Eksodo 22 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Eksodo 22:1-31

Za Kuteteza Katundu

1“Ngati munthu aba ngʼombe kapena nkhosa ndi kuyipha kapena kuyigulitsa, iye abweze ngʼombe zisanu pa ngʼombe imodzi ndi nkhosa zinayi pa nkhosa imodzi.

2“Ngati mbala ipezeka ikuthyola nyumba ndipo imenyedwa nʼkufa, amene wapha mbalayo sanalakwe. 3Koma akayipha dzuwa litatuluka, woyiphayo ali ndi mlandu wakupha.

“Mbala iyenera kubweza ndithu koma ngati ilibe kalikonse igulitsidwe, kulipira zomwe yabazo.

4“Ngati chiweto chobedwacho chipezeka chamoyo mʼmanja mwake, kaya ndi ngʼombe kapena bulu kapena nkhosa, mbalayo ibwezere ziweto ziwiri pa chiweto chobedwacho.

5“Ngati munthu alekerera ziweto zake kukalowa mʼmunda wa munthu wina kukadya mbewu zake, munthuyo amubwezere mwini mundawo mbewu zina zabwino kapena mpesa wina wabwino kwambiri.

6“Ngati munthu ayatsa moto, motowo ndikukafika mpaka ku munda ndi kuwotcha mulu wa tirigu kapena tirigu wosadula, kapena munda wonse, ndiye kuti munthu amene anayatsa motoyo alipire.

7“Ngati munthu asungitsidwa ndi mnzake ndalama kapena katundu, ndipo zinthu zija nʼkubedwa mʼnyumba mwake, wakubayo ngati agwidwa, ayenera kubwezera kawiri chobedwacho. 8Koma ngati mbalayo sipezeka, mwini nyumbayo ayenera kukaonekera ku bwalo lamilandu kuti akamve ngati anaba katundu wa mnzakeyo. 9Ngati pali kukangana kokhudza ngʼombe, bulu, nkhosa, zovala kapena kanthu kalikonse kotayika, ndipo mmodzi ndikunena kuti chinthucho nʼchake, awiriwo abwere nawo mlandu wawowo pamaso pa Mulungu ndipo amene mlandu umugomere adzayenera kumulipira mnzakeyo kawiri.

10“Ngati munthu wina anasungitsa mnzake bulu, ngʼombe, nkhosa, kapena chiweto chilichonse ndipo chiweto chija nʼkufa kapena kupweteka kapena kutengedwa popanda wina kuona, 11ndiye kuti anthu awiriwo ayenera kulumbira pamaso pa Mulungu kuti asatenge chinthu cha mnzake. Zikatero mwini katundu uja avomereze zimenezi ndipo asabwezeredwe kanthu. 12Koma ngati chiwetocho chinabedwa, iye ayenera kubwezera mwini wakeyo. 13Ngati chinagwidwa ndi zirombo, iye ayenera kubweretsa zotsalira ngati umboni ndipo sadzalipira kanthu.

14“Ngati munthu abwereka chiweto cha mnzake ndipo chiweto chija nʼkuvulala kapena kufa chikanali ndi iyebe, wobwerekayo ayenera kulipira. 15Koma ngati mwini wakeyo ali ndi chiwetocho, wobwerekayo sadzalipira. Ngati anapereka ndalama pobwereka chiwetocho, ndalama anaperekazo zilowa mʼmalo mwa chiweto chakufacho.

Malamulo a Kakhalidwe ka Anthu

16“Ngati munthu anyenga namwali wosadziwa mwamuna amene sanapalidwe ubwenzi ndi kugona naye, munthuyo ayenera kulipira malowolo ndipo adzakhala mkazi wake. 17Ngati abambo ake akanitsitsa kwamtuwagalu kumupereka kuti amukwatire, munthuyo aperekebe malowolo woyenera namwaliyo.

18“Musayilole mfiti yayikazi kuti ikhale ndi moyo.

19“Aliyense wogonana ndi chiweto ayenera kuphedwa.

20“Aliyense wopereka nsembe kwa mulungu wina osati Yehova awonongedwe.

21“Musazunze mlendo kapena kumuchitira nkhanza, pakuti inu munali alendo mʼdziko la Igupto.

22“Musazunze mkazi wamasiye kapena mwana wamasiye. 23Ngati muwazunza ndipo iwo nʼkulirira kwa Ine, ndidzamva kulira kwawo. 24Ine ndidzakukwiyirani ndipo ndidzakuphani ndi lupanga. Akazi anu adzakhala amasiye ndiponso ana anu adzakhala wopanda abambo.

25“Ngati mukongoza ndalama kwa mʼbale wanu amene ndi mʼmphawi pakati panu, musadzamuchite monga zimene amachita wokongoza ndalama. Musadzamuyikire chiwongoladzanja. 26Mukatenga chovala cha mnzanu kuti chikhale chikole mumubwezere dzuwa lisanalowe 27chifukwa chovala chimene amadzifundira nacho nʼchomwecho. Nanga usiku adzafunda chiyani? Tsonotu ngati adzandilirira, Ine ndidzamva pakuti ndine wachifundo.

