Levitiko 27 – CCL & TNCV

The Word of God in Contemporary Chichewa

Levitiko 27:1-34

Kuwombola Zomwe ndi za Yehova

1Yehova anawuza Mose kuti, 2“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ngati munthu anachita lumbiro lapadera loti adzapereka munthu mnzake kwa Yehova ndipo akufuna kuti amuwombole, 3mtengo wake ukhale masekeli a siliva makumi asanu, molingana ndi kawerengedwe ka ku Nyumba ya Mulungu, ngati munthuyo ndi wamwamuna wa zaka zapakati pa 20 ndi 60. 4Ndipo ngati ndi wamkazi, mtengo wake ukhale masekeli makumi atatu. 5Mtengo wa munthu wamwamuna wa zaka zapakati pa zisanu ndi makumi awiri ukhale masekeli makumi awiri ndipo munthu wamkazi ukhale masekeli khumi. 6Ngati ndi munthu wamwamuna wa pakati pa mwezi umodzi ndi zaka zisanu, mtengo wa munthu wamwamuna ukhale masekeli asanu a siliva ndipo ngati ndi wamkazi, ukhale masekeli atatu a siliva. 7Ngati ndi munthu wa zaka makumi asanu ndi limodzi kapena kuposerapo, mtengo wa wamwamuna ukhale masekeli khumi ndi asanu, ndipo wamkazi ukhale masekeli khumi. 8Ngati munthu amene anachita lumbiro ndi wosauka kwambiri kuti sangathe kulipira ndalama zimenezo, abwere ndi munthu woperekedwa uja kwa wansembe, ndipo wansembeyo ayike mtengo woti munthu wolumbirayo angathe kulipira.

9“ ‘Ngati chimene anachitira lumbiro kuti apereke ndi nyama imene amapereka kukhala nsembe kwa Yehova, zonse zimene amapereka kwa Yehova nʼzopatulika. 10Munthu asasinthanitse ndi ina kapena kupereka ina yabwino mʼmalo mwa yoyipa, kapena yoyipa mʼmalo mwa yabwino. Ngati asinthitsa nyama ina mʼmalo mwa ina, nyamayo pamodzi ndi inzake wasinthitsayo zikhala zopatulika. 11Ngati chimene anachitira lumbiro ndi nyama yodetsedwa, nyama imene siloledwa kuyipereka kukhala nsembe kwa Yehova, nyamayo abwere nayo kwa wansembe, 12ndipo wansembeyo atchule mtengo wake poona ngati ndi yabwino kapena ndi yoyipa. Mtengo umene wansembe atchule ndiwo udzakhale mtengo wake. 13Ngati mwini wakeyo akufuna kuwombola nyamayo, awonjezere pa mtengo wake wa nyamayo chimodzi mwa zigawo zisanu zamtengowo.

14“ ‘Ngati munthu apereka nyumba yake kuti ikhale yopatulika kwa Yehova, wansembe atchule mtengo wake poona ngati ndi yabwino kapena ndi yoyipa. Mtengo umene wansembe atchule ndiwo udzakhale mtengo wake. 15Ngati munthu amene wapereka nyumbayo afuna kuyiwombola nyumbayo, awonjezere pamtengo wake wa nyumbayo, limodzi mwa magawo asanu amtengowo. Ndipo nyumbayo idzakhalanso yake.

16“ ‘Ngati munthu apereka kwa Yehova mbali ina ya malo a makolo ake, mtengo umene awuyike ukhale wolingana ndi mtengo wa mbewu zimene zimadzabzalidwamo. Zikhale mbewu za barele za makilogalamu makumi awiri ndipo mtengo wake ukhale masekeli makumi asanu. 17Ngati munthu apereka munda wake kuyambira chaka chokondwerera zaka makumi asanu, mtengo wake ukhale umene unakhazikitsidwa. 18Koma ngati apereka mundawo chaka chokondwerera zaka makumi asanu chitapita, wansembe adzatchula mtengo molingana ndi zaka zomwe zatsala kuti chifike chaka china chokondwerera zaka makumi asanu, ndipo mtengo wake udzakhala wotsikirapo. 19Ngati munthu amene wapereka munda afuna kuwuwombola, ayenera kuwonjezera pa mtengo wake wa mundawo, limodzi mwa magawo asanu a mtengowo. Ndipo mundawo udzakhalanso wake. 20Koma ngati sawuwombola mundawo, kapena ngati waugulitsa kwa munthu wina, mundawo sudzawomboledwanso. 21Mwini mundawo akawusiya mʼchaka chokondwerera zaka makumi asanu ndiye kuti mundawo udzakhala wopatulika monga woperekedwa kwa Yehova: udzakhala munda wa ansembe.

