Levitiko 4 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Levitiko 4:1-35

Nsembe Yopepesera Tchimo

1Yehova anayankhula ndi Mose kuti, 2“Awuze Aisraeli kuti, ‘Munthu akachimwa mosadziwa ndi kuchita chilichonse chimene Yehova walamula kuti asachite, azichita izi:

3“ ‘Ngati wansembe wodzozedwa achimwa, ndi kuchimwitsa anthu onse, iyeyu ayenera kupereka mwana wangʼombe wamphongo wopanda chilema chifukwa cha tchimo limene wachitalo. Imeneyi ndi nsembe ya Yehova yopepesera tchimo lake. 4Wansembeyo abwere nayo ngʼombeyo pa khomo la tenti ya msonkhano pamaso pa Yehova. Asanjike dzanja lake pamutu pa ngʼombeyo ndipo ayiphe pamaso pa Yehova. 5Kenaka wansembe wodzozedwa atengeko magazi a ngʼombeyo ndi kulowa nawo mu tenti ya msonkhano. 6Iye aviyike chala chake mʼmagazi, ndipo awawaze kasanu ndi kawiri pamaso pa Yehova, patsogolo pa katani yotchinga malo wopatulika. 7Kenaka wansembe apake magaziwo pa nyanga za guwa lofukizira lubani limene lili pamaso pa Yehova mu tenti ya msonkhano. Magazi ena otsalawo awathire pa tsinde pa guwa lansembe zopsereza, limene lili pa khomo la tenti ya msonkhano. 8Pambuyo pake achotse mafuta onse a ngʼombe yayimuna yopepesera machimoyo: mafuta okuta zamʼkati kapena mafuta onse amʼkatimo. 9Achotsenso ndi kubwera ndi impsyo zonse ziwiri pamodzi ndi mafuta onse ndiponso mafuta onse amene aphimba chiwindi ndi impsyo 10monga momwe amachotsera mafuta a ngʼombe yoperekedwa kuti ikhale chopereka chachiyanjano. Tsono wansembe atenthe zimenezi pa guwa lansembe zopsereza. 11Koma chikopa cha ngʼombe yayimunayo ndi mnofu wake wonse, pamodzi ndi mutu ndi miyendo, zamʼkati ndi matumbo, 12kapena kuti ngʼombe yonse yotsalayo apite nayo kunja kwa msasa ku malo woyeretsedwa, kumene amatayako phulusa ndi kuyitentha pa nkhuni, pa phulusapo.

13“ ‘Ngati gulu lonse la Aisraeli lichimwa mosadziwa, nachita chomwe ndi choletsedwa ndi Yehova, ngakhale kuti gulu lonselo silikudziwa kuti lachimwa, anthuwo ndi olakwa ndithu. 14Akazindikira tchimo limene achita, gulu lonse lipereke mwana wangʼombe wamphongo kuti akhale chopereka chopepesera tchimo ndipo abwere naye pa khomo la tenti ya msonkhano. 15Akuluakulu a anthuwo asanjike manja awo pa mutu pa ngʼombe pamaso pa Yehova, ndipo ayiphe pomwepo pamaso pa Yehova. 16Tsono wansembe wodzozedwa atengeko magazi a ngʼombeyo ndi kulowa nawo mu tenti ya msonkhano. 17Aviyike chala chake mʼmagaziwo ndi kuwawaza pamaso pa Yehova kasanu ndi kawiri patsogolo pa nsalu yotchinga. 18Pambuyo pake iye apake magaziwo pa nyanga za guwa limene lili pamaso pa Yehova mu tenti ya msonkhano. Magazi ena otsalawo awathire pa tsinde pa guwa lansembe zopsereza limene lili pa khomo la tenti ya msonkhano. 19Kenaka achotse mafuta onse a ngʼombeyo ndi kuwatentha pa guwa, 20ndipo achite ndi ngʼombe yayimunayi monga anachitira ndi ngʼombe yayimuna yopepesera machimo. Potero, wansembe adzapereka nsembe yopepesera anthu, ndipo machimo awo adzakhululukidwa. 21Kenaka atulutse ngʼombeyo kunja kwa msasa ndi kuyitentha monga anatenthera ngʼombe yoyamba ija. Imeneyi ndiyo nsembe yopepesera machimo a gulu lonse.

