Ezara 4 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezara 4:1-24

Atsutsa za Kumanganso Nyumba ya Yehova

1Adani a Yuda ndi Benjamini anamva kuti anthu obwera ku ukapolo aja akumangira Nyumba Yehova, Mulungu wa Israeli. 2Tsono anapita kwa Zerubabeli ndi kwa atsogoleri a mabanja awo ndi kunena kuti, “Mutilole kuti tikuthandizeni kumangaku chifukwa ife timapembedza Mulungu wanu monga momwe mumachitira inu, ndipo takhala tikupereka nsembe kwa Iye kuyambira nthawi ya Esrahadoni, mfumu ya ku Asiriya, amene anabwera nafe kuno.”

3Koma Zerubabeli, Yesuwa ndi atsogoleri ena otsala a mabanja a Aisraeli anayankha kuti, “Inu simungatithandize kumangira Nyumba Yehova, Mulungu wathu. Tokha tidzamumangira Nyumba Yehova, Mulungu wa Aisraeli, monga mfumu Koresi, mfumu ya Perisiya inatilamulira.”

4Tsono anthu a mʼdzikomo anayamba kuchititsa ulesi anthu a ku Yuda, ndi kuwachititsa mantha kuti aleke ntchito yomangayo. 5Analemba alangizi ena kuti alepheretse cholinga chawo pa ntchitoyo pa nthawi yonse ya Koresi, mfumu ya ku Perisiya, ndiponso mpaka pamene Dariyo mfumu ya ku Perisiya ankalamulira dzikolo.

Kutsutsa Kwina pa Nthawi ya Ahasiwero ndi Aritasasita

6Mfumu Ahasiwero atangoyamba kulamulira dzikolo, adani aja analemba kalata yoneneza anthu a Yuda ndi Yerusalemu.

7Ndiponso mʼnthawi ya Aritasasita mfumu ya Perisiya, Bisilamu, Mitiredati, Tabeeli ndi anzawo ena analemba kalata inanso kwa Aritasasita. Kalatayo inalembedwa mʼChiaramu ndipo ankatanthauzira poyiwerenga.

8Rehumu mkulu wankhondo ndi Simisai mlembi, nawonso analemba kalata yawo yoneneza anthu a ku Yerusalemu kwa mfumu Aritasasita. Anayilemba motere:

9Kalata yochokera kwa Rehumu, mkulu wa gulu lankhondo, mlembi Simisai ndi anzawo awa: oweruza, nduna, akuluakulu ena, anthu a ku Peresiya, Ereki, Babuloni, Susa mʼdziko la Elamu, 10ndi mitundu ina imene mkulu wolemekezeka, Osanipara anayisamutsa ndi kuyikhazika mʼmizinda ya Samariya ndi mʼmadera ena apatsidya la Yufurate.

11Mawu a mʼkalata ya kwa Aritasasita anali awa:

Kwa mfumu Aritasasita:

Kuchokera kwa atumiki anu, anthu a kutsidya kwa Yufurate:

12Amfumu tati mudziwe kuti Ayuda amene anabwera kuno kuchokera kwanuko apita ku Yerusalemu ndipo akumanganso mzinda wa anthu owukira ndi oyipa uja. Akumaliza makoma ake ndipo akukonzanso maziko.

13Kuwonjeza apo amfumu mudziwe kuti ngati amalize kumanganso mzindawu ndi kukonzanso makoma ake, adzaleka kukhoma msonkho, kulipira ndalama zakatundu olowa mʼdziko kapena msonkho wina uliwonse, ndipo chuma cha thumba la ufumu chidzachepa. 14Popeza tsono ife timadya nawo kwa mfumu sitiyenera tizingoonerera zinthu zochititsa mfumu manyazi. Nʼchifukwa chake tikutumiza uthenga kwa inu a mfumu kuti mudziwe zonse. 15Choncho pachitike kafukufuku mʼbuku la mbiri yakale ya makolo anu. Mʼbuku la mbiri zakale mudzapezamo ndi kuwerenga kuti mzinda umenewu ndi waupandu, wosautsa mafumu ndi nduna zamʼmadera zomwe. Kuyambira kale wakhala ukuwukira ulamuliro uliwonse. Nʼchifukwa chake mzinda umenewu anawuwononga. 16Tsono tikukudziwitsani amfumu kuti ngati mzinda umenewu umangidwanso ndi makoma ake nʼkutsirizidwanso ndiye kuti inu simudzalamuliranso chigawo cha patsidya pa Yufurate.