22“ ‘Ngati munthu apereka kwa Yehova munda umene anagula, umene si malo a makolo ake, 23wansembe atchule mtengo wake kufikira pa chaka chokondwerera zaka makumi asanu, ndipo munthuyo apereke ndalama zokwanira mtengo wake pa tsikulo monga ndalama zopatulika kwa Yehova. 24Pa chaka chokondwerera zaka makumi asanu, mundawo udzabwezedwa kwa munthu amene anawugulitsayo, amene malowo anali ake. 25Potchula mtengo uliwonse wansembe awerengere molingana ndi mtengo wa sekeli wa ku Nyumba ya Mulungu: magera makumi awiri pa sekeli imodzi.

26“ ‘Koma pasapezeke munthu wopereka mwana woyamba kubadwa wa nyama, popeza mwana woyamba kubadwa ali kale wa Yehova, kaya ndi ngʼombe kapena nkhosa, zimenezi ndi za Yehova. 27Ngati ili nyama yodetsedwa, ayiwombole pa mtengo umene wansembe wawuyika, ndi kuwonjezeranso pa mtengo wake wa nyamayo, limodzi mwa magawo asanu amtengowo. Ngati sayiwombola, igulitsidwe pa mtengo umene wansembe awuyike.

28“ ‘Koma chinthu chilichonse choperekedwa kwa Yehova, kaya ndi munthu, nyama, kaya ndi malo a makolo, chimenechi chisagulitsidwe kapena kuwomboledwa. Choperekedwa kwa Yehova motere nʼchopatulika kwambiri.

29“ ‘Munthu amene waperekedwa kotheratu sangawomboledwe. Munthuyo ayenera kuphedwa.

30“ ‘Chakhumi chilichonse chochokera mʼdziko, kaya ndi tirigu wochokera mʼnthaka kapena chipatso cha mʼmitengo ndi za Yehova. Chimenecho ndi chopatulika kwa Yehova. 31Ngati munthu afuna kuwombola chakhumi chilichonse, awonjezere pamtengo wake chimodzi mwa zigawo zisanu za mtengowo. 32Chakhumi cha ngʼombe ndi nkhosa, kapena kuti nyama iliyonse ya khumi imene mʼbusa wayiwerenga idzakhala yopatulikira kwa Yehova. 33Palibe amene adzaloledwa kusankha nyama yomwe ili yabwino kapena kusinthitsa. Ngati asinthitsa, nyamayo pamodzi ndi inzakeyo zidzakhala zopatulika ndipo sangaziwombole.’ ”

34Amenewa ndi malamulo amene Yehova anamupatsa Mose pa Phiri la Sinai kuti awuze Aisraeli.

Thai New Contemporary Version

เลวีนิติ 27:1-34

การไถ่สิ่งที่เป็นขององค์พระผู้เป็นเจ้า

1องค์พระผู้เป็นเจ้าตรัสกับโมเสสว่า 2“จงแจ้งชนอิสราเอลว่า ‘หากคนใดได้ปฏิญาณไว้ว่าจะอุทิศถวายผู้หนึ่งผู้ใดแด่องค์พระผู้เป็นเจ้า โดยการถวายสิ่งมีค่าจำนวนต่อไปนี้แทนคือ 3ผู้ชายอายุยี่สิบปีถึงหกสิบปีให้ตั้งค่าตัวเป็นเงินหนัก 50 เชเขล ตามเชเขลของสถานนมัสการ27:3 1 เชเขล คือเงินหนักประมาณ 11.5 กรัม มีค่าเท่ากับค่าแรงสองเดือน เช่นเดียวกับข้อ 4,5,6,7 และ 16 4ถ้าหากเป็นผู้หญิง ให้ตั้งราคาค่าตัวเป็นเงินหนัก 30 เชเขล 5ผู้ที่อายุห้าถึงยี่สิบปี ถ้าเป็นผู้ชายให้ตั้งราคาค่าตัวเป็นเงินหนัก 20 เชเขล ถ้าเป็นผู้หญิงให้ตั้งราคาค่าตัวเป็นเงินหนัก 10 เชเขล 6ผู้ที่อายุหนึ่งเดือนถึงห้าขวบ ถ้าเป็นผู้ชายให้ตั้งราคาค่าตัวเป็นเงินหนัก 5 เชเขล ถ้าเป็นผู้หญิงให้ตั้งราคาค่าตัวเป็นเงินหนัก 3 เชเขล 7ผู้ที่อายุหกสิบปีขึ้นไป ถ้าเป็นผู้ชายให้ตั้งราคาค่าตัวเป็นเงินหนัก 15 เชเขล ถ้าเป็นผู้หญิงให้ตั้งราคาค่าตัวเป็นเงินหนัก 10 เชเขล 8หากผู้ที่ถวายคำปฏิญาณยากจนเกินกว่าที่จะถวายเงินตามที่ระบุไว้ ให้พาบุคคลที่เขาประสงค์จะถวายตัวมาพบปุโรหิต ซึ่งจะกำหนดมูลค่าที่ผู้ปฏิญาณจะสามารถถวายได้

