Levitiko 6 – CCL & SNC

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Levitiko 6:1-30

1Yehova anawuza Mose kuti, 2“Ngati munthu wina aliyense achimwa, nachita zinthu mosakhulupirika kwa Yehova chifukwa cha kunyenga mnzake pokana kumubwezera zimene anamusungitsa, kapena kumubera kapenanso kumulanda, 3kapena ndi kunama kuti sanatole chinthu chimene chinatayika, kapena kulumbira mwachinyengo pa chinthu chilichonse chimene munthu akachita amachimwa nacho, 4ndi wopalamula ndithu, ndipo ayenera kubweza zimene anabazo, zimene analanda mwachinyengozo, zimene anamusungitsazo, zimene anatolazo 5kapena zimene analumbira monyengazo. Pa tsiku limene apezeke kuti wapalamuladi, iye ayenera kumubwezera mwini wake zinthu zonsezi ndi kuwonjezerapo chimodzi mwa zigawo zisanu zilizonse. 6Pambuyo pake apereke kwa Yehova nsembe yopalamula. Nsembe yake ikhale nkhosa yayimuna yopanda chilema ndipo mtengo wake wogwirizana ndi nsembe yopepesera machimo. 7Kenaka wansembe achite mwambo wopepesera tchimo la munthuyo pamaso pa Yehova, ndipo adzakhululukidwa chilichonse chomwe anachita kuti akhale wopalamula.”

Nsembe Yopsereza

8Yehova anawuza Mose kuti, 9“Lamula Aaroni ndi ana ake kuti, ‘Lamulo la nsembe yopsereza ndi ili: Nsembe yopserezayo izikhala pa moto pa guwa usiku wonse mpaka mmawa, ndipo moto wa paguwapo uzikhala ukuyaka nthawi zonse. 10Tsono wansembe avale mkanjo wake wa nsalu yofewa ndi yosalala. Mʼkati avalenso kabudula wofewa, wosalala. Pambuyo pake atenge phulusa la nyama imene yatenthedwa pa guwa lansembe paja ndi kulithira pambali pa guwa lomwelo. 11Akatero avule zovala zakezo ndi kuvala zovala zina. Kenaka atulutse phulusalo ndi kukaliyika pa malo woyeretsedwa kunja kwa chithando. 12Moto wa pa guwa uzikhala ukuyaka nthawi zonse, usamazime. Mmawa uliwonse wansembe aziwonjezerapo nkhuni pa motopo ndi kukonza nsembe yopsereza, ndi kutentha mafuta a nsembe yachiyanjano pamenepo. 13Moto uzikhala ukuyaka pa guwa nthawi zonse ndipo usazimepo.

Nsembe Zachakudya

14“ ‘Lamulo la nsembe yachakudya ndi ili: ana a Aaroni azibwera nayo nsembeyo pamaso pa Yehova, patsogolo pa guwa. 15Wansembe mmodzi atapeko dzanja limodzi la ufa wosalala wa nsembe yachakudya ija kuti ukhala ufa wachikumbutso ndi mafuta pamodzi ndi lubani yense amene ali pa nsembe ya chakudyacho, ndipo azitenthe pa guwa kuti zilandiridwe ndi Yehova mʼmalo mwa nsembe yonse kuti zikhale nsembe ya fungo lokomera Yehova. 16Aaroni ndi ana ake azidya zimene zatsala koma azidya zopanda yisiti ku malo wopatulika, ku bwalo la tenti ya msonkhano. 17Poziphika asathire yisiti. Ndawapatsa zotsalazo kuti zikhale gawo lawo la nsembe zanga zopsereza. Zonsezi ndi zopatulika kwambiri monga nsembe yopepesera tchimo ndiponso nsembe yopepesera machimo. 18Mwana aliyense wamwamuna wa Aaroni azidyako za nsembe zopsereza zopereka kwa Yehova. Ndi gawo lake lokhazikika la chopereka chopsereza kwa Yehova pa mibado yanu yonse. Chilichonse chimene chidzakhudza nsembezo chidzakhala chopatulika.’ ”

19Yehova anawuzanso Mose kuti, 20“Nsembe imene Aaroni ndi ana ake ayenera kupereka kwa Yehova pa tsiku limene wansembe akudzozedwa ndi iyi: ufa wosalala kilogalamu imodzi ngati chopereka chachakudya cha nthawi zonse. Azipereka theka limodzi mmawa ndipo theka linalo madzulo. 21Ipangidwe ndi mafuta pa chiwaya ndipo ubwere nayo ili yosakaniza bwino, yophikidwa mitandamitanda monga amachitira ndi nsembe yachakudya. Iphikidwe moti itulutse fungo lokomera Yehova. 22Mwana wa fuko la Aaroni amene adzadzozedwe kukhala wansembe kulowa mʼmalo mwa Aaroni ndiye amene azidzakonza ndi kupereka nsembeyi kwa Yehova nthawi zonse monga kunalembedwera. 23Nsembe iliyonse yachakudya ya wansembe izitenthedwa kwathunthu, isamadyedwe.”