17Mfumu inatumiza yankho ili:

Mkulu wa gulu lankhondo Rehumu, mlembi Simisai ndi anzanu onse amene akukhala ku Samariya ndi mʼzigawo zina zonse za Patsidya pa Yufurate.

Landirani moni.

18Kalata imene munatumiza ija yawerengedwa bwino lomwe pamaso panga. 19Ine nditalamula kuti afufuze nkhaniyi kwapezekadi kuti mzinda umenewu uli ndi mbiri yowukira mafumu ndi kuti zaupandu ndi zowukira zinkachitikadi mʼmenemo. 20Mafumu amphamvu akhala akulamulira Yerusalemu ndi chigawo chonse cha Patsidya pa Yufurate. Iwo ankalandira msonkho ndi kulipira ndalama zakatundu olowa mʼdziko pa kanthu kena kalikonse. 21Tsopano inu khazikitsani lamulo kuti anthu amenewo asiye ntchitoyo, asamangenso mzindawo mpaka ine nditalamula 22Musachedwe kuchita zimenezi. Kodi ine ndingalole bwanji kuti zowononga zotere zikule ndi kupweteka ine mfumu?

23Kalata ya mfumu Aritasasitayi itangowerengedwa pamaso pa Rehumu ndi Simisai mlembi uja, ndi anzawo onse, iwo anapita msangamsanga ku Yerusalemu kukawaletsa Ayuda aja mwamphamvu kuti asapitirire ntchito yawo.

24Motero ntchito yomanga Nyumba ya Mulungu ku Yerusalemu inayimitsidwa mpaka chaka cha chiwiri cha ulamuliro wa Dariyo mfumu ya ku Perisiya.

Persian Contemporary Bible

عزرا 4:1-24

مخالفت با بازسازی خانهٔ خدا

1وقتی دشمنان مردم يهودا و بنيامين شنيدند كه يهوديان تبعيد شده بازگشته‌اند و مشغول بازسازی خانهٔ خداوند، خدای اسرائيل هستند، 2نزد زروبابل و سران قوم آمدند و گفتند: «بگذاريد ما هم در بازسازی خانهٔ خدا با شما همكاری كنيم، چون ما هم مثل شما، خدای يگانه را می‌پرستيم. از وقتی كه اسرحدون، امپراتور آشور، ما را به اينجا آورده است هميشه برای خدای شما قربانی كرده‌ايم.»

3ولی زروبابل و يهوشع و ساير سران قوم يهود جواب دادند: «به شما اجازه نمی‌دهيم در اين كار شريک باشيد. خانهٔ خداوند، خدای اسرائيل، همانطور كه کوروش پادشاه پارس فرمان داده است، بايد به دست قوم اسرائيل ساخته شود.»

4پس ساكنان آنجا به تضعيف روحيهٔ يهوديان پرداخته، در كار بازسازی خانهٔ خدا موانع بسيار ايجاد كردند. 5در ضمن به برخی از مقامات رشوه دادند تا عليه آنها اقدام كنند. اين كارشكنيها در تمام دوران سلطنت کوروش وجود داشت و تا سلطنت داريوش ادامه يافت.4‏:5 دنبالهٔ اين مطلب را در آيه 24‏ بخوانيد. رويدادهايی که در آيات 6‏-23‏ آمده، حدود يک قرن بعد اتفاق افتاده است.‏

مخالفت با بازسازی اورشليم

6در آغاز سلطنت خشايارشا، دشمنان مردم يهودا و اورشليم شكايت‌نامه‌ای عليه آنها برای پادشاه، فرستادند.

