Deuteronomo 28 – CCL & TNCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 28:1-68

Madalitso Akumvera

1Ngati mumvera Yehova Mulungu wanu ndi kutsatira mosamalitsa malamulo ake onse amene ndikukupatsani lero lino, Yehova Mulungu wanu adzakukwezani pamwamba pa mitundu yonse ya pa dziko lapansi. 2Madalitso awa adzabwera kwa inu ndi kuyenda nanu ngati mumvera Yehova Mulungu wanu:

3Mudzadalitsika mʼmizinda yanu ndi kudalitsika mʼdzikolo.

4Yehova adzadalitsa ana anu, zokolola za mʼdziko lanu, ngʼombe zanu pamodzi ndi ziweto zanu zonse.

5Dengu lanu ndi chiwaya chanu cha buledi zidzadalitsika.

6Mudzadalitsika pa kulowa kwanu ndi pa kutuluka kwanu.

7Yehova adzaonetsetsa kuti adani anu amene adzakuwukirani agonjetsedwe pamaso panu. Iwo adzabwera kwa inu kuchokera mbali imodzi koma adzakuthawani ku mbali zisanu ndi ziwiri.

8Yehova adzatumiza madalitso pa nkhokwe zanu ndi pa chilichonse chimene muchikhudza. Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani mʼdziko limene akukupatsani.

9Yehova Mulungu wanu adzachititsa kuti mukhale anthu ake opatulika, monga momwe analonjezera pa malumbiro ake, ngati musunga malamulo ake ndi kuyenda mʼnjira zake. 10Pamenepo anthu onse a dziko lapansi adzaona kuti mumadziwika ndi dzina la Yehova ndipo adzakuopani. 11Yehova adzakupambanitsani kwambiri ndipo adzakupatsani ana ambiri, ziweto zambiri, ndi zokolola zochuluka, mʼdziko limene Yehova analumbira kwa makolo anu kuti adzakupatsani.

12Yehova adzatsekula kumwamba kumene amasungirako chuma chake, kutumiza mvula mʼdziko lanu pa nthawi yake ndi kudalitsa ntchito yonse ya manja anu. Mudzakongoza mitundu yambiri koma inu simudzakongola kwa aliyense. 13Yehova adzakuthandizani kukhala mutu osati mchira. Mukakhala ndi chidwi ndi malamulo a Yehova Mulungu wanu amene ndikukupatsani lero lino ndi kuwatsata mosamalitsa, inu mudzakhala apamwamba nthawi zonse osati apansi. 14Musapatukire ku dzanja lamanja kapena lamanzere pa lamulo lina lililonse limene ndikukupatsani lero lino ndi kumatsatira kapena kuyitumikira milungu ina.

Matemberero Akusamvera

15Koma ngati simumvera Yehova Mulungu wanu ndi kusatsata mosamalitsa malamulo ake ndi malangizo ake onse amene ndikukupatsani lero lino, matemberero awa adzabwera pa inu ndikukugonjetsani:

16Mudzatembereredwa mu mzinda ndi kutembereredwa mʼmudzi.

17Dengu lanu ndi chiwaya chanu cha buledi zidzatembereredwa.

18Zipatso za mʼmimba mwanu zidzatembereredwa, ndiponso zomera za mʼdziko lanu, ana angʼombe zanu ndi ana ankhosa zanu zidzatembereredwa.

19Mudzatembereredwa pa kulowa kwanu ndi pa kutuluka kwanu.

20Yehova adzakutumizirani matemberero, chisokonezo ndi minyozo pa chilichonse chimene mudzachichita mpaka mudzawonongedwa ndi kukhala bwinja mofulumira chifukwa cha zoyipa zimene mwazichita pa kumutaya Yehova. 21Yehova adzakugwetserani mliri wa matenda mpaka atakuwonongani mʼdziko limene mukulowa kukalitengali. 22Yehova adzakukanthani ndi nthenda yowondetsa, ya malungo ndi ya zotupatupa, ndi kutentha kwakukulu ndi chilala, ndi chinsikwi ndi chiwawu zimene zidzakusautsani mpaka mutawonongeka. 23Mitambo ya pamutu panu idzawuma ngati mkuwa ndipo sidzagwetsa mvula mpaka nthaka yanu idzawuma gwaa ngati chitsulo. 24Mʼmalo mwa mvula Yehova adzakupatsani fumbi ndi dothi ndipo lidzakugwerani kuchokera kumwamba mpaka mutawonongeka.

