Deuteronomo 33 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 33:1-29

Mose Adalitsa Mafuko a Aisraeli

1Awa ndi madalitso amene Mose, munthu wa Mulungu, anawapereka kwa Aisraeli asanafe. 2Iye anati:

“Yehova anabwera kuchokera ku Sinai

ndipo anatulukira kuchokera ku Seiri;

anawala kuchokera pa Phiri la Parani.

Iye anabwera ndi chiwunyinji cha angelo

kuchokera kummwera, moto woyaka uli mʼdzanja mwake.

3Ndithu ndinu amene mumakonda anthu anu;

opatulika ake onse ali mʼmanja mwake.

Onse amagwada pansi pa mapazi anu

kuchokera kwa inu amalandira malangizo,

4malamulo amene Mose anatipatsa,

chuma chopambana cha mtundu wa Yakobo.

5Iye anali mfumu ya Yesuruni

pamene atsogoleri a anthu anasonkhana,

pamodzi ndi mafuko a Israeli.

6“Lolani Rubeni akhale ndi moyo ndipo asafe,

anthu ake asachepe pa chiwerengero.”

7Ndipo ponena za Yuda anati:

“Inu Yehova, imvani kulira kwa Yuda;

mubweretseni kwa anthu ake.

Ndi manja ake omwe adziteteze yekha.

Inu khalani thandizo lake polimbana ndi adani ake!”

8Za fuko la Alevi anati:

“Tumimu wanu ndi Urimu ndi za

mtumiki wanu wokhulupirika.

Munamuyesa ku Masa;

munalimbana naye ku madzi a ku Meriba.

9Iye ananena za abambo ake ndi amayi ake kuti,

‘Sindilabadira za iwo.’

Sanasamale za abale ake

kapena ana ake,

koma anayangʼanira mawu anu

ndipo anateteza pangano lanu.

10Iye amaphunzitsa Yakobo malangizo anu

ndi malamulo anu kwa Israeli.

Amafukiza lubani pamaso panu

ndiponso amapereka nsembe zanu zonse zopsereza pa guwa lanu.

11Inu Yehova, dalitsani luso lake lonse

ndipo mukondwere ndi ntchito za manja ake.

Menyani adani awo mʼchiwuno

kanthani amene amuwukira kuti asadzukenso.”

12Za fuko la Benjamini anati:

“Wokondedwa wa Yehova akhale mwamtendere mwa Iye,

pakuti amamuteteza tsiku lonse,

ndipo amene Yehova amamukonda amawusa pa mapewa ake.”

13Za fuko la Yosefe anati:

“Yehova adalitse dziko lake

ndi mame ambiri ochokera kumwamba

ndiponso madzi ambiri ochokera pansi pa nthaka;

14ndi zinthu zambiri zimene zimacha ndi dzuwa

ndiponso ndi zokolola zabwino kwambiri zimene zimacha ndi mwezi uliwonse;

15ndi zipatso zabwino kwambiri zochokera mʼmapiri amakedzanawa

ndiponso zokolola zochuluka zochokera ku zitunda zakalekale;

16ndi mphatso zabwino kwambiri zochokera pa dziko lapansi ndi zonse zimene zili mʼmenemo

ndiponso kukoma mtima kwa Iye amene amakhala mʼchitsamba choyaka moto.

Madalitso onsewa akhale pa mutu pa Yosefe,

wapaderadera pakati pa abale ake.

17Ulemerero wake uli ngati ngʼombe yayimuna yoyamba kubadwa;

nyanga zake zili ngati za njati.

Ndi nyanga zakezo adzapirikitsa anthu a mitundu ina,

ngakhale iwo amene akukhala ku malekezero a dziko lapansi.

Nyanga zimenezi ndiye anthu miyandamiyanda a Efereimu;

nyanga zimenezi ndiye anthu 1,000 a Manase.”

18Za fuko la Zebuloni anati:

“Kondwera Zebuloni, pamene ukutuluka,

ndipo iwe, Isakara, kondwera mʼmatenti ako.

