa Ambuye.”

18Zakariya anamufunsa mngeloyo kuti, “Kodi ndingatsimikize bwanji zimenezi? Ine ndine wokalamba ndipo mkazi wanga ali ndi zaka zambiri.”

19Mngeloyo anayankha kuti, “Ine ndine Gabrieli. Ndimayima pamaso pa Mulungu, ndipo ndatumidwa kwa iwe kudzakuwuza uthenga wabwinowu. 20Ndipo kuyambira tsopano sudzatha kuyankhula kufikira izi zitachitika chifukwa sunakhulupirire mawu awa, amene adzakwaniritsidwe pa nthawi yake yoyenera.”

21Pa nthawiyi, anthu ankadikira Zakariya ndipo anadabwa chifukwa anatenga nthawi yayitali ali mʼNyumba ya Mulungu. 22Atatuluka sanathe kuyankhulana nawo. Anazindikira kuti anaona masomphenya mʼNyumbamo, chifukwa ankasonyeza zizindikiro kwa iwo koma sankatha kuyankhula.

23Nthawi yake yotumikira itatha, anabwerera kwawo. 24Zitatha izi, mkazi wake Elizabeti anakhala ndi pakati ndipo anadzibisa kwa miyezi isanu. 25Iye anati, “Ambuye wandichitira izi, kuti mʼmasiku ano wandionetsera kukoma mtima kwake ndi kuchotsa manyazi anga pakati pa anthu.”

Aneneratu za Kubadwa kwa Yesu

26Mwezi wachisanu ndi chimodzi, Mulungu anatuma mngelo Gabrieli ku Nazareti, mudzi wa ku Galileya, 27kwa namwali wopalidwa ubwenzi ndi Yosefe, wa fuko la Davide. Dzina la namwaliyo linali Mariya. 28Mngeloyo anafika kwa iye nati, “Moni, inu amene Ambuye wakukomerani mtima kwambiri! Ambuye ali ndi inu.”

29Mariya anavutika kwambiri ndi mawu awa ndipo anadabwa ndi kulonjera kotere. 30Koma mngeloyo anati kwa iye, “Usachite mantha Mariya, pakuti wapeza chisomo pamaso Mulungu. 31Udzakhala woyembekezera ndipo udzabala mwana wamwamuna ndipo udzamupatse dzina loti Yesu. 32Iye adzakhala wamkulu ndipo adzatchedwa Mwana wa Wammwambamwamba. Ambuye Mulungu adzamupatsa Iye mpando waufumu wa abambo ake Davide, 33ndipo adzalamulira pa nyumba ya Yakobo ku nthawi zonse; ufumu wake sudzatha.”

34Mariya anafunsa mngeloyo kuti, “Izi zingatheke bwanji popeza ine sindidziwa mwamuna?”

35Mngelo anayankha kuti, “Mzimu Woyera adzabwera pa iwe ndipo mphamvu ya Wammwambamwamba idzakuphimba, ndipo Woyerayo amene adzabadwe adzatchedwa Mwana wa Mulungu. 36Ngakhale Elizabeti mʼbale wako adzakhala ndi mwana mu ukalamba wake ndipo iye amene amati ndi wosabereka, uno mwezi wake wachisanu ndi chimodzi. 37Pakuti palibe chinthu chosatheka ndi Mulungu.”

38Mariya anayankha kuti, “Ine ndine mtumiki wa Ambuye. Zikhale kwa ine monga mwanenera.”

Mariya Acheza kwa Elizabeti

39Nthawi imeneyo anakonzeka ndipo anapita mofulumira ku mudzi wa ku mapiri a dziko la Yudeya, 40kumene anakalowa mʼnyumba ya Zakariya nalonjera Elizabeti. 41Elizabeti atamva moni wa Mariya, mwana anatakataka mʼmimba mwake, ndipo Elizabeti anadzazidwa ndi Mzimu Woyera. 42Anafuwula ndi mawu akulu kuti, “Ndiwe wodala pakati pa akazi, ndipo ndi wodala mwana amene udzabereke! 43Koma nʼchifukwa chiyani andikomera mtima kuti amayi a Ambuye anga abwere kwa ine? 44Nthawi yomwe ndinamva mawu akulonjera kwanu, mwana anatakataka mʼmimba mwanga chifukwa cha chimwemwe. 45Wodala iye amene wakhulupirira kuti chimene Ambuye wanena kwa iye chidzakwaniritsidwa!”