25Yehova adzalola kuti adani anu akugonjetseni. Mudzadzera njira imodzi pokalimbana ndi adani anu koma pothawa mudzabalalika mbali zisanu ndi ziwiri. Mudzakhala chinthu chochititsa mantha pakati pa maufumu onse a dziko lapansi. 26Mitembo yanu idzadyedwa ndi mbalame zamumlengalenga ndi nyama zakutchire, ndipo palibe amene adzaziyingitse. 27Yehova adzakusautsani ndi zithupsa za ku Igupto ndi zotupatupa, zipere, ndi mphere zimene simudzachiritsika nazo. 28Yehova adzakusautsani inu ndi misala, khungu ndi chisokonekero cha maganizo. 29Masanasana mudzayenda ngati muli mu mdima, kumafufuzira njira ngati wosaona. Mudzakhala olephera pa chilichonse mungachite. Tsiku ndi tsiku mudzaponderezedwa ndi kuberedwa wopanda wokupulumutsani.

30Mudzachita chinkhoswe ndi mkazi, koma wina adzakulandani ndi kumukwatira. Mudzamanga nyumba koma simudzagonamo. Mudzalima munda wamphesa koma simudzadyako zipatso zake. 31Ngʼombe yanu yamtheno idzaphedwa inu muli pomwepo koma simudzadyako. Bulu wanu adzalandidwa kwa inu mwamakani osabwera nayenso. Nkhosa zanu zidzapatsidwa kwa adani anu, ndipo palibe amene adzazipulumutsa. 32Ana anu aamuna ndi aakazi adzaperekedwa kwa anthu a mitundu ina ndipo inu mudzafika potopa ndi kulefuka nʼkudikirira tsiku ndi tsiku kuti mwina anawo abwerako. 33Anthu amene simukuwadziwa adzakudyerani zokolola zanu, ndipo mudzakhala mukuponderezedwa mwankhanza masiku onse. 34Zimene muzidzaziona zidzakusokonezani mitu. 35Yehova adzakusautsani ndi zithupsa zaululu ndi zosachiritsika za mʼmawondo ndi mʼmiyendo ndipo zidzafalikira kuchoka kuphazi mpaka kumutu.

36Yehova adzakuthamangitsirani, inu ndi mafumu anu amene muwayika, ku dziko losadziwika kwa inu ndi kwa makolo anu. Kumeneko mudzakapembedza milungu ina, milungu ya mitengo ndi miyala. 37Inu mudzakhala chinthu chochititsa mantha kuchisunga ndiponso chinthu chotukwanidwa ndi chonyozeka kwa anthu a mitundu yonse kumene Yehova adzakuthamangitsirani.

38Mudzadzala mbewu zambiri ku munda koma mudzakolola pangʼono, chifukwa dzombe lidzaziwononga. 39Mudzadzala mpesa ndi kulimirira koma vinyo wake simudzamumwa kapena kukolola mphesazo, chifukwa mphutsi zidzadya mphesazo. 40Mudzakhala ndi mitengo ya olivi mʼdziko lanu lonse koma simudzagwiritsa ntchito mafuta ake, chifukwa zipatso zake zidzayoyoka. 41Mudzabereka ana aamuna ndi aakazi koma sadzakhala anu, chifukwa adzapita ku ukapolo. 42Magulumagulu a dzombe adzawononga mitengo yanu ndi mbewu za mʼdziko lanu.

43Mlendo wokhala pakati panu adzatukuka kuposa inu, koma inuyo mudzaloweralowera pansi. 44Iye adzakubwereketsani, koma inu simudzatha kubwereketsa. Iye adzakhala mutu ndipo inu mudzakhala mchira.

