Genesis 44 – CCL & CARSA

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 44:1-34

Chikho Chasiliva Mʼthumba la Benjamini

1Pambuyo pake Yosefe analamulira wantchito wa mʼnyumba mwake kuti, “Adzazire chakudya anthuwa mʼmatumba mwawo monga mmene anganyamulire, ndipo uwayikire ndalama zawo pakamwa pa matumba awowo. 2Tsono uyike chikho changa cha siliva chija, pakamwa pa thumba la wamngʼono kwambiriyu pamodzi ndi ndalama zake za chakudya” Ndipo iye anachita monga Yosefe ananenera.

3Mmawa kutacha anthu aja analoledwa kuti apite ndi abulu awo. 4Atangotuluka mu mzinda muja, koma asanapite patali, Yosefe anati kwa wantchito wake, “Nyamuka atsatire anthu aja msanga. Ndipo ukawapeza, uwafunse kuti, ‘Bwanji mwabwezera zoyipa ndi zabwino? 5Mwaberanji chikho chimene mbuye wanga amamweramo ndi kugwiritsa ntchito akafuna kuwombeza? Chimene mwachitachi ndi chinthu choyipa.’ ”

6Wantchito uja atawapeza ananena mawu anawuzidwa aja. 7Koma iwo anati kwa iye, “Kodi mbuye wanga mukuneneranji zimenezi? Sizingatheke ndi pangʼono pomwe kuti antchito anufe nʼkuchita zoterozo ayi! 8Paja ife pobwera kuchokera ku Kanaani tinatenga ndalama kubwezera zimene tinazipeza mʼmatumba mwathu. Ndiye pali chifukwa chanji kuti tikabe siliva kapena golide mʼnyumba mwa mbuye wanu? 9Ngati wantchito wanu wina pano atapezeka nacho chikhocho, ameneyo aphedwe ndipo ena tonsefe tidzakhala akapolo anu, mbuye wathu.”

10Iye anati, “Chabwino, tsono zikhale monga mwaneneramu. Komatu aliyense amene angapezeke nacho chikhocho adzakhala kapolo wanga, ndipo ena nonsenu muzipita mwaufulu.”

11Tsono onse anafulumira kutsitsa pansi aliyense thumba lake ndi kulitsekula. 12Kenaka anayamba kufufuza, kuyambira pa wamkulu mpaka pa wamngʼono. Ndipo chikhocho chinapezeka mʼthumba mwa Benjamini. 13Apo onse anangʼamba zovala zawo ndi chisoni. Ndipo anasenzetsa abulu katundu wawo nabwerera ku mzinda konkuja.

14Pamene Yuda ndi abale ake ankafika ku nyumba kwa Yosefe nʼkuti Yosefe akanali komweko. Ndipo anadzigwetsa pansi pamaso pake. 15Yosefe anafunsa kuti, “Nʼchiyani mwachitachi? Kodi simudziwa kuti munthu ngati ine ndikhoza kuona zinthu mwakuwombeza?”

16Yuda anayankha, “Kodi tinganenenji kwa mbuye wanga? Tinena chiyani? Tingadzilungamitse bwanji? Mulungu waulula kulakwa kwa antchito anu. Ndipo tsopano ndife akapolo a mbuye wanga, ife tonse pamodzi ndi amene wapezeka ndi chikhocho.”

17Koma Yosefe anati, “Sindingachite choncho ayi! Yekhayo amene wapezeka ndi chikhocho ndi amene akhale kapolo wanga. Ena nonsenu, bwererani kwa abambo anu mu mtendere.”

18Ndipo Yuda anamuyandikira iye nati, “Chonde mbuye wanga mulole kapolo wanune ndinene mawu pangʼono kwa mbuye wanga. Musandipsere mtima, kapolo wanune, popeza inu muli ngati Farao yemwe. 19Mbuye wanga munafunsa akapolo anufe kuti, ‘Kodi muli ndi abambo anu kapena mʼbale wanu?’ 20Ndipo ife tinayankha, ‘Inde mbuye wathu, ife tili ndi abambo athu wokalamba, ndipo pali mwana wamwamuna wamngʼono amene anabadwa abambo athu atakalamba kale. Mʼbale wake anafa ndipo ndi yekhayo mʼmimba mwa amayi ake amene watsala ndipo abambo ake amamukonda.’

