Genesis 13 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 13:1-18

Abramu Asiyana ndi Loti

1Choncho Abramu pamodzi ndi mkazi wake ndi zonse anali nazo, anachoka ku Igupto kupita ku Negevi. Loti naye anapita nawo. 2Abramu anali wolemera kwambiri; anali ndi ziweto ndiponso siliva ndi golide.

3Atachoka ku Negevi, anayenda malo osiyanasiyana mpaka anafika ku Beteli, ku malo a pakati pa Beteli ndi Ai, kuja kumene anamanga tenti poyamba, 4ndiponso kumene Abramu anamangira Yehova guwa lansembe kwa nthawi yoyamba ndi kupemphera mʼdzina la Yehova.

5Loti amene ankayendayenda ndi Abramu nayenso anali ndi ziweto zosiyanasiyana ndi matenti. 6Motero dziko linayamba kuwachepera kuti onse nʼkukhala pamodzi, popeza katundu wawo anali wochuluka kwambiri moti sakanatha kukhala pamodzi. 7Mikangano inayambika pakati pa abusa a Abramu ndi abusa a Loti. Nthawi imeneyo nʼkuti Akanaani ndi Aperezi akukhalanso mʼdziko lomwelo.

8Tsono Abramu anati kwa Loti, “Pasakhale mikangano pakati pa iwe ndi ine kapena pakati pa abusa ako ndi anga, popeza ndife abale. 9Kodi dziko lonseli silili pamaso pako? Tiye tisiyane. Iwe ukalowera kumanzere, ine ndilowera kumanja; ukalowera kumanja, ine ndipita kumanzere.”

10Loti atamwazamwaza maso anaona kuti chigwa chonse cha mtsinje wa Yorodani chinali chothiriridwa bwino ngati munda wa Yehova, kapena ngati dziko la ku Igupto mpaka ku Zowari. (Nthawi iyi nʼkuti Yehova asanawononge Sodomu ndi Gomora). 11Choncho Loti anadzisankhira yekha chigwa chonse cha Yorodani nanyamuka kulowera cha kummawa. Choncho anthu awiriwa anasiyana. 12Abramu anakhala mʼdziko la Kanaani, pamene Loti anakakhala pakati pa mizinda ikuluikulu ya mʼchigwamo. Anamanga tenti yake pafupi ndi Sodomu. 13Tsono anthu a ku Sodomu anali oyipa ndiponso ankachimwira Yehova kwambiri.

14Loti atachoka, Yehova anati kwa Abramu, “Kuchokera pamene ulipo tayangʼanayangʼana cha kumpoto, kummwera, kummawa ndi kumadzulo. 15Dziko lonse ukulionalo ndidzalipereka kwa iwe ndi zidzukulu zako mpaka muyaya. 16Ndidzakupatsa zidzukulu zochuluka ngati fumbi lapansi moti amene angathe kuwerenga fumbilo ndiye kuti angathenso kuwerenga zidzukulu zako. 17Dzuka ndipo uyendere dziko lonseli mulitali ndi mulifupi pakuti ndalipereka kwa iwe.”

18Choncho Abramu anasamutsa tenti yake napita kukakhala pafupi ndi mitengo ikuluikulu ija ya thundu ya ku Mamre ku Hebroni, kumene anamangira Yehova guwa lansembe.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

創世記 13:1-18

亞伯蘭與羅得分道揚鑣

1亞伯蘭帶著妻子、侄兒羅得和所有的一切離開埃及去南地。 2這時候亞伯蘭已經擁有很多牲畜和金銀。 3-4他從南地漸漸遷移到伯特利,到了他從前在伯特利中間搭帳篷和築壇的地方。他又在那裡求告耶和華。 5亞伯蘭同行的羅得也有牛群、羊群和帳篷。 6他們的牲畜很多,那地方容納不下,他們無法住在一起。 7亞伯蘭的牧人和羅得的牧人彼此爭執。那時,迦南人和比利洗人也住在那裡。

8亞伯蘭羅得說:「我們不該彼此爭執,我們的牧人也不該互相爭執,因為我們是骨肉至親。 9整片土地不就在你面前嗎?我們分開吧。如果你往左邊去,我就往右邊走;如果你往右邊去,我就往左邊走。」 10羅得舉目眺望,看見整個約旦河平原,遠至瑣珥,水源充足。在耶和華還沒有毀滅所多瑪蛾摩拉之前,那地方就好像耶和華的伊甸園,又像埃及11於是,羅得選了整個約旦河平原,向東遷移,他們便分開了。 12亞伯蘭住在迦南羅得則住在平原的城邑裡,並漸漸把帳篷遷移到所多瑪附近。 13所多瑪人極其邪惡,在耶和華眼中罪惡滔天。

14羅得離開後,耶和華對亞伯蘭說:「從你站的地方向東西南北眺望, 15你所能看見的地方,我都要賜給你和你的後代,直到永遠。 16我要使你的後代多如地上的塵土,人若能數算地上的塵土,才能數算你的後代。 17你起來走遍這片土地,因為我要把這片土地賜給你。」 18亞伯蘭就把帳篷遷移到希伯崙幔利的橡樹那裡居住,在那裡為耶和華築了一座祭壇。