Ezekieli 14 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 14:1-23

Yehova Adzudzula Opembedza Mafano

1Tsiku lina ena mwa akuluakulu a Israeli anabwera kwa ine ndipo anakhala pansi pamaso panga. 2Ndipo Yehova anandipatsa uthenga uwu nati, 3“Iwe mwana wa munthu, anthu awa ayika mtima pa mafano awo. Ayikanso maso awo pa zinthu zina zoyipa zopunthwitsa. Kodi ayembekezera kuti ndiwayankhe chimene atandifunse? 4Tsono yankhula nawo ndi kuwawuza kuti zimene akunena Ambuye Yehova: ‘Ngati Mwisraeli aliyense ayika mtima wake pa mafano ndi kuyika maso ake pa zinthu zoyipa zopunthwitsa, kenaka nʼkupita kwa mneneri, Ineyo Yehova mwini wakene ndidzamuyankha molingana ndi kuchuluka kwa mafano ake. 5Ine ndidzachita zimenezi kuti mwina nʼkukopa mitima ya anthu a Israeli, amene andisiya chifukwa cha mafano awo.’

6“Nʼchifukwa chake uwawuze Aisraeli kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: Lapani! Siyani mafano anu ndi ntchito zanu zonse zonyansa!

7“ ‘Ngati Mwisraeli wina aliyense kapena mlendo wina aliyense wokhala pakati pa Israeli adzichotsa yekha kwa Ine ndi kuyika mtima pa mafano ake ndi kuyikanso maso ake pa zinthu zopunthwitsa ndipo kenaka nʼkupita kwa mneneri kukafunsa nzeru, Ineyo Yehova mwini wakene ndidzamuyankha. 8Ine ndidzalimbana naye munthu ameneyo ndipo ndidzamusandutsa chitsanzo ndi chisudzo. Ndidzamuchotsa pakati pa anthu anga. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.

9“ ‘Ndipo ngati mneneri anyengedwa nanenera, Ine Yehova ndiye ndamunyenga mneneri ameneyo, ndipo ndidzatambasula dzanja langa kumukantha ndi kumuwononga pakati pa anthu anga Aisraeli. 10Iwo adzalangidwa chifukwa cha kulakwa kwawo. Chilango cha wodzafunsira nzeru kwa mneneri chidzafanana ndi chilango cha mneneriyo. 11Ndidzachita zimenezi kuti Aisraeli asasocherenso kundisiya Ine ndi kuti asadziyipitsenso ndi machimo awo. Adzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wawo, akutero Ambuye Yehova.’ ”

Chilango Chosathawika

12Yehova anayankhula nane kuti, 13“Iwe mwana wa munthu, ngati dziko lindichimwira posandikhulupirira, Ine ndidzatambasula dzanja langa kulikantha pochepetsa chakudya chake. Ndidzatumiza njala pa dzikolo ndi kuwononga anthu ake ndi nyama zomwe. 14Ngakhale anthu atatu awa, Nowa, Danieli ndi Yobu akanakhala mʼmenemo, akanangopulumutsa moyo wawo chifukwa cha chilungamo chawo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.

15“Kapena ndikanatumiza zirombo mʼdziko monse ndi kulisiya lopanda anthu, ndipo dzikolo nʼkukhala chipululu chakuti munthu sangadutse chifukwa cha zirombo. 16Apanso, ndikunenetsa Ine Ambuye Yehova kuti, ‘Ngakhale anthu atatu awa akanakhalamo, sakanatha kupulumutsa ana awo aamuna ndi aakazi. Iwo okha akanapulumuka, koma dziko likanasanduka chipululu.’

17“Kapena ndikanatumiza lupanga mʼdzikolo ndi kunena kuti, ‘Lupanga lipite mʼdziko monse,’ ndi kuwononga anthu ake ndi nyama zomwe. 18Apanso ndikunenetsa Ine Ambuye Yehova kuti, ‘Ngakhale anthu atatu awa akanakhalamo, sakanatha kupulumutsa ana awo aamuna kapena ana aakazi. Iwo okha akanapulumuka.’

19“Kapena ndikanatumiza mliri mʼdzikomo ndi kuonetsa ukali wanga pokhetsa magazi, kuwononga anthu ake ndi nyama zomwe. 20Apanso ndikunenetsa Ine Ambuye Yehova kuti ngakhale Nowa, Danieli ndi Yobu akanakhala mʼmenemo, sakanatha ngakhale kupulumutsa mwana wamwamuna kapena wamkazi. Akanangodzipulumutsa okha chifukwa cha chilungamo chawo.

