Hagai 1 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Hagai 1:1-15

Za Kumanga Nyumba ya Yehova

1Chaka chachiwiri cha Mfumu Dariyo, tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chimodzi, Yehova anapatsa mneneri Hagai uthenga wopita kwa Zerubabeli mwana wa Sealatieli, bwanamkubwa wa Yuda, ndiponso kwa mkulu wa ansembe Yoswa mwana wa Yehozadaki:

2Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Anthu awa amanena kuti, ‘Nthawi sinafike yoti nʼkumanga Nyumba ya Yehova.’ ”

3Tsono Yehova anayankhula ndi mneneri Hagai kuti, 4“Kodi ino ndi nthawi yoti inuyo muzikhala mʼnyumba zomanga bwino, pamene Nyumba yangayi ikanali bwinja?”

5Tsono zimene Yehova Wamphamvuzonse akunena ndi izi, “Ganizirani bwino njira zanu. 6Mwadzala zambiri, koma mwakolola zochepa. Mumadya, koma simukhuta. Mumamwa, koma ludzu lanu silitha. Mumavala, koma simumva kutentha. Mumalandira malipiro, koma ndalama zanu zimatha ngati mwaziyika mʼthumba lobowoka.”

7Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ganizirani bwino njira zanu. 8Pitani ku mapiri ndipo mukatenge matabwa oti mudzamangire Nyumba yanga, kuti ndikondwere nayo ndi kulandiramo ulemu,” akutero Yehova. 9“Mumayembekezera zambiri, koma taonani mwapeza pangʼono pokha. Zimene munazibweretsa ku nyumba, Ine ndinazimwaza. Nʼchifukwa chiyani?” Akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Chifukwa Nyumba yanga ikanali bwinja, pamene aliyense wa inu watanganidwa kumanga nyumba yake. 10Choncho, chifukwa cha inu, mitambo yaleka kugwetsa mvula ndipo dziko lapansi laleka kutulutsa zomera. 11Ndabweretsa chilala pa minda ndi pa mapiri, chilala chawumitsa tirigu, mphesa, mafuta a olivi ndi chilichonse chimene chimamera pa nthaka, pa anthu ndi pa ngʼombe, ndi pa ntchito zonse za manja anu.”

12Pamenepo Zerubabeli mwana wa Sealatieli, mkulu wa ansembe Yoswa mwana wa Yehozadaki, ndi anthu onse otsala anamvera mawu a Yehova Mulungu wawo ndi uthenga wa Hagai, chifukwa anatumidwa ndi Yehova Mulungu wawo. Ndipo anthuwo anaopa Yehova.

13Tsono Hagai, mthenga wa Yehova, anapereka kwa anthuwo uthenga uwu wa Yehova: “Ine ndili nanu,” akutero Yehova. 14Kotero Yehova anakhudza mtima wa Zerubabeli mwana wa Sealatieli, bwanamkubwa wa Yuda, mtima wa Yoswa mwana wa Yehozadaki, mkulu wa ansembe, ndiponso mitima ya anthu onse otsala. Iwo anabwera ndi kuyamba ntchito yomanga Nyumba ya Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wawo, 15pa tsiku la 24 la mwezi wachisanu ndi chimodzi, wa chaka chachiwiri cha Mfumu Dariyo.

Bibelen på hverdagsdansk

Haggajs Bog 1:1-15

Gud befaler folket at genopbygge templet

1Profeten Haggaj modtog følgende budskab fra Herren den første dag i den sjette måned af kong Dareios’ andet regeringsår. Haggaj fik besked på at give det videre til Judas guvernør, Zerubbabel, søn af Shealtiel, og ypperstepræsten Josva, søn af Jotzadak.

2„Hør hvad Gud, den Almægtige, siger: Hvorfor siger folk, at tiden endnu ikke er inde til at genopbygge mit tempel? 3-4Mener I virkelig, at det er rigtigt af jer at bo i fornemme huse, når mit hus stadig ligger i ruiner? 5Tænk over, hvordan det går med jer: 6I planter og sår, men får en dårlig høst. I mangler både mad og drikke og tøj, og jeres arbejdsløn forsvinder som i en hullet pung. 7Se jer omkring og tænk over situationen.

8Gå nu op i bjergene og hent tømmer, så mit tempel kan blive færdigbygget, og jeg kan glæde mig over det og vise jer min herlighed.

9I håber på en god høst, men det bliver kun til lidt, og den smule I henter hjem, forsvinder som dug for solen. Hvorfor? Fordi mit hus ligger i ruiner, mens I har travlt med at bygge huse til jer selv. 10Derfor holder jeg regnen tilbage, så I får en dårlig høst. 11Jeg lader tørken ramme både lavland og højland, korn og druer, oliven og de øvrige afgrøder. Både mennesker og kvæg lider under det. Alt jeres møjsommelige arbejde er spildt.”

12Da adlød de alle sammen Herrens ord, som kom til dem gennem profeten Haggaj. Både guvernøren Zerubbabel, ypperstepræsten Josva og den rest af befolkningen, som var kommet tilbage til landet, adlød, for de var klar over, at budskabet var fra Gud, og de tog det alvorligt.

13Profeten Haggaj gav da folket følgende ord fra Herren: „Jeg vil være med jer og velsigne jer!” 14-15Og Gud gjorde Zerubbabel, Josva og hele folket så opsat på at genopbygge Herrens, den Almægtiges, tempel, at de allerede den 24. i samme måned tog fat på arbejdet.