Nyimbo ya Mariya

46Ndipo Mariya anati:

“Moyo wanga ulemekeza Ambuye.

47Ndipo mzimu wanga ukondwera mwa Mulungu Mpulumutsi wanga,

48pakuti wakumbukira

kudzichepetsa kwa mtumiki wake.

Kuyambira tsopano mibado yonse idzanditcha wodala,

49pakuti Wamkuluyo wandichitira ine zinthu zazikulu,

dzina lake ndi loyera.

50Chifundo chake chifikira kwa iwo amene amuopa Iye

kufikira mibadomibado.

51Iye wachita zamphamvu ndi dzanja lake;

Iye anabalalitsa iwo amene ali onyada mʼmaganizo awo.

52Iye anachotsa olamulira pa mipando yawo yaufumu,

koma wakweza odzichepetsa.

53Iye wakhutitsa a njala ndi zinthu zabwino

koma anachotsa olemera wopanda kanthu.

54Iye anathandiza mtumiki wake Israeli,

pokumbukira chifundo chake.

55Kwa Abrahamu ndi zidzukulu zake ku nthawi zonse

monga ananena kwa makolo athu.”

56Mariya anakhala ndi Elizabeti pafupifupi miyezi itatu ndipo kenaka anabwerera kwawo.

Kubadwa kwa Yohane Mʼbatizi

57Itakwana nthawi yoti Elizabeti abereke, anabereka mwana wamwamuna. 58Anansi ndi abale ake anamva kuti Ambuye anamuchitira chifundo chachikulu ndipo anakondwera naye pamodzi.

59Pa tsiku lachisanu ndi chitatu anabwera ndi mwana kuti adzachitidwe mdulidwe, ndipo anafuna kumupatsa dzina la abambo ake Zakariya, 60koma amayi ake anayankhula nati, “Ayi, atchulidwe kuti Yohane.”

61Iwo anati kwa iye, “Palibe mmodzi mwa abale ake amene ali ndi dzina limeneli.”

62Pamenepo anapanga zizindikiro kwa abambo ake kuti adziwe dzina limene akanakonda kumutcha mwanayo. 63Iye anapempha poti alembepo, ndipo chodabwitsa kwa aliyense analemba kuti, “Dzina lake ndi Yohane.” 64Nthawi yomweyo pakamwa pake panatsekuka ndi lilime lake linamasuka ndipo anayamba kuyankhula, nayamika Mulungu. 65Anansi onse anachita mantha kwambiri, ndipo ku madera onse a kumapiri a Yudeya, anthu anayankhula zinthu zonsezi. 66Aliyense amene anamva izi anadabwa nazo nafunsa kuti, “Kodi mwana uyu adzakhala wotani?” Pakuti dzanja la Ambuye lili pa iye.

Nyimbo ya Zakariya

67Abambo ake, Zakariya, anadzazidwa ndi Mzimu Woyera ndipo ananenera kuti,

68“Alemekezeke Ambuye, Mulungu wa Israeli

chifukwa wabwera ndi kuwombola anthu ake.

69Iye wakweza nyanga yachipulumutso kwa ife

mu nyumba ya mtumiki wake Davide.

70(Monga mmene ananenera kudzera mwa aneneri oyera),

71chipulumutso kuchoka kwa adani athu

ndi kuchoka mʼdzanja la onse otida,

72kuonetsa chifundo kwa makolo athu

ndi kukumbukira pangano lake loyera,

73lumbiro limene analumbira kwa kholo lathu Abrahamu:

74kutilanditsa ife mʼdzanja la adani athu,

ndi kutipanga ife timutumikire Iye mopanda mantha,

75mʼchiyero ndi mʼchilungamo masiku athu onse.

76“Ndipo iwe mwana wanga udzatchedwa mneneri wa Wammwambamwamba;

pakuti udzapita patsogolo pa Ambuye kukonza njira yake,

77kupatsa anthu ake chidziwitso cha chipulumutso

kudzera mwa chikhululukiro cha machimo awo,

78chifukwa cha chifundo chachikulu cha Mulungu wathu,

ndipo kuwala kwa dzuwa kudzafikira ife kuchokera kumwamba,

79kuwalira iwo okhala mu mdima

ndi mu mthunzi wa imfa,

kutsogolera mapazi athu mu njira yamtendere.”

