Levitiko 17 – CCL & TNCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Levitiko 17:1-16

Za Kusadya Magazi

1Yehova anawuza Mose kuti, 2“Uza Aaroni ndi ana ake, pamodzi ndi Aisraeli onse kuti, ‘Chimene Yehova walamula ndi ichi: 3Mwisraeli aliyense amene apha ngʼombe, mwana wankhosa kapena mbuzi mu msasa kapena kunja kwa msasa, 4mʼmalo mobwera nayo pa khomo la tenti ya msonkhano pamaso pa Yehova ndi kuyipereka kuti ikhale nsembe ya Yehova, ameneyo wapalamula mlandu wa magazi, wakhetsa magazi ndipo ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu anzake. 5Izi zili choncho kuti Aisraeli azibwera ndi nyama zawo za nsembe zimene akanaphera ku malo kwina kulikonse. Aisraeli azibwera nazo nyamazo kwa Yehova, kwa wansembe wokhala pa khomo la tenti ya msonkhano ndipo aziphere pomwepo kuti zikhale nsembe za chiyanjano. 6Wansembe awaze magazi ake pa guwa la Yehova limene lili pa khomo la tenti ya msonkhano ndipo atenthe mafuta ake kuti atulutse fungo lokomera Yehova. 7Motero asadzapherenso nsembe fano la mbuzi limene amachita nalo zadama. Limeneli ndi lamulo la muyaya kwa iwo ndi mibado ya mʼtsogolo.’ ”

8“Uwawuze kuti, ‘Mwisraeli aliyense kapena mlendo amene amakhala pakati pawo akapereka nsembe yopsereza kapena nsembe ina iliyonse 9popanda kubwera nayo pa khomo la tenti ya msonkhano kudzayipereka pamaso pa Yehova, munthu ameneyo achotsedwe pakati pa anthu anzake.’ ”

10“Mwisraeli aliyense kapena mlendo aliyense wokhala pakati panu amene adya magazi, ndidzamufulatira ndipo ndidzamuchotsa pakati pa anthu anzake. 11Pakuti moyo wa cholengedwa chilichonse uli mʼmagazi, ndipo ndawupereka kwa inu kuti muzichitira mwambo wopepesera machimo a moyo wanu pa guwa. Pajatu magazi ndiwo amachotsa machimo chifukwa moyo uli mʼmenemo. 12Choncho ndikuwawuza Aisraeli kuti, ‘Pasapezeke aliyense wa inu wodya magazi, ngakhale mlendo wokhala pakati panu.’ ”

13“Mwisraeli aliyense kapena mlendo aliyense wokhala pakati panu amene amasaka ndi kupha nyama zakuthengo kapena mbalame zimene amadya, ataye magazi ake pansi ndi kuwakwirira ndi dothi, 14chifukwa moyo wa cholengedwa chilichonse uli mʼmagazi ake. Nʼchifukwa chake ndinawawuza Aisraeli kuti, ‘Musamadye magazi a cholengedwa chilichonse, chifukwa moyo wa cholengedwa chilichonse uli mʼmagazi. Aliyense wodya magaziwo ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu anzake.

15“ ‘Munthu aliyense, kaya ndi mbadwa kapena mlendo, amene amadya chilichonse chofa chokha, kapena chojiwa ndi zirombo, achape zovala zake ndi kusamba, komabe adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo. Kenaka adzakhala woyeretsedwa. 16Koma ngati sachapa zovala zake ndi kusamba, adzasenzabe machimo ake.’ ”