22“ ‘Ngati mtsogoleri achimwa mosadziwa nachita zimene ndi zoletsedwa ndi Yehova Mulungu wake, ndiye kuti wapalamula. 23Ndipo ngati wauzidwa za tchimo limene wachita, iye abwere ndi mbuzi yayimuna yopanda chilema kuti ikhale chopereka chake. 24Asanjike dzanja lake pa mutu wa mbuziyo ndi kuyiphera pamalo pamene amaphera zopereka zopsereza pamaso pa Yehova. Ichi ndi chopereka chopepesera tchimo. 25Pambuyo pake wansembe atengeko magazi a chopereka chopepesera tchimocho ndi chala chake, ndipo awapake pa nyanga za guwa lansembe zopsereza. Athire magazi otsalawo pa tsinde la guwalo. 26Wansembeyo atenthe mafuta onse pa guwapo monga amatenthera chopereka chachiyanjano. Pochita zimenezi, wansembe adzapereka nsembe yopepesera tchimo la munthuyo, ndipo adzakhululukidwa.

27“ ‘Ngati munthu wamba achimwa mosadziwa nachita zimene ndi zoletsedwa ndi Yehova, ndiye kuti wapalamula. 28Ndipo ngati wauzidwa za tchimo limene wachita, abweretse mbuzi yayikazi yopanda chilema kuti ikhale chopereka chopepesera tchimo. 29Asanjike dzanja lake pamutu pa mbuziyo ndipo ayiphe pamalo pamene amaphera chopereka chopsereza. 30Ndipo wansembe atenge magazi ndi chala chake ndi kuwapaka pa nyanga za guwa lansembe zopsereza ndi kuthira magazi wotsalawo pa tsinde la guwalo. 31Kenaka iye achotse mafuta onse monga momwe anachotsera mafuta a chopereka chachiyanjano, ndipo awatenthe pa guwa kuti akhale fungo lokomera Yehova. Potero, wansembe adzapereka nsembe yopepesera tchimo la munthuyo ndipo adzakhululukidwa.

32“ ‘Ngati munthu apereka mwana wankhosa ngati chopereka chopepesera tchimo lake, abwere ndi mwana wankhosa wamkazi wopanda chilema. 33Asanjike dzanja lake pa mutu wa mwana wankhosayo ndipo amuphe pamalo pamene amaphera chopereka chopsereza. 34Kenaka wansembe atengeko ndi chala chake magazi a mwana wankhosa uja ndi kuwapaka pa nyanga za guwa lansembe zopsereza. Magazi otsalawo athire pa tsinde la guwalo. 35Iye achotse mafuta onse, monga amachotsera mafuta a mwana wankhosa wa chopereka chachiyanjano, ndipo wansembe awatenthe pa guwa pamodzi ndi zopereka zina zopsereza za Yehova. Potero, wansembe adzapereka nsembe yopepesera tchimo limene munthuyo anachita ndipo adzakhululukidwa.

Persian Contemporary Bible

لاويان 4:1-35

قربانی گناه

1خداوند به موسی فرمود تا 2به قوم اسرائيل بگويد كه هر كه سهواً مرتكب گناهی شود و يكی از قوانين خداوند را زير پا گذارد، بايد طبق اين مقررات عمل كند:

3اگر خطا از كاهن اعظم سر زده باشد و بدين ترتيب قوم را نيز گناهكار ساخته باشد، برای گناه خود بايد گوساله‌های سالم و بی‌عيب به خداوند تقديم كند. 4گوساله را دم در خيمهٔ عبادت بياورد، دستش را روی سر آن بگذارد و همانجا در حضور خداوند سرش را ببرد. 5كاهن اعظم مقداری از خون گوساله را به داخل خيمهٔ عبادت ببرد، 6انگشت خود را در خون فرو برد و در حضور خداوند آن را هفت بار جلو پردهٔ قدس‌الاقداس بپاشد. 7سپس در حضور خداوند قدری از خون را روی شاخهای قربانگاه بخور كه داخل خيمه است، بمالد. باقيماندهٔ خون را به پای قربانگاه قربانی سوختنی كه نزديک در خيمهٔ عبادت است، بريزد. 8آنگاه تمام پيه داخل شكم، 9قلوه‌ها و چربی روی آنها، و سفيدی روی جگر را بردارد، 10و آنها را روی قربانگاه قربانی سوختنی بسوزاند، درست همانطور كه پيه گاو قربانی سلامتی را می‌سوزاند. 11‏-12اما باقيماندهٔ گوساله، يعنی پوست، گوشت، كله، پاچه، دل و روده و سرگين را به مكان طاهری ببرد كه در خارج از اردوگاه برای ريختن خاكستر قربانگاه مقرر شده است و در آنجا آنها را روی هيزم بسوزاند.