9“ ‘ถ้าสิ่งที่เขาปฏิญาณว่าจะถวายนั้นเป็นสัตว์ที่ยอมรับเป็นเครื่องบูชาแด่องค์พระผู้เป็นเจ้าสัตว์ตัวนั้นที่ถวายแด่องค์พระผู้เป็นเจ้าต้องถือว่าบริสุทธิ์ 10เขาจะเอาตัวอื่นมาเปลี่ยนไม่ได้ เอาดีมาแทนไม่ดี หรือเอาไม่ดีมาแทนดีก็ไม่ได้ หากเขาเปลี่ยนตัว ทั้งตัวแรกและตัวที่มาเปลี่ยนจะเป็นของบริสุทธิ์ 11หากสิ่งที่เขาปฏิญาณจะถวายเป็นสัตว์ที่เป็นมลทินตามระเบียบพิธี ซึ่งไม่ยอมรับเป็นเครื่องบูชาแด่องค์พระผู้เป็นเจ้าจะต้องนำสัตว์นั้นมามอบให้ปุโรหิต 12ผู้ที่จะประเมินคุณภาพว่าดีหรือไม่ดี ปุโรหิตกำหนดราคาเท่าใด ก็ให้เป็นไปตามนั้น 13หากเจ้าของต้องการจะไถ่สัตว์ตัวนั้น ก็ให้จ่ายเพิ่มอีกหนึ่งในห้าของราคาที่ตั้งไว้

14“ ‘ผู้ใดถวายบ้านเป็นของบริสุทธิ์แด่องค์พระผู้เป็นเจ้าปุโรหิตจะประเมินคุณภาพว่าดีหรือไม่ดี ปุโรหิตกำหนดราคาเท่าใด ก็ให้ถือตามนั้น 15ถ้าผู้ถวายบ้านจะไถ่คืน เขาต้องจ่ายเพิ่มอีกหนึ่งในห้าของราคา แล้วบ้านจะกลับคืนเป็นของเขา

16“ ‘ผู้ใดถวายที่ดินส่วนหนึ่งของตระกูลแด่องค์พระผู้เป็นเจ้าจะตีราคาตามปริมาณเมล็ดพืชซึ่งจะใช้หว่านในที่นั่นคือ เงินหนัก 50 เชเขลต่อเมล็ดข้าวบาร์เลย์ประมาณ 220 ลิตร27:16 ภาษาฮีบรูว่า 1 โฮเมอร์ 17หากผู้ใดถวายที่ดินในปีกึ่งศตวรรษให้ตีราคาเต็มตามอัตรา 18หากถวายหลังปีกึ่งศตวรรษ ปุโรหิตจะพิจารณาราคาตามจำนวนปีที่เหลืออยู่ก่อนถึงปีกึ่งศตวรรษรอบต่อไปและราคาที่ตั้งไว้จะลดลง 19หากคนนั้นตกลงจะไถ่ที่ดินคืน เขาจะจ่ายเงินเพิ่มอีกหนึ่งในห้าของราคาประเมิน และรับที่ดินคืนเป็นของเขาอีก 20แต่หากเขาไม่ไถ่คืน หรือหากขายที่ดินนั้นแก่คนอื่น ที่ดินนั้นจะไถ่คืนอีกไม่ได้เลย 21เมื่อที่ดินคืนสู่เจ้าของเดิมในปีกึ่งศตวรรษ ที่ดินผืนนี้จะถือเป็นของบริสุทธิ์เหมือนที่ดินซึ่งถวายแด่องค์พระผู้เป็นเจ้าที่ดินนี้จะกลายเป็นกรรมสิทธิ์ของบรรดาปุโรหิต