19Adzayitanira mitundu ya anthu kumapiri,

kumeneko adzaperekako nsembe zachilungamo;

kumeneko adzadyerera zinthu zochuluka zochokera ku nyanja,

chuma chobisika mu mchenga.”

20Za fuko la Gadi anati:

“Wodala amene amakulitsa malire a Gadi!

Gadi amakhala kumeneko ngati mkango,

kukhadzula mkono kapena mutu.

21Iye anadzisankhira dziko labwino kwambiri;

gawo la mtsogoleri anasungira iye.

Pamene atsogoleri a anthu anasonkhana,

anachita chifuniro cha Yehova molungama,

ndiponso malamulo onena za Israeli.”

22Za fuko la Dani anati:

“Dani ndi mwana wamkango,

amene akutuluka ku Basani.”

23Za fuko la Nafutali anati:

“Nafutali wadzaza ndi kukoma mtima kwa Yehova

ndipo ndi wodzaza ndi madalitso ake;

cholowa chake chidzakhala mbali ya kummwera kwa nyanja.”

24Za fuko la Aseri anati:

“Mwana wodalitsika kwambiri ndi Aseri;

abale ake amukomere mtima,

ndipo asambe mapazi ake mʼmafuta.

25Zotsekera za zipata zako zidzakhala za chitsulo ndi za mkuwa,

ndi mphamvu zako zidzakhala ngati masiku a moyo wako.

26“Palibe wina wofanana ndi Mulungu wa Yesuruni,

amene amakwera pa thambo kukuthandizani

ndiponso pa mitambo ya ulemerero wake.

27Mulungu wamuyaya ndiye pothawirapo pathu,

ndipo pa dziko lapansi amakusungani ndi mphamvu zosatha.

Adzathamangitsa patsogolo panu mdani wanu,

adzanena kuti, ‘Muwonongeni!’

28Motero Israeli adzakhala yekha mwamtendere;

zidzukulu za Yakobo zili pa mtendere

mʼdziko la tirigu ndi vinyo watsopano,

kumene thambo limagwetsa mame.

29Iwe Israeli, ndiwe wodala!

Wofanana nanu ndani

anthu opulumutsidwa ndi Yehova?

Iye ndiye chishango ndi mthandizi wanu

ndi lupanga lanu la ulemerero.

Adani ako adzakugonjera,

ndipo iwe udzapondereza pansi malo awo achipembedzo.”

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Второзаконие 33:1-29

Мусо благословляет роды Исроила

1Вот благословение, которое пророк Мусо дал исроильтянам перед смертью.

2Он сказал:

– Вечный пришёл от Синая,

взошёл над Своим народом от Сеира;

воссиял от горы Паран33:2 Синай, Сеир и Паран – места, которые ассоциируются с заключением священного соглашения исроильского народа со Всевышним и получением Закона (см. Исх. 19:18; Суд. 5:4-5; Авв. 3:3)..

Он шёл с мириадами святых

с юга, со склонов Своей горы.

3Истинно Он любит Свой народ33:3 Или: «народы».:

все Его святые в Его руке.

Все они припадают к Его стопам

и получают от Него наставление,

4Закон, который дал нам Мусо, –

наследие потомков Якуба.

5Вечный стал царём в Исроиле,

когда собирались вожди народа

вместе с родами Исроила.

6Пусть живёт Рувим и не умирает,

пусть не будут33:6 Или: «но пусть будут». малочисленны его потомки.

7А это он сказал об Иуде:

– Услышь, о Вечный, крик Иуды,

приведи его к его народу.

Своими руками пусть он защитит себя.

Будь ему подмогой против врагов!

8О Леви он сказал:

– Пусть Твой священный жребий33:8 Букв.: «туммим («совершенство») и урим («свет»)». С помощью этих предметов определяли волю Всевышнего, но как именно, сегодня не известно. принадлежит

благочестивому человеку33:8 Благочестивый человек – это может быть либо род Леви, либо Мусо или Хорун, как представители этого рода..