80Ndipo mwanayo anakula nakhala wamphamvu mu mzimu; ndipo anakhala ku chipululu mpaka pamene anaonekera poyera mu Israeli.

Tagalog Contemporary Bible

Lucas 1:1-80

Pasimula

1-3Kagalang-galang na Teofilus:

Marami na ang sumulat tungkol sa mga nangyari rito sa atin. Isinulat nila ang tungkol kay Jesus, na isinalaysay din sa amin ng mga taong nangaral ng salita ng Dios at nakasaksi mismo sa mga pangyayari mula pa noong una. Pagkatapos kong suriing mabuti ang lahat ng ito mula sa simula, minabuti kong sumulat din ng isang maayos na salaysay para sa iyo, 4upang lubusan mong matiyak na totoo ang mga aral na itinuro sa iyo.

Nagpakita ang Anghel kay Zacarias

5Noong si Herodes ang hari sa Judea, may isang pari na ang pangalan ay Zacarias na kabilang sa grupo ng mga pari na tinatawag na “Grupo ni Abijah.” Ang asawa niya ay si Elizabet na kabilang din sa angkan ni Aaron. 6Silang dalawa ay kapwa matuwid sa harap ng Dios. Maingat nilang sinusunod ang lahat ng utos at mga tuntunin ng Panginoon. 7Wala silang anak dahil baog si Elizabet, at matanda na silang pareho.

8Isang araw, ang grupo ni Zacarias ang nakatalagang maglingkod sa templo ng Panginoon. 9At katulad ng nakaugalian nila bilang mga pari, nagpalabunutan sila, at si Zacarias ang nabunot. Kaya siya ang pumasok sa loob ng templo para magsunog ng insenso sa altar. 10Habang nagsusunog siya roon ng insenso, maraming tao ang nananalangin sa labas. 11Biglang nagpakita kay Zacarias ang isang anghel ng Panginoon. Nakatayo ang anghel sa bandang kanan ng altar na pinagsusunugan ng insenso. 12Nabagabag at natakot si Zacarias nang makita niya ang anghel. 13Pero sinabi sa kanya ng anghel, “Huwag kang matakot, Zacarias! Dininig ng Dios ang panalangin mo. Magkakaanak ng isang lalaki ang asawa mong si Elizabet, at Juan ang ipapangalan mo sa kanya. 14Matutuwa kayo at magiging maligaya dahil sa kanya, at marami ang magagalak sa pagsilang niya, 15dahil magiging dakila siya sa harap ng Panginoon. Hindi siya dapat uminom ng alak o anumang inuming nakakalasing. Sa sinapupunan pa lang ng kanyang ina ay sasakanya na ang Banal na Espiritu. 16Maraming Israelita ang panunumbalikin niya sa Panginoon na kanilang Dios. 17Mauuna siya sa Panginoon upang ihanda ang mga tao sa pagdating ng Panginoon. Gagawin niya ito sa tulong ng Banal na Espiritu at sa pamamagitan ng kapangyarihang katulad ng kay Elias noon. Tuturuan niya ang mga magulang1:17 magulang: sa literal, ama. na mahalin ang kanilang mga anak, at ibabalik niya sa matuwid na pag-iisip ang mga taong masuwayin sa Dios.”

18Sinabi ni Zacarias sa anghel, “Paano po mangyayari ang mga sinabi nʼyo? Matanda na ako, at ganoon din ang asawa ko.”

19Sumagot ang anghel, “Ako si Gabriel na naglilingkod sa harapan ng Dios. Siya ang nagsugo sa akin para sabihin sa iyo ang magandang balitang ito. 20Ngunit dahil hindi ka naniwala sa sinabi ko, magiging pipi ka. Hindi ka makakapagsalita hanggaʼt hindi natutupad ang sinabi ko sa iyo. Sapagkat tiyak na mangyayari ang sinabi ko pagdating ng panahong itinakda ng Dios.”

21Samantala, hinihintay ng mga tao ang paglabas ni Zacarias. Nagtataka sila kung bakit nagtagal siya sa loob ng templo. 22Nang lumabas siya, hindi na siya makapagsalita at sumesenyas na lang siya. Kaya inisip nila na may nakita siyang pangitain sa loob ng templo. At mula noon naging pipi na siya.