28“Musachite chipongwe Mulungu wanu kapena kutemberera mtsogoleri wa anthu anu.

29“Musachedwe kupereka kwa Ine zokolola zanu zochuluka ndi vinyo wanu wochuluka.

“Mundipatse ana anu achisamba aamuna. 30Muchite chimodzimodzi ndi ngʼombe zanu ndi nkhosa zanu. Mwana woyamba kubadwa azikhala ndi amayi ake masiku asanu ndi awiri. Koma pa tsiku lachisanu ndi chitatu mwanayo muzimupereka kwa Ine.

31“Inu mukhale anthu anga opatulika. Choncho musadye nyama ya chiweto chimene chaphedwa ndi zirombo. Nyamayo muwaponyere agalu.”

New Russian Translation

Исход 22:1-31

Законы об имуществе

1– Если кто-то украдет вола или овцу и зарежет их или продаст, то он заплатит пять волов за вола и четыре овцы за овцу. 2Если вора застигнут при взломе и изобьют так, что он умрет, то тот, кто его бил, не виноват в убийстве. 3Но если это случится после восхода солнца, тогда он виноват. Вор должен возместить украденное. Если у него ничего нет, то пусть его продадут в рабство, чтобы возместить украденное. 4Если краденый скот будет найден у него живым, то все равно, вол это, осел или овца, он должен заплатить вдвое.

5Если кто-то потравит чужое поле или виноградник, пустив скотину на чужое поле, то пусть возместит за потраву лучшим урожаем со своего поля или виноградника.

6Если загорится огонь и, охватив терновые кусты, спалит скирды или несжатое зерно в поле, то тот, кто пустил огонь, должен возместить сгоревшее.

7Если кто-то отдаст ближнему на хранение серебро или вещи и их украдут из дома поручившегося, то вор, если его поймают, заплатит вдвое. 8Но если вора не найдут, поручившийся должен предстать перед судьями22:8 Или: «перед Богом». и поклясться, что не посягал на чужое добро.

9При всяком споре о праве на имущество, будь то вол, осел, овца, одежда или другое пропавшее имущество, о котором кто-то говорит: «Это мое», обе стороны должны представить дело судьям22:9 Или: «Богу».. Тот, кого судьи объявят22:9 Или: «кого Бог объявит». неправым, заплатит истцу вдвое.

10Если кто-то отдаст ближнему осла, вола, овцу или другую скотину на хранение, и она умрет, или будет покалечена, или угнана, когда никто не видит, 11то его спор с ответчиком будет решен клятвой перед Господом, что ответчик не посягал на чужое добро. Истец должен принять клятву, и возмещения не будет. 12Но если скотину у ответчика украли, то он должен возместить истцу за украденное. 13Если скотину растерзали дикие звери, то пусть ответчик принесет труп животного для доказательства. Тогда он не будет возмещать убытки за растерзанное животное.

14Если кто-то возьмет у ближнего скотину взаймы, а она получит увечье или умрет, когда хозяина не будет рядом, то он должен возместить. 15Но если хозяин будет в тот момент рядом, то взявший ее взаймы не будет платить. Если скотина была взята внаем, пусть потерю покроет плата за наем.

Общественные законы

16– Если человек соблазнит девушку, которая не давала обещания выйти замуж, и переспит с ней, то он должен заплатить свадебный выкуп, и она станет его женой. 17Если же отец откажется отдать ее ему, он все равно должен заплатить выкуп, какой полагается за девушку.

18Не оставляй в живых колдунью.

19Всякого, кто совокупляется с животным, следует предать смерти.

20Всякого, приносящего жертвы иному богу, кроме Господа, следует истребить22:20 На языке оригинала стоит слово, которое говорит о полном посвящении предметов или людей Господу, часто осуществлявшемся через их уничтожение..

21Не притесняй поселенцев, не угнетай их: вы сами были поселенцами в Египте.

22Не притесняй вдов и сирот. 23Если вы будете делать это, они призовут на помощь Меня, и Я непременно услышу. 24Мой гнев вспыхнет, и Я убью вас мечом. Ваши жены сами станут вдовами, а дети – сиротами.

25Если даешь взаймы бедняку из Моего народа, то не будь, как ростовщик – не налагай процентов. 26Если возьмешь у ближнего в залог одежду, то верни ее к закату: 27может быть, ему больше нечем укрыться, кроме этой одежды. Как ему спать без нее? Когда он взмолится ко Мне, Я услышу, потому что Я милостив.

28Не оскорбляй Бога22:28 Или: «судей». и не говори плохо о вожде твоего народа.

29Не медли совершать приношения из твоих амбаров и кувшинов22:29 Смысл этого места в еврейском тексте неясен..

Отдавайте Мне первенцев из своих сыновей. 30Отдавайте Мне первородное из крупного и мелкого скота. Пусть животные остаются семь дней с матерью, а на восьмой день отдавайте их Мне.

31Будьте Моим святым народом: не ешьте мясо животного, растерзанного дикими зверями. Бросайте его собакам.