45Matemberero onsewa adzabwera pa inu. Adzakulondolani ndi kukugonjetsani mpaka mutawonongeka, chifukwa simunamvere Yehova Mulungu wanu ndi kusunga malamulo ndi malangizo amene anakupatsani. 46Matemberero amenewa adzakhala chizindikiro ndi chozizwitsa kwa inu ndi zidzukulu zanu mpaka kalekale. 47Pakuti inu simunatumikire Yehova Mulungu wanu pa nthawi imene zinthu zinkakuyenderani bwino, 48chomwecho pa nthawi ya njala ndi ludzu, ya maliseche ndi umphawi woopsa, mudzatumikira adani amene Yehova adzakutumizirani. Iye adzayika goli lachitsulo mʼkhosi mwanu kufikira atakuwonongani.

49Yehova adzakutumizirani mtundu wa anthu kuchokera kutali kumapeto kwa dziko lapansi nudzachita ngati mphungu yowulukira pansi, mtundu wa anthu umene chiyankhulo chawo simudzachimva, 50mtundu wooneka wochititsa mantha, wopanda ulemu kwa okalamba kapena chisoni kwa ana. 51Iwo adzagwira ana a ziweto zanu, natenga zokolola za mʼdziko lanu kufikira mutawonongeka. Iwo sadzakusiyirani tirigu, vinyo watsopano kapena mafuta a olivi, kapena mwana wangʼombe aliyense kapena mwana wankhosa mpaka mutasanduka bwinja. 52Iwo adzathira nkhondo mizinda yonse mʼdziko lanu lonse mpaka malinga anu ataliatali omwe mumadalira aja atagwa. Adzathira nkhondo mizinda yonse ya mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.

53Chifukwa cha zosautsa zimene mdani wanu adzabweretsa pa nthawi yokuthirani nkhondo, inu mudzadya ana anu, mnofu wa ana anu aamuna ndi aakazi amene Yehova Mulungu wanu wakupatsani. 54Ngakhale munthu woleza mtima ndi wachifundo kwambiri pakati panu sadzakhala ndi chifundo pa mʼbale wake weniweni kapena mkazi wake amene iye amamukonda kapena ana ake otsalawo, 55ndipo sadzagawirako aliyense wa iwo mnofu wa ana ake amene akudyawo. Kadzakhala kali komweko basi kamene kamutsalira chifukwa cha msautso umene mdani wanu adzagwetsa pa nthawi yothira nkhondo mizinda yanu yonse. 56Mayi woleza mtima ndi wachifundo kwambiri pakati panu, uja woti sangayerekeze kuponda pansi, adzabisira mwamuna wake amene amamukonda ndi ana ake omwe aamuna ndi aakazi 57zotsalira za uchembere zochoka mʼmimba mwake ndi ana amene wabereka. Pakuti adzafuna kuti adye zimenezi yekha mobisa pa nthawi yothiridwa nkhondo chifukwa cha masautso amene mdani wanu adzagwetsa pa inu mʼmizinda yanu.

58Ngati simutsata mosamalitsa mawu onse a malamulo awa amene alembedwa mʼbuku lino, komanso ngati simuopa dzina la ulemerero ndi loopsa, dzina la Yehova Mulungu wanu, 59Yehova adzatumiza pa inu ndi zidzukulu zanu miliri yoopsa, zosautsa zowawa ndi zokhalitsa, ndi matenda aakulu ndi ovuta kuchiritsika. 60Adzakubweretserani matenda onse a ku Igupto aja mumawaopawa ndipo adzakukanirirani. 61Yehova adzakubweretseraninso mtundu uliwonse wa matenda ndi zosautsa zimene sizinalembedwe mʼbuku la malamulo lino, mpaka mutawonongeka. 62Inu aja munali ochuluka ngati nyenyezi zakumwamba mudzatsala ochepa chabe chifukwa simunamvere Yehova Mulungu wanu. 63Monga kunamukomera Yehova kukulemeretsani ndi kukuchulukitsani, momwemonso kudzamukondweretsa kukunthani ndi kukuwonongani. Inu mudzazulidwa kukuchotsani mʼdziko limene mukulowa kukalitengali.

