Hoseya 11 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Hoseya 11:1-12

Chikondi cha Mulungu pa Israeli

1“Israeli ali mwana, ndinamukonda,

ndipo ndinayitana mwana wanga kuti atuluke mu Igupto.

2Koma ndimati ndikamapitiriza kuyitana

iwo amandithawa kupita kutali.

Ankapereka nsembe kwa Abaala

ndipo ankafukiza lubani kwa mafano.

3Ndi Ine amene ndinaphunzitsa Efereimu kuyenda,

ndipo ndinawagwira pa mkono;

koma iwo sanazindikire

kuti ndine amene ndinawachiritsa.

4Ndinawatsogolera ndi zingwe zachifundo cha anthu

ndi zomangira za chikondi;

ndinachotsa goli mʼkhosi mwawo

ndipo ndinawerama nʼkuwadyetsa.

5“Sadzabwerera ku Igupto,

koma Asiriya ndiye adzakhala mfumu yawo

pakuti akana kutembenuka.

6Malupanga adzangʼanima mʼmizinda yawo,

ndipo adzawononga mipiringidzo ya zipata zawo

nadzathetseratu malingaliro awo.

7Anthu anga atsimikiza zondifulatira Ine.

Ngakhale atayitana Wammwambamwamba,

sizidzatheka kuti Iye awakwezenso.

8“Kodi ndingakusiye bwanji iwe Efereimu?

Kodi ndingakupereke bwanji iwe Israeli?

Kodi ndingakuchitire bwanji zimene ndinachitira Adima?

Kodi ndingathe bwanji kukuchitira zimene ndinachitira Zeboimu?

Mtima wanga wakana kutero;

chifundo changa chonse chikusefukira.

9Sindidzalola kuti ndikulange ndi mkwiyo wanga woopsa,

kapena kutembenuka ndi kuwononga Efereimu.

Pakuti Ine ndine Mulungu osati munthu,

Woyerayo pakati panu.

Sindidzabwera mwaukali.

10Iwo adzatsatira Yehova;

Iye adzabangula ngati mkango.

Akadzabangula,

ana ake adzabwera akunjenjemera kuchokera kumadzulo.

11Adzabwera akunjenjemera

ngati mbalame kuchokera ku Igupto,

ngati nkhunda kuchokera ku Asiriya.

Ine ndidzawakhazikanso mʼnyumba zawo,”

akutero Yehova.

Tchimo la Israeli

12Efereimu wandizungulira ndi mabodza,

nyumba ya Israeli yandizungulira ndi chinyengo.

Ndipo Yuda wawukira Mulungu,

wawukira ngakhale Woyerayo amene ndi wokhulupirika.

Persian Contemporary Bible

هوشع 11:1-12

محبت خدا نسبت به اسرائيل

1زمانی كه اسرائيل طفل بود او را مثل پسر خود دوست می‌داشتم و او را از مصر فرا خواندم. 2ولی هر چه بيشتر او را به سوی خود خواندم، بيشتر از من دور شد و برای بعل قربانی كرد و برای بتها بخور سوزانيد. 3از بچگی او را تربيت كردم، او را در آغوش گرفتم و راه رفتن را به او ياد دادم؛ ولی او نخواست بفهمد كه اين من بودم كه او را پروراندم. 4با كمند محبت، اسرائيل را به سوی خود كشيدم؛ بار از دوشش برداشتم و خم شده، او را خوراک دادم.

5ولی او به سوی من بازگشت نمی‌كند، پس دوباره به مصر خواهد رفت و آشور بر او سلطنت خواهد كرد. 6آتش جنگ در شهرهايش شعله‌ور خواهد شد. دشمنانش به دروازه‌های او حمله خواهند كرد و او در ميان سنگرهای خود به دام دشمن خواهد افتاد. 7قوم من تصميم گرفته‌اند مرا ترک كنند، پس من هم آنها را به اسارت می‌فرستم و هيچكس نخواهد توانست آنان را رهايی بخشد.

8ای اسرائيل، چگونه تو را از دست بدهم؟ چگونه بگذارم بروی؟ چگونه می‌توانم تو را مثل ادمه و صبوئيم رها كنم؟ آه از دلم برمی‌خيزد! چقدر آرزو دارم به تو كمک كنم! 9در شدت خشم خود تو را مجازات نخواهم كرد و ديگر تو را از بين نخواهم برد؛ زيرا من خدا هستم، نه انسان. من خدايی مقدس هستم و در ميان شما ساكنم. من ديگر با خشم به سراغ شما نخواهم آمد.

10«قوم من از من پيروی خواهند كرد و من مثل شير بر دشمنانشان خواهم غريد. ايشان شتابان از غرب باز خواهند گشت؛ 11مثل دستهٔ بزرگی از پرندگان از مصر و مانند كبوتران از آشور پرواز خواهند كرد. من دوباره ايشان را به خانه‌شان باز می‌گردانم.» اين وعده‌ای است از جانب خداوند.

گناه اسرائيل

12خداوند می‌فرمايد: «اسرائيل با دروغ و فريب مرا احاطه كرده است، و يهودا هنوز نسبت به من كه خدای امين و مقدس هستم، سركشی می‌كند.»