21“Ndipo inu munatiwuza kuti, ‘Mubwere naye kwa ine kuti ndidzamuone ndekha.’ 22Ife tinati, ‘Mbuye wathu, mnyamatayo sangasiye abambo ake, akawasiya ndiye kuti abambo akewo adzafa.’ 23Koma inu munatichenjeza kuti, ‘Pokhapokha mutabwera naye mʼbale wanu wamngʼono kwambiri, simudzandionanso.’ 24Ndiye pamene tinafika kwa kapolo wanu, abambo athu tinawawuza zonse zimene munanena.

25“Abambo athu anatiwuza kuti, ‘Pitaninso mukagule kachakudya pangʼono.’ 26Koma tinati, ‘Sitingathe kupitanso. Sitingapite pokhapokha mngʼono wathuyu apite nafe chifukwa munthu uja anati sitingaonane naye ngati mngʼono wathuyu sakhala nafe.’

27“Koma kapolo wanu, abambo athu anatiwuza kuti, ‘Inu mukudziwa kuti mkazi wanga anandiberekera ana aamuna awiri. 28Mmodzi wa iwo anandisiya. Ine ndimati anadyedwa ndi chirombo popeza sindinamuonenso mpaka lero. 29Tsopano mukanditengeranso uyu, nakaphedwa mu njira ndiye kuti mudzandikankhira ku manda ndi chisoni.’

30“Tsono ngati tizibwerera kwa mtumiki wanu, abambo athu popanda mnyamatayu, amene moyo wa abambo ake uli pa iyeyu, 31ndipo akakaona kuti mnyamatayu palibe, basi akafa. Ife tidzakhala ngati takankhira abambo athu ku manda ndi chisoni. 32Ndiponsotu ine ndinadzipereka kwa abambo anga kukhala chikole chotsimikiza kuti mnyamatayu ndidzamuteteza, ndipo ndinati, ‘Ngati sindibwerera naye mnyamatayu kwa inu, ndiye kuti ndidzakhala wochimwira inu abambo anga moyo wanga wonse.’

33“Tsono, chonde mulole kuti ine kapolo wanu nditsalire kuno kukhala kapolo wa mbuye wathu mʼmalo mwa mnyamatayu. Koma iye apite pamodzi ndi abale akewa. 34Ndingabwerere bwanji kwa abambo anga ngati sindingapite ndi mnyamatayu? Ayi! Sindifuna kukaona tsoka limene lingakagwere abambo anga.”

Священное Писание (Восточный перевод), версия с «Аллахом»

Начало 44:1-34

Потерянная чаша

1Юсуф приказал своему управляющему:

– Наполни мешки этих людей едой, сколько смогут унести, и положи серебро каждому обратно в мешок. 2Положи мою чашу, мою серебряную чашу, в мешок к младшему вместе с его серебром за зерно.

И тот сделал, как велел Юсуф.

3Как только рассвело, братьев отправили в путь вместе с их ослами. 4Они были ещё недалеко от города, когда Юсуф сказал управляющему:

– Немедленно отправляйся в погоню за этими людьми и, когда догонишь, скажи им: «Почему вы заплатили злом за добро? 5Ведь это чаша моего господина, из которой он пьёт и на которой он гадает!44:5 Гадание – ненавистно для Аллаха и запрещено законами Таурата (см. Лев. 19:26; Втор. 18:10-12). Может быть, Юсуф никогда сам не гадал, но сказал это с определённой целью. Но также не исключено, что Юсуф был повинен в этом грехе, так как все люди, даже пророки, не без греха (см. 20:1-7; 2 Цар. 11–12; Рим. 3:23), исключая лишь Ису (см. 1 Пет. 2:21-23; 2 Кор. 5:20-21; Евр. 4:15). См. также ст. 15. Вы совершили недобрый поступок!»