7در دوران سلطنت اردشير نيز شكايت‌نامه‌ای عليه مردم يهودا و اورشليم نوشته شد. اين شكايت‌نامه را بشلام، ميتراداد، طبئيل و رفقای ايشان به خط و زبان ارامی4‏:7 از 4‏:8 تا 6‏:18 اين کتاب به زبان عبری نيست بلکه به آرامی است که زبان رسمی سرزمين پارس بود.‏ برای اردشير، پادشاه پارس نوشتند. 8‏-9كسان ديگری كه در نوشتن اين شكايت‌نامه بر ضد مردم يهودا و اورشليم دست داشتند عبارت بودند از: رحوم فرماندار، شمشائی کاتب، عده‌ای از قضات و مقامات ديگری كه از ارک، بابل و شوش (كه در عيلام است) بودند، 10و نيز عده‌ای از قومهای مختلف ديگر كه آشور بانيپال بزرگ و قدرتمند، آنها را از سرزمينهای خود بيرون آورده در سامره و ساير شهرهای غرب رود فرات اسكان داده بود.

11اين است متن نامه‌ای كه برای اردشير پادشاه پارس، فرستادند:

«ما بندگانت كه از ساكنان غرب رود فرات هستيم، 12پادشاه را آگاه می‌نماييم كه يهوديانی كه به فرمان شما به اورشليم منتقل شده‌اند، می‌خواهند اين شهر را كه محل شورش و آشوب بوده است بازسازی كنند. آنها مشغول ساختن حصار و تعمير پايه‌هايش هستند. 13پادشاه آگاه باشند كه اگر اين شهر و حصارهايش دوباره ساخته شود، بی‌گمان به زيان پادشاه خواهد بود، زيرا بعد از آن يهوديان ديگر به شما باج و خراج نخواهند داد. 14چون ما نان و نمک پادشاه را می‌خوريم، شايسته نيست كه زيان پادشاه را ببينيم. برای همين، نامه‌ای فرستاديم تا پادشاه را از اين ماجرا آگاه سازيم. 15استدعا داريم دستور فرماييد در اين مورد كتاب تاريخ نياكانتان را بررسی نمايند تا معلوم گردد كه در قرون گذشته در اين شهر چه شورشهايی بر پا گشته است. در حقيقت اين شهر به سبب آن خراب شده است كه ساكنان آن بر ضد پادشاهان و حكامی كه می‌خواستند بر آن حكومت كنند، مدام شورش می‌كردند. 16پس پادشاه را آگاه می‌سازيم كه اگر اين شهر و حصارهايش ساخته شوند، پادشاه، ديگر قادر به نگهداری اين قسمت از قلمرو خويش كه در غرب رود فرات است، نخواهند بود.»

17‏-18پس پادشاه به رحوم فرماندار و شمشائی کاتب و همدستان ايشان كه در سامره و نواحی غرب رود فرات ساكن بودند، چنين جواب داد:

«درود بر شما! نامه‌ای كه فرستاده بوديد رسيد و پس از ترجمه برای من خوانده شد. 19دستور دادم تحقيق و بررسی كنند. معلوم شد كه ساكنان اين شهر از ديرباز هميشه عليه پادشاهان شورش و آشوب بر پا كرده‌اند. 20همچنين فهميدم كه پادشاهانی قدرتمند در اورشليم بوده‌اند كه بر سراسر غرب رود فرات فرمانروايی می‌كردند، و جزيه و باج و خراج می‌گرفتند. 21بنابراين، به اين مردان دستور بدهيد دست نگه دارند و تا فرمانی از جانب من صادر نشود شهر را بازسازی نكنند. 22فوری اقدام كنيد و جلو اين فتنه را بگيريد.»

23وقتی نامهٔ اردشير، پادشاه پارس، برای رحوم و شمشائی و همدستان ايشان خوانده شد، آنها با عجله به اورشليم رفتند و يهوديان را به زور مجبور كردند دست از كار بكشند.

بازسازی خانهٔ خدا دوباره شروع می‌شود

24كار بازسازی خانه خدا تا سال دوم سلطنت داريوش، پادشاه پارس متوقف مانده بود.