21“Pakuti Ambuye Yehova akuti: Kudzakhala zoopsa kwambiri pamene ndidzatumiza pa Yerusalemu zilango zanga zinayi izi: lupanga, njala, zirombo ndi mliri kuti ziwononge anthu ake ndi nyama zomwe! 22Komabe padzakhala ena opulumuka, ana aamuna ndi ana aakazi amene adzatulutsidwa mʼdzikomo. Iwo adzabwera kwa inu, ndipo mukadzaona makhalidwe awo ndi zochita zawo, mitima yanu idzakhala pansi mukadzakumbukira chilango chimene ndinachita pa Yerusalemu. 23Mitima yanu idzakhala pansi mukadzaona makhalidwe awo ndi zochita zawo. Tsono mudzadziwa kuti Yerusalemu sindinamuchite zimenezi popanda chifukwa, akutero Ambuye Yehova.”

New Serbian Translation

Књига пророка Језекиља 14:1-23

Оправданост Божије казне

1Затим су дошли неки од израиљских старешина и сели пред мене. 2И дође ми реч Господња: 3„Сине човечији, ови људи носе идоле у свом срцу и стављају пред себе оно што их наводи на неправду. Зар да им одговорим на оно што ме питају? 4Зато им говори и реци им: ’Говори Господ Бог: сваки човек из израиљског дома, који у срцу носи своје идоле и пред себе ставља оно што га наводи на неправду, па дође к пророку, томе ћу ја, Господ, одговорити према мноштву његових идола, 5да задобијем срце дома Израиљевог које се отуђило од мене због свих њихових идола.’

6Стога, реци дому Израиљевом: ’Говори Господ Бог: покајте се! Одвратите се од својих идола и окрените леђа свим својим гадостима.

7Јер, ко год се од дома Израиљева и од странаца који пребивају у Израиљу одврати од мене и постави идола у свом срцу и стави пред себе оно што га наводи на неправду, а онда дође к пророку да тражи савет од мене, томе ћу ја, Господ лично одговорити. 8Окренућу своје лице према том човеку учинићу да буде опомена и поука; истребићу га из свог народа. Тада ћете знати да сам ја Господ.

9А ако би се пророк преварио, па саопштио какву поруку, то сам ја, Господ, завео тог пророка. Ја ћу, онда, испружити руку на њега и истребити га из свог народа Израиља. 10Обојица ће примити своју кривицу; кривица ће бити иста и за оног који тражи савет, и за пророка 11Тако дом Израиљев неће више одступати од мене, и неће се више скрнавити свим преступима. И биће мој народ, а ја ћу им бити Бог – говори Господ Бог.’“

Суд Јерусалима је неизбежан

12И дође ми реч Господња: 13„Сине човечији, када ми нека земља згреши тако што учини неверство, и ја дигнем руку на њу и пресечем јој снабдевање хлебом, па пошаљем на њу глад и истребим из ње и људе и стоку, 14чак и да су у њој ова тројица: Ноје, Данило и Јов, њихова би праведност спасла само њих – говори Господ Бог.

15Или, ако пустим на ту земљу дивље звери да их остављају без деце, па постане пустара где нико не пролази због звери, 16живота ми мога, чак и да су ова тројица у њој – говори Господ Бог – ни они не би могли да спасу своје синове и ћерке; само би се они спасли. А земља ће се претворити у пустару.

17Или, ако пустим мач на ту земљу и кажем: ’Мачу, прођи земљом и истреби из ње и људе и стоку’, 18чак и да су у њој и ова тројица, живота ми мога – говори Господ Бог – не би се спасли ни њихови синови и ћерке; само би се они спасли.

19Или, ако пошаљем заразу на ту земљу и излијем на њу свој гнев чинећи крвопролиће, да истребим из ње људе и стоку, 20чак и да су у њој и ова тројица: Ноје, Данило и Јов, живота ми мога – говори Господ Бог – не би се спасли ни њихови синови и ћерке; они сами би се спасли због своје праведности.

21Јер, говори Господ Бог: ’Чак и да пошаљем на Јерусалим своја четири страшна суда: мач, глад, дивље звери и заразу, да истребим из њега и људе и стоку, 22у њему ће, ипак, остати преживели; њихови синови и ћерке ће изаћи из њега. Када дођу к вама и кад видите њихове путеве и њихова дела, утешићете се за невоље које сам довео на Јерусалим, за све што сам довео на њега. 23Они ће вас утешити кад будете видели њихове путеве и њихова дела. Тада ћете знати да сам ја све то урадио – говори Господ Бог.’“