Thai New Contemporary Bible

เลวีนิติ 17:1-16

ห้ามกินเลือด

1องค์พระผู้เป็นเจ้าตรัสกับโมเสสว่า 2“จงกล่าวแก่อาโรนกับบรรดาบุตรชายและปวงชนอิสราเอลว่า ‘องค์พระผู้เป็นเจ้าทรงบัญชาไว้ดังนี้ว่า 3ชาวอิสราเอลคนใดถวายวัว17:3 ในภาษาฮีบรูคำนี้เป็นได้ทั้งตัวผู้และตัวเมีย ลูกแกะหรือแพะในค่ายหรือนอกค่าย 4แทนที่จะนำมาที่ทางเข้าเต็นท์นัดพบ เพื่อถวายเป็นเครื่องบูชาแด่องค์พระผู้เป็นเจ้าหน้าพลับพลาขององค์พระผู้เป็นเจ้าให้ถือว่าชายคนนั้นได้ทำผิดในเรื่องทำให้โลหิตตก และจะถูกตัดออกจากหมู่ประชากรของเขา 5กฎข้อนี้มีไว้เพื่อให้ชนอิสราเอลเลิกถวายเครื่องบูชากลางแจ้ง พวกเขาต้องนำมาให้ปุโรหิต นั่นคือนำมาถวายแด่องค์พระผู้เป็นเจ้าตรงทางเข้าเต็นท์นัดพบ แล้วเผาถวายเป็นเครื่องสันติบูชา 6ปุโรหิตจะพรมเลือดบนแท่นบูชาตรงทางเข้าเต็นท์นัดพบ และเผาไขมันเป็นกลิ่นหอมซึ่งองค์พระผู้เป็นเจ้าพอพระทัย 7ประชากรจะได้เลิกถวายเครื่องบูชาแก่เทวรูปแพะ17:7 หรือผีมารซาตาน อันเป็นการทำตัวแพศยา นี่เป็นข้อปฏิบัติถาวรสำหรับเจ้าทั้งหลายสืบไปทุกชั่วอายุ’

8“จงกล่าวแก่พวกเขาว่า ‘เราขอย้ำว่าผู้ใดก็ตามไม่ว่าชาวอิสราเอลหรือคนต่างด้าวซึ่งอาศัยอยู่ในหมู่พวกเขาที่ถวายเครื่องเผาบูชาหรือเครื่องบูชาในที่อื่น 9และไม่ได้นำมาตรงทางเข้าเต็นท์นัดพบเพื่อถวายแด่องค์พระผู้เป็นเจ้า จะต้องถูกตัดออกจากหมู่ประชากรของเขา

10“ ‘เราจะเป็นปฏิปักษ์กับทุกคนที่กินเลือดทุกชนิด ไม่ว่าคนนั้นจะเป็นคนอิสราเอลหรือคนต่างด้าวซึ่งอาศัยอยู่ในหมู่พวกเขา เราจะตัดคนนั้นออกจากหมู่ประชากรของเขา 11เพราะชีวิตของสิ่งมีชีวิตอยู่ในเลือด และเราได้ให้เลือดแก่เจ้าเพื่อลบบาปสำหรับตัวเจ้าบนแท่นบูชา เลือดนั้นเองที่ได้ลบบาปสำหรับชีวิตของคนๆ หนึ่ง 12ฉะนั้นเราจึงสั่งชาวอิสราเอลว่า “พวกเจ้าและคนต่างด้าวซึ่งอาศัยอยู่ในหมู่พวกเจ้าจะต้องไม่กินเลือด”

13“ ‘ใครก็ตาม ไม่ว่าชาวอิสราเอลหรือคนต่างด้าวซึ่งอาศัยอยู่ในหมู่พวกเจ้าที่ล่าสัตว์ แล้วฆ่าสัตว์หรือนกที่อนุญาตให้เป็นอาหารได้ จะต้องรินเลือดออกมาแล้วเอาดินกลบ 14เพราะชีวิตของสิ่งมีชีวิตทุกอย่างคือเลือด นั่นเป็นเหตุที่เราพูดกับชาวอิสราเอลว่า “เจ้าจะต้องไม่กินเลือดของสิ่งมีชีวิตใดๆ เพราะชีวิตของสิ่งมีชีวิตทุกชนิดคือเลือดของมัน ผู้ใดกินเลือดจะต้องถูกตัดออก”

15“ ‘ผู้ใดไม่ว่าคนอิสราเอลโดยกำเนิดหรือคนต่างด้าว ซึ่งกินซากของสัตว์ใดที่ตายเองหรือถูกสัตว์ร้ายฆ่าตาย จะต้องซักเสื้อผ้าและอาบน้ำ และเป็นมลทินตามระเบียบพิธีจนถึงเวลาเย็น แล้วเขาจึงจะสะอาด 16แต่หากเขาไม่อาบน้ำและซักเสื้อผ้า เขาจะต้องรับผิดชอบ’ ”