Ezekieli 41 – CCL & NIVUK

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 41:1-26

1Ndipo munthuyo anapita nane mʼchipinda chopatulika cha Nyumba ya Mulungu ndipo anayeza khonde lake; mulifupi mwa khondelo munali mamita atatu mbali iliyonse kutalika kwake. 2Mulifupi mwa khomo munali motalika mamita asanu. Makoma a mbali zonse anali a mamita awiri ndi theka mulifupi mwake. Anayezanso kutalika kwa chipinda chopatulika chija ndipo mulitali mwake munali motalika mamita makumi awiri ndi mulifupi mwake munali mamita khumi.

3Kenaka munthuyo anakalowa mʼkati ndipo anayeza khonde la pa khomo; khondelo linali mita imodzi mulifupi mwake. Mulifupi mwa khondelo munali mamita atatu. 4Ndiponso anayeza kutalika kwa chipinda chopatulika chenichenicho. Mulitali mwake munali mamita khumi, ndipo mulifupi mwake munali mamita khumi. Munthuyo anandiwuza kuti, “Ichi ndicho chipinda chopatulika kwambiri.”

5Tsono munthuyo anayeza khoma la Nyumba ya Mulungu; kuchindikira kwake kunali mamita atatu. Panalinso zipinda zina kuzungulira Nyumba ya Mulungu ndipo chilichonse chinali cha mamita awiri mulifupi wake. 6Zipindazo zinali zitatu zosanjikizana. Chigawo chilichonse chinali ndi zipinda makumi atatu. Pa makoma a Nyumba ya Mulungu panali zochirikiza zipindazo kuti zisatsamire khoma la Nyumba ya Mulungu. 7Zipinda za mʼmbalizo zinkapita zikulirakulira pomakwera chipinda ndi chipinda potsata kukulirakulira kwa zochirikiza za zipinda zija. Pambali pa Nyumba ya Mulungu panali makwerero okwerera pamwamba, kuchokera chigawo chapansi kudzera chapakati, mpaka kukafika pamwamba.

8Ndinaona chiwundo kuzungulira Nyumba ya Mulungu. Chinapanga maziko a zipindazo ndipo chinali cha mamita atatu. 9Khoma lakunja la zipindazo linali la mamita awiri ndi theka kuchindikira kwake. Pakati pa chiwundocho 10ndi zipinda za Nyumba ya Mulungu panali bwalo limeneli la mamita khumi kupingasa kwake kuzungulira Nyumba yonse ya Mulungu. 11Zitseko za zipinda zamʼmbalizo zinali zotsekulira ku chiwundo. Chitseko chimodzi chinkayangʼana kumpoto ndipo china chinkayangʼana kummwera. Chiwundo chosamangapo kanthu chinali mamita awiri ndi theka kukula kwake kuzungulira ponseponse.

12Nyumba imene inali chakummwera moyangʼanana ndi bwalo la Nyumba ya Mulungu inali mamita 35 mulifupi mwake. Khoma la nyumbayo linali mamita awiri ndi theka kuchindikira kwake kuzungulira ponseponse, ndipo mulitali mwake linali mamita 45.

13Ndipo munthuyo anayeza Nyumba ya Mulungu ndipo mulitali mwake inali mamita makumi asanu. Nyumbayo ndi makoma ake, zonse zinali za mamita makumi asanu. 14Kumaso kwa Nyumba ya Mulungu chakummawa kwa bwalolo mulifupi mwake munali mamita makumi asanu.

15Kenaka anayeza kutalika kwa nyumba yoyangʼanana ndi bwalo chakumadzulo kwa Nyumba ya Mulungu, kuphatikizapo njira zamʼkati ku mbali iliyonse. Kutalika kwake kunali mamita makumi asanu.

Chipinda chachikulu cha Nyumba ya Mulungu, chimene chili chamʼkati, khonde lamʼkati loyangʼanana ndi bwalo, 16mazenera ndi maferemu ake, zonsezi zinali zokutidwa ndi matabwa. Pamwamba moyangʼanana ndi chiwundo, Nyumba ya Mulungu inakutidwa ndi matabwa kuyambira pansi mpaka ku mazenera, (mazenerawo anali okutidwa), 17pamwamba pa khomo lolowera ku malo opatulika amʼkati komanso kuzungulira makoma onse kunja ndi mʼkati, 18anajambulapo zithunzi za kerubi mmodzi atakhala pakati pa kanjedza muwiri. Kerubi aliyense anali ndi nkhope ziwiri: 19imodzi inali nkhope ya munthu yoyangʼana kanjedza mbali imodzi, ndi ina inali nkhope ya mkango yoyangʼana kanjedza mbali ina. Zinajambulidwa kuzungulira Nyumba ya Mulungu yonse. 20Motero kuyambira pansi mpaka pamwamba pa khomo komanso pa makoma onse a chipinda chachikulu cha Nyumba ya Mulungu, anajambula zithunzi za akerubi ndi kanjedza pa makoma onse a malo opatulika.

