Deuteronomo 33 – CCL & SNC

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 33:1-29

Mose Adalitsa Mafuko a Aisraeli

1Awa ndi madalitso amene Mose, munthu wa Mulungu, anawapereka kwa Aisraeli asanafe. 2Iye anati:

“Yehova anabwera kuchokera ku Sinai

ndipo anatulukira kuchokera ku Seiri;

anawala kuchokera pa Phiri la Parani.

Iye anabwera ndi chiwunyinji cha angelo

kuchokera kummwera, moto woyaka uli mʼdzanja mwake.

3Ndithu ndinu amene mumakonda anthu anu;

opatulika ake onse ali mʼmanja mwake.

Onse amagwada pansi pa mapazi anu

kuchokera kwa inu amalandira malangizo,

4malamulo amene Mose anatipatsa,

chuma chopambana cha mtundu wa Yakobo.

5Iye anali mfumu ya Yesuruni

pamene atsogoleri a anthu anasonkhana,

pamodzi ndi mafuko a Israeli.

6“Lolani Rubeni akhale ndi moyo ndipo asafe,

anthu ake asachepe pa chiwerengero.”

7Ndipo ponena za Yuda anati:

“Inu Yehova, imvani kulira kwa Yuda;

mubweretseni kwa anthu ake.

Ndi manja ake omwe adziteteze yekha.

Inu khalani thandizo lake polimbana ndi adani ake!”

8Za fuko la Alevi anati:

“Tumimu wanu ndi Urimu ndi za

mtumiki wanu wokhulupirika.

Munamuyesa ku Masa;

munalimbana naye ku madzi a ku Meriba.

9Iye ananena za abambo ake ndi amayi ake kuti,

‘Sindilabadira za iwo.’

Sanasamale za abale ake

kapena ana ake,

koma anayangʼanira mawu anu

ndipo anateteza pangano lanu.

10Iye amaphunzitsa Yakobo malangizo anu

ndi malamulo anu kwa Israeli.

Amafukiza lubani pamaso panu

ndiponso amapereka nsembe zanu zonse zopsereza pa guwa lanu.

11Inu Yehova, dalitsani luso lake lonse

ndipo mukondwere ndi ntchito za manja ake.

Menyani adani awo mʼchiwuno

kanthani amene amuwukira kuti asadzukenso.”

12Za fuko la Benjamini anati:

“Wokondedwa wa Yehova akhale mwamtendere mwa Iye,

pakuti amamuteteza tsiku lonse,

ndipo amene Yehova amamukonda amawusa pa mapewa ake.”

13Za fuko la Yosefe anati:

“Yehova adalitse dziko lake

ndi mame ambiri ochokera kumwamba

ndiponso madzi ambiri ochokera pansi pa nthaka;

14ndi zinthu zambiri zimene zimacha ndi dzuwa

ndiponso ndi zokolola zabwino kwambiri zimene zimacha ndi mwezi uliwonse;

15ndi zipatso zabwino kwambiri zochokera mʼmapiri amakedzanawa

ndiponso zokolola zochuluka zochokera ku zitunda zakalekale;

16ndi mphatso zabwino kwambiri zochokera pa dziko lapansi ndi zonse zimene zili mʼmenemo

ndiponso kukoma mtima kwa Iye amene amakhala mʼchitsamba choyaka moto.

Madalitso onsewa akhale pa mutu pa Yosefe,

wapaderadera pakati pa abale ake.

17Ulemerero wake uli ngati ngʼombe yayimuna yoyamba kubadwa;

nyanga zake zili ngati za njati.

Ndi nyanga zakezo adzapirikitsa anthu a mitundu ina,

ngakhale iwo amene akukhala ku malekezero a dziko lapansi.

Nyanga zimenezi ndiye anthu miyandamiyanda a Efereimu;

nyanga zimenezi ndiye anthu 1,000 a Manase.”

18Za fuko la Zebuloni anati:

“Kondwera Zebuloni, pamene ukutuluka,

ndipo iwe, Isakara, kondwera mʼmatenti ako.

19Adzayitanira mitundu ya anthu kumapiri,

kumeneko adzaperekako nsembe zachilungamo;

kumeneko adzadyerera zinthu zochuluka zochokera ku nyanja,

chuma chobisika mu mchenga.”

20Za fuko la Gadi anati:

“Wodala amene amakulitsa malire a Gadi!

Gadi amakhala kumeneko ngati mkango,

kukhadzula mkono kapena mutu.

21Iye anadzisankhira dziko labwino kwambiri;

gawo la mtsogoleri anasungira iye.

Pamene atsogoleri a anthu anasonkhana,

anachita chifuniro cha Yehova molungama,

ndiponso malamulo onena za Israeli.”

22Za fuko la Dani anati:

“Dani ndi mwana wamkango,

amene akutuluka ku Basani.”

23Za fuko la Nafutali anati:

“Nafutali wadzaza ndi kukoma mtima kwa Yehova

ndipo ndi wodzaza ndi madalitso ake;

cholowa chake chidzakhala mbali ya kummwera kwa nyanja.”

24Za fuko la Aseri anati:

“Mwana wodalitsika kwambiri ndi Aseri;

abale ake amukomere mtima,

ndipo asambe mapazi ake mʼmafuta.

25Zotsekera za zipata zako zidzakhala za chitsulo ndi za mkuwa,

ndi mphamvu zako zidzakhala ngati masiku a moyo wako.

26“Palibe wina wofanana ndi Mulungu wa Yesuruni,

amene amakwera pa thambo kukuthandizani

ndiponso pa mitambo ya ulemerero wake.

27Mulungu wamuyaya ndiye pothawirapo pathu,

ndipo pa dziko lapansi amakusungani ndi mphamvu zosatha.

