Eksodo 34 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Eksodo 34:1-35

Miyala ina Yatsopano

1Yehova anati kwa Mose, “Sema miyala iwiri yofanana ndi yoyamba ija, ndipo Ine ndidzalembapo mawu amene anali pa miyala yoyamba ija, imene unayiphwanya. 2Ukonzeke mmamawa, ndipo ubwere ku Phiri la Sinai. Udzaonekera pamaso panga pamwamba pa phiri. 3Palibe amene abwere nawe kapena kuoneka pena paliponse pafupi ndi phiri. Ndipo ngakhale nkhosa kapena ngʼombe zisadye mʼmbali mwa phirilo.”

4Choncho Mose anasema miyala iwiri yofanana ndi yoyamba ija ndipo anapita ku Phiri la Sinai mmawa atanyamula miyala iwiri mʼmanja mwake monga momwe Yehova anamulamulira. 5Ndipo Yehova anatsika mu mtambo ndi kuyima pamodzi ndi Mose ndi kulengeza dzina lake lakuti Yehova. 6Ndipo Iye anadutsa kutsogolo kwa Mose akulengeza kuti, “Yehova, Yehova, Mulungu wachifundo ndi wokoma mtima, wosapsa mtima msanga, wodzaza ndi chikondi chosasinthika ndi kukhulupirika, 7waonetsa chikondi chosasinthika kwa anthu miyandamiyanda, wokhululukira zoyipa, kuwukira, ndiponso tchimo, komatu salekerera ochimwa kuti asalangidwe. Iye amalanga ana ndi zidzukulu chifukwa cha machimo a makolo awo mpaka mʼbado wachitatu ndi wachinayi.”

8Pamenepo Mose anawerama pansi napembedza. 9Iye anati, “Chonde Ambuye, ngati ndapeza chisomo pamaso panu, lolani Ambuye kuti mupite nafe pamodzi. Ngakhale kuti anthuwa ndi nkhutukumve, khululukirani zoyipa ndi machimo athu, ndipo mutenge ife kukhala anthu anu.”

10Choncho Yehova anati: “Ine ndikuchita nanu pangano. Ndidzachita zodabwitsa pamaso pa anthu onse zimene sizinachitikenso ndi mtundu wina uliwonse wa anthu pa dziko lonse lapansi. Anthu amene mudzakhala pakati pawo adzaona kuopsa kwa ntchito imene Ine Yehova ndidzakuchitireni. 11Mverani zimene ndikukulamulirani lero. Ine ndidzathamangitsa pamaso panu Aamori, Akanaani, Ahiti, Aperezi, Ahivi, ndi Ayebusi. 12Musamale kuti musakachite mgwirizano ndi anthu amene akukhala mʼdziko limene mukupitalo, chifukwa mukadzatero iwo adzakhala ngati msampha pakati panu. 13Mukagumule maguwa awo ansembe, mukaswe miyala yawo yachipembedzo, ndipo mukadule mitengo yawo ya Asera. 14Musapembedze mulungu wina, pakuti Yehova amene dzina lake ndi Nsanje, ndi Mulungu wa nsanje.

15“Musamale kuti musakachite mgwirizano ndi anthu amene akukhala mʼdziko limene mukupitalo, chifukwa iwo akamakachita zadama ndi milungu yawo ndi kupereka nsembe, adzakuyitanani ndipo inu mudzadya nsembe zawo. 16Ndipo inu mukasankha ena mwa ana awo aakazi kukhala akazi a ana anu, akaziwo akakachita zadama ndi milungu yawo, akatsogolera ana anu aamuna kuchita chimodzimodzi.

17“Musadzipangire milungu yosungunula.

18“Muzichita chikondwerero cha buledi wopanda yisiti. Kwa masiku asanu ndi awiri muzidya buledi wopanda yisiti monga momwe ndinakulamulirani. Muzichita zimenezi pa nthawi yoyikika mwezi wa Abibu, pakuti mwezi umenewu inu munatuluka mʼdziko la Igupto.