64Kenaka Yehova adzakubalalitsani pakati pa anthu a mitundu yonse, kuchokera ku mapeto a dziko kufika ku mapeto ena. Kumeneko mudzapembedza milungu ina, milungu ya mitengo ndi ya miyala, imene inu eni kapena makolo anu sanayidziwepo. 65Pakati pa mitundu ya anthu imeneyi simudzapeza mpata, popanda malo woti nʼkuyikapo phazi. Kumeneko Yehova adzakupatsani moyo wa nkhawa, maso otopa ndi chiyembekezo, ndi mtima wosakhazikika. 66Inu mudzakhala osakhazikika mopitirira, odzazidwa ndi mantha usiku ndi usana womwe, osowa chitsimikizo cha pa moyo wanu. 67Mmawa muzidzati, “Chikhala anali madzulo!” ndipo madzulo mudzati, “Chikhala unali mmawa!” Mudzanena zimenezi chifukwa cha mantha amene adzakhale mu mtima mwanu ndi chifukwa cha zomwe muzidzaziona. 68Yehova adzakubwezani ku Igupto pa sitima zapamadzi paulendo umene Ine ndinati musawuyendenso. Kumeneko mudzadzitsatsa nokha kwa adani anu monga akapolo aamuna ndi aakazi, koma palibe amene adzakuguleni.

Thai New Contemporary Bible

เฉลยธรรมบัญญัติ 28:1-68

พระพรสำหรับการเชื่อฟัง

1หากท่านเชื่อฟังพระยาห์เวห์พระเจ้าของท่านอย่างครบถ้วน และหมั่นปฏิบัติตามพระบัญชาทั้งปวงซึ่งข้าพเจ้าแจ้งท่านในวันนี้ พระยาห์เวห์พระเจ้าของท่านจะทรงเชิดชูท่านเหนือประชาชาติทั้งปวงในโลก 2พรทั้งหมดนี้จะมีมาถึงท่านและดำรงอยู่กับท่าน หากท่านเชื่อฟังพระยาห์เวห์พระเจ้าของท่าน

3ท่านจะได้รับพรทั้งในเมืองและในทุ่งนา

4ท่านจะได้รับพรให้มีบุตรหลานมากมาย ให้ท้องทุ่งของท่านเกิดผลมาก และให้ฝูงสัตว์และฝูงแพะแกะของท่านมีลูกดก

5ท่านจะได้รับพรให้ตะกร้ามีพืชผลล้นหลาม และรางนวดแป้งเต็มไปด้วยขนมปัง

6ท่านจะได้รับพรไม่ว่าจะไปทางไหน

7องค์พระผู้เป็นเจ้าจะทรงปราบศัตรูทั้งหลายต่อหน้าท่าน พวกเขาจะเดินทัพมาสู้ท่านทางเดียว แต่แตกฉานซ่านเซ็นไปเจ็ดทาง

8องค์พระผู้เป็นเจ้าจะทรงอวยพรยุ้งฉางของท่านและทุกสิ่งที่ท่านลงมือทำ พระยาห์เวห์พระเจ้าของท่านจะทรงอวยพรท่านในดินแดนซึ่งพระองค์ประทานแก่ท่าน

9หากท่านถือรักษาพระบัญชาของพระยาห์เวห์พระเจ้าของท่านและดำเนินตามทางของพระองค์ องค์พระผู้เป็นเจ้าก็จะทรงตั้งท่านให้มั่นคงในฐานะชนชาติบริสุทธิ์ของพระองค์ตามที่ทรงสัญญาไว้กับท่านด้วยคำปฏิญาณ 10แล้วประชาชาติทั้งปวงในโลกจะเห็นว่าท่านได้รับการขนานนามตามพระนามของพระยาห์เวห์ และพวกเขาจะเกรงกลัวท่าน 11องค์พระผู้เป็นเจ้าจะประทานความเจริญรุ่งเรืองอย่างล้นเหลือแก่ท่าน ในเรื่องบุตรหลาน ลูกอ่อนของฝูงสัตว์ และพืชผลจากแผ่นดิน ในดินแดนที่ทรงปฏิญาณไว้กับบรรพบุรุษของท่านว่าจะยกให้ท่าน

