Eksodo 15 – CCL & SNC

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Eksodo 15:1-27

Nyimbo ya Mose ndi Miriamu

1Ndipo Mose ndi Aisraeli anayimbira Yehova nyimbo iyi:

“Ine ndidzayimbira Yehova

pakuti wakwezeka mʼchigonjetso.

Kavalo ndi wokwera wake,

Iye wawaponya mʼnyanja.

2Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga;

ndiye chipulumutso changa.

Iye ndiye Mulungu wanga, ndipo ndidzamutamanda,

Mulungu wa makolo anga, ine ndidzamukweza.

3Yehova ndi wankhondo;

Yehova ndilo dzina lake.

4Magaleta a Farao ndi asilikali ake ankhondo

Iye wawaponya mʼnyanja.

Akatswiri ankhondo amphamvu a Farao

amizidwa mʼNyanja Yofiira.

5Nyanja yakuya inawaphimba;

Iwo anamira pansi ngati mwala.”

6Yehova, dzanja lanu lamanja

ndi laulemerero chifukwa cha mphamvu zake.

Ndithu Yehova, dzanja lanu lamanja

linaphwanya mdani.

7Ndi ulemerero wanu waukulu,

munagonjetsa okutsutsani.

Inu munatumiza mkwiyo wanu waukulu;

ndipo unawapsereza ngati udzu.

8Ndi mpweya wotuluka mʼmphuno mwanu

madzi anawunjikana pamodzi.

Nyanja yakuya ija inasanduka

madzi owuma gwaa kufika pansi.

9Mdaniyo anati,

“Ine ndidzawalondola, ndipo ndidzawagwira.

Ndidzagawa chuma chawo;

ndiye chokhumba changa chidzakwaniritsidwa.

Ine ndidzasolola lupanga langa,

ndi mkono wanga ndidzawawononga.”

10Koma Inu munawuzira mphepo yanu,

ndipo nyanja inawaphimba.

Iwo anamira ngati chitsulo

mʼmadzi amphamvu.

11Ndithu Yehova, pakati pa milungu,

ndani afanana nanu? Inu amene muli woyera,

ndiponso wotamandika wolemekezeka,

chifukwa cha ntchito zanu,

zazikulu ndi zodabwitsa?

12Munatambasula dzanja lanu lamanja

ndipo dziko linawameza.

13Ndi chikondi chanu chosasinthika mudzatsogolera

anthu amene munawawombola.

Ndi mphamvu zanu munawatsogolera

ku malo anu woyera.

14Anthu amitundu ina anamva za mbiriyi ndipo ananjenjemera ndi mantha,

mantha woopsa agwira anthu a dziko la Filisiti.

15Tsopano mafumu a ku Edomu agwidwa ndi mantha aakulu,

otsogolera a dziko la Mowabu akunjenjemera ndi mantha,

ndipo anthu a ku Kanaani asungunuka ndi mantha.

16Onse agwidwa ndi mantha woopsa.

Popeza anaona mphamvu zanu zazikulu,

iwo ayima chilili ngati mwala mpaka anthu anu,

Inu Yehova atadutsa;

inde mpaka atadutsa anthu amene munawagula.

17Inu mudzawalowetsa ndi kuwakhazikitsa

pa phiri lanu.

Pa malo pamene Inu Yehova munawapanga kuti muzikhalapo;

malo wopatulika amene Inu Ambuye munawakonza ndi manja anu.

18“Yehova adzalamula

mpaka muyaya.”

19Akavalo a Farao, magaleta ndi oyendetsa akavalo atalowa mʼnyanja, Yehova anawabwezera madziwo mʼnyanja ndi kuwamiza, koma Aisraeli anawoloka nyanjayo powuma. 20Ndipo Miriamu mneneri wamkazi, mlongo wa Aaroni anatenga zoyimbira ndipo akazi onse anamutsatira pambuyo, akuyimba ndi zoyimbira ndi kuvina. 21Miriamu anawayimbira nyimbo iyi:

“Imbirani Yehova,

chifukwa iye wapambana.

Kavalo ndi wokwerapo wake

Iye wawamiza mʼnyanja.”

Madzi a ku Mara ndi Elimu

22Ndipo Mose anatsogolera Israeli kuchoka ku nyanja yofiira ndi kupita ku chipululu cha Suri. Anayenda mʼchipululu masiku atatu wosapeza madzi. 23Ndipo anafika ku Mara. Koma sanathe kumwa madzi akumeneko chifukwa anali owawa. (Ndi chifukwa chake malowo amatchedwa Mara). 24Tsono anthu aja anadandaulira Mose ndi kumufunsa kuti, “Kodi tikumwa chiyani?”

25Ndipo Mose anapemphera kwa Yehova, ndipo Yehova anamuonetsa kamtengo. Iye anakaponya mʼmadzimo ndipo madzi anakhala abwino.