21Mphuthu za chipinda chachikulu cha Nyumba ya Mulungu kutalika kwake mbali zonse kunali kofanana. Ndipo kumaso kwa malo opatulika kunali chinthu china chooneka ngati 22guwa lansembe la matabwa. Msinkhu wake unali mita imodzi ndi theka, mulitali mwake munali mita imodzi, mulifupi mwake munalinso mita imodzi. Mphuthu zake, tsinde lake ndi mbali zonse zinali za matabwa. Munthuyo anandiwuza kuti, “Tebulo limeneli ndilo limakhala pamaso pa Yehova.” 23Chipinda chachikulu chija chinali ndi zitseko ziwiri. Malo opatulika aja analinso ndi zitseko ziwiri. 24Chitseko chilichonse chinali ndi zigawo ziwiri zopatukana. 25Ndipo pa zitsekopo anajambulipo zithunzi za akerubi ndi kanjedza monga zomwe anajambulapo pa makoma. Kunja kwake kunali ngati denga lamatabwa pamwamba pa khonde lamʼkati. 26Pa mbali zonse za khonde lamʼkatilo panali mazenera, ndipo pa makoma ake onse anajambulapo zithunzi za kanjedza.

New International Version – UK

Ezekiel 41:1-26

1Then the man brought me to the main hall and measured the jambs; the width of the jambs was six cubits41:1 That is, about 3.2 metres; also in verses 3, 5 and 8 on each side.41:1 One Hebrew manuscript and Septuagint; most Hebrew manuscripts side, the width of the tent 2The entrance was ten cubits41:2 That is, about 5.3 metres wide, and the projecting walls on each side of it were five cubits41:2 That is, about 2.7 metres; also in verses 9, 11 and 12 wide. He also measured the main hall; it was forty cubits long and twenty cubits wide.41:2 That is, about 21 metres long and 11 metres wide

3Then he went into the inner sanctuary and measured the jambs of the entrance; each was two cubits41:3 That is, about 1.1 metres; also in verse 22 wide. The entrance was six cubits wide, and the projecting walls on each side of it were seven cubits41:3 That is, about 3.7 metres wide. 4And he measured the length of the inner sanctuary; it was twenty cubits, and its width was twenty cubits across the end of the main hall. He said to me, ‘This is the Most Holy Place.’

5Then he measured the wall of the temple; it was six cubits thick, and each side room round the temple was four cubits41:5 That is, about 2.1 metres wide. 6The side rooms were on three levels, one above another, thirty on each level. There were ledges all round the wall of the temple to serve as supports for the side rooms, so that the supports were not inserted into the wall of the temple. 7The side rooms all round the temple were wider at each successive level. The structure surrounding the temple was built in ascending stages, so that the rooms widened as one went upwards. A stairway went up from the lowest floor to the top floor through the middle floor.

8I saw that the temple had a raised base all round it, forming the foundation of the side rooms. It was the length of the rod, six long cubits. 9The outer wall of the side rooms was five cubits thick. The open area between the side rooms of the temple 10and the priests’ rooms was twenty cubits wide all round the temple. 11There were entrances to the side rooms from the open area, one on the north and another on the south; and the base adjoining the open area was five cubits wide all round.

12The building facing the temple courtyard on the west side was seventy cubits41:12 That is, about 37 metres wide. The wall of the building was five cubits thick all round, and its length was ninety cubits.41:12 That is, about 48 metres

13Then he measured the temple; it was a hundred cubits41:13 That is, about 53 metres; also in verses 14 and 15 long, and the temple courtyard and the building with its walls were also a hundred cubits long. 14The width of the temple courtyard on the east, including the front of the temple, was a hundred cubits.

15Then he measured the length of the building facing the courtyard at the rear of the temple, including its galleries on each side; it was a hundred cubits.

The main hall, the inner sanctuary and the portico facing the court, 16as well as the thresholds and the narrow windows and galleries round the three of them – everything beyond and including the threshold was covered with wood. The floor, the wall up to the windows, and the windows were covered. 17In the space above the outside of the entrance to the inner sanctuary and on the walls at regular intervals all round the inner and outer sanctuary 18were carved cherubim and palm trees. Palm trees alternated with cherubim. Each cherub had two faces: 19the face of a human being towards the palm tree on one side and the face of a lion towards the palm tree on the other. They were carved all round the whole temple. 20From the floor to the area above the entrance, cherubim and palm trees were carved on the wall of the main hall.

21The main hall had a rectangular door-frame, and the one at the front of the Most Holy Place was similar. 22There was a wooden altar three cubits41:22 That is, about 1.5 metres high and two cubits square41:22 Septuagint; Hebrew long; its corners, its base41:22 Septuagint; Hebrew length and its sides were of wood. The man said to me, ‘This is the table that is before the Lord.’ 23Both the main hall and the Most Holy Place had double doors. 24Each door had two leaves – two hinged leaves for each door. 25And on the doors of the main hall were carved cherubim and palm trees like those carved on the walls, and there was a wooden overhang on the front of the portico. 26On the side walls of the portico were narrow windows with palm trees carved on each side. The side rooms of the temple also had overhangs.