Genesis 5 – CCL & BDS

The Word of God in Contemporary Chichewa

Genesis 5:1-32

Mibado Kuyambira pa Adamu Mpaka Nowa

1Ndondomeko ya mibado ya Adamu ndi iyi:

Pamene Mulungu analenga munthu, anamulenga mʼchifaniziro cha Mulungu. 2Iye analenga mwamuna ndi mkazi. Anawadalitsa ndipo anawatcha “Munthu.”

3Pamene Adamu anali ndi zaka 130, anabereka mwana wamwamuna wofanana naye ndipo anamutcha Seti. 4Atabadwa Seti, Adamu anakhala ndi moyo zaka zina 800 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi. 5Zaka zonse za Adamu zinali 930 ndipo anamwalira.

6Pamene Seti anali ndi zaka 105, anabereka Enosi. 7Atabadwa Enosi, Seti anakhala ndi moyo zaka zina 807 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi. 8Zaka zonse za Seti zinali 912 ndipo anamwalira.

9Pamene Enosi anali ndi zaka 90, anabereka Kenani. 10Atabadwa Kenani, Enosi anakhala ndi moyo zaka zina 815 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi. 11Zaka zonse za Enosi pamodzi zinali 905 ndipo anamwalira.

12Pamene Kenani anali ndi zaka 70, anabereka Mahalaleli. 13Atabadwa Mahalaleli, Kenani anakhala ndi moyo zaka zina 840 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi. 14Zaka zonse za Kenani zinali 910, ndipo anamwalira.

15Pamene Mahalaleli anali ndi zaka 65, anabereka Yaredi. 16Atabadwa Yaredi, Mahalaleli anakhala ndi moyo zaka zina 830 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi. 17Zaka zonse za Mahalaleli zinali 895 ndipo anamwalira.

18Pamene Yaredi anali ndi zaka 162, anabereka Enoki. 19Atabadwa Enoki, Yaredi anakhala ndi moyo zaka zina 800 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi. 20Zaka zonse za Yaredi zinali 962 ndipo anamwalira.

21Pamene Enoki anali ndi zaka 65, anabereka Metusela. 22Atabadwa Metusela, Enoki anayenda ndi Mulungu zaka 300 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi. 23Zaka zonse za Enoki zinali 365. 24Enoki anayenda ndi Mulungu; ndipo iye sanaonekenso chifukwa Mulungu anamutenga.

25Pamene Metusela anali ndi zaka 187, anabereka Lameki. 26Ndipo atabadwa Lameki, Metusela anakhala ndi moyo zaka zina 782 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi. 27Zaka zonse za Metusela zinali 969, ndipo anamwalira.

28Pamene Lameki anali ndi zaka 182, anabereka mwana wamwamuna. 29Ndipo anamutcha Nowa ndipo anati, “Iyeyu adzatipumulitsa ku ntchito zathu zolemetsazi, zolima nthaka imene Yehova anayitemberera.” 30Atabadwa Nowa, Lameki anakhala zaka zina 595 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi. 31Zaka zonse za Lameki zinali 777, ndipo kenaka anamwalira.

32Pamene Nowa anali ndi zaka 500, anabereka Semu, Hamu ndi Yafeti.

La Bible du Semeur (The Bible of the Sower)

Genèse 5:1-32

L’histoire de la famille d’Adam

D’Adam aux fils de Noé

1Voici l’histoire de la famille d’Adam. Quand Dieu créa les êtres humains, il les fit de telle sorte qu’ils lui ressemblent. 2Il les créa homme et femme, il les bénit et leur donna le nom d’hommes le jour où ils furent créés.

3Adam était âgé de 130 ans quand il eut un fils qui lui ressemble, qui soit son image. Il lui donna le nom de Seth. 4Après cela, Adam vécut encore 800 ans et il eut d’autres enfants. 5La durée totale de sa vie fut de 930 ans, puis il mourut.

6Quand Seth fut âgé de 105 ans, il eut pour fils5.6 Autre traduction, de même que dans les versets suivants : descendant. Enosh. 7Après cela, il vécut encore 807 ans et il eut d’autres enfants. 8Il mourut à l’âge de 912 ans.

9Quand Enosh fut âgé de 90 ans, il eut pour fils Qénân. 10Après cela, il vécut encore 815 ans et il eut d’autres enfants. 11Il mourut à l’âge de 905 ans.

12Quand Qénân fut âgé de 70 ans, il eut pour fils Mahalaléel. 13Après cela, il vécut encore 840 ans et il eut d’autres enfants. 14Il mourut à l’âge de 910 ans.

15Quand Mahalaléel fut âgé de 65 ans, il eut pour fils Yéred. 16Après cela, Mahalaléel vécut encore 830 ans et il eut d’autres enfants. 17Il mourut à l’âge de 895 ans.

18Quand Yéred fut âgé de 162 ans, il eut pour fils Hénok. 19Après cela, il vécut encore 800 ans, et il eut d’autres enfants. 20Il mourut à l’âge de 962 ans.

21Quand Hénok fut âgé de 65 ans, il eut pour fils Mathusalem. 22Après cela, Hénok mena sa vie sous le regard de Dieu durant 300 ans et il eut d’autres enfants. 23La durée totale de sa vie fut de 365 ans.

24Hénok vécut en communion avec Dieu puis il disparut, car Dieu le prit5.24 Voir Hé 11.5 ; Jd 14..

25Quand Mathusalem fut âgé de 187 ans, il eut pour fils Lémek. 26Après cela, il vécut encore 782 ans et il eut d’autres enfants. 27Il mourut à l’âge de 969 ans.

28Quand Lémek fut âgé de 182 ans, il eut un fils. 29Il l’appela Noé (Consolation5.29 En hébreu, le nom Noé évoque le verbe traduit par consolera.) en disant : Celui-ci nous consolera de notre travail et de la tâche pénible que nous impose ce sol que l’Eternel a maudit. 30Après cela, Lémek vécut encore 595 ans, et il eut d’autres enfants. 31Il mourut à l’âge de 777 ans.

32Quand Noé fut âgé de 500 ans, il eut pour fils Sem, Cham et Japhet.