Hoseya 14 – CCL & CARSA

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Hoseya 14:1-9

Kulapa Kubweretsa Madalitso

1Iwe Israeli bwerera kwa Yehova Mulungu wako.

Machimo anu ndi amene akugwetsani!

2Bweretsani zopempha zanu

ndipo bwererani kwa Yehova.

Munene kwa Iye kuti,

“Tikhululukireni machimo athu onse

ndi kutilandira mokoma mtima,

kuti tithe kukuyamikani ndi mawu a pakamwa pathu.

3Asiriya sangatipulumutse;

ife sitidzakwera pa akavalo ankhondo,

sitidzanenanso kuti, ‘Milungu yathu’

kwa zimene manja athu omwe anazipanga,

pakuti ndinu amene mumachitira chifundo ana amasiye.”

4Ine ndidzachiza kusakhulupirika kwawo

ndipo ndidzawakonda mwaufulu

pakuti ndaleka kuwakwiyira.

5Ndidzakhala ngati mame kwa Israeli

Ndipo iye adzachita maluwa ngati kakombo.

Adzazika mizu yake pansi

ngati mkungudza wa ku Lebanoni;

6mphukira zake zidzakula.

Kukongola kwake kudzakhala ngati mtengo wa olivi,

kununkhira kwake ngati mkungudza wa ku Lebanoni.

7Anthu adzakhalanso mu mthunzi wake.

Iye adzakula bwino ngati tirigu.

Adzachita maluwa ngati mphesa

ndipo kutchuka kwake kudzakhala ngati vinyo wochokera ku Lebanoni.

8Efereimu adzati, “Ndidzachita nawonso chiyani mafano?

Ine ndidzamuyankha ndi kumusamalira.

Ine ndili ngati mtengo wa payini wobiriwira;

zipatso zako zimachokera kwa Ine.”

9Ndani ali ndi nzeru? Adzazindikire zinthu izi.

Ndani amene amamvetsa zinthu? Adzamvetse izi.

Njira za Yehova ndi zolungama;

anthu olungama amayenda mʼmenemo,

koma anthu owukira amapunthwamo.

Священное Писание (Восточный перевод), версия с «Аллахом»

Осия 14:1-10

1Народ Самарии должен понести своё наказание,

потому что он восстал против своего Бога.

Они падут от меча,

их дети будут разорваны на куски,

их беременные женщины – рассечены на части.

Покаяние принесёт благословение

2Вернись, Исраил, к Вечному, своему Богу.

Твои грехи были твоим падением!

3Вернитесь к Вечному,

взяв с собой слова покаяния.

Скажите Ему:

«Прости все наши грехи

и милостиво прими нас,

и мы, как жертвенных быков,

принесём Тебе хвалу наших уст.

4Ассирия не может спасти нас;

мы не будем садиться на боевых коней

и не станем более говорить

изделиям наших рук: „Боги наши“,

потому что у Тебя сироты находят милость».

5– Я исцелю их неверность

и изберу любовь к ним,

потому что больше не гневаюсь на них.

6Я буду росой для Исраила,

и он расцветёт, как лилия.

Он пустит свои корни,

как ливанский кедр.

7Его побеги прорастут,

и он будет красив, как оливковое дерево,

будет благоухать, как ливанский кедр.

8Люди снова будут жить под его тенью.

Он будет расти, как зерно,

расцветёт, как виноградная лоза,

и прославится, как ливанское вино.

9Ефраим, какое Мне дело до идолов?14:9 Или: «Какое Ефраиму дело до идолов?»

Я отвечаю ему и забочусь о нём.

Я – как вечнозелёный кипарис,

и от Меня твоя плодовитость.

Заключение

10Тот, кто мудр, уразумеет эти вещи,

кто проницателен, поймёт их.

Пути Вечного правильны,

и праведники будут идти по ним,

а грешники на них споткнутся.