Genesis 32 – CCL & SNC

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 32:1-32

Yakobo Akonzekera Kukumana ndi Esau

1Nayenso Yakobo analowera njira yake, ndipo angelo a Mulungu anakumana naye. 2Pamene Yakobo anawaona anati, “Ili ndi gulu la Mulungu.” Choncho anawatcha malowo Mahanaimu.

3Yakobo anatumiza amithenga ake kwa mʼbale wake Esau ku dera la Seiri, dziko la Edomu. 4Anawalangiza kuti, “Zimene mukanene ndi izi kwa mbuye wanga Esau: ‘Mtumiki wanu Yakobo akuti, Ine ndakhala ndi kukhala ndi Labani mpaka tsopano. 5Ndili ndi ngʼombe, abulu, nkhosa ndi mbuzi, antchito aamuna ndi aakazi. Tsopano ndikutumiza mawu amenewa kwa mbuye wanga, kuti mundikomere mtima.’ ”

6Pamene amithenga aja anabwerera kwa Yakobo, anati, “Tinapita kwa mʼbale wanu Esau, ndipo tsopano iye akubwera kudzakumana nanu. Ali ndi anthu 400.”

7Yakobo anali ndi mantha ndi nkhawa yayikulu kwambiri. Tsono anagawa anthu onse amene anali naye, ndiponso nkhosa, mbuzi, ngʼombe ndi ngamira mʼmagulu awiri. 8Mʼmaganizo ake iye ankanena kuti, “Ngati Esau atabwera ndi kuthira nkhondo gulu limodzi, gulu lina lotsalalo likhoza kupulumuka.”

9Pamenepo Yakobo anapemphera, “Haa, Mulungu wa kholo langa Abrahamu, Mulungu wa abambo anga Isake, Aa Yehova amene munati kwa ine, ‘Bwerera ku dziko la kwanu ndi kwa abale ako, ndipo ndidzakuchitira zabwino.’ 10Ine siwoyenera kulandira kukoma mtima kwanu ndi kukhulupirika kwanu kumene mwaonetsa wantchito wanu. Ndinali ndi ndodo yokha pamene ndinawoloka Yorodani uyu koma tsopano ndili ndi magulu awiri. 11Ndipulumutseni mʼdzanja la mʼbale wanga Esau, popeza ndikuopa kuti mwina akubwera kudzandithira nkhondo pamodzi ndi akazi ndi ana omwe. 12Paja Inu munandilonjeza kuti simudzalephera kundichitira zabwino ndi kuti zidzukulu zanga zidzakhala zosawerengeka ngati mchenga wa ku nyanja.”

13Iye anagona pomwepo usiku umenewo. Pambuyo pake anasankhula pa chuma chimene anali nacho zinthu izi ngati mphatso za Esau, mʼbale wake: 14Anasankhula mbuzi zazikazi 200 ndi atonde makumi awiri, nkhosa zazikazi 200 ndi nkhosa zazimuna makumi awiri, 15ngamira za mkaka 30 ndi ana awo, ngʼombe zazikazi 40 ndi zazimuna khumi, ndipo abulu aakazi makumi awiri ndi abulu aamuna khumi. 16Iye anazipereka kwa antchito ake kuti azikuse, gulu lililonse pa lokha, ndipo anati kwa antchito akewo, “Tsogolani ndipo muonetsetse kuti pali mpata pakati pa gulu ndi gulu linzake.”

17Anawuza mnyamata wa gulu loyamba kuti, “Ngati ukumana naye mʼbale wanga Esau nakufunsa kuti, ‘Ndinu antchito a yani, ndipo mukupita kuti? Nanga ziweto zonse zili patsogolo pakozi ndi za yani?’ 18Pamenepo ukayankhe kuti, ‘Zimenezi ndi za wantchito wanu, Yakobo, ndipo wazipereka kwa inu, Esau, mbuye wake ngati mphatso. Mtumiki wanuyu akubwera mʼmbuyo mwathumu.’ ”

19Anawuza mawu omwewo kwa wachiwiri, wachitatu ndi ena onse amene ankayenda motsogoza ziwetozo kuti, “Inunso munene zomwezo kwa Esau mukakumana naye. 20Muzikanena kuti, ‘Wantchito wanu Yakobo akubwera mʼmbuyo mwathumu.’ ” Popeza anaganiza kuti, “Ndidzamutsitsa mtima ndi mphatso ndazitsogozazi. Apo tsono ndikadzakumana naye, mwina adzandilandira bwino.” 21Choncho mphatso za Yakobo zinatsogola, koma iye mwini anagona pa msasa pomwepo usiku umenewo.

Yakobo Alimbana ndi Mulungu

22Usiku umenewo Yakobo anauka natenga akazi ake awiri, antchito ake awiri ndi ana ake aamuna khumi ndi mmodzi nawoloka pa dooko la mtsinje wa Yaboki. 23Atatha kuwawolotsa pa mtsinjewo anawolotsanso katundu wake yense. 24Tsono Yakobo anatsala yekha. Tsono munthu wina anadzalimbana naye mpaka mʼmbandakucha. 25Pamene munthuyo anaona kuti sangathe kumugonjetsa, anakhudza nyungʼunyu ya pa ntchafu ya Yakobo ndipo inaguluka polimbanapo. 26Kenaka munthuyo anati, “Ndisiye ndizipita, popeza kunja kukucha.”

Koma Yakobo anayankha, “Sindikulolani kupita pokhapokha mutandidalitsa.”

27Munthu uja anamufunsa Yakobo kuti, “Kodi dzina lako ndiwe yani?”