19“Mwana aliyense woyamba kubadwa ndi wanga, pamodzi ndi ziweto zoyamba kubadwa zazimuna kuchokera ku ngʼombe kapena nkhosa. 20Muziwombola mwana woyamba kubadwa wa bulu popereka mwana wankhosa. Mukapanda kumuwombola mupheni. Muziwombola ana anu onse aamuna.

“Palibe ndi mmodzi yemwe adzaonekere pamaso panga wopanda kanthu mʼdzanja lake.

21“Muzigwira ntchito masiku asanu ndi limodzi, koma tsiku lachisanu ndi chiwiri, musagwire ntchito ina iliyonse, Ngakhale nthawi yolima ndi yokolola muyenera kupuma.

22“Muzichita Chikondwerero cha Masabata, chifukwa ndi chikondwerero cha tirigu woyambirira kucha, ndiponso ndi chikondwerero cha kututa zokolola pakutha pa chaka. 23Amuna onse azionekera pamaso pa Yehova Mulungu wa Israeli, katatu pa chaka. 24Ine ndidzapirikitsa mitundu inayo pamene inu mukufikako ndi kukulitsa malire anu. Palibe ndi mmodzi yemwe adzafune kulanda dziko lanu ngati inu muzidzapita katatu pa chaka pamaso pa Yehova Mulungu wanu, chaka chilichonse.

25“Musapereke magazi anyama ngati nsembe kwa Ine pamodzi ndi chilichonse chimene chili ndi yisiti, ndipo musasunge nsembe ya pa Chikondwerero cha Paska mpaka mmawa.

26“Muzibwera ndi zipatso zoyambirira kucha zabwino kwambiri ku nyumba ya Yehova Mulungu wanu.

“Musamaphike kamwana kambuzi mu mkaka wa mayi wake.”

27Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Lemba mawu awa pakuti potsatira mawuwa, ine ndipangana pangano ndi iwe ndi Israeli.” 28Mose anakhala kumeneko pamodzi ndi Yehova masiku 40, usana ndi usiku, wosadya kanthu kapena kumwa madzi. Ndipo iye analemba pa miyala ija mawu a pangano, malamulo khumi.

Nkhope ya Mose Inyezimira

29Mose anatsika kuchokera mʼPhiri la Sinai pamodzi ndi miyala iwiri ija ya pangano mʼmanja mwake. Iye sanazindikire kuti nkhope yake imanyezimira pakuti anayankhula ndi Yehova. 30Aaroni ndi Aisraeli ataona kuti nkhope ya Mose imanyezimira anaopa kumuyandikira. 31Koma Mose anawayitana. Kotero Aaroni ndi atsogoleri onse a gululo anabwera kwa iye, ndipo anawayankhula. 32Kenaka Aisraeli onse anamuyandikira, ndipo anawapatsa malamulo onse omwe Yehova anamupatsa pa Phiri la Sinai.

33Mose atamaliza kuyankhula nawo anaphimba nkhope yake. 34Koma nthawi zonse popita pamaso pa Yehova kukayankhula naye amachotsa chophimbacho mpaka atatuluka. Ndipo akatuluka kudzawuza Aisraeli zimene walamulidwa, 35iwo amaona nkhope yake ikunyezimira. Choncho Mose amaphimba nkhope yake ngakhale pamene amapita kukayankhula ndi Yehova.

New Serbian Translation

2. Мојсијева 34:1-35

Нове плоче Закона

1Господ рече Мојсију: „Исклеши себи две камене плоче као што су биле оне прве, а ја ћу на њима исписати исте речи које су биле написане на првим плочама које си разбио. 2Буди готов до јутра, а ујутро се успни на гору Синај и стани тамо, на врху горе, пред мене. 3Нека се нико не пење с тобом; нико не сме да се појави на целој гори. Ни овце ни говеда нека не пасу пред гором.“

4Мојсије је исклесао две камене плоче као што су биле пређашње, па се ујутро попео на гору Синај носећи у рукама две камене плоче, како му је Господ заповедио. 5Тада је Господ сишао у облаку, стао код Мојсија и изговорио своје име: „Господ!“ 6Господ је прошао покрај њега и изговорио своје име: „Господ! Господ! Бог милостиви и милосрдни, спор на срџбу, богат милошћу и верношћу, 7исказује милост хиљадама, опрашта кривицу, преступ и грех, али кривца не оставља некажњена, него кажњава грех отаца на њиховој деци и унуцима све до трећег и четвртог колена.“

