Deuteronomo 14 – CCL & TNCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 14:1-29

Zoletsedwa pa Maliro

1Inu ndinu ana a Yehova Mulungu wanu. Osamadzichekacheka kapena kudzimeta pamphumi chifukwa cha abale anu amene amwalira, 2pakuti ndinu anthu opatulika a Yehova Mulungu wanu. Pakati pa anthu onse pa dziko lonse lapansi, Yehova wasankha inu kuti chikhale chuma chake chamtengo wapatali.

3Musamadye chinthu chilichonse chonyansa. 4Nyama zomwe mukhoza kudya ndi izi: ngʼombe, nkhosa, mbuzi, 5mbawala, gwape, mphoyo, mphalapala, ngoma, nyumbu ndi mbalale. 6Nyama iliyonse imene ili ndi chipondero chogawikana pakati ndi yobzikula mukhoza kudya. 7Komabe pakati pa nyama zimene zimabzikula kapena zogawikana zipondero, zimene simukuyenera kudya ndi ngamira, kalulu ndi mbira. Zimenezi ngakhale zimabzikula, zipondero zake sizogawikana, choncho ndi zodetsedwa, musadye. 8Nkhumba simabzikula ndi yodetsedwanso ngakhale ili ndi zipondero zogawikana. Musamadye nyama yake kapena kukhudza imene yafa.

9Mwa zamoyo zonse zimene zimakhala mʼmadzi, mukhoza kudya chilichonse chimene chili ndi minga ya pa msana ndi mamba. 10Koma chilichonse chimene chilibe minga ya pa msana ndi mamba musadye pakuti nʼchodetsedwa.

11Mukhoza kudya mbalame iliyonse yoyenera kudya. 12Koma simukuyenera kudya izi: mphungu, nkhwazi, mwimba, 13nankapakapa, akamtema, akhungubwi a mitundu yonse, ndi mtundu uliwonse wa miphamba, 14mtundu uliwonse wa khwangwala, 15kadzidzi wamphondo, kadzidzi wodzuma, chipudo, mtundu uliwonse wa akabawi, 16kadzidzi wamngʼono, chiswankhono ndi mantchichi, 17tsekwe, vuwo, dembo, 18indwa, zimeza za mitundu yonse, nsadzu ndi mleme.

19Zowuluka zonse za miyendo inayi ndi zodetsedwa. Musamadye zimenezi. 20Koma chowuluka chilichonse choyenera kudya mukhoza kudya.

21Musamadye chilichonse chimene mwachipeza chofaifa. Mukhoza kupatsa mlendo amene akukhala mu mzinda wina uliwonse wa mizinda yanu. Iyeyo akhoza kudya kapena mukhoza kugulitsa kwa wina aliyense amene sali wa mtundu wanu. Koma inu ndinu anthu opatulika a Yehova Mulungu wanu.

Musamaphike mwana wambuzi mu mkaka wa mayi wake.

Za Chakhumi

22Muzionetsetsa kuti mukupatula chakhumi pa zokolola zanu chaka chilichonse. 23Muzidyera chakhumi cha tirigu wanu, vinyo wanu watsopano ndi mafuta, ndi ana oyamba kubadwa a ngʼombe zanu pamaso pa Yehova Mulungu wanu pa malo amene adzasankhe ngati kokhalako dzina lake, kuti muphunzire kuopa Yehova Mulungu wanu. 24Koma ngati malo amenewa ali kutali kwambiri ndipo kuti inu mwadalitsidwa ndi Yehova Mulungu wanu, ndipo simungathe kunyamula chakhumi chanu (chifukwa chakuti malo amene Yehova adzasankha kukayikako dzina lake ali kutali kwambiri), 25ndiye musinthitse chakhumi chanucho ndi siliva, ndipo mutenge silivayo ndi kupita naye kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhe. 26Gwiritsani ntchito silivayo kugula chilichonse chimene muchifuna monga ngʼombe, nkhosa, vinyo kapena zakumwa zina zosasitsa, kapena china chilichonse chimene muchifuna. Ndipo inu ndi anthu a pa banja panu mudzazidyera komweko pamaso pa Yehova Mulungu wanu ndi kukondwera. 27Alevi okhala mʼmizinda yanu musaleke kuwathandiza popeza alibe gawo lawo la chuma kapena cholowa chawochawo.

28Kumapeto kwa zaka zitatu zilizonse muzibweretsa zakhumi zonse pa zokolola za chaka chimenecho ndi kuzisunga mʼmidzi yanu, 29kuti Alevi (amene alibe gawo lawo la chuma kapena cholowa chawochawo), alendo, ana ndi akazi amasiye, amene akukhala mʼmizinda yanu akhoza kubwera kudzadya ndi kukhuta. Ndipo kuti akutero Yehova Mulungu wanu akudalitseni pa ntchito zanu zonse.