23Nang matapos na ang panahon ng kanyang paglilingkod, umuwi na si Zacarias. 24Hindi nagtagal, nagbuntis si Elizabet, at sa loob ng limang buwan ay hindi siya umalis ng bahay. 25Sinabi niya, “Napakabuti ng Panginoon. Inalis niya ang kahihiyan ko sa mga tao bilang isang baog.”

Nagpakita kay Maria ang Anghel

26Nang ikaanim na buwan ng pagbubuntis ni Elizabet, inutusan ng Dios ang anghel na si Gabriel na pumunta sa nayon ng Nazaret sa Galilea. 27Pinapunta siya sa isang birhen1:27 birhen: o, dalaga. na ang pangalan ay Maria. Nakatakda nang ikasal si Maria kay Jose na mula sa lahi ni Haring David. 28Sinabi ni Gabriel kay Maria, “Matuwa ka,1:28 Matuwa ka: o, Binabati kita. Maria, ikaw na pinagpala ng Dios. Sumasaiyo ang Panginoon.”

29Nabagabag si Maria sa sinabi ng anghel. Inisip niyang mabuti kung ano ang ibig sabihin noon. 30Kaya sinabi sa kanya ng anghel, “Huwag kang matakot, Maria, dahil pinagpala ka ng Dios. 31Magbubuntis ka at manganganak ng isang lalaki, at papangalanan mo siyang Jesus. 32Magiging dakila siya at tatawaging Anak ng Kataas-taasang Dios. Ibibigay sa kanya ng Panginoong Dios ang trono ng ninuno niyang si David. 33Maghahari siya sa mga lahi ni Jacob magpakailanman; ang paghahari niya ay walang katapusan.”

34Nagtanong si Maria sa anghel, “Paano po ito mangyayari gayong dalaga pa ako?”

35Sumagot ang anghel, “Sasaiyo ang Banal na Espiritu at lililiman ka ng kapangyarihan ng Kataas-taasang Dios. Kaya ang banal na sanggol na ipapanganak mo ay tatawaging Anak ng Dios. 36Maging ang kamag-anak mong si Elizabet ay buntis din sa kabila ng kanyang katandaan. Alam ng lahat na baog siya, pero anim na buwan na siyang buntis ngayon. 37Sapagkat walang imposible sa Dios.”

38Sumagot si Maria, “Alipin po ako ng Panginoon. Mangyari nawa sa akin ang mga sinabi ninyo.” At iniwan siya ng anghel.

Ang Pagdalaw ni Maria kay Elizabet

39Hindi nagtagal, nag-ayos si Maria at dali-daling pumunta sa isang bayan sa kabundukan ng Judea kung saan nakatira sina Zacarias. 40Pagdating niya sa bahay nina Zacarias, binati niya si Elizabet. 41Nang marinig ni Elizabet ang pagbati ni Maria, naramdaman niyang gumalaw nang malakas ang sanggol sa kanyang sinapupunan. Napuspos ng Banal na Espiritu si Elizabet 42at malakas niyang sinabi, “Higit kang pinagpala ng Dios sa lahat ng babae, at pinagpala rin niya ang magiging anak mo! 43Isang malaking karangalan na dalawin ako ng ina ng aking Panginoon. 44Nang marinig ko ang pagbati mo sa akin, gumalaw nang malakas sa tuwa ang sanggol sa sinapupunan ko. 45Mapalad ka dahil naniwala kang matutupad ang sinabi sa iyo ng Panginoon.”

Ang Awit ni Maria

46At sinabi ni Maria,

“Buong puso kong pinupuri ang Panginoon,

47at nagagalak ang aking espiritu sa Dios na aking Tagapagligtas!

48Sapagkat inalala niya ako na kanyang abang lingkod.

Mula ngayon ay ituturing akong mapalad ng lahat ng henerasyon,

49dahil sa dakilang mga bagay na ginawa sa akin ng Makapangyarihang Dios.

Banal siya!

50Kinaaawaan niya ang mga taong may takot sa kanya sa bawat henerasyon.

51Ipinakita niya ang dakila niyang mga gawa sa pamamagitan ng kanyang kapangyarihan.