22“ ‘หากผู้ใดถวายที่ดินซึ่งเขาซื้อมาแด่องค์พระผู้เป็นเจ้า แต่ไม่ใช่ที่ดินส่วนมรดกของครอบครัว 23ปุโรหิตจะประเมินราคานับถึงปีกึ่งศตวรรษ และเขาจะถวายเงินจำนวนดังกล่าวแด่องค์พระผู้เป็นเจ้าในวันนั้น เป็นสิ่งที่บริสุทธิ์แด่องค์พระผู้เป็นเจ้า 24ในปีกึ่งศตวรรษ ที่ดินนั้นจะคืนให้เจ้าของเดิมซึ่งขายที่ดินให้ 25ราคาประเมินทั้งหมดระบุตามเชเขลของสถานนมัสการ ซึ่ง 20 เกราห์เท่ากับ 1 เชเขล

26“ ‘เจ้าไม่ควรคิดว่าจะถวายลูกวัวหรือลูกแกะหัวปีแด่องค์พระผู้เป็นเจ้าเพราะลูกหัวปีเป็นขององค์พระผู้เป็นเจ้าอยู่แล้ว 27หากเป็นลูกหัวปีของสัตว์ที่เป็นมลทิน เจ้าของจะซื้อคืนตามราคาที่ปุโรหิตประเมิน และจ่ายเพิ่มอีกหนึ่งในห้า หากเจ้าของไม่ไถ่คืน ปุโรหิตก็จะขายให้แก่ผู้อื่นตามราคาที่ตั้งไว้

28“ ‘อย่างไรก็ตามสิ่งที่ถวายเป็นสิทธิ์ขาดแด่องค์พระผู้เป็นเจ้าไม่ว่าจะเป็นตัวบุคคล สัตว์ หรือที่ดินมรดกย่อมเป็นสิทธิ์ขาด ไม่มีการซื้อขายหรือไถ่คืน เพราะเป็นของบริสุทธิ์ที่สุดแด่องค์พระผู้เป็นเจ้า

29“ ‘ผู้ใดถูกถวายเป็นสิทธิ์ขาดเพื่อให้ทำลายล้าง27:29 คำนี้ในภาษาฮีบรูหมายถึง สิ่งของหรือบุคคลที่ถวายแด่องค์พระผู้เป็นเจ้าแล้วไม่อาจเรียกคืนได้ มักจะต้องทำลายให้หมดสิ้นไป จะไถ่คืนไม่ได้ เขาจะต้องถูกประหารชีวิต

30“ ‘หนึ่งในสิบของผลผลิตจากแผ่นดิน ไม่ว่าเมล็ดข้าวจากผืนดินหรือผลไม้จากต้นเป็นขององค์พระผู้เป็นเจ้า และถือเป็นสิ่งบริสุทธิ์แด่องค์พระผู้เป็นเจ้า 31หากผู้ใดต้องการไถ่คืนสิบลดของเขา จะต้องจ่ายเพิ่มอีกหนึ่งในห้าของราคา 32หนึ่งในสิบของฝูงสัตว์ทั้งหมดคือ ทุกตัวที่สิบที่ผ่านไปใต้ไม้เท้าของผู้เลี้ยง จะเป็นส่วนบริสุทธิ์แด่องค์พระผู้เป็นเจ้า 33จะไม่มีการเลือกว่าตัวนั้นดีตัวนี้ไม่ดี หรือเอาตัวหนึ่งมาแทนอีกตัวหนึ่ง เพราะหากมีการเปลี่ยนตัว ทั้งตัวที่ถูกเปลี่ยนกับตัวที่เอามาเปลี่ยนย่อมเป็นของบริสุทธิ์แด่พระเจ้า ไถ่คืนไม่ได้’ ”

34ทั้งหมดนี้คือพระบัญชาซึ่งองค์พระผู้เป็นเจ้าประทานแก่โมเสสบนภูเขาซีนายสำหรับประชากรอิสราเอล