Thai New Contemporary Bible

เฉลยธรรมบัญญัติ 14:1-29

อาหารที่ไม่เป็นมลทิน และอาหารที่เป็นมลทิน

(ลนต.11:1-23)

1ท่านทั้งหลายเป็นบุตรของพระยาห์เวห์พระเจ้าของท่าน ฉะนั้นเมื่อท่านไว้ทุกข์ให้ผู้ตาย อย่าเชือดเนื้อเถือหนังตัวเองหรือโกนหัว 2ท่านเป็นประชาชาติบริสุทธิ์แด่พระยาห์เวห์พระเจ้าของท่าน องค์พระผู้เป็นเจ้าทรงเลือกสรรท่านจากประชาชาติทั้งหลายบนพื้นโลกให้เป็นกรรมสิทธิ์ล้ำค่าของพระองค์

3อย่ารับประทานสิ่งใดๆ ซึ่งน่าขยะแขยง 4สัตว์ต่อไปนี้ท่านรับประทานได้ คือ วัว แกะ แพะ 5กวาง ละมั่ง เก้ง แพะป่า สมัน โครำขาว และแกะภูเขา 6ท่านรับประทานสัตว์ที่มีกีบแยกและเคี้ยวเอื้องได้ 7แต่อย่ารับประทานสัตว์ใดที่ไม่มีคุณสมบัติครบทั้งสองข้อนี้ ฉะนั้นอย่ารับประทานอูฐ กระต่าย กระจงผา ซึ่งเคี้ยวเอื้องแต่กีบไม่แยก สัตว์เหล่านี้เป็นมลทินตามระเบียบพิธีสำหรับท่าน 8อย่ารับประทานหมู ซึ่งแม้กีบแยกแต่ไม่เคี้ยวเอื้อง และอย่าแตะต้องซากของสัตว์เหล่านี้

9ท่านรับประทานสัตว์น้ำทั้งปวงที่มีครีบและเกล็ดได้ 10ท่านอย่ารับประทานสัตว์น้ำชนิดอื่นๆ ที่ไม่มีครีบและเกล็ดเพราะถือว่าเป็นมลทินสำหรับท่าน

11ท่านรับประทานสัตว์ปีกทั้งหลายที่ไม่เป็นมลทินได้ 12แต่นกเหล่านี้ท่านอย่ารับประทานคือ นกอินทรี แร้งหนวดแพะ แร้งดำ 13เหยี่ยวแดง เหยี่ยวดำ เหยี่ยวปีกแหลมพันธุ์ต่างๆ 14กาพันธุ์ต่างๆ 15นกเค้าใหญ่ นกเค้า นกนางนวล เหยี่ยวพันธุ์ต่างๆ 16นกฮูก นกทึดทือ นกแสก 17นกเค้าป่า นกออก นกกาน้ำ 18นกกระสา นกยางพันธุ์ต่างๆ นกกะรางหัวขวาน และค้างคาว

19แมลงมีปีกเป็นมลทินสำหรับท่าน อย่ารับประทานเลย 20ส่วนสัตว์มีปีกที่ไม่เป็นมลทิน ท่านรับประทานได้

21อย่ารับประทานสัตว์ที่ตายเอง ท่านอาจจะยกหรือขายให้คนต่างด้าวที่อาศัยในเมืองของท่าน เขารับประทานได้ ส่วนท่านอย่ารับประทานเพราะท่านเป็นชนชาติบริสุทธิ์แด่พระยาห์เวห์พระเจ้าของท่าน

อย่าต้มลูกแพะในน้ำนมแม่ของมัน

บทบัญญัติเรื่องสิบลด

22จงแยกหนึ่งในสิบของผลิตผลทั้งหมดจากไร่นาของท่านในแต่ละปีไว้ต่างหาก 23จงนำสิบลดนี้มารับประทานต่อหน้าพระยาห์เวห์พระเจ้าของท่านในที่ซึ่งพระองค์จะทรงเลือกเป็นที่สถาปนาพระนามของพระองค์ คือสิบลดจากเมล็ดข้าว เหล้าองุ่นใหม่ น้ำมัน และลูกหัวปีจากฝูงแพะแกะและฝูงวัว เพื่อท่านจะได้เรียนรู้ที่จะยำเกรงพระยาห์เวห์พระเจ้าของท่านเสมอ 24หากที่นั่นไกลมากและพระยาห์เวห์พระเจ้าของท่านทรงอวยพรท่าน และท่านไม่สามารถขนสิบลดมา (เนื่องจากสถานที่ซึ่งองค์พระผู้เป็นเจ้าทรงเลือกเป็นที่สถาปนาพระนามนั้นอยู่ไกลมาก) 25ท่านก็จงแลกสิบลดเป็นเงินแล้วนำมายังสถานที่ซึ่งพระยาห์เวห์พระเจ้าของท่านจะทรงเลือก 26จงใช้เงินนั้นซื้อสิ่งใดก็ได้ที่ท่านต้องการ ไม่ว่าจะเป็นวัว แกะ เหล้าองุ่นใหม่ หรือเครื่องดื่มอื่นๆ ที่ได้จากการหมัก หรือสิ่งของอื่นๆ ที่ท่านต้องการ แล้วท่านและครอบครัวจะรับประทานด้วยความปีติยินดีต่อหน้าพระยาห์เวห์พระเจ้าของท่าน 27อย่าละเลยคนเลวีในเมืองของท่าน เพราะพวกเขาไม่ได้รับส่วนแบ่งหรือมีกรรมสิทธิ์ของตน

28ทุกปลายปีที่สามจงนำสิบลดทั้งหมดของพืชผลของปีนั้นมาสะสมไว้ในเมืองของท่าน 29เพื่อชนเลวี (ผู้ซึ่งไม่มีส่วนแบ่งหรือกรรมสิทธิ์ของเขา) คนต่างด้าว ลูกกำพร้าพ่อ และหญิงม่ายที่อยู่ในเมืองของท่านจะได้รับประทานอย่างอิ่มหนำ แล้วพระยาห์เวห์พระเจ้าของท่านจะทรงอวยพรท่านในการงานทุกอย่างที่ท่านทำ