Hoseya 1 – CCL & NUB

The Word of God in Contemporary Chichewa

Hoseya 1:1-11

1Awa ndi mawu amene Yehova anayankhula kwa Hoseya mwana wa Beeri pa nthawi ya ulamuliro wa Uziya, Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a ku Yuda ndiponso pa nthawi ya ulamuliro wa Yeroboamu mwana wa Yowasi mfumu ya ku Israeli.

Mkazi wa Hoseya ndi Ana Ake

2Yehova atayamba kuyankhula kudzera mwa Hoseya, Yehova anati kwa Hoseyayo, “Pita kakwatire mkazi wachiwerewere ndipo ubereke naye ana mʼchiwerewere chake pakuti anthu a mʼdziko muno achimwa pochita chigololo choyipitsitsa, posiya Yehova.” 3Motero Hoseya anakwatira Gomeri mwana wamkazi wa Dibulaimu, ndipo mkaziyo anakhala woyembekezera nabala mwana wamwamuna.

4Tsono Yehova anati kwa Hoseya, “Umutche dzina loti Yezireeli, pakuti ndili pafupi kulanga banja la Yehu chifukwa cha anthu amene anawapha ku Yezireeli ndipo ndidzathetsa ufumu wa Israeli. 5Tsiku limenelo ndidzathyola uta wa Israeli mʼchigwa cha Yezireeli.”

6Gomeri anakhala woyembekezeranso ndipo anabereka mwana wamkazi. Ndipo Yehova anati kwa Hoseya, “Umutche dzina loti ‘Sakondedwa’ pakuti sindidzaonetsanso chikondi changa pa nyumba ya Israeli, kuti ndingawakhululukire konse. 7Komatu ndidzaonetsa chikondi pa nyumba ya Yuda; ndipo ndidzawapulumutsa, osati ndi uta, lupanga kapena nkhondo, kapena akavalo ndi okwerapo ake, koma ine Yehova Mulungu wawo ndidzawapulumutsa.”

8Sakondedwa ataleka kuyamwa, Gomeri anabereka mwana wina wamwamuna. 9Pamenepo Yehova anati, “Umutche dzina loti Sianthuanga,” pakuti inu si ndinu anthu anga ndipo Ine si ndine Mulungu wanu.

10“Komabe Aisraeli adzachuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja umene sangathe kuwuyeza kapena kuwuwerenga. Pamalo omwe ananena kuti, ‘Sindinu anthu anga,’ pomweponso adzawatchula kuti ‘Ana a Mulungu wamoyo.’ 11Anthu a ku Yuda ndi anthu a ku Israeli adzasonkhananso pamodzi ndipo adzasankha mtsogoleri mmodzi ndi kutuluka mʼdzikomo, pakuti tsiku la Yezireeli lidzakhala lalikulu kwambiri.”

Swedish Contemporary Bible

Hosea 1:1-11

Hoseas äktenskap – en symbol

(1:1—3:5)

1Detta är Herrens ord som kom till Hosea, Beeris son, när Ussia, Jotam, Achas och Hiskia var kungar i Juda och Jerobeam, Joashs son, regerade i Israel.

Hoseas familj

2Så här börjar Herrens tal genom Hosea. Herren sa till honom: ”Gå och skaffa dig en sköka till hustru och barn som föds i otukt, för landet bedriver otukt gentemot Herren.” 3Han gifte sig då med Gomer, dotter till Divlajim, och hon blev med barn och födde honom en son. 4Herren sa till honom: ”Ge honom namnet Jisreel, för snart ska jag straffa Jehus släkt för hans massaker i Jisreel och göra slut på Israels kungadöme. 5Den dagen ska jag bryta sönder Israels båge i Jisreels dal.”

6Hon blev åter med barn och födde en dotter. Herren sa till Hosea: ”Ge henne namnet Lo Ruchama, för jag ska inte längre förbarma mig över israeliterna så att jag förlåter dem.1:6 Lo Ruchama betyder hon som inte får förbarmande (Lo är en negation). I slutet av versen (förlåter ) är grundtextens innebörd osäker. 7Men jag ska förbarma mig över Juda folk och rädda dem genom Herren, deras Gud. Jag ska inte rädda dem genom båge eller svärd, strid, hästar eller ryttare.”

8När Gomer hade slutat amma Lo Ruchama, blev hon med barn igen och födde en son. 9Herren sa: ”Ge honom namnet Lo Ammi1:9 Betyder inte mitt folk., för ni är inte mitt folk och jag finns inte till för er.

10Men antalet israeliter ska bli som sandkornen på havsstranden, omöjliga att mäta och räkna. Där det nu sägs till dem: ’Ni är inte mitt folk’, där ska de kallas ’Den levande Gudens barn.’ 11Då ska Juda och Israels folk förenas och ha en gemensam ledare. De ska växa upp ur landet, och Jisreels dag blir stor.