13اگر تمام قوم اسرائيل سهواً مرتكب گناهی شوند و يكی از قوانين خداوند را زير پا بگذارند، هر چند اين كار را ندانسته انجام داده باشند، مقصر محسوب می‌شوند. 14وقتی آنها به گناه خود پی بردند، بايد گوساله‌ای برای كفارهٔ گناه خود قربانی كنند. گوساله را به خيمهٔ عبادت بياورند 15و در آنجا بزرگان قوم در حضور خداوند دستهای خود را روی سر حيوان بگذارند و آن را ذبح كنند. 16آنگاه كاهن اعظم مقداری از خون گوساله را به داخل خيمهٔ عبادت بياورد 17و انگشت خود را در خون فرو برد و در حضور خداوند آن را هفت بار جلو پردهٔ قدس‌الاقداس بپاشد. 18بعد در حضور خداوند قدری از خون را بر شاخهای قربانگاه بخور كه در خيمهٔ عبادت است، بمالد و باقی ماندهٔ خون را به پای قربانگاه قربانی سوختنی كه نزديک در خيمه است، بريزد. 19تمام پيه بايد روی قربانگاه سوزانده شود. 20كاهن اعظم بايد از همان روش قربانی گناه پيروی كند. به اين طريق برای قوم خدا كفاره خواهد كرد و خطای آنان بخشيده خواهد شد. 21او گوسالهٔ قربانی شده را از اردوگاه بيرون ببرد و بسوزاند، همانطور كه گوسالهٔ قربانی گناه خود را می‌سوزاند. اين قربانی گناه تمام قوم اسرائيل است.

22اگر يكی از رهبران سهواً مرتكب گناهی شود و يكی از قوانين خداوند، خدای خود را زير پا گذارد، مقصر محسوب می‌شود. 23وقتی او به گناهش پی برد، بايد يک بز نر سالم و بی‌عيب تقديم كند. 24دست خود را روی سر بز بگذارد و در جايی كه قربانیهای سوختنی را سر می‌برند آن را ذبح كند و به خداوند تقديم نمايد. اين، قربانی گناه اوست. 25بعد كاهن قدری از خون قربانی گناه را بگيرد و با انگشت خود روی شاخهای قربانگاه قربانی سوختنی بمالد و بقيهٔ خون را به پای قربانگاه بريزد. 26تمام پيه بايد مثل پيه قربانی سلامتی، روی قربانگاه سوزانده شود. به اين ترتيب كاهن برای گناه رهبر كفاره خواهد كرد و او بخشيده خواهد شد.

27اگر يک فرد عادی سهواً مرتكب گناهی شود و يكی از قوانين خداوند را زير پا گذارد، مقصر محسوب می‌شود. 28وقتی او به گناه خود پی برد، بايد يک بز مادهٔ سالم و بی‌عيب بياورد تا آن را برای گناهش قربانی كند. 29بز را به مكانی بياورد كه قربانیهای سوختنی را سر می‌برند. در آنجا دست خود را روی سر حيوان بگذارد و آن را ذبح كند. 30كاهن با انگشت خود قدری از خون را روی شاخهای قربانگاه قربانی سوختنی بمالد و بقيهٔ خون را به پای قربانگاه بريزد. 31تمام پيه بايد مثل پيه قربانی سلامتی، روی قربانگاه سوزانده شود و اين مورد پسند خداوند خواهد بود. به اين ترتيب كاهن گناه آن شخص را كفاره خواهد كرد و او بخشيده خواهد شد.

32اگر آن شخص بخواهد برای كفارهٔ گناهش بره قربانی كند، بايد آن بره، ماده و بی‌عيب باشد. 33او بايد دست خود را روی سر بره بگذارد و آن را در مكانی كه قربانیهای سوختنی را سر می‌برند، به عنوان قربانی گناه ذبح كند. 34كاهن با انگشت خود قدری از خون را بر شاخهای قربانگاه قربانی سوختنی بمالد و بقيهٔ خون را به پای قربانگاه بريزد. 35پيه آن مثل پيه برهٔ قربانی سلامتی روی قربانگاه سوزانده شود. كاهن آن را مانند قربانیهایی كه بر آتش به خداوند تقديم می‌شود، بسوزاند. به اين ترتيب كاهن گناه آن شخص را كفاره خواهد كرد و او بخشيده خواهد شد.