Ezekieli 1 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 1:1-28

Zolengedwa za Moyo ndi Ulemerero wa Yehova

1Tsiku lachisanu la mwezi wachinayi, chaka cha makumi atatu, ine ndinali pakati pa amʼndende mʼmbali mwa mtsinje wa Kebara. Tsono kumwamba kunatsekuka ndipo ndinaona maonekedwe a Mulungu mʼmasomphenya.

2Pa tsiku lachisanu la mwezi, chaka chachisanu Yehoyakini ali mʼndende, 3Yehova anayankhula ndi wansembe Ezekieli, mwana wa Buzi, mʼmbali mwa mtsinje wa Kebara mʼdziko la Ababuloni. Dzanja la Yehova linali pa iye kumeneko.

4Ndinayangʼana ndipo ndinangoona mphepo yamkuntho ikubwera kuchokera kumpoto. Panali mtambo waukulu wozunguliridwa ndi kuwala ndipo moto unali lawilawi kuchokera mu mtambowo. Pakati pa motowo pankaoneka ngati mkuwa wonyezimira. 5Mʼkatikati mwa motowo munali zinthu zinayi zamaonekedwe a nyama. Thupi lawo limaoneka ngati la munthu 6koma chilichonse chinali ndi nkhope zinayi ndiponso mapiko anayi. 7Miyendo yake inali yowongoka; mapazi ake anali a ziboda ngati phazi la mwana wangʼombe. Ndipo zibodazo zinkawala ngati mkuwa wonyezimira. 8Mʼmunsi mwa mapiko awo kumbali zonse zinayi, nyamazo zinali ndi manja a munthu. Zonse zinayi zinali ndi nkhope ndi mapiko, 9ndipo mapiko awowo anakhudzana. Chilichonse chimapita molunjika kutsogolo; sizimatembenuka pamene zimayenda.

10Nkhope zawo zimaoneka motere: Chilichonse chinali ndi nkhope ya munthu, ndipo mbali ya kumanja chilichonse chinali ndi nkhope zinayi zosiyana motere: nkhope ya munthu, nkhope ya mkango ku dzanja lamanja, nkhope ya ngʼombe ku dzanja lamanzere, ndipo kumbuyo kwake nkhope ya chiwombankhanga. 11Ndi mʼmene zinalili nkhope zawo. Mapiko awo anali otambasukira mmwamba. Chamoyo chilichonse chinali ndi mapiko awiri okhudzana ndi mapiko a chinzake. Chinalinso ndi mapiko ena awiri ophimbira thupi lake. 12Zamoyozo zinkayenda molunjika kutsogolo. Kulikonse kumene mzimu umazitsogolera kupita, nazonso zimapita kumeneko, osatembenuka pamene zikupita. 13Pakati pa zamayozo panali chinthu chooneka ngati makala oyaka kapena miyuni yoyaka. Moto umayendayenda pakati pa zamayozo; wowala kwambiri, ndipo mphenzi zimatuluka pakati pawo. 14Zamoyozo zinkathamanga uku ndi uko ngati kungʼanima kwa mphenzi.

15Pamene ndinali kuyangʼana zamoyozo, ndinangoona mikombero ndipo pansi pambali pa chamoyo chilichonse panali mkombero umodzi. 16Maonekedwe a mikomberoyo anali ngati mwala wonyezimira. Mikombero yonse inali yofanana ndipo mapangidwe awo anali ngati wongolowanalowana. 17Mikombero ija poyenda inkatha kupita mbali iliyonse yomwe zamoyozo zinayangʼana popanda kutembenuka. 18Marimu a mikomberoyo anali aatali ndi ochititsa mantha ndipo marimu onse anayi anali ndi maso ponseponse.

19Zamoyozo zinkati zikamayenda, mikomberoyo imayendanso mʼmbali mwake; ndipo zamoyozo zinkati zikamakwera mmwamba, mikomberoyo imakweranso. 20Kulikonse kumene mzimu wake unkazitsogolera, zamoyozo zinkapita komweko. Ndipo mikombero ija inkapita nawo pamodzi popeza kuti mzimu wa zamoyozo ndiwo umayendetsa mikombero ija. 21Zamoyo zija zinkati zikamayenda mikombero imayendanso. Zamoyozo zimati zikayima, nayonso mikombero inkayima. Zamoyozo zinkati zikawuluka, mikomberonso imawuluka nazo pamodzi chifukwa mzimu wa zamoyo zija ndiwo umayendetsa mikombero ija.

22Pamwamba pa mitu ya zamoyozo panali chinthu chonga thambo, lowala ndipo kunyezimira kwake ngati galasi loyangʼanitsa ku dzuwa, loyalidwa pamwamba pa mitu yake. 23Zamoyozo zinatambalitsa mapiko ake mʼmunsi mwa thambo lija, mapiko ake ena kumakhudzana, mapiko awiri kumaphimba thupi lake. 24Pamene zamoyo zimayenda ndimamva phokoso la mapiko ake, ngati mkokomo wa madzi ambiri, ngati liwu la Wamphamvuzonse, ngati phokoso la gulu lankhondo. Zimati zikayima zinkagwetsa mapiko ake.