Adzathamangitsa patsogolo panu mdani wanu,

adzanena kuti, ‘Muwonongeni!’

28Motero Israeli adzakhala yekha mwamtendere;

zidzukulu za Yakobo zili pa mtendere

mʼdziko la tirigu ndi vinyo watsopano,

kumene thambo limagwetsa mame.

29Iwe Israeli, ndiwe wodala!

Wofanana nanu ndani

anthu opulumutsidwa ndi Yehova?

Iye ndiye chishango ndi mthandizi wanu

ndi lupanga lanu la ulemerero.

Adani ako adzakugonjera,

ndipo iwe udzapondereza pansi malo awo achipembedzo.”

Slovo na cestu

5 Mojžíšova 33:1-29

1Toto pak jest požehnání, kterýmž požehnal Mojžíš, muž Boží, synů Izraelských před svou smrtí, 2A řekl: Hospodin z Sinai přišel, a vzešel jim z Seir, zastkvěl se s hory Fáran, a přišel s desíti tisíci svatých, z jehožto pravice oheň zákona svítil jim. 3Jak velice miluješ lidi! Všickni svatí jeho jsou v ruce tvé, oni také přivinuli se k nohám tvým, vezmouť prospěch z výmluvností tvých. 4Zákon vydal nám Mojžíš, dědičný shromáždění Jákobovu, 5(Nebo byl v Izraeli jako král), když přední z lidu shromáždili se, i všecka pokolení Izraelská. 6Buď živ Ruben a neumírej, a muži jeho ať jsou bez počtu. 7Tolikéž požehnal i Judovi a řekl: Vyslyš, Hospodine, hlas Judův, a k lidu svému jej sprovozuj; ruce jeho budou bojovati za něj, a ty jemu spomáhati budeš proti nepřátelům jeho. 8O Léví také řekl: Thumim tvé a urim tvé bylo, Pane, při muži svatém tvém, kteréhož jsi zkusil v pokušení, a kterýž podlé tebe měl nesnáz při vodách Meribah, 9Kterýž řekl otci svému a matce své: Neohlédám se na vás; a bratří svých neznal, a o synech svých nevěděl; nebo ostříhají výmluvností tvých, a smlouvu tvou zachovávají. 10Vyučovati budou soudům tvým Jákoba, a zákonu tvému Izraele, a klásti budou kadidlo před tváří tvou, a obět zápalnou na oltáři tvém. 11Požehnejž, Hospodine, rytěřování jeho, a v práci rukou jeho zalib se tobě. Zlomuj ledví nepřátel jeho a těch, kteříž ho nenávidí, aby nepovstali. 12A o Beniaminovi řekl: Milý jest Hospodinu, bezpečně s ním bydliti bude; ochraňovati jej bude každého dne, a mezi rameny jeho přebývati. 13O Jozefovi pak řekl: Požehnaná země jeho od Hospodina pro nejlepší věci nebeské, pro rosu a vrchoviště zespod se prýštící, 14A pro nejlepší úrody sluncem vyzralé, a pro nejlepší věci časem měsíců došlé, 15I pro rozkoše hor nejstarších, a pro rozkoše pahrbků věčných, 16Pro nejlepší věci země i plnost její, vyplývající z milosti ve kři přebývajícího. Přijdiž to požehnání na hlavu Jozefovu, a na vrch hlavy odděleného z jiných bratří jeho. 17Prvorozeného, vola toho krása veliká bude, a rohové jednorožce rohové jeho, jimiž on trkati bude národy napořád až do končin země. A toť jsou mnozí tisícové Efraimovi a tisícové Manassesovi. 18O Zabulonovi také řekl: Vesel se Zabulon u vycházení svém, a Izachar v staních svých. 19Lidi na horu Boží svolají, a budou obětovati oběti spravedlnosti; nebo hojnost mořskou ssáti budou, a skryté poklady v písku. 20Gádovi pak řekl: Požehnaný, kterýž rozšiřuje Gáda. Onť jakožto lev bydliti bude, a uchvátí rameno i s hlavou. 21Kterýž opatřil ho prvotinami; nebo tam podílem skrze vydavatele zákona ubezpečen jest. Protož pobéřeť se s knížaty lidu, a spravedlnost Hospodinovu i soudy jeho s Izraelem vykonávati bude. 22O Danovi pak řekl: Dan jako lvíče lvové vyskakovati bude z Bázan. 23A Neftalímovi řekl: Ó Neftalíme, sytý přízní Páně, plný požehnání Hospodinova, západní a polední stranu přijmi za dědictví. 24O Asserovi také řekl: Asser požehnaný nad jiné syny, budeť milý bratřím svým, omočí v oleji nohu svou. 25Železo a měď pod šlepějemi tvými; pokudž trvati budou dnové tvoji, slovoutný budeš. 26Neníť žádného, jako Bůh silný, ó Izraeli, kterýž se vznáší na nebesích ku pomoci tobě, a u velebnosti své na oblacích nejvyšších. 27Ochrana tvá buď Bůh věčný, a zespod ramena věčnosti, kterýž vyžene nepřátely před tebou, aneb řekne: Vyhlaď je, 28Aby sám bezpečně bydlil Izrael, rodina Jákobova, a to v zemi obilím a vínem oplývající, jehož nebesa také i rosu vydávati budou. 29Blahoslavený jsi, Izraeli. Kdo jest podobný tobě, lide vysvobozený skrze Hospodina, jenž jest pavéza spomožení tvého a meč důstojnosti tvé? Tvoji zajisté nepřátelé poníženi budou, ale ty po všech vyvýšenostech jejich šlapati budeš.