Genesis 15 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 15:1-21

Pangano la Mulungu ndi Abramu

1Zitatha izi, Yehova anayankhula ndi Abramu mʼmasomphenya nati:

“Usaope Abramu.

Ine ndili ngati chishango chokutchinjiriza.

Mphotho yako idzakhala yayikulu.”

2Koma Abramu anati, “Haa! Ambuye Yehova, mukhoza kundipatsa chiyani popeza ndikanali wopanda mwana ndipo amene adzatenge chuma changa ndi Eliezara wa ku Damasiko? 3Inu simunandipatse ana kotero kuti wantchito wa ku nyumba kwanga ndiye amene adzalowe mʼmalo mwanga.”

4Yehova anayankhula naye nati: “Munthu uyu sadzalowa mʼmalo mwako, koma mwana wako weniweni wamwamuna, wobereka wekha ndiye adzalowe mʼmalo mwako.” 5Yehova anapita naye Abramu panja nati, “Tayangʼana kumwambaku, ndipo chifukwa cha chimenechi uwerenge nyenyezi ngati ungathe kuziwerenga.” Ndipo anamuwuza kuti, “Ndi mmene adzakhalire ana ako ndi zidzukulu zako.”

6Abramu anakhulupirira Yehova, ndipo ichi chinamuchititsa kukhala wolungama.

7Ndipo anamuwuza kuti, “Ine ndine Yehova amene ndinakuchotsa iwe ku mzinda wa Uri wa ku Akaldeya kuti ndikupatse dziko ili kuti likhale lako.”

8Koma Abramu anati, “Haa! Ambuye Yehova, kodi ndingadziwe bwanji kuti lidzakhaladi langa?”

9Kotero Yehova anati kwa iye, “Kanditengere kamsoti kangʼombe ka zaka zitatu, kamsoti ka mbuzi ka zaka zitatu, ndi nkhosa yayimuna ya zaka zitatu pamodzi ndi nkhunda ndi kamwana ka njiwa.”

10Abramu anabweretsadi zonsezi nadula chilichonse pakati nʼkuzindandalika, chidutswa chilichonse kuyangʼanana ndi chinzake; koma njiwa ndi nkhunda sanazidule pakati. 11Pamene miphamba inabwera kuti itole nyama ija, Abramu anayipirikitsa.

12Pamene dzuwa limalowa Abramu anagona tulo tofa nato ndipo mdima wandiweyani ndi wochititsa mantha unamuphimba. 13Tsono Yehova anati kwa iye, “Uyenera kudziwa mosakayika kuti zidzukulu zako zidzakhala alendo mʼdziko lachilendo ndipo zidzakhala akapolo ndi kuzunzidwa zaka 400. 14Koma ndidzalanga dziko limene zidzukulu zako zidzagwireko ukapolo ndipo pambuyo pake iwo adzatulukamo ndi chuma chambiri. 15Komabe iweyo udzamwalira mu mtendere ndi kuyikidwa mʼmanda utakalamba bwino. 16Patapita mibado inayi, adzukulu ako adzabwereranso kuno popeza tchimo la Aamori silinafike pachimake kuti alangidwe.”

17Dzuwa litalowa ndipo mdima utagwa, panaoneka mʼphika wofuka nthunzi ya moto ndi sakali yoyaka ndipo zinadutsa pakati pa zidutswa za nyama zija. 18Pa tsiku limenelo, Yehova anachita pangano ndi Abramu nati, “Ndikulonjeza kuti ndidzapereka dziko ili kwa zidzukulu zako, kuchokera ku mtsinje wa ku Igupto mpaka ku mtsinje waukulu wa Yufurate. 19Ndidzakupatsani dziko la Akeni, Akenizi, Akadimoni, 20Ahiti, Aperezi, Arefaimu, 21Aamori, Akanaani, Agirigasi ndi Ayebusi.”

Bibelen på hverdagsdansk

1. Mosebog 15:1-21

Guds løfte til Abram

1Senere talte Herren til Abram i et syn: „Vær ikke bange, Abram, for jeg er med dig, og jeg vil belønne dig rigeligt.” 2-3„Men almægtige Herre,” udbrød Abram, „hvad skal jeg med din velsignelse, hvis jeg dør barnløs? Min tjener Eliezer kommer til at arve al min rigdom, for du har jo ikke givet mig en søn.” 4Men Herren svarede: „Nej, han skal ikke være din arving. Det skal din egen søn!”

5Herren førte nu Abram udenfor og sagde: „Kig op mod himlen og prøv at tælle stjernerne. Dine efterkommere skal blive lige så talrige.” 6Abram troede på Herren, og derfor blev han accepteret.

7Herren fortsatte: „Jeg er Herren, som førte dig fra din hjemby Ur for at give dig det land, du nu bor i.” 8Men Abram indvendte: „Almægtige Herre, hvordan kan jeg være sikker på, at du vil give mig det?” 9Da sagde Herren: „Bring mig en treårs kvie, en treårs ged, en treårs vædder, en turteldue og en ung due.”15,9 Et offer for at bekræfte indgåelsen af en pagt. 10Abram hentede dyrene og slagtede dem. Så skar han dem midt igennem på langs og lagde halvdelene overfor hinanden. Dog skar han ikke fuglene over. 11Straks slog gribbene ned på de døde dyr, men Abram jog dem bort.

12Hen mod aften faldt Abram i en dyb søvn, og et stort og frygteligt mørke sænkede sig over ham.

13Da sagde Herren til Abram: „Dine efterkommere vil komme til at bo i et fremmed land i 400 år og opleve slaveri og undertrykkelse, 14men jeg vil straffe det folk, som undertrykker dem, og til sidst skal dit folk rejse bort derfra med megen rigdom. 15(Dette skal dog ikke ske i din tid. Du skal nå en høj alder og dø i fred.) 16Fire generationer15,16 Folk levede længe dengang, så en generation kunne være op til 100 år. senere skal de vende tilbage til dette land. På det tidspunkt er amoritternes synd blevet så voldsom, at jeg må straffe dem.”

17Da Abram vågnede, var solen gået ned, og han så noget som en rygende ovn eller en flammende fakkel passere midt imellem halvdelene af de døde dyr. 18Sådan bekræftede Herren den dag pagten med Abram. „Jeg giver dette land til dig og dine efterkommere,” sagde han, „lige fra grænsen til Egypten mod syd og op til Eufratfloden mod nord—hele det område, 19som bebos af kenitterne, kenizzitterne, kadmonitterne, 20hittitterne, perizzitterne, refaitterne, 21amoritterne, kana’anæerne, girgashitterne og jebusitterne.”