25Ndipo panamveka mawu kuchokera pamwamba pa thambo la pa mitu ya zamoyo zija. Nthawi iyi nʼkuti zamoyozo zitayima ndi kugwetsa pansi mapiko ake. 26Pamwamba pa thambo la pa mitu yake panali chinthu chimene chimaoneka ngati mpando waufumu wopangidwa ndi mwala wa safiro, ndipo pamwamba pa mpando waufumuwo panali chinthu chooneka ngati munthu. 27Ndinaona kuti mmwamba mwa chiwuno chake munali ngati chitsulo chowala konsekonse ngati moto. Mʼmunsi mwa chiwuno chake munalinso ngati moto wokhawokha. Kuwala kwa mphamvu kunamuzungulira munthuyo. 28Kuwalako kunali ndi maonekedwe a utawaleza mʼmitambo tsiku limene kwagwa mvula.

Umu ndi mmene ulemerero wa Yehova umaonekera. Pamene ndinawuona ndinagwa pansi ndipo ndinamva mawu akundiyankhula.

New International Reader’s Version

Ezekiel 1:1-28

The Lord Gives Ezekiel Visions of His Glory

1I was 30 years old. I was with my people. We had been taken away from our country. We were by the Kebar River in the land of Babylon. On the fifth day of the fourth month, the heavens were opened. I saw visions of God.

2It was the fifth day of the month. Jehoiachin had been king of Judah. It was the fifth year since he had been brought to Babylon as a prisoner. 3A message from the Lord came to me. I was by the Kebar River in Babylon. The power of the Lord came on me there. I am Ezekiel the priest, the son of Buzi.

4I looked up and saw a windstorm coming from the north. I saw a huge cloud. The fire of lightning was flashing out of it. Bright light surrounded it. The center of the fire looked like glowing metal. 5I saw in the fire something that looked like four living creatures. They appeared to have the shape of a human being. 6But each of them had four faces and four wings. 7Their legs were straight. Their feet looked like the feet of a calf. They were as bright as polished bronze. 8The creatures had human hands under their wings on their four sides. All four of them had faces and wings. 9The wings of one touched the wings of another. Each of the creatures went straight ahead. They didn’t change their direction as they moved.

10Here’s what their faces looked like. Each of the four creatures had the face of a human being. On the right side each had the face of a lion. On the left each had the face of an ox. Each one also had an eagle’s face. 11That’s what their faces looked like. They each had two wings that spread out and lifted up. Each wing touched the wing of another creature on either side. They each had two other wings that covered their bodies. 12All the creatures went straight ahead. Anywhere their spirits would lead them to go, they would go. They didn’t change their direction as they went. 13The living creatures looked like burning coals of fire or like torches. Fire moved back and forth among the creatures. It was bright. Lightning flashed out of it. 14The creatures raced back and forth like flashes of lightning.

15As I looked at the living creatures, I saw wheels on the ground beside them. Each creature had four faces. 16Here’s how the wheels looked and worked. They gleamed like topaz. All four of them looked alike. Each one seemed to be made like a wheel inside another wheel at right angles. 17The wheels could go in any one of the four directions the creatures faced. The wheels didn’t change their direction as the creatures moved. 18Their rims were high and terrifying. All four rims were full of eyes all the way around them.

19When the living creatures moved, the wheels beside them moved. When the creatures rose from the ground, the wheels also rose. 20Anywhere their spirits would lead them to go, they would go. And the wheels would rise along with them. That’s because the spirits of the living creatures were in the wheels. 21When the living creatures moved, the wheels also moved. When the creatures stood still, they also stood still. When the creatures rose from the ground, the wheels rose along with them. That’s because the spirits of the living creatures were in the wheels.

22Something that looked like a huge space was spread out above the heads of the living creatures. It gleamed like crystal. It was terrifying. 23The wings of the creatures were spread out under the space. They reached out toward one another. Each creature had two wings covering its body. 24When the living creatures moved, I heard the sound of their wings. It was like the roar of rushing waters. It sounded like the thundering voice of the Mighty God. It was like the loud noise an army makes. When the creatures stood still, they lowered their wings.

25Then a voice came from above the huge space over their heads. They stood with their wings lowered. 26Above the space over their heads was something that looked like a throne made out of lapis lazuli. On the throne high above was a figure that appeared to be a man. 27From his waist up he looked like glowing metal that was full of fire. From his waist down he looked like fire. Bright light surrounded him. 28The glow around him looked like a rainbow in the clouds on a rainy day.

That’s what the glory of the Lord looked like. When I saw it, I fell with my face toward the ground. Then I heard the voice of someone speaking.