Kumeneko Yehova anawayikira lamulo ndi maweruziro. Kumenekonso Yehova anawayesa. 26Yehova anati, “Ngati inu mudzamvetsa bwino mawu anga, kuchita zolungama, kumvera malamulo anga ndi kusamalitsa zimene ndikukuwuzani ndiye kuti Ine sindidzayika pa inu matenda amene ndinayika pa anthu a ku Igupto popeza ndine Yehova amene ndimakuchiritsani.”

27Kenaka anafika ku Elimu, kumene kunali akasupe khumi ndi awiri ndi mitengo ya migwalangwa makumi asanu ndi awiri, ndipo anamanga misasa yawo kumeneko pafupi ndi madzi.

Slovo na cestu

2 Mojžíšova 15:1-27

1Tehdy zpíval Mojžíš a synové Izraelští píseň tuto Hospodinu, a řekli takto: Zpívati budu Hospodinu, neboť jest slavně zveleben; koně i s jezdcem uvrhl do moře. 2Síla má a píseň jest Hospodin, nebo vysvobodil mne. Onť jest Bůh můj silný, protož stánek vzdělám jemu; onť jest Bůh otce mého, protož vyvyšovati ho budu. 3Hospodin jest udatný bojovník, Hospodin jméno jeho. 4Vozy Faraonovy i vojsko jeho uvrhl do moře; a nejpřednější hejtmané jeho ztopeni jsou v moři Rudém. 5Propasti přikryly je; vpadli do hlubiny jako kámen. 6Pravice tvá, Hospodine, zvelebena jest v síle, pravice tvá, ó Hospodine, potřela nepřítele. 7A ve mnohé vyvýšenosti své podvrátil jsi povstávající proti tobě; pustils hněv svůj, kterýžto sežral je jako strniště. 8A duchem chřípí tvých shromážděny jsou vody, stály tekuté vody jako hromada, ssedly se propasti u prostřed moře. 9Řekl nepřítel: Honiti budu, dohoním se, budu děliti loupeže, nasytí se jimi duše má, vytrhnu meč svůj, zahladí je ruka má. 10Povanul jsi větrem svým, i přikrylo je moře; pohlceni jsou jako olovo v prudkých vodách. 11Kdo podobný tobě mezi silnými, ó Hospodine? Kdo jest tak, jako ty, velebný v svatosti, hrozný v chvalách, činící divy? 12Vztáhls pravici svou, i požřela je země. 13Zprovodíš v milosrdenství svém lid tento, kterýž jsi vykoupil; laskavě povedeš jej v síle své k příbytku svatosti své. 14Uslyší lidé, bouřiti se budou; bolest zachvátí obyvatele Filistinské. 15Tedy zkormoucena budou knížata Idumejská, silné Moábské podejme strach, rozplynou se všickni obyvatelé Kananejští. 16Připadne na ně strach a lekání, pro velikost ramene tvého; mlčeti budou jako kámen, dokudž nepřejde lid tvůj, ó Hospodine, dokudž nepřejde lid ten, kteréhožs sobě dobyl. 17Uvedeš je, a štípíš je na hoře dědictví svého, na místě, kteréž jsi k příbytku svému připravil, Hospodine, v svatyni, kterouž utvrdí ruce tvé, Pane. 18Hospodin kralovati bude na věky věků. 19Nebo vešli koni Faraonovi s vozy jeho i s jezdci jeho do moře, a obrátil na ně Hospodin vody mořské, synové pak Izraelští šli po suše u prostřed moře. 20I vzala Maria prorokyně, sestra Aronova, buben v ruku svou, a vyšly za ní všecky ženy s bubny a s píšťalami. 21I odpovídala jim Maria: Zpívejte Hospodinu, poněvadž slavně zveleben jest; koně i s jezdcem uvrhl do moře. 22Hnul pak Mojžíš lidem Izraelským od moře Rudého, a táhli na poušť Sur. I šli tři dni po poušti, a nenalezli vod. 23A přišedše do Marah, nemohli píti vod z Marah, nebo byly hořké; protož nazváno jest jméno jeho Marah. 24Z té příčiny reptal lid na Mojžíše, řka: Co budeme píti? 25I volal k Hospodinu, a ukázal mu Hospodin dřevo, kteréž jakž uvrhl do vod, učiněny jsou sladké vody. Tu vydal jemu práva a soudy, a tu ho zkusil. 26A řekl: Jestliže skutečně poslouchati budeš hlasu Hospodina Boha svého, a činiti budeš, což spravedlivého jest před očima jeho, a nakloníš uší k přikázaním jeho, a ostříhati budeš všech ustavení jeho: žádné nemoci, kterouž jsem dopustil na Egypt, nedopustím na tebe; nebo já jsem Hospodin, kterýž tě uzdravuji. 27I přišli do Elim, kdež bylo dvanácte studnic vod a sedmdesáte palm; i rozbili tu stany při vodách.