Iye anayankha, “Ndine Yakobo.”

28Pamenepo munthuyo anati, “Dzina lako silidzakhalanso Yakobo koma Israeli, chifukwa walimbana ndi Mulungu ndi anthu ndipo wapambana.”

29Yakobo anati, “Chonde, uzeni dzina lanu.”

Koma munthuyo anati, “Chifukwa chiyani ukundifunsa dzina?” Kenaka anamudalitsa pomwepo.

30Choncho Yakobo anawatcha malowo Penueli, popeza anati, “Ndinaonana ndi Mulungu maso ndi maso koma sindinafe.”

31Dzuwa linamutulukira Yakobo pamene amachoka pa Penueli. Tsono ankayenda chotsimphina chifukwa cha nyungʼunyu yake ija. 32Nʼchifukwa chake mpaka lero Aisraeli sadya nyama ya pa nyungʼunyu chifukwa Yakobo anakhudzidwa pa nyungʼunyu.

Slovo na cestu

1 Mojžíšova 32:1-32

1Jákob pak odšel cestou svou, a potkali se s ním andělé Boží. 2I řekl Jákob, když je viděl: Vojsko Boží jest toto. A nazval jméno místa toho Mahanaim. 3Poslal pak Jákob posly před sebou k bratru svému Ezau, do země Seir, do kraje Idumejského. 4A přikázal jim, řka: Takto povězte pánu mému Ezau: Totoť vzkazuje služebník tvůj Jákob: U Lábana jsem byl pohostinu, a zůstával až do tohoto času. 5A mám voly a osly, ovce, a služebníky i děvky; a poslal jsem, abych se ohlásil pánu svému, a našel milost před očima tvýma. 6I navrátili se poslové k Jákobovi, řkouce: Přišli jsme k bratru tvému Ezau, kterýž také jde proti tobě, a čtyři sta mužů s ním. 7Jákob pak bál se velmi, a rmoutil se náramně. Tedy rozdělil lid, kterýž s sebou měl, ovce také a voly, a velbloudy na dva houfy. 8Nebo řekl: Jestliže by přišel Ezau k houfu jednomu, a pobil by jej, bude aspoň zadní houf zachován. 9I řekl Jákob: Bože otce mého Abrahama, a Bože otce mého Izáka, Hospodine, kterýž jsi mi řekl: Navrať se do země své, a k příbuznosti své, a dobře učiním tobě, 10Menší jsem všech milosrdenství a vší pravdy, kterouž jsi učinil s služebníkem svým; nebo s holí svou přešel jsem Jordán tento, nyní pak dva houfy mám. 11Vytrhni mne, prosím, z ruky bratra mého, z ruky Ezau; nebť se ho bojím, aby přijda, nepohubil mne i matky s dětmi. 12Však jsi ty řekl: Dobře učiním tobě, a rozmnožím símě tvé jako písek mořský, kterýžto pro množství sečten býti nemůže. 13I zůstal tu noci té; a vzal z toho, což bylo před rukama, poctu bratru svému Ezau: 14Totiž dvě stě koz, a kozlů dvadceti, ovec dvě stě, a beranů dvadceti, 15Velbloudů s mladými jich třidceti, krav čtyřidceti, volů deset, oslic dvadceti, a oslátek deset. 16A poručil je služebníkům svým, každé stádo obzvláštně, a řekl služebníkům svým: Jděte přede mnou, a stádo od stáda ať jde opodál. 17I poručil přednímu, řka: Když se potká s tebou Ezau bratr můj, a optá se tebe, řka Èí jsi? a kam jdeš? a čí jest to stádo před tebou? 18Řekneš: Jsem služebníka tvého Jákoba, a dar tento jest poslán pánu mému Ezau; a teď i sám jde za námi. 19Poručil také druhému i třetímu, a všechněm jdoucím za těmi stády, řka: V táž slova mluvte k Ezau, když byste naň trefili. 20A díte také: Aj, služebník tvůj Jákob za námi; nebo řekl: Ukrotím tvář jeho darem, kterýž jde přede mnou, a potom uzřím tvář jeho; snad přijme tvář mou. 21A tak předšel dar před ním; on pak zůstal tu noc při houfu. 22A vstav ještě v noci, vzal obě ženy své, a dvě děvky své, a jedenácte synů svých, a přešel přes brod Jabok. 23Vzav tedy je, přepravil je přes tu řeku; přepravil také i vše, což měl. 24A zůstal Jákob sám; a tu zápasil s ním muž až do svitání. 25A vida, že ho nepřemůže, obrazil jej v příhbí vrchní stehna jeho; i vyvinulo se příhbí stehna Jákobova, když zápasil s ním. 26A řekl: Pusť mne, nebť zasvitává. I řekl: Nepustím tě, leč mi požehnáš. 27I řekl jemu: Jaké jest jméno tvé? Odpověděl: Jákob. 28I dí: Nebude více nazýváno jméno tvé toliko Jákob, ale také Izrael; nebo jsi statečně zacházel s Bohem i lidmi, a přemohls. 29I otázal se Jákob, řka: Oznam, prosím, jméno své. Kterýžto odpověděl: Proč se ptáš na jméno mé? I dal mu tu požehnání. 30Tedy nazval Jákob jméno místa toho Fanuel; nebo jsem prý viděl Boha tváří v tvář, a zachována jest duše má. 31I vzešlo mu slunce, když pominul místa toho Fanuel, a kulhal na nohu svou. 32Protož nejedí synové Izraelští až do tohoto dne té žily krátké, kteráž jest v vrchním příhbí stehna, proto že obrazil příhbí stehna Jákobova na žile krátké.