12องค์พระผู้เป็นเจ้าจะทรงเปิดฟ้าสวรรค์ซึ่งเป็นคลังอันอุดมสมบูรณ์ของพระองค์ ให้ฝนตกในแผ่นดินของท่านตามฤดูกาล และจะทรงอวยพรงานทุกอย่างที่ท่านทำ ท่านจะให้หลายชาติกู้ยืม แต่ไม่ยืมจากใครเลย 13องค์พระผู้เป็นเจ้าจะทรงกระทำให้ท่านเป็นหัวไม่ใช่หาง ถ้าเพียงแต่ท่านใส่ใจพระบัญชาของพระยาห์เวห์พระเจ้าของท่านซึ่งข้าพเจ้าแจ้งท่านในวันนี้ และปฏิบัติตามอย่างเคร่งครัด ท่านจะอยู่เบื้องบนสุดเสมอ ไม่เคยอยู่เบื้องล่างเลย 14อย่าหันเหจากพระบัญชาซึ่งข้าพเจ้าแจ้งท่านในวันนี้ไปทางขวาหรือทางซ้าย อย่าไปติดตามและปรนนิบัติพระอื่นใด

คำสาปแช่งสำหรับการไม่เชื่อฟัง

15แต่หากท่านไม่เชื่อฟังพระยาห์เวห์พระเจ้าของท่านและไม่ใส่ใจปฏิบัติตามพระบัญชาและกฎหมายทั้งปวงซึ่งข้าพเจ้ากำลังแจ้งท่านในวันนี้ คำสาปแช่งทั้งปวงนี้ก็จะตกมาถึงท่าน

16ท่านจะถูกสาปแช่งทั้งในเมืองและในทุ่งนา

17ท่านจะถูกสาปแช่งโดยให้ตะกร้าของท่านปราศจากพืชผลและรางนวดแป้งไม่มีขนมปัง

18ท่านจะถูกสาปแช่งโดยให้มีลูกหลานน้อย และให้ท้องทุ่งของท่านไม่เกิดผล และฝูงวัวฝูงแพะแกะก็ไม่มีลูก

19ท่านจะถูกสาปแช่งไม่ว่าท่านจะไปทางไหน

20องค์พระผู้เป็นเจ้าจะทรงให้คำสาปแช่งตกอยู่แก่ท่าน ท่านจะเดือดร้อนวุ่นวายและล้มเหลวในกิจการทุกอย่างที่ท่านทำจนกว่าท่านจะถูกทำลายล้าง และถึงแก่หายนะอย่างรวดเร็ว เพราะความชั่วร้ายของท่านที่ได้ละทิ้งพระองค์28:20 ภาษาฮีบรูว่าเรา 21องค์พระผู้เป็นเจ้าจะลงโทษท่านด้วยโรคภัยไข้เจ็บต่างๆ จนกว่าพระองค์จะทำลายท่านให้หมดไปจากดินแดนที่ท่านจะเข้ายึดครอง 22องค์พระผู้เป็นเจ้าจะทรงบันดาลโรคภัยกัดกร่อนชีวิต ด้วยความเจ็บไข้และการอักเสบ ด้วยความร้อนระอุและความแห้งแล้ง ด้วยเชื้อราและแมลงทำลายต้นไม้ ซึ่งจะเล่นงานท่านจนท่านพินาศไป 23ท้องฟ้าเหนือศีรษะของท่านจะเป็นเหมือนทองสัมฤทธิ์ และแผ่นดินเบื้องล่างจะเป็นเหมือนเหล็ก 24องค์พระผู้เป็นเจ้าจะบันดาลให้ฝนกลายเป็นฝุ่นผงลงมาจากท้องฟ้าจนกว่าท่านจะถูกทำลายล้างไป

