Eksodo 35 – CCL & OL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Eksodo 35:1-35

Malamulo Osunga Sabata

1Mose anasonkhanitsa gulu lonse la Aisraeli ndipo anawawuza kuti, “Zinthu zimene Yehova wakulamulirani kuti muzichite ndi izi: 2Muzigwira ntchito zanu pa masiku asanu ndi limodzi, koma tsiku la chisanu ndi chiwiri likhale la Sabata, tsiku lanu lopuma, lopatulika kwa Yehova. Aliyense amene adzagwira ntchito iliyonse pa tsikuli ayenera kuphedwa. 3Pa tsiku la Sabata musakoleze moto paliponse pamene mukhala.”

Zopereka ku Malo Opatulika

4Mose ananena kwa gulu lonse la Aisraeli kuti, “Zimene Yehova wakulamulirani ndi izi: 5Kuchokera pa zomwe muli nazo, mutenge chopereka cha Yehova. Aliyense amene ali ndi mtima wofuna kupereka abweretse kwa Yehova zopereka izi: Golide, siliva ndi mkuwa; 6nsalu zobiriwira, zapepo, zofiira, nsalu zofewa; ubweya wambuzi; 7zikopa za nkhosa zazimuna za utoto wofiira ndi zikopa za akatumbu; matabwa amtengo wa mkesha, 8mafuta anyale a olivi, zonunkhiritsa mafuta odzozera ndi zopangira lubani wonunkhira; 9miyala yokongola ya mtundu wa onikisi ndi ina yabwino yoyika pa Efodi ndi pa chovala cha pachifuwa.

10“Anthu onse aluso pakati panu abwere ndi kupanga zonse zimene Yehova walamula: 11Chihema ndi tenti yake ndiponso chophimba chake, ngowe zake, maferemu ake, mitanda yake, mizati yake ndi matsinde ake; 12Bokosi la Chipangano pamodzi ndi mitengo yake yonyamulira ndiponso chovundikira chake cha bokosilo ndi nsalu zophimba bokosilo; 13tebulo pamodzi ndi mitengo yake yonyamulira pamodzi ndi zipangizo zake zonse ndiponso buledi wokhala pamaso pa Yehova; 14choyikapo nyale yowunikira pamodzi ndi zipangizo zake, nyale ndi mafuta anyalezo; 15guwa lofukizira lubani pamodzi ndi mitengo yake yonyamulira, mafuta odzozera ndi lubani onunkhira; nsalu yotchinga pa khomo lolowera mʼchihema; 16guwa lansembe yopsereza pamodzi ndi sefa yamkuwa, mitengo yake yonyamulira ndi zipangizo zake zonse, beseni losambira lamkuwa ndi miyendo yake; 17nsalu yotchingira bwalo pamodzi ndi mizati yake ndi matsinde ake, ndiponso nsalu yotchingira pa khomo lolowera ku bwalo; 18zikhomo za tenti ya chihema ndiponso za bwalo, ndi zingwe zake; 19zovala zolukidwa zovala potumikira kumalo opatulika, zovala zopatulika za wansembe, Aaroni pamodzi ndi za ana ake aamuna pamene akutumikira monga ansembe.”

20Kenaka gulu lonse la Aisraeli linachoka pamaso pa Mose, 21ndipo aliyense amene anakhudzidwa mu mtima mwake nafuna kupereka, anabwera kudzapereka chopereka kwa Yehova cha ntchito yokonza tenti ya msonkhano, cha ntchito zonse za mʼtentimo ndi cha zovala zopatulika. 22Onse amene anali ndi mtima wofuna, amuna ndi amayi omwe anabwera kudzapereka zodzikometsera zagolide za mtundu uliwonse: zomangira zovala, ndolo, mphete ndi zokometsera. Onse anapereka golide wawo monga nsembe yoweyula pamaso pa Yehova. 23Aliyense amene anali ndi nsalu ya mtundu wa mtambo, yapepo kapena yofiira kapena yofewa, yosalala, kapena ubweya wambuzi, zikopa za nkhosa zonyika mu utoto wofiira kapena zikopa anazibweretsa. 24Onse amene anapereka chopereka cha siliva kapena mkuwa anabweretsa monga chopereka kwa Yehova. Ndipo aliyense amene anali ndi matabwa a mtengo wa mkesha kuti awagwiritse ntchito mbali ina iliyonse ya ntchitoyo, anabweretsa. 25Mayi aliyense waluso analuka ndi manja ake ndi kubweretsa chomwe analuka cha mtundu wa mtambo, chapepo kapena chofiira kapena chofewa, chosalala. 26Ndipo amayi onse amene anali ndi mtima wofuna ndipo anali ndi luso analuka ubweya wa mbuzi. 27Atsogoleri anabweretsa miyala ya onikisi ndi miyala yokongola yoyika pa efodi ndi chovala chapachifuwa. 28Anabweretsanso zonunkhiritsa ndiponso mafuta owunikira a olivi ndi odzozera ndi zofukizira zonunkhira. 29Aisraeli onse aamuna ndi aakazi amene anali ndi mtima wofuna, anabweretsa kwa Yehova chopereka chaufulu ku ntchito yonse ya Yehova imene analamulira kudzera mwa Mose kuti achite.