6Догнав их, он повторил им эти слова. 7Они ответили:

– Почему господин говорит такие слова? Разве станут твои рабы делать подобное! 8Ведь мы даже принесли тебе обратно из земли Ханаана то серебро, которое нашли у себя в мешках. Зачем же нам воровать серебро или золото из дома твоего господина? 9Если вещь найдётся у одного из нас, пусть он умрёт, а остальные станут рабами нашего господина.

10Он сказал:

– Хорошо, пусть будет так, как вы говорите: у кого найдётся чаша, тот станет моим рабом, а остальные будут свободны от ответа.

11Братья быстро опустили каждый свой мешок на землю и развязали их. 12Управляющий начал искать, начиная со старшего, кончая младшим; чаша нашлась в мешке у Вениамина. 13Они в скорби разорвали на себе одежду, нагрузили каждый своего осла и вернулись в город.

14Иуда и его братья вернулись в дом Юсуфа, который всё ещё был там. Они бросились перед ним на землю.

15Юсуф сказал им:

– Что же вы сделали? Разве вы не знали, что такой человек, как я, может всё узнать через гадание?

16– Что мы можем сказать моему господину? – ответил Иуда. – Как нам возразить? Как доказать нашу невиновность? Аллах открыл нашу вину. Теперь мы рабы моего господина – и мы, и тот, у кого нашлась чаша.

17Юсуф сказал:

– Разве я стану делать такое! Только тот, у кого нашлась чаша, будет моим рабом, а вы возвращайтесь к отцу с миром.

Иуда просит об освобождении Вениамина

18Тогда Иуда подошёл к нему и сказал:

– Пожалуйста, мой господин, позволь твоему рабу сказать моему господину слово. Не гневайся на твоего раба, хотя ты равен самому фараону. 19Мой господин спросил своих рабов: «Есть ли у вас отец или брат?» 20И мы ответили: «У нас есть престарелый отец и есть его юный сын, рождённый ему в старости. Его родной брат умер, и из сыновей своей матери он остался один, поэтому отец особенно любит его».

21Тогда ты сказал своим рабам: «Приведите его ко мне, чтобы мне посмотреть на него». 22А мы ответили моему господину: «Мальчик не может оставить отца, а если оставит, то отец не переживёт разлуки с ним». 23Но ты сказал своим рабам: «Пока ваш брат не придёт сюда с вами, не показывайтесь мне на глаза».

24Вернувшись к твоему рабу, моему отцу, мы пересказали ему, что сказал мой господин. 25Наш отец сказал: «Вернитесь и купите ещё немного еды». 26Но мы ответили: «Мы не можем пойти; только если младший брат пойдёт с нами, тогда мы пойдём. Мы не можем и на глаза показаться тому человеку, если не будет с нами младшего брата».

27Твой раб, мой отец, сказал нам: «Вы сами знаете, что моя жена Рахиля родила мне двоих сыновей. 28Один из них ушёл от меня, и я сказал: „Конечно, он был растерзан на куски“, – и с тех пор я его не видел. 29Если вы возьмёте у меня и другого, и с ним случится беда, вы сведёте мою седую голову в могилу от горя».

30Поэтому, если мальчика не будет с нами, когда я вернусь к твоему рабу, моему отцу, и если мой отец, который так привязан к этому мальчику, 31увидит, что его с нами нет, он умрёт. Твои рабы этой скорбью сведут седую голову нашего отца в могилу. 32Твой раб поручился за безопасность мальчика перед отцом. Я сказал: «Если я не приведу его к тебе, то вина перед тобой, отец, будет на мне всю жизнь».

33Итак, молю тебя, мой господин, позволь твоему рабу остаться здесь вместо мальчика, и позволь мальчику вернуться с братьями. 34Как я могу вернуться к отцу, если мальчика со мной не будет? Да не увижу я горя моего отца.