Itinaboy niya ang mga taong mataas ang tingin sa sarili.

52Ibinagsak niya ang mga makapangyarihang hari mula sa kanilang mga trono,

at itinaas niya ang mga nasa mababang kalagayan.

53Binusog niya ng mabubuting bagay ang mga nagugutom,

ngunit pinaalis niya na walang dala ang mayayaman.

54-55Tinulungan niya ang Israel na kanyang lingkod. Sapagkat hindi niya kinalimutan ang kanyang ipinangako sa ating mga ninuno, kay Abraham at sa kanyang lahi, na kaaawaan niya sila magpakailanman.”

56At nakitira si Maria kina Elizabet ng mga tatlong buwan bago siya umuwi.

Ang Pagsilang kay Juan na Tagapagbautismo

57Dumating na ang oras ng panganganak ni Elizabet, at nagsilang siya ng isang lalaki. 58Nabalitaan ng mga kapitbahay at mga kamag-anak niya kung paano siya pinagpala ng Panginoon, at nakigalak sila sa kanya.

59Nang walong araw na ang sanggol, dumalo ang mga kapitbahay at mga kamag-anak sa pagtutuli sa kanya. Zacarias sana ang ipapangalan nila sa bata dahil iyon din ang pangalan ng kanyang ama. 60Pero sinabi ni Elizabet, “Hindi! Juan ang ipapangalan sa kanya.” 61Sumagot ang mga tao, “Pero wala namang may ganyang pangalan sa pamilya ninyo.” 62Kaya tinanong nila ang ama sa pamamagitan ng senyas kung ano ang gusto niyang ipangalan sa sanggol. 63Sumenyas siya na bigyan siya ng masusulatan. Pagkatapos ay isinulat niya, “Juan ang ipapangalan sa kanya.” Nagtaka silang lahat. 64Noon din ay nakapagsalita na si Zacarias at nagpuri sa Dios. 65Nangilabot ang lahat ng kapitbahay nila, at naging usap-usapan sa buong kabundukan ng Judea ang pangyayaring iyon. 66Ang lahat ng nakabalita ay nag-isip at nagtanong, “Magiging ano kaya ang batang ito kapag lumaki na siya?” Sapagkat malinaw na sumasakanya ang Panginoon.

Ang Pahayag ni Zacarias

67Napuspos ng Banal na Espiritu ang ama ni Juan na si Zacarias at kanyang ipinahayag:

68“Purihin ang Panginoong Dios ng Israel!

Sapagkat inalala niya at tinubos ang kanyang bayan.

69Sinugo niya sa atin ang makapangyarihang Tagapagligtas mula sa angkan ng lingkod niyang si David.

70Itoʼy ayon sa ipinangako niya noon pang unang panahon sa pamamagitan ng kanyang mga banal na propeta.

71Ipinangako niya na ililigtas niya tayo sa ating mga kaaway at sa lahat ng napopoot sa atin.

72Kaaawaan niya ang ating mga ninuno, at tutuparin ang banal niyang kasunduan sa kanila

73na ipinangako niya sa ninuno nating si Abraham.

74Ayon nga sa kanyang kasunduan, ililigtas niya tayo sa ating mga kaaway upang makapaglingkod tayo sa kanya nang walang takot,

75at maging banal at matuwid sa kanyang paningin habang tayo ay nabubuhay.”

76Sinabi naman ni Zacarias sa anak niya,

“Ikaw naman, anak ay tatawaging propeta ng Kataas-taasang Dios,

dahil mauuna ka sa Panginoon upang ihanda ang mga tao sa kanyang pagdating.

77Ituturo mo sa mga mamamayan niya kung paano sila maliligtas sa pamamagitan ng kapatawaran ng kanilang mga kasalanan,

78dahil maawain at mapagmahal ang ating Dios.

Tulad ng pagsikat ng araw, ipapadala niya sa atin ang Tagapagligtas 79upang maliwanagan ang mga taong nasa kadiliman at takot sa kamatayan.

At tuturuan niya tayo kung paano mamuhay nang may mabuting relasyon sa Dios at sa kapwa.”

80Lumaki ang batang si Juan at lumakas sa espiritu. Nanirahan siya sa ilang hanggang sa araw na nagsimula siyang mangaral sa mga Israelita.