Ezekieli 2 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 2:1-10

Kuyitanidwa kwa Ezekieli

1Iye anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, imirira kuti ndiyankhule nawe.” 2Pamene ankayankhula nane, Mzimu wa Mulungu unalowa mwa ine ndipo unandiyimiritsa, ndipo ndinamva Iye akundiyankhula.

3Iye anati, “Iwe mwana wa munthu, Ine ndikukutuma kwa Aisraeli, mtundu wa anthu owukira umene wandiwukira Ine; Iwo ndi makolo awo akhala akundiwukira Ine mpaka lero lino. 4Ndikukutuma kwa anthu okanika ndiponso nkhutukumve. Ndikukutuma kuti akawawuze zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena. 5Kaya akamva kaya sakamvera, pakuti iwo ndi anthu opanduka, komabe adzadziwa kuti mneneri ali pakati pawo. 6Tsono iwe mwana wa munthu, usachite nawo mantha kapena kuopa zimene azikanena. Usachite mantha, ngakhale minga ndi mkandankhuku zikuzinge ndipo ukukhala pakati pa zinkhanira. Usachite mantha ndi zimene akunena kapena kuopsedwa ndi nkhope zawo, popeza anthuwa ndi awupandu. 7Ukawawuze ndithu mawu anga, kaya akamva kaya sakamva. Paja anthuwa ndi awupandu. 8Koma iwe mwana wa munthu, mvetsera zimene ndikukuwuza. Usakhale wowukira ngati iwowo. Tsono yasama pakamwa pako kuti udye chimene ndikukupatsa.”

9Nditayangʼana ndinangoona dzanja litaloza ine, litagwira mpukutu wolembedwa. 10Anawufunyulura pamaso panga. Mpukutu wonse unali wolembedwa kuseri nʼkuseri. Ndipo mawu amene analembedwa mʼmenemo anali a madandawulo, maliro ndi matemberero.

Persian Contemporary Bible

حزقيال 2:1-10

دعوت خدا از حزقيال

1او به من فرمود: «ای انسان خاكی، برخيز و بايست تا با تو سخن گويم.» 2هنگامی كه او با من تكلم می‌كرد، روح خدا داخل من شد و مرا برخيزاند. آنگاه آن صدا را باز شنيدم، 3كه به من گفت: «ای انسان خاكی، من تو را نزد بنی‌اسرائيل می‌فرستم، نزد قومی ياغی كه عليه من طغيان كرده‌اند. ايشان و پدرانشان همواره نسبت به من گناه ورزيده‌اند. 4آنان قومی هستند سنگدل و سركش، اما من تو را می‌فرستم تا كلام مرا به ايشان بيان نمايی. 5اين ياغيان چه بشنوند، چه نشنوند، اين را خواهند دانست كه در ميان آنها نبی‌ای وجود دارد.

6«ای انسان خاكی، از ايشان نترس! اگرچه تهديدهای اين قوم ياغی مانند خار و همچون نيش عقرب باشد، باكی نداشته باش! 7چه گوش بدهند، چه ندهند، تو كلام مرا به گوش آنها برسان و فراموش نكن كه ايشان، قومی ياغی و سركش هستند.

8«ای انسان خاكی، به آنچه كه به تو می‌گويم گوش كن و مانند ايشان ياغی نباش! دهانت را باز كن و هر چه به تو می‌دهم، بخور.»

9‏-10آنگاه نگاه كردم و ديدم دستی به طرف من آمد و طوماری با خود آورد. وقتی طومار را باز كرد، ديدم كه هر دو طرفش مطالبی نوشته شده، مطالبی كه حاكی از اندوه، ماتم و نابودی است.