8Мојсије одмах паде на земљу и поклони се Господу. 9Мојсије рече: „Ако сам стекао наклоност пред тобом, молим те, Господе, да пођеш са нама. Иако је овај народ тврдоврат, опрости нам кривицу и грехе, па нас прихвати као своју баштину.“

10Господ на то рече: „Ево, склапам савез: учинићу таква чуда пред твојим народом каква никада нису била учињена ни у којој земљи, ни у којем народу. Тада ће сваки народ усред кога боравиш видети шта Господ чини, јер оно што ћу учинити за тебе, биће страшно. 11Држи све што ти заповедам данас. Ево, ја ћу протерати пред тобом Аморејце, Хананце, Хетите, Фережане, Евејце и Јевусејце. 12Чувај се да не склопиш савез са становништвом земље у коју улазиш, да не постану замка у твојој средини. 13Него, порушите њихове жртвенике, оборите њихове стубове и посеците Аштартине стубове. 14Не служите ни једном другом богу! Господ је на гласу по својој љубомори, јер је он љубоморни Бог.

15Не склапај савез са становницима оне земље! Јер, када буду блудничили са својим боговима и приносили им жртве, позиваће и тебе, те ћеш јести од њихових жртава, 16и узимати својим синовима њихове ћерке. Онда ће оне, када буду блудничиле са својим боговима, навести и твоје синове на блуд са својим боговима.

17Не изливај себи ливене идоле.

18Одржавај празник Бесквасних хлебова. Седам дана једи бесквасне хлебове, како сам ти заповедио – у одређено време у месецу авиву, јер си у том месецу изашао из Египта.

19Сваки првенац мајчине утробе мени припада, као и свака првина од твоје ситне и крупне стоке. 20Првину магарца откупи јагњетом, а ако га не откупиш, заврни му врат. Откупи сваког првенца од својих синова.

Не појављујте се преда мном празних руку!

21Шест дана ради, а седмога отпочини; мораш отпочинути чак и за време орања или жетве.

22Слави празник Седмица – првих снопова пшеничне жетве и празник Бербе при крају године. 23Трипут годишње нека се сви твоји мушки појаве пред Господом, Богом Израиљевим. 24Ја ћу, наиме, изгнати народе пред тобом и проширити твоје границе, тако да нико неће жудети за твојом земљом кад трипут годишње будеш ишао да се појавиш пред Господом, Богом својим.

25Не приноси ми крв жртве са квасцем, нити остављај жртву принесену за празник Пасхе до јутра.

26Најбоље првине своје земље донеси у дом Господа, свога Бога.

Не кувај јаре у млеку његове мајке.“

27Господ рече Мојсију: „Напиши ове речи које сам ти рекао, јер сам на основу ових речи склопио савез са тобом и са Израиљем.“ 28Мојсије је провео са Господом четрдесет дана и четрдесет ноћи током којих није јео хлеба нити пио воде. Тада је на плочама написао речи савеза – десет заповести.

Мојсијево лице сјаји

29Мојсије је сишао са горе Синај. Док је силазио са горе носећи у рукама две плоче Сведочанства, није знао да му се лице сјаји због разговора са Господом. 30Када су Арон и Израиљци видели да му се лице сјаји, плашили су се да му приђу. 31Мојсије их је позвао, па су се вратили к њему Арон и сви кнезови заједнице. Тада је Мојсије разговарао са њима. 32Затим су му пришли и сви Израиљци, а он им је пренео све речи које му је Господ рекао на гори Синај.

33Кад је Мојсије завршио разговор са њима, покрио је себи лице велом. 34Кад год је Мојсије улазио пред Господа да разговара са њим, скидао би вео све док не изађе. Кад би изашао и пренео Израиљцима што му је Господ заповедио, 35они би видели да се Мојсијево лице сјаји. Тада би Мојсије враћао вео на своје лице, све док не уђе да разговара са Господом.