25องค์พระผู้เป็นเจ้าจะทรงทำให้ท่านพ่ายแพ้ศัตรู ท่านจะออกไปประจันหน้ากับพวกเขาทางเดียว แต่เตลิดหนีจากเขาเจ็ดทาง และท่านจะกลายเป็นสิ่งที่น่าสยดสยองแก่อาณาจักรทั้งปวงในโลก 26ซากศพของพวกท่านจะตกเป็นเหยื่อของนกในอากาศและสัตว์ป่าในแผ่นดินโลก และจะไม่มีผู้ใดขับไล่พวกมันไป 27องค์พระผู้เป็นเจ้าจะทรงใช้ฝีอย่างที่เคยเกิดกับอียิปต์ เนื้องอก แผล เนื้อร้าย และโรคคันซึ่งรักษาไม่หายทรมานท่าน 28องค์พระผู้เป็นเจ้าจะใช้ความคลุ้มคลั่ง ความมืดบอด และความวุ่นวายใจทรมานท่าน 29เวลากลางวันแสกๆ ท่านจะคลำสะเปะสะปะเหมือนคนตาบอดอยู่ในความมืด ท่านจะไม่ประสบความสำเร็จในกิจการใดๆ ที่ท่านทำเลย ท่านจะถูกกดขี่ข่มเหงและถูกปล้นชิงวันแล้ววันเล่าโดยไม่มีใครช่วยท่าน

30ท่านจะหมั้นหมายหญิงสาวไว้เป็นภรรยาแต่ชายอื่นจะข่มขืนนาง ท่านจะสร้างบ้านแต่ไม่ได้อาศัยในบ้านนั้น ท่านจะลงแรงปลูกสวนองุ่นแต่ไม่มีวันได้กินผลของมัน 31วัวของท่านจะถูกเชือดต่อหน้าต่อตาท่านแต่ท่านจะไม่ได้ลิ้มรสมันเลย ลาของท่านจะถูกไล่ต้อนไปต่อหน้าท่านและไม่ได้กลับคืนมา แกะของท่านจะถูกยกให้แก่ศัตรูและจะไม่มีใครช่วยปกป้องมัน 32บุตรชายบุตรสาวของท่านจะถูกยกให้เป็นทาสของชาติอื่น ท่านจะตั้งตาคอยลูกวันแล้ววันเล่าแต่ไม่อาจช่วยอะไรเขาได้ 33คนต่างชาติซึ่งท่านไม่เคยรู้จักจะมากินผลผลิตซึ่งท่านลงแรงเพาะปลูก ตลอดวันคืนแห่งชีวิตของท่านจะมีแต่การกดขี่ข่มเหงอันโหดร้ายทารุณ 34ท่านจะคลุ้มคลั่งไปเพราะเหตุการณ์โศกสลดที่เห็น 35องค์พระผู้เป็นเจ้าจะทรงทรมานกายของท่านด้วยฝีที่เจ็บปวดซึ่งรักษาไม่หาย เป็นแผลลามตั้งแต่ส้นเท้าขึ้นไปถึงกลางกระหม่อม

36องค์พระผู้เป็นเจ้าจะทรงเนรเทศท่านและกษัตริย์ซึ่งท่านเลือกให้ปกครองท่านนั้นไปยังชนชาติซึ่งท่านหรือบรรพบุรุษไม่เคยรู้จัก ท่านจะนมัสการพระอื่นๆ ซึ่งสร้างขึ้นจากไม้และหินที่นั่น 37ท่านจะกลายเป็นสิ่งที่น่าสยดสยอง เป็นขี้ปากและคำถากถางในหมู่ชาติต่างๆ ที่องค์พระผู้เป็นเจ้าทรงขับไล่ไสส่งท่านไป

38ท่านจะหว่านมากแต่จะเก็บเกี่ยวได้น้อยเพราะตั๊กแตนมากัดกินพืชผล 39ท่านจะปลูกสวนองุ่นและดูแลรักษา แต่ไม่ได้ดื่มเหล้าองุ่นหรือเก็บผลองุ่นเพราะมีหนอนมากัดกิน 40ท่านจะมีต้นมะกอกทั่วแผ่นดิน แต่ไม่มีน้ำมันให้ใช้เพราะผลมะกอกจะร่วงหมด 41ท่านจะมีบุตรชายบุตรสาว แต่ท่านจะรักษาเขาไว้ไม่ได้เพราะพวกเขาจะถูกฉุดคร่าไปเป็นเชลย 42ฝูงตั๊กแตนจะทำลายต้นไม้และพืชผลในแผ่นดินของท่านจนหมดสิ้น

