Eksodo 2 – CCL & TNCV

The Word of God in Contemporary Chichewa

Eksodo 2:1-25

Kubadwa kwa Mose

1Ndipo munthu wina wa fuko la Levi anakwatira mkazi wa fuko lomwelo. 2Mkaziyo anatenga pathupi ndipo anabereka mwana wamwamuna. Ataona kuti mwanayo anali wokongola, anamubisa kwa miyezi itatu. 3Koma mwanayo atafika pa msinkhu woti sakanathanso kubisidwa, amayi ake anatenga kadengu kopangidwa ndi bango nakamata phula. Kenaka anayika mwanayo mʼmenemo ndi kukamuyika pa mabango mu mtsinje wa Nailo. 4Mlongo wake wa mwanayo anayima pataliko kuti aone chimene chidzamuchitikira mwanayo.

5Mwana wamkazi wa Farao anapita ku mtsinje wa Nailo kukasamba ndipo adzakazi ake ankayenda mʼmbali mwa mtsinjewo. Tsono mwana wa Farao uja anaona kadenguko pakati pa mabango ndipo anatuma mdzakazi wake kuti akakatenge. 6Iye atavundukula anaona mwana wamwamuna akungolira. Iye anamva naye chisoni mwana uja, nati, “Ameneyu ndi mmodzi mwa ana a Chihebri.”

7Kenaka mlongo wake wa mwanayo anafunsa mwana wa Farao kuti, “Ndingapite kukakupezerani mmodzi mwa amayi a Chihebri kuti azikakulererani mwanayu?”

8Iye anayankha kuti, “Inde, pita.” Ndipo mtsikanayo anapita nakayitana amayi a mwanayo. 9Mwana wa Farao anati, “Tengani mwanayu mukandilerere, ndidzakulipirani.” Mayiyo anatenga mwanayo kukamulera. 10Mwanayo atakula anakamupereka kwa mwana wa Farao ndipo anakhala mwana wake. Iye anamutcha dzina lake Mose, popeza anati, “Ndinamuvuwula mʼmadzi.”

Mose Athawira ku Midiyani

11Tsiku lina, Mose atakula, anapita kumene kunali anthu a mtundu wake ndipo anawaona akugwira ntchito yowawa. Iye anaona Mwigupto akumenya Mhebri, mmodzi mwa anthu a mtundu wake. 12Atayangʼana uku ndi uku, naona kuti panalibe wina aliyense, Mose anamupha Mwiguptoyo ndipo anamukwirira mu mchenga. 13Mmawa mwake Mose anapita ndipo anaona anthu awiri a Chihebri akumenyana. Iye anafunsa amene anali wolakwa kuti, “Chifukwa chiyani ukumenya Mhebri mnzako?”

14Munthu uja anati, “Kodi ndani anakuyika kuti ukhale wotilamulira ndi wotiweruza? Kodi ukufuna kundipha monga momwe unaphera Mwigupto uja?” Mose anachita mantha ndipo anati mu mtima mwake, “Chimene ndinachita chija chadziwika.”

15Farao atamva zimenezi anafuna kuti aphe Mose, koma Mose anathawa ndipo anapita kukakhala ku Midiyani. Ali kumeneko, tsiku lina anakhala pansi pafupi ndi chitsime. 16Wansembe wa ku Midiyaniko anali ndi ana aakazi asanu ndi awiri. Iwowa anabwera kudzatunga madzi ndi kudzaza mu zomwera kuti amwetse nkhosa za abambo awo. 17Koma kunabwera abusa ena amene anathamangitsa atsikana aja. Ndiye Mose anayimirira nawathandiza atsikana aja ndi kumwetsa nkhosa zawo.

18Atsikana aja atabwerera kwa abambo awo Reueli, iye anawafunsa kuti, “Chifukwa chiyani lero mwabwera msanga?”