Ты, Вечный, испытал Леви в Массе;

спорил с ним у вод Меривы33:8 Масса и Мерива – см. Исх. 17:1-7 и Чис. 20:1-13..

9Он говорил об отце и матери:

«Мне нет дела до них».

Не признал своих братьев,

не знал своих детей.

Ведь левиты соблюдают Твоё слово

и хранят Твоё священное соглашение33:9 Когда Мусо был на горе Синай, исроильский народ сделал себе золотого тельца и поклонялся ему. После возвращения Мусо многие из рода Леви помогали ему восстановить порядок в лагере и наказать тех, кто поклонялся идолу, убивая даже своих родственников (см. Исх. 32:25-29)..

10Они учат Твоим правилам потомков Якуба

и Твоему Закону народ Исроила.

Они кладут перед Тобой благовония

и всесожжения на Твой жертвенник.

11Благослови, о Вечный, его силу

и благоволи к делу его рук.

Порази чресла восстающих на него,

порази ненавидящих его,

чтобы они не смогли больше встать.

12О Вениамине он сказал:

– Пусть возлюбленный Вечным безопасно покоится при Нём,

ведь Он защищает его весь день.

Тот, кого любит Вечный,

покоится между Его плечами.

13О Юсуфе он сказал:

– Пусть благословит Вечный его землю

драгоценной росой с небес

и ручьями, бегущими из земли;

14лучшим, что даёт солнце,

лучшим урожаем каждого месяца;

15отборнейшими дарами древних гор

и плодородием вечных холмов;

16лучшими дарами земли и её полнотой,

милостью Того, Кто пребывал в горящем кусте33:16 См. Исх. 3:2..

Пусть все эти благословения снизойдут на голову Юсуфа,

на темя вождя между братьями33:16 Или: «темя отделённого от своих братьев»..

17Величием он подобен первородному быку,

его сила – сила дикого быка.

Рогами он станет бодать народы,

даже те, что на краях земли.

Его рога – десятки тысяч Ефраима,

его рога – тысячи Манассы.

18О Завулоне он сказал:

– Радуйся, Завулон, когда выходишь,

и ты, Иссокор, в своих шатрах.

19Они призовут народы к горе

и принесут там предписанные жертвы.

Они будут наслаждаться изобилием морей,

сокровищами, скрытыми в песке.

20О Гаде он сказал:

– Благословен расширяющий владения Гада!

Гад живёт там, подобно льву,

терзая и мышцу, и голову.

21Он выбрал себе лучшую землю,

ему отведена доля вождя.

Когда собрались главы народа,

он исполнил праведную волю Вечного

и Его правосудие Исроилу.

22О Доне он сказал:

– Дон – львёнок,

прыгающий с Бошона.

23О Неффалиме он сказал:

– Неффалим насыщен благоволением Вечного

и исполнен Его благословением.

Он унаследует Генисаретское озеро и землю на юге.

24Об Ошере он сказал:

– Ошер – благословеннейший из сыновей;

пусть будут благосклонны к нему братья.

Пусть его оливы принесут столько масла,

что он даже сможет омывать в нём ноги.

25Засовы твоих ворот будут из железа и бронзы,

твоё богатство будет неисчислимым, как твои дни.

26Нет подобного Богу Исроила,

Который мчится по небесам к тебе на помощь,

на облаках в Своём величии.

27Извечный Бог – твоё прибежище,

руки вечные носят тебя.

Он прогонит врага от тебя,

и скажет: «Истреби его!»

28И будет Исроил жить в безопасности,

источник Якуба будет защищён

в земле пшеницы и молодого вина,

где небеса источают росу.

29Благословен ты, Исроил!

Кто подобен тебе,

народу, спасённому Вечным?

Он тебе щит и помощник,

и славный твой меч.

Враги твои будут пресмыкаться пред тобой,

а ты будешь попирать их капища33:29 Или: «шею»..