43คนต่างด้าวซึ่งอาศัยอยู่ในหมู่พวกท่านจะรุ่งเรืองยิ่งขึ้นเรื่อยๆ แต่ท่านจะตกต่ำลงทุกที 44เขาจะเป็นฝ่ายให้ท่านยืม ไม่ใช่ท่านเป็นฝ่ายให้เขายืม เขาจะเป็นหัว ส่วนท่านจะเป็นหาง

45คำสาปแช่งทั้งหมดนี้จะตกแก่ท่าน และจะตามเล่นงานท่านจนย่อยยับไป เนื่องจากท่านไม่ได้เชื่อฟังพระยาห์เวห์พระเจ้าของท่านและไม่รักษาพระบัญชาและกฎหมายต่างๆ ที่ทรงให้ท่านไว้ 46สิ่งเหล่านี้จะเป็นหมายสำคัญและการอัศจรรย์แก่ท่านและแก่วงศ์วานของท่านตลอดไป 47เพราะท่านไม่ได้ปรนนิบัติพระยาห์เวห์พระเจ้าของท่านด้วยความชื่นชมยินดีและด้วยความเต็มใจในยามที่ท่านรุ่งเรือง 48ฉะนั้นท่านจะต้องปรนนิบัติศัตรูซึ่งองค์พระผู้เป็นเจ้าส่งมาเล่นงานท่านอย่างหิวโหยและกระหาย อย่างเปลือยกายและสิ้นเนื้อประดาตัว พระองค์จะทรงวางแอกเหล็กบนคอของท่านจนกว่าพระองค์จะทรงทำลายท่านให้สิ้นไป

49องค์พระผู้เป็นเจ้าจะทรงนำชนชาติหนึ่งจากแดนไกล จากสุดปลายแผ่นดินโลกซึ่งพูดภาษาที่ท่านไม่อาจเข้าใจมาต่อสู้กับท่านดั่งอินทรีโฉบ 50เป็นชนชาติซึ่งหน้าตาดุร้าย ไม่เคารพนับถือคนชราหรือเวทนาเด็กเล็ก 51พวกเขาจะกลืนกินลูกอ่อนจากฝูงสัตว์ของท่าน และพืชผลจากแผ่นดินของท่านจนท่านถูกทำลายสิ้น พวกเขาจะไม่เหลือเมล็ดข้าว เหล้าองุ่นใหม่ น้ำมัน ลูกวัว หรือลูกแกะจากฝูงสัตว์ของท่านจนกว่าท่านจะพินาศ 52ชนชาตินี้จะล้อมเมืองต่างๆ ทั่วดินแดนของท่าน ตราบจนกำแพงสูงซึ่งท่านเชื่อมั่นจะพังลง พวกเขาจะล้อมเมืองทั้งสิ้นทั่วดินแดนซึ่งพระยาห์เวห์พระเจ้าของท่านกำลังจะประทานแก่ท่าน

53ในช่วงถูกยึดเมืองซึ่งศัตรูทรมานท่านอย่างโหดร้ายทารุณนั้น ท่านถึงกับกินผลแห่งครรภ์ของท่าน คือกินเนื้อบุตรชายบุตรสาวที่พระยาห์เวห์พระเจ้าของท่านประทานแก่ท่าน 54แม้แต่ชายที่อ่อนโยนและใจอ่อนที่สุดในพวกท่านก็ยังใจดำต่อพี่น้องของตนเอง ต่อภรรยาที่รักและบุตรของเขาที่ยังรอดชีวิตอยู่ 55เขาจะไม่ยอมแบ่งเนื้อบุตรของตนที่เคี้ยวอยู่ให้คนเหล่านั้นสักคนเดียว นั่นเป็นทั้งหมดที่เขาเหลืออยู่ เพราะความทุกข์ยากที่ศัตรูก่อขึ้นขณะมาล้อมเมืองทั้งหมดของท่าน 56หญิงที่อ่อนโยนและใจอ่อนที่สุดในพวกท่าน ผู้ซึ่งเท้าแทบจะไม่แตะดิน จะไม่ยอมแบ่งปันให้กับสามีที่รักหรือบุตรชายบุตรสาวของตน 57นางจะซุกซ่อนทารกที่เพิ่งคลอดใหม่ของนางเพื่อเก็บไว้กินคนเดียวในช่วงยึดเมืองท่ามกลางความทุกข์ลำเค็ญด้วยน้ำมือของศัตรูในเมืองต่างๆ ของท่าน

58หากท่านไม่ใส่ใจปฏิบัติตามถ้อยคำทั้งปวงในบทบัญญัติซึ่งบันทึกไว้ในหนังสือเล่มนี้ และไม่ยำเกรงพระนามอันทรงเกียรติสิริและน่าเกรงขามของพระยาห์เวห์พระเจ้าของท่านทั้งหลาย 59องค์พระผู้เป็นเจ้าจะทรงส่งภัยพิบัติอันน่าสะพรึงกลัว ภัยพิบัติอันรุนแรงและเนิ่นนาน โรคภัยอันร้ายแรงและเรื้อรังมาเหนือท่านและวงศ์วานของท่าน 60พระองค์จะทรงนำโรคร้ายทั้งปวงแห่งอียิปต์ซึ่งท่านขยาดกลัวยิ่งนักมายังท่าน โรคนั้นจะคงอยู่กับท่าน 61องค์พระผู้เป็นเจ้าจะทรงนำโรคภัยและภัยพิบัติสารพัดแม้ไม่ได้บันทึกในหนังสือบทบัญญัตินี้มายังท่าน จนกว่าท่านจะถูกทำลายไป 62แม้ว่าท่านเคยมีจำนวนมากมายเหมือนดวงดาวในท้องฟ้า ท่านก็จะเหลืออยู่เพียงน้อยนิด เพราะท่านไม่เชื่อฟังพระยาห์เวห์พระเจ้าของท่าน 63เช่นเดียวกับที่องค์พระผู้เป็นเจ้าพอพระทัยจะให้ท่านเจริญและทวีจำนวนขึ้น พระองค์ก็จะพอพระทัยในการทำลายล้างท่าน ท่านจะถูกขุดรากถอนโคนจากแผ่นดินที่ท่านจะเข้าไปยึดครอง

64แล้วองค์พระผู้เป็นเจ้าจะทรงทำให้ท่านกระจัดกระจายไปตามชนชาติต่างๆ จากสุดโลกด้านหนึ่งไปยังอีกด้านหนึ่ง ท่านจะกราบไหว้พระอื่นๆ ซึ่งทำจากไม้และหินที่นั่น เป็นพระที่ท่านหรือบรรพบุรุษของท่านไม่เคยรู้จักมาก่อน 65ท่านจะไม่ได้อยู่อย่างสงบสุขเลยในหมู่ชนชาติเหล่านั้น ไม่มีแม้แต่ที่ให้วางเท้า องค์พระผู้เป็นเจ้าจะให้ท่านหวาดวิตก ทำให้ดวงตาอ่อนระโหยและดวงใจหดหู่สิ้นหวัง 66ชีวิตของท่านจะแขวนอยู่ในความสงสัย ท่านจะวิตกว้าวุ่นทั้งกลางวันและกลางคืน ไม่มีความมั่นใจใดๆ ในชีวิต 67ยามเช้าท่านจะพูดว่า “อยากให้เป็นเวลาเย็น!” และในยามเย็นท่านจะพูดว่า “อยากให้เป็นเวลาเช้า!” เพราะความอกสั่นขวัญแขวนที่จะเต็มล้นในใจของท่านและภาพต่างๆ ที่ตาของท่านจะเห็น 68องค์พระผู้เป็นเจ้าจะทรงส่งท่านลงเรือกลับไปอียิปต์ซึ่งข้าพเจ้าได้เตือนไม่ให้ท่านกลับไปที่นั่นอีก ท่านจะเสนอขายตัวเองเป็นทาสชายหญิงให้แก่ศัตรูของท่านที่นั่นแต่จะไม่มีใครซื้อ