19Atsikanawo anayankha kuti, “Mwigupto wina ndiye watilanditsa kwa abusa. Ndiponso anatitungira madzi ndi kumwetsa ziweto zathu.”

20Tsono Reueli anafunsa ana ake kuti, “Ndiye ali kuti munthuyo? Chifukwa chiyani mwamusiya? Kamuyitaneni kuti adzadye.”

21Mose anavomera kukhala ndi Reueli, ndipo anamupatsa Zipora kuti akhale mkazi wake. 22Zipora anabereka mwana wa mwamuna amene Mose anamutcha Geresomu, popeza anati, “Ndakhala mlendo mʼdziko la eni.”

23Nthawi yonseyo nʼkuti ana a Israeli akulira chifukwa cha ukapolo wawo uja. Iwo anafuwula kupempha thandizo, ndipo kulira kwawoko kunafika kwa Mulungu. 24Mulungu anamva kubuwula kwawo ndipo anakumbukira pangano lake ndi Abrahamu, Isake ndi Yakobo. 25Mulungu ataona Aisraeli aja ndi masautso awo, Iye anawamvera chifundo.

Thai New Contemporary Version

อพยพ 2:1-25

กำเนิดโมเสส

1มีชายหญิงตระกูลเลวีคู่หนึ่งอยู่กินเป็นสามีภรรยากัน 2ฝ่ายภรรยาตั้งครรภ์และให้กำเนิดบุตรชายคนหนึ่ง เมื่อนางเห็นว่าบุตรของตนน่ารักจึงซ่อนตัวเขาไว้เป็นเวลาสามเดือน 3แต่เมื่อนางไม่อาจซ่อนเด็กไว้ได้ต่อไป นางจึงนำต้นกกมาสานเป็นตะกร้า ยาด้วยชันและยางมะตอย แล้ววางเด็กลงในตะกร้า ปล่อยให้ลอยอยู่กลางกอปรือริมแม่น้ำไนล์ 4พี่สาวของทารกนั้นจับตาดูอยู่ห่างๆ คอยดูว่าจะเกิดอะไรขึ้นกับน้องชาย

5เมื่อพระธิดาของฟาโรห์เสด็จมาสรงน้ำที่แม่น้ำไนล์ และบรรดานางกำนัลกำลังเดินเลียบตลิ่ง พระนางทรงสังเกตเห็นตะกร้าในกอปรือจึงรับสั่งให้ทาสสาวไปนำมา 6เมื่อทรงเปิดดูก็เห็นทารกเพศชายกำลังร้องไห้ พระนางจึงรู้สึกสงสารและตรัสว่า “นี่ต้องเป็นทารกชาวฮีบรูแน่ๆ”

7พี่สาวของทารกนั้นจึงทูลถามพระธิดาว่า “ให้หม่อมฉันไปหาแม่นมชาวฮีบรูมาเลี้ยงเด็กให้ไหม?”

8พระนางรับสั่งว่า “ตกลง ไปหามาเถิด” เด็กหญิงนั้นจึงกลับบ้านไปตามมารดาของทารกนั้นมา 9พระธิดาของฟาโรห์ตรัสกับนางว่า “เอาเด็กคนนี้ไปเลี้ยงดูแทนฉันด้วย แล้วฉันจะให้ค่าจ้าง” ดังนั้นนางจึงอุ้มทารกกลับไปเลี้ยงดู 10ต่อมาเมื่อเด็กคนนั้นเติบโตขึ้น นางก็นำกลับมาเข้าเฝ้าพระธิดาของฟาโรห์ พระนางทรงรับเลี้ยงเขาเป็นโอรส และประทานนามว่าโมเสส2:10 คำว่าโมเสสมีเสียงคล้ายคำภาษาฮีบรูที่มีความหมายว่าฉุดขึ้นมา เพราะพระนางทรงตรัสว่า “เราได้ฉุดเขาขึ้นมาจากน้ำ”

โมเสสหนีไปมีเดียน

11เมื่อโมเสสเติบโตเป็นหนุ่มแล้ว วันหนึ่งเขาไปหาคนชนชาติเดียวกันกับเขา เห็นพวกเขาต้องตรากตรำทำงานหนัก และได้เห็นชาวอียิปต์คนหนึ่งทุบตีชาวฮีบรูชนชาติเดียวกันกับตน 12โมเสสเหลียวซ้ายแลขวาเห็นว่าไม่มีใครจึงฆ่าชาวอียิปต์คนนั้นแล้วหมกไว้ในทราย 13วันต่อมาเมื่อเขาออกไปและเห็นชาวฮีบรูสองคนต่อสู้กันอยู่จึงถามคนที่เป็นฝ่ายผิดว่า “ทำไมถึงทุบตีพี่น้องชาวฮีบรูของท่านอย่างนี้?”

14คนนั้นกล่าวว่า “ใครตั้งเจ้าเป็นเจ้านายปกครองและเป็นตุลาการตัดสินพวกเรา เจ้าคิดจะฆ่าฉันอย่างที่ฆ่าชาวอียิปต์คนนั้นหรือ?” โมเสสตกใจกลัวและคิดว่า “ผู้คนคงรู้สิ่งที่เราทำกันหมดแล้ว”

15เมื่อฟาโรห์ทรงทราบเรื่องก็พยายามจะประหารโมเสส แต่โมเสสหนีฟาโรห์ไปอาศัยอยู่ในดินแดนมีเดียน ขณะที่เขานั่งอยู่ริมบ่อน้ำแห่งหนึ่ง 16มีหญิงสาวเจ็ดคนซึ่งเป็นธิดาของปุโรหิตชาวมีเดียนออกมาตักน้ำใส่รางให้ฝูงสัตว์ของบิดากิน 17แล้วมีพวกคนเลี้ยงแกะมาไล่หญิงสาวเหล่านี้ แต่โมเสสลุกขึ้นมาช่วยและให้น้ำแก่ฝูงสัตว์ของพวกนาง

18เมื่อหญิงเหล่านั้นกลับไปหาเรอูเอลผู้เป็นบิดา เรอูเอลถามว่า “ทำไมวันนี้กลับบ้านเร็ว?”

19พวกนางตอบว่า “มีชายชาวอียิปต์คนหนึ่งช่วยป้องกันพวกเราจากคนเลี้ยงแกะ ทั้งยังช่วยตักน้ำให้ฝูงสัตว์ด้วย”

20บิดาจึงถามบุตรสาวทั้งหลายว่า “เขาอยู่ที่ไหน? ทำไมจึงทิ้งเขาไว้? ไปเชิญเขามารับประทานอาหารด้วยกันเถิด”

21โมเสสตกลงใจอาศัยอยู่กับเรอูเอล เรอูเอลได้ยกศิปโปราห์บุตรสาวให้เป็นภรรยาของโมเสส 22ศิปโปราห์คลอดบุตรชาย โมเสสตั้งชื่อให้ว่าเกอร์โชม2:22 คำว่าเกอร์โชมมีเสียงคล้ายคำภาษาฮีบรูที่มีความหมายว่าคนต่างด้าวที่นั่น ตามที่โมเสสกล่าวว่า “เราเป็นคนต่างด้าวในต่างแดน”

23หลายปีต่อมา กษัตริย์อียิปต์สิ้นพระชนม์ ชาวอิสราเอลคร่ำครวญเนื่องจากการเป็นทาสและร่ำร้องทูลขอความช่วยเหลือ เสียงร้องของพวกเขาขึ้นไปถึงพระเจ้า 24พระองค์ทรงได้ยินเสียงคร่ำครวญของพวกเขาและทรงระลึกถึงพันธสัญญาที่ให้ไว้กับอับราฮัม อิสอัค และยาโคบ 25ดังนั้นพระเจ้าทอดพระเนตรชนชาติอิสราเอลและทรงห่วงใยพวกเขา