Bezaleli ndi Oholiabu

30Kenaka Mose anati kwa Aisraeli, “Taonani, Yehova wasankha Bezaleli mwana wa Uri, mwana wa Huri, wa fuko la Yuda, 31ndipo wamudzaza ndi Mzimu wa Mulungu kotero kuti ali ndi luso ndi nzeru zomvetsa zinthu, ndipo akudziwa bwino ntchito zonse zamanja monga izi: 32Kulemba ndondomeko ya ntchito zaluso ndi kupanga zinthu zagolide, zasiliva ndi zamkuwa, 33kusema ndi kuyika miyala yokongola, kukonza zinthu zamatabwa ndiponso kugwira ntchito ina iliyonse yamanja. 34Ndipo Iye wapereka kwa Bezaleli pamodzi ndi Oholiabu mwana wa Ahisamaki, wa fuko la Dani luso lophunzitsa ena. 35Mulungu wawapatsa maluso osiyanasiyana, maluso ogoba, olemba ndondomeko, opeta zokometsera pa nsalu zamtundu wamtambo, zapepo ndi zofiira ndiponso zofewa zosalala ndi zoluka. Onsewa ndi amisiri a ntchito zamanja ndi zokonza ndondomeko.

O Livro

Êxodo 35:1-35

As instruções sobre o sábado

1Moisés convocou todo o povo de Israel e disse-lhes: “Estas são as leis do Senhor a que devem obedecer.

2Trabalharão apenas seis dias. O sétimo é um dia de solene repouso, um dia santo. Todo aquele que trabalhar nesse dia deverá morrer. 3Nem sequer acendam o fogo nas vossas casas nesse dia.”

Ofertas para o tabernáculo

(Êx 25.1-9; 39.32-43)

4E continuou: “Isto é o que o Senhor vos ordenou: 5Todos os que tiverem um coração generoso podem trazer, se assim o desejarem, estas ofertas ao Senhor:

ouro, prata, bronze;

6tecido azul, púrpura e vermelho, feito de linho fino retorcido ou de pelo de cabra;

7peles de carneiro tingidas de vermelho e curtidas, assim como, especialmente, peles de couro fino; madeira de acácia;

8azeite para os candeeiros; especiarias para o óleo da unção e para o incenso aromático;

9pedras de ónix, e pedras para serem usadas no éfode e no peitoral.

10Que todos aqueles que são habilidosos no trabalho manual, e os que têm talentos especiais, venham para construir o que o Senhor mandou:

11o tabernáculo, as suas cobertas, colchetes, tábuas, barras, colunas e bases;

12a arca e as varas de transporte; o propiciatório; o véu para separar o lugar santo;

13a mesa e as varas para transportá-la, assim como os seus utensílios; o pão da Presença,

14o candelabro, com as lâmpadas e o óleo respetivo;

15o altar do incenso e as varas de transporte; o óleo da unção e o incenso aromático; o véu da porta do tabernáculo;

16o altar dos holocaustos; as grelhas de bronze para o altar e as suas respetivas varas e utensílios; a bacia e a sua base;

17os véus das divisórias do pátio e as suas colunas e bases; os véus da entrada do pátio;

18as estacas do pátio do tabernáculo mais as suas cordas;

19os fatos dos sacerdotes, para usarem no ministério do lugar santo; as vestimentas santas para Aarão e os seus filhos.”

20Todo o povo saiu da presença de Moisés e foi para as tendas preparar estes donativos, 21e todos aqueles que sentiram boa vontade e coração generoso foram levar a sua oferta ao Senhor para a construção da tenda do encontro, bem como para as vestimentas sagradas. 22Tanto homens como mulheres, vieram todos aqueles que dispuseram o seu coração para tal. Assim trouxeram ao Senhor ofertas de ouro, pedras preciosas, brincos, anéis e colares e toda a espécie de objetos em ouro, com um gesto de apresentação cerimonial. 23Outros trouxeram tecidos de linho fino retorcido, ou pelos de cabra, em azul, púrpura e vermelho, assim como peles de carneiro tingidas de vermelho, especialmente peles de couro fino. 24Outros ainda trouxeram prata e bronze como oferta para o Senhor. Por fim houve quem trouxesse madeira de acácia necessária para a construção.

25As mulheres hábeis a fiar e coser trouxeram já preparado fio e tecido, e linho fino retorcido em azul, púrpura e vermelho. 26Outras usaram com alegria os seus dons especiais para fiar e fazer tecido de pelo de cabra. 27Os chefes trouxeram pedras de ónix para serem postas no éfode e no peitoral, 28assim como especiarias e óleo, tanto para as luzes, como para a composição do óleo da unção e do incenso aromático. 29E foi desta maneira que o povo de Israel, todos os homens e mulheres que quiseram colaborar na obra que lhes foi dada por mandamento do Senhor a Moisés, trouxeram de livre vontade as suas ofertas ao Senhor.

Os chefes do projeto

(Êx 31.1-11)

30E Moisés disse-lhes: “O Senhor designou especialmente Bezalel, filho de Uri e neto de Hur, da tribo de Judá, como superintendente-geral deste santo projeto. 31O Espírito de Deus encheu-o de sabedoria, capacidade e conhecimentos para a construção do tabernáculo e de tudo o que deve conter. 32Ele está, pois, altamente dotado como artista e desenhador de todas as peças feitas em ouro, prata e bronze. 33Será capaz de trabalhar pedras preciosas e tal como um joalheiro fará também belas gravações. Na verdade é um homem dotado para tudo.

34Deus também dispôs o coração dele e de Aoliabe para ensinarem a outros aquilo que sabem. Aoliabe é filho de Aisamaque da tribo de Dan. 35Deus encheu-os a ambos com um talento pouco vulgar para serem joalheiros, carpinteiros, bordadores em linho e tecidos de azul, púrpura e vermelho, e ainda tecelãos. Eles serão excelentes em todas as tarefas que é preciso executar para esta obra.