Genesis 33 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 33:1-20

Yakobo Akumana ndi Esau

1Yakobo atakweza maso ake anaona Esau akubwera ndi anthu ake 400. Choncho ana ake anawagawira Leya, Rakele ndi antchito awiri aja. 2Anayika antchito ndi ana awo patsogolo, kenaka nʼkubwera Leya ndi ana ake, ndipo pambuyo pawo Rakele ndi Yosefe. 3Iye mwini anakhala patsogolo nawerama mpaka kukhudza pansi kasanu ndi kawiri pamene amayandikira mʼbale wake.

4Koma Esau anathamanga kukakumana ndi Yakobo ndipo anamukupatira namupsompsona. Onse awiri ankangolira. 5Kenaka Esau ataona amayi ndi ana awo anamufunsa Yakobo kuti, “Kodi anthu amene uli nawowa ndi a ndani?”

Yakobo anayankha kuti, “Awa ndi ana amene Mulungu, mwa kukoma mtima kwake, wapereka kwa mtumiki wanune.”

6Tsono antchito aja anayandikira naweramitsa mitu pansi. 7Kenaka, Leya ndi ana ake anabwera. Nawonso anaweramitsa mitu pansi. Potsiriza pa onse anabwera Yosefe ndi Rakele naweramitsanso mitu yawo pansi.

8Esau anafunsa kuti, “Kodi gulu la ziweto ndakumana nalo lija ndi layani?”

Yakobo anayankha nati, “Mbuye wanga, gulu lija ndi lanu kuti mundikomere mtima.”

9Koma Esau anati, “Mʼbale wanga, ine ndili nazo kale zambiri. Zinthu zakozi sunga.”

10Yakobo anati, “Chonde musatero. Ngati mwandikomera mtima, landirani mphatso yangayi kuchokera kwa ine. Pakuti ndi mmene mwandirandira bwinomu, ine ndikamaona nkhope yanu ndikuchita ngati ndikuona nkhope ya Mulungu. 11Chonde, landirani mphatso imene ndakutengeraniyi, popeza Mulungu wandikomera mtima kwambiri moti ndili ndi zonse zimene ndizifuna.” Ndipo popeza kuti Yakobo anamuwumiriza, Esau analandira.

12Ndipo Esau anati, “Tiyeni tizipita; nditsagana nanu.”

13Koma Yakobo anati kwa iye, “Mbuye wanga, inu mudziwa kuti anawa ndi a nthete ndiponso ndiyenera kusamalira nkhosa ndi ngʼombe zimene zikuyamwitsa ana awo. Ngati ndizimenya kuti zifulumire, tsiku limodzi lokha nyamazo zidzafa. 14Choncho, mbuye wanga lolani kuti mutsogole. Ine ndiziyenda pangʼonopangʼono pambuyo pa ziwetozi ndi anawa mpaka ndikafika ku Seiri.”

15Esau anati, “Ndiye bwanji ndikusiyireko ena mwa anthu anga.”

Koma Yakobo anati, “Koma muchitiranji zimenezi? Chachikulu nʼkuti mwandilandira bwino, mbuye wanga.”

16Choncho tsiku limenelo Esau anayamba ulendo wobwerera ku Seiri. 17Komabe Yakobo anapita ku Sukoti. Kumeneko anamanga nyumba yake ndi makola a ziweto zake. Nʼchifukwa chake malowa amatchedwa Sukoti.

18Mmene ankabwerera kuchokera ku Padanaramu, Yakobo anafika ku Salemu, mzinda wa Sekemu ku Kanaani. Anamanga msasa pamalopo moyangʼanana ndi mzindawo. 19Malo amenewo anagula kwa zidzukulu za Hamori, abambo a Sekemu ndi ndalama 100 zasiliva. 20Pamalopo anamanganso guwa lansembe, nalitcha Eli Elohe Israeli.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

創世記 33:1-20

弟兄重逢

1雅各遠遠看見以掃帶著四百人迎面而來,便把孩子們分別交給利亞拉結和兩個婢女, 2又吩咐兩個婢女和她們的孩子走在前面,利亞和她的孩子跟在後面,拉結約瑟走在最後。 3他自己則走在他們前面,接連俯伏下拜七次,直到他哥哥跟前。

4以掃見到雅各,就跑上去擁抱他,親吻他,二人抱頭痛哭。 5以掃看見跟在雅各後面的婦女和孩子,就問:「這些和你同行的是誰?」雅各說:「這些孩子是上帝施恩賜給你僕人的。」 6雅各的兩個婢女和她們的孩子上前下拜, 7利亞也和她的孩子上前下拜,最後約瑟拉結也上前向以掃下拜。

8以掃說:「我在路上遇見的那一群群牲畜是怎麼回事?」雅各回答說:「我帶來這些是要得到我主的恩待。」 9以掃說:「弟弟,我已經有很多了,你自己留著吧!」 10雅各說:「不,你若賞臉,就請收下!我見了你的面就像見了上帝的面,因為你這樣善侍我。 11請你收下我的禮物吧,因為上帝恩待了我,使我富足。」雅各再三懇求,以掃才收下。

12以掃說:「我們走吧!我陪你們走。」 13雅各卻說:「我主知道孩子們還小,而且,我還要照料正在哺乳的牛羊,如果整天趕路,牛羊會累死。 14倒不如請我主先走,我遷就牲畜和孩子慢慢走,我在西珥與我主會合。」

15以掃說:「讓我給你留幾個幫手吧。」雅各說:「不用了,能得到我主的恩待就夠了。」 16於是,以掃在當天先回西珥去了, 17雅各卻去了疏割,在那裡為自己建造房屋,為牲畜搭起棚子。因此那地方叫疏割33·17 疏割」意思是「棚子」。

18這樣,雅各巴旦·亞蘭平安地回到迦南示劍城,在城外搭營居住。 19他搭營居住的這塊地是他用一百塊銀子向示劍的父親哈抹的子孫買的。 20雅各在那裡築了一座壇,稱之為伊利·伊羅伊·以色列33·20 伊利·伊羅伊·以色列」意思是「以色列的上帝」。