Nsembe Yopepesera Tchimo

24Yehova anawuza Mose kuti 25“Uza Aaroni ndi ana ake kuti, ‘Malamulo a nsembe ya tchimo ndi awa: Nsembeyi iziphedwa pamaso pa Yehova pa malo pamene mumaphera nsembe yopsereza popeza ndi nsembe yopatulika. 26Wansembe amene apereke nsembeyi adyere ku malo wopatulika ndiye kuti mʼbwalo la tenti ya msonkhano. 27Chilichonse chimene chidzakhudza nsembeyo chidzakhala chopatulika, ndipo ngati magazi ake agwera pa chovala, muchape chovalacho pa malo opatulika. 28Mʼphika wadothi umene aphikira nyamayo auphwanye. Koma ngati yaphikidwa mu mʼphika wa mkuwa, awukweche ndi kuwutsukuluza ndi madzi. 29Munthu wamwamuna aliyense wa mʼbanja la wansembe angathe kuyidya popeza nsembeyi ndi yopatulika kwambiri. 30Koma nsembe yopepesera tchimo imene magazi ake amabwera nawo mu tenti ya msonkhano kudzachita mwambo wopepesera tchimo ku malo opatulika isadyedwe, mʼmalo mwake itenthedwe.’ ”

Slovo na cestu

3 Mojžíšova 6:1-30

1Mluvil opět Hospodin k Mojžíšovi, řka: 2Kdyby člověk zhřešil a přestoupením přestoupil proti Hospodinu, buď že by oklamal bližního svého v věci sobě svěřené, aneb v spolku nějakém, aneb mocí by vzal něco, aneb lstivě podvedl bližního svého, 3Buď že nalezna ztracenou věc, za přelby mu ji, buď že by přisáhl falešně, kteroukoli věcí z těch, kterouž přihází se člověku učiniti a zhřešiti jí, 4Když by tedy zhřešil a vinen byl: navrátí zase tu věc, kterouž mocí sobě vzal, aneb tu, kteréž lstivě s útiskem dosáhl, aneb tu, kteráž mu svěřena byla, aneb ztracenou věc, kterouž nalezl, 5Aneb o kterékoli věci falešně přisáhl: tedy navrátí to z cela, a nad to pátý díl toho přidá tomu, číž bylo; to navrátí v den oběti za hřích svůj. 6Obět pak za hřích svůj přivede Hospodinu z drobného dobytku, skopce bez poškvrny, vedlé ceny tvé, v obět za vinu knězi. 7I očistí jej kněz před Hospodinem, a odpuštěno mu bude, jedna každá z těch věcí, kterouž by učinil a jí vinen byl. 8I mluvil Hospodin k Mojžíšovi, řka: 9Přikaž Aronovi i synům jeho a rci: Tento bude řád při oběti zápalné: (slove pak obět zápalná od pálení na oltáři celou noc až do jitra, nebo oheň na oltáři vždycky hořeti bude), 10Obleče se kněz v roucho své lněné, a košilku lněnou vezme na tělo své, a vyhrabe popel, když oheň spálí obět zápalnou na oltáři, a vysype jej u oltáře. 11Potom svleče šaty své a obleče se v roucho jiné, a vynese popel ven z stanů na místo čisté. 12Oheň pak, kterýž jest na oltáři, bude hořeti na něm, nebude uhašován. A bude zapalovati jím kněz dříví každého jitra, a zpořádá na něm obět zápalnou, a páliti bude na něm tuk pokojných obětí. 13Oheň ustavičně hořeti bude na oltáři, a nebudeť uhašen. 14Tento pak bude řád při oběti suché, kterouž obětovati budou synové Aronovi Hospodinu u oltáře: 15Vezme hrst bělné mouky z oběti té a z oleje jejího, se vším tím kadidlem, kteréž bude na oběti suché, a páliti to bude na oltáři u vůni líbeznou, pamětné její Hospodinu. 16Což pak zůstane z ní, to jísti budou Aron i synové jeho; přesné jísti se bude na místě svatém, v síni stánku úmluvy jísti to budou. 17Nebude vařeno s kvasem, nebo jsem jim to dal za díl z obětí mých ohnivých; svaté svatých to jest, jako i obět za hřích a jako obět za vinu. 18Každý mužského pohlaví z synů Aronových jísti bude to právem věčným po rodech vašich, z ohnivých obětí Hospodinových. Což by se koli dotklo toho, svaté bude. 19I mluvil Hospodin k Mojžíšovi, řka: 20Tato jest obět Aronova a synů jeho, kterouž obětovati budou Hospodinu v den pomazání jeho: Desátý díl míry efi mouky bělné za obět suchou ustavičnou, polovici toho ráno a polovici u večer. 21Na pánvici s olejem strojena bude; smaženou přineseš ji, a pečené kusy oběti suché obětovati budeš u vůni spokojující Hospodina. 22A kněz, kterýž z synů jeho po něm pomazán bude, ať ji obětuje právem věčným. Hospodinu všecko to páleno bude. 23A všeliká suchá obět kněžská celá spálena bude; nebudeť jedena. 24Mluvil pak Hospodin k Mojžíšovi, řka: 25Mluv Aronovi a synům jeho a rci: Tento bude řád oběti za hřích: Na místě, kdež se zabijí obět zápalná, zabita bude obět za hřích před Hospodinem; svatá svatých jest. 26Kněz obětující tu obět za hřích budeť jísti ji; na místě svatém jedena bude v síni stánku úmluvy. 27Což by se koli dotklo masa jejího, svaté bude; a jestliže by krví její šaty skropeny byly, to, což skropeno jest, obmyješ na místě svatém. 28A nádoba hliněná, v níž by vařeno bylo, rozražena bude; pakli by v nádobě měděné vařeno bylo, vytřena a vymyta bude vodou. 29Všeliký pohlaví mužského mezi kněžími jísti to bude; svaté svatých jest. 30Ale žádná obět za hřích, (z jejížto krve něco vneseno bylo by do stánku úmluvy k očištění v svatyni